< Psaumes 118 >

1 Célébrez Yahweh, car il est bon, car sa miséricorde est éternelle.
Yamikani Yehova chifukwa ndi wabwino; pakuti chikondi chake chosasinthika ndi chosatha.
2 Qu’Israël dise: « Oui, sa miséricorde est éternelle! »
Israeli anene kuti: “Chikondi chake ndi chosatha.”
3 Que la maison d’Aaron dise: « Oui, sa miséricorde est éternelle! »
Banja la Aaroni linene kuti, “Chikondi chake ndi chosatha.”
4 Que ceux qui craignent Yahweh disent: « Oui, sa miséricorde est éternelle! » Pendant le trajet.
Iwo amene amaopa Yehova anene kuti: “Chikondi chake ndi chosatha.”
5 Du sein de ma détresse j’ai invoqué Yahweh: Yahweh m’a exaucé et m’a mis au large.
Ndili mʼmasautso anga ndinalirira Yehova, ndipo Iye anayankha pondichotsa mʼmasautsowo.
6 Yahweh est pour moi, je ne crains rien: que peuvent me faire des hommes?
Yehova ali nane; sindidzachita mantha. Munthu angandichite chiyani?
7 Yahweh est pour moi parmi ceux qui me secourent; je verrai la ruine de ceux qui me haïssent.
Yehova ali nane; Iye ndiye thandizo langa. Ndidzayangʼana adani anga mwachipambano.
8 Mieux vaut chercher un refuge en Yahweh, que de se confier aux hommes.
Nʼkwabwino kuthawira kwa Yehova kusiyana ndi kudalira munthu.
9 Mieux vaut chercher un refuge en Yahweh, que de se confier aux princes.
Nʼkwabwino kuthawira kwa Yehova kusiyana ndi kudalira mafumu.
10 Toutes les nations m’environnaient: au nom de Yahweh, je les taille en pièces.
Anthu a mitundu yonse anandizinga, koma mʼdzina la Yehova ndinawawononga.
11 Elles m’environnaient et m’enveloppaient: au nom de Yahweh, je les taille en pièces.
Anandizinga mbali zonse, koma mʼdzina la Yehova ndinawawononga.
12 Elles m’environnaient comme des abeilles: elles s’éteignent comme un feu d’épines; au nom de Yahweh, je les taille en pièces.
Anandizinga ngati njuchi, koma anatha msanga ngati moto wapaminga; mʼdzina la Yehova ndinawawononga.
13 Tu me poussais violemment pour me faire tomber, mais Yahweh m’a secouru.
Anandikankha uku ndi uko ndipo ndinali pafupi kugwa, koma Yehova anandithandiza.
14 Yahweh est ma force et l’objet de mes chants; il a été mon salut.
Yehova ndiye mphamvu yanga ndi nyimbo yanga; Iye wakhala chipulumutso changa.
15 Des cris de triomphe et de délivrance retentissent dans les tentes des justes. La droite de Yahweh a déployé sa force;
Mfuwu wachimwemwe ndi chipambano ukumveka mʼmatenti a anthu olungama mtima kuti: “Dzanja lamanja la Yehova lachita zamphamvu!
16 la droite de Yahweh est élevée, la droite de Yahweh a déployé sa force.
Dzanja lamanja la Yehova latukulidwa mmwamba Dzanja lamanja la Yehova lachita zamphamvu!”
17 Je ne mourrai pas, je vivrai, et je raconterai les œuvres de Yahweh.
Sindidzafa koma ndidzakhala ndi moyo ndipo ndidzalalika za ntchito ya Yehova.
18 Yahweh m’a durement châtié, mais il ne m’a pas livré à la mort. Le chef, arrivé devant le temple.
Yehova wandilanga koopsa, koma sanandipereke ku imfa.
19 Ouvrez-moi les portes de la justice, afin que j’entre et que je loue Yahweh. Les prêtres.
Tsekulireni zipata zachilungamo, kuti ndifike kudzayamika Yehova.
20 C’est la porte de Yahweh; les justes peuvent y entrer. Le chef du peuple.
Ichi ndicho chipata cha Yehova chimene olungama mtima okha adzalowerapo.
21 Je te célébrerai, parce que tu m’as exaucé, et que tu as été mon salut.
Ndidzakuyamikani chifukwa Inu munandiyankha; mwakhala chipulumutso changa.
22 La pierre rejetée par ceux qui bâtissaient est devenue la pierre angulaire. Les prêtres
Mwala umene amisiri omanga nyumba anawukana wasanduka wapangodya;
23 C’est l’œuvre de Yahweh, c’est une chose merveilleuse à nos yeux. Le peuple, en entrant.
Yehova ndiye wachita zimenezi ndipo nʼzodabwitsa pamaso pathu.
24 Voici le jour que Yahweh a fait; livrons-nous à l’allégresse et à la joie.
Lero ndiye tsiku limene Yehova walipanga; tiyeni tikondwere ndi kusangalala nalo.
25 O Yahweh, donne le salut! O Yahweh, donne la prospérité! Les prêtres, au chef.
Inu Yehova, tipulumutseni; Yehova, tipambanitseni.
26 Béni soit celui qui vient au nom de Yahweh! Nous vous bénissons de la maison de Yahweh!
Wodala amene akubwera mʼdzina la Yehova. Tikukudalitsani kuchokera ku nyumba ya Yehova.
27 Yahweh est Dieu, il fait briller sur nous la lumière. Les prêtres, au peuple. Attachez la victime avec des liens, jusqu’aux cornes de l’autel. Le peuple.
Yehova ndi Mulungu, ndipo kuwala kwake kwatiwunikira Ife. Lowani nawo pa mʼdipiti wa ku chikondwerero mutanyamula nthambi mʼdzanja lanu, mpaka ku nyanga za guwa.
28 Tu es mon Dieu, et je te célébrerai; mon Dieu, et je t’exalterai. Tous ensemble.
Inu ndinu Mulungu wanga, ndipo ndidzakuyamikani; Inu ndinu Mulungu wanga, ndipo ndidzakukwezani.
29 Célébrez Yahweh, car il est bon, car sa miséricorde est éternelle.
Yamikani Yehova chifukwa ndi wabwino; pakuti chikondi chake chosasinthika ndi chosatha.

< Psaumes 118 >