< Psaumes 51 >

1 Au maître de chant. Psaume de David. Lorsque Nathan le prophète vint le trouver, après qu’il fut allé vers Bethsabée. Aie pitié de moi, ô Dieu, selon ta bonté; selon ta grande miséricorde efface mes transgressions.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Pamene Mneneri Natani anabwera kwa iye atachita chigololo ndi Batiseba. Mundichitire chifundo, Inu Mulungu, molingana ndi chikondi chanu chosasinthika; molingana ndi chifundo chanu chachikulu mufafanize mphulupulu zanga.
2 Lave-moi complètement de mon iniquité, et purifie-moi de mon péché.
Munditsuke zolakwa zanga zonse ndipo mundiyeretse kuchotsa tchimo langa.
3 Car je reconnais mes transgressions, et mon péché est constamment devant moi.
Pakuti ndikudziwa mphulupulu zanga, ndipo tchimo langa lili pamaso panga nthawi zonse.
4 C’est contre toi seul que j’ai péché, j’ai fait ce qui est mal à tes yeux, afin que tu sois trouvé juste dans ta sentence, sans reproche dans ton jugement.
Motsutsana ndi Inu, Inu nokha, ndachimwa ndipo ndachita zoyipa pamaso panu, Kotero kuti inu mwapezeka kuti ndinu wolungama pamene muyankhula ndi pamene muweruza.
5 Voici que je suis né dans l’iniquité et ma mère m’a conçu dans le péché.
Zoonadi ine ndinali wochimwa pomwe ndimabadwa, wochimwa kuyambira pa nthawi imene amayi anga anakhala woyembekezera ine.
6 Voici que tu veux que la sincérité soit dans le cœur au dedans de moi fais-moi connaître la sagesse.
Zoonadi inu mumafuna choonadi mu ziwalo zamʼkati mwanga; mumandiphunzitsa nzeru mʼkati mwanga mwenimweni.
7 Purifie-moi avec l’hysope, et je serai pur; lave-moi, et je serai plus blanc que la neige.
Mundiyeretse ndi hisope ndipo ndidzayera, munditsuke ndipo ndidzayera kuposa matalala
8 Annonce-moi la joie et l’allégresse, et les os que tu as brisés se réjouiront.
Mundilole ndimve chimwemwe ndi chisangalalo, mulole kuti mafupa amene mwawamphwanya akondwere.
9 Détourne ta face de mes péchés, efface toutes mes iniquités.
Mufulatire machimo anga ndi kufafaniza zolakwa zanga zonse.
10 O Dieu, crée en moi un cœur pur, et renouvelle au dedans de moi un esprit ferme.
Mulenge mʼkati mwanga mtima woyera Inu Mulungu ndi kukonzanso mzimu wokhazikika mwa ine.
11 Ne me rejette pas loin de ta face, ne me retire pas ton esprit saint.
Musandichotse pamaso panu kapena kuchotsa Mzimu wanu Woyera mwa ine.
12 Rends-moi la joie de ton salut, et soutiens-moi par un esprit de bonne volonté.
Bwezeretsani mwa ine chimwemwe cha chipulumutso chanu ndipo mundipatse mzimu wofuna kumvera kuti undilimbitse.
13 J’enseignerai tes voies à ceux qui les transgressent, et les pécheurs reviendront à toi.
Pamenepo ndidzaphunzitsa anthu amphulupulu njira zanu kuti ochimwa adzabwerere kwa inu.
14 O Dieu, Dieu de mon salut, délivre-moi du sang versé, et ma langue célébrera ta justice.
Mundipulumutse ku tchimo lokhetsa magazi, Inu Mulungu, Mulungu wa chipulumutso changa, ndipo lilime langa lidzayimba zachilungamo chanu.
15 Seigneur, ouvre mes lèvres, et ma bouche publiera ta louange.
Inu Ambuye tsekulani milomo yanga, ndipo pakamwa panga padzalengeza matamando anu.
16 Car tu ne désires pas de sacrifices, — je t’en offrirais, — tu ne prends pas plaisir aux holocaustes.
Inu simusangalatsidwa ndi nsembe wamba. Ndikanapereka nsembe yopsereza, Inu simukondwera nayo.
17 Les sacrifices de Dieu, c’est un esprit brisé; ô Dieu, tu ne dédaignes pas un cœur brisé et contrit.
Nsembe za Mulungu ndi mzimu wosweka; mtima wosweka ndi wachisoni Inu Mulungu simudzawunyoza.
18 Dans ta bonté, répands tes bienfaits sur Sion, bâtis les murs de Jérusalem!
Mwa kukoma mtima kwanu mupange Ziyoni kuti alemere; mumange makoma a Yerusalemu.
19 Alors tu agréeras les sacrifices de justice, l’holocauste et le don parfait; alors on offrira des taureaux sur ton autel.
Kotero kudzakhala nsembe zachilungamo, nsembe yonse yopsereza yokondweretsa Inu; ndipo ngʼombe zazimuna zidzaperekedwa pa guwa lanu la nsembe.

< Psaumes 51 >