< Psaumes 109 >
1 Au maître de chant. Psaume de David. Dieu de ma louange, ne garde pas le silence!
Kwa mtsogoleri wamayimbidwe. Salimo la Davide. Mulungu amene ndimakutamandani, musakhale chete,
2 Car la bouche du méchant, la bouche du perfide, s’ouvre contre moi. Ils parlent contre moi avec une langue de mensonge,
pakuti anthu oyipa ndi achinyengo atsekula pakamwa pawo kutsutsana nane; iwo ayankhula motsutsana nane ndi malilime abodza.
3 ils m’assiègent de paroles haineuses, et ils me font la guerre sans motif.
Andizungulira ndi mawu audani, amandinena popanda chifukwa.
4 En retour de mon affection, ils me combattent, et moi, je ne fais que prier.
Mʼmalo mwa chikondi changa amandineneza, koma ine ndine munthu wapemphero.
5 Ils me rendent le mal pour le bien, et la haine pour l’amour.
Iwo amandibwezera zoyipa mʼmalo mwa zabwino, ndi udani mʼmalo mwa chikondi changa.
6 Mets-le au pouvoir d’un méchant, et que l’accusateur se tienne à sa droite!
Sankhani munthu woyipa kuti amutsutse iye; lolani wotsutsa ayime ku dzanja lake lamanja.
7 Quand on le jugera, qu’il sorte coupable, et que sa prière soit réputée péché!
Pamene aweruzidwa, apezeke kuti ndi wolakwa, ndipo mapemphero ake amutsutse.
8 Que ses jours soient abrégés, et qu’un autre prenne sa charge!
Masiku ake akhale owerengeka; munthu wina atenge malo ake a utsogoleri.
9 Que ses enfants deviennent orphelins, que son épouse soit veuve!
Ana ake akhale amasiye ndipo mkazi wake akhale wopanda mwamuna.
10 Que ses enfants soient vagabonds et mendiants, cherchant leur pain loin de leurs maisons en ruines!
Ana ake akhale oyendayenda ndi opemphapempha; apirikitsidwe kuchoka pa mabwinja a nyumba zawo.
11 Que le créancier s’empare de tout ce qui est à lui, et que les étrangers pillent ce qu’il a gagné par son travail!
Wokongoza alande zonse zimene ali nazo; alendo afunkhe ntchito za manja ake.
12 Qu’il n’ait personne qui lui garde son affection, que nul n’ait pitié de ses orphelins!
Pasapezeke ndi mmodzi yemwe womukomera mtima kapena kumvera chisoni ana ake amasiye.
13 Que ses descendants soient voués à la ruine, et que leur nom soit effacé à la seconde génération!
Zidzukulu zake zithe nʼkufa, mayina awo afafanizidwe mu mʼbado wotsatirawo.
14 Que l’iniquité de ses pères reste en souvenir devant Yahweh, et que la faute de leur mère ne soit pas effacée!
Mphulupulu za makolo ake zikumbukiridwe pamaso pa Yehova; tchimo la amayi ake lisadzafafanizidwe.
15 Qu’elles soient toujours devant Yahweh, et qu’il retranche de la terre leur mémoire!
Machimo awo akhale pamaso pa Yehova nthawi zonse, kuti Iye achotse chikumbutso chawo pa dziko lapansi.
16 Parce qu’il ne s’est pas souvenu d’exercer la miséricorde, parce qu’il a persécuté le malheureux et l’indigent, et l’homme au cœur brisé pour le faire mourir.
Pakuti iye sanaganizirepo zochita chifundo, koma anazunza mpaka kuwapha anthu osauka ndi osweka mtima.
17 Il aimait la malédiction: elle tombe sur lui; il dédaignait la bénédiction: elle s’éloigne de lui.
Anakonda kutemberera, matembererowo abwerere kwa iye; sanakondwe nʼkudalitsa anthu ena, choncho madalitso akhale kutali naye.
18 Il s’est revêtu de la malédiction comme d’un vêtement; comme l’eau elle entre au-dedans de lui, et comme l’huile elle pénètre dans ses os.
Anavala kutemberera ngati chovala; kutemberera kunalowa mʼthupi lake ngati madzi, kulowa mʼmafupa ake ngati mafuta.
19 Qu’elle soit pour lui le vêtement qui l’enveloppe, la ceinture qui ne cesse de l’entourer!
Matemberero akhale ngati chofunda chodzikutira nacho, ngati lamba wovala tsiku ndi tsiku.
20 Tel soit, de la part de Yahweh le salaire de mes adversaires, et de ceux qui parlent méchamment contre moi.
Awa akhale malipiro ochokera kwa Yehova pa onditsutsa anga, kwa iwo amene amayankhula zoyipa za ine.
21 Et toi, Seigneur Yahweh, prends ma défense à cause de ton nom; dans ta grande bonté, délivre-moi.
Koma Inu Ambuye Wamphamvuzonse, muchite nane molingana ndi dzina lanu, chifukwa cha ubwino wa chikondi chanu, pulumutseni.
22 Car je suis malheureux et indigent, et mon cœur est blessé au-dedans de moi.
Pakuti ndine wosauka ndi wosowa, ndipo mtima wanga ukuwawa mʼkati mwanga.
23 Je m’en vais comme l’ombre à son déclin, je suis emporté comme la sauterelle.
Ndikuzimirira ngati mthunzi wa kumadzulo, ndapirikitsidwa ngati dzombe.
24 A force de jeûne mes genoux chancellent, et mon corps est épuisé de maigreur.
Mawondo anga afowoka chifukwa cha kusala zakudya, thupi langa lawonda ndi mutu wanga womwe.
25 Je suis pour eux un objet d’opprobre; ils me regardent et branlent de la tête.
Ndine chinthu chotonzedwa kwa otsutsana nane; akandiona, amapukusa mitu yawo.
26 Secours-moi, Yahweh, mon Dieu! Sauve-moi dans ta bonté!
Thandizeni Inu Yehova Mulungu wanga; pulumutseni molingana ndi chikondi chanu.
27 Qu’ils sachent que c’est ta main, que c’est toi, Yahweh, qui l’a fait!
Adaniwo adziwe kuti limeneli ndi dzanja lanu, kuti Inu Yehova mwachita zimenezi.
28 Eux, ils maudissent; mais toi, tu béniras; ils se lèvent, mais ils seront confondus, et ton serviteur sera dans la joie.
Angathe kutemberera, koma Inu mudzadalitsa; pamene iwo andiputa adzachititsidwa manyazi, koma mtumiki wanu adzasangalala.
29 Mes adversaires seront revêtus d’ignominie, ils seront enveloppés de leur honte comme d’un manteau.
Onditsutsa adzavekedwa mnyozo, ndipo adzadzifunditsa manyazi ngati chovala.
30 Mes lèvres loueront hautement Yahweh; je le célébrerai au milieu de la multitude;
Ndi pakamwa panga ndidzathokoza Yehova kwambiri; ndidzamutamanda mʼgulu lalikulu la anthu.
31 car il se tient à la droite du pauvre, pour le sauver de ceux qui le condamnent.
Popeza Iye amayima ku dzanja lamanja la munthu wosowayo, kupulumutsa moyo wake kwa iwo amene agamula molakwa.