< Néhémie 11 >
1 Les chefs du peuple s’établirent à Jérusalem. Le reste du peuple tira au sort, pour qu’un sur dix vînt habiter Jérusalem, la ville sainte, les neuf autres parties restant dans les autres villes.
Nthawi imeneyo atsogoleri a anthu ankakhala ku Yerusalemu. Tsono anthu ena onse anachita maere kuti apeze munthu mmodzi pa anthu khumi aliwonse kuti azikhala ku Yerusalemu, mzinda wopatulika. Anthu asanu ndi anayi otsalawo ankakhala mʼmidzi yawo.
2 Le peuple bénit tous ceux qui se décidèrent d’eux-mêmes à résider à Jérusalem.
Anthu anayamikira onse amene anadzipereka kuti azikhala mu Yerusalemu.
3 Voici les chefs de famille de la province qui s’établirent à Jérusalem. Dans les villes de Juda, chacun s’établit dans sa propriété, dans sa ville: Israël, les prêtres et les lévites, les Nathinéens et les fils des serviteurs de Salomon:
Aisraeli wamba, ansembe, Alevi, ogwira ntchito ku Nyumba ya Mulungu ndiponso zidzukulu za antchito a Solomoni ankakhala mʼmidzi yawo, aliyense mu dera lake. Koma atsogoleri a chigawo cha Yuda anali atakhazikika mu Yerusalemu.
4 A Jérusalem s’établirent des fils de Juda et des fils de Benjamin. — Des fils de Juda: Athaïas, fils d’Aziam, fils de Zacharie, fils d’Amarias, fils de Saphatias, fils de Malaléel, des fils de Pharès;
Ku Yerusalemu kunkakhalanso anthu ena a mafuko a Yuda ndi Benjamini. Ena mwa zidzukulu za Yuda ndi awa: Ataya, mwana wa Uziya, mwana wa Zekariya, mwana wa Amariya mwana wa Sefatiya, mwana wa Mahalaleli. Onsewa anali ana a Perezi.
5 et Maasias, fils de Baruch, fils de Cholhoza, fils de Hazias, fils d’Adaïas, fils de Joïarib, fils de Zacharie, fils de Séla.
Ena ndi awa: Maaseya mwana wa Baruki, mwana wa Koli-Hoze mwana wa Hazaya, mwana wa Adaya, mwana wa Yowaribu, Zekariya mwana wa Msiloni.
6 Total des fils de Pharès qui s’établirent à Jérusalem: quatre cent soixante-huit hommes vaillants.
Zidzukulu zonse za Perezi, anthu amphamvu zawo amene ankakhala ku Yerusalemu analipo anthu okwanira 468.
7 — Voici les fils de Benjamin: Sellum, fils de Mosollam, fils de Joëd, fils de Phadaïas, fils de Colaïas, fils de Maasias, fils d’Ethéel, fils d’Isaïe,
Nazi zidzukulu za Benjamini: Salu mwana wa Mesulamu, mwana wa Yowedi, mwana wa Pedaya, mwana wa Kolaya, mwana wa Maaseiya, mwana wa Itieli, mwana wa Yesaiya.
8 et après lui Gebbaï-Sellaï: neuf cent vingt-huit.
Abale ake anali Gabayi ndi Salaya. Onse pamodzi anali 928.
9 Joël, fils de Zéchri, était leur chef, et Juda, fils de Sénua, était le second chef de la ville.
Yoweli mwana wa Zikiri ndiye anali mtsogoleri wawo, ndipo Yuda mwana wa Hasenuya ndiye amayangʼanira chigawo cha chiwiri cha mzinda.
10 Des prêtres: Idaïas, fils de Joïarib, Jachin,
Ansembe anali awa: Yedaya mwana wa Yowaribu; Yakini;
11 Saraïas, fils de Helcias, fils de Mosollam, fils de Sadoc, fils de Méraïoth, fils d’Achitob, prince de la maison de Dieu,
Seraya mwana wa Hilikiya mwana wa Mesulamu, mwana wa Zadoki, mwana wa Merayoti, mwana wa Ahitubi amene anali woyangʼanira Nyumba ya Mulungu,
12 et leurs frères qui faisaient le travail dans la maison: huit cent vingt-deux; Adaïas, fils de Jéroham, fils de Phéléias, fils d’Amsi, fils de Zacharie, fils de Phashur, fils de Melchias,
ndi abale awo, amene ankagwira ntchito ku Nyumba ya Mulungu. Onse pamodzi anali 822. Panalinso Adaya mwana wa Yerohamu, mwana wa Pelaliya, mwana wa Amizi, mwana wa Zekariya, mwana wa Pasi-Huri, mwana wa Malikiya,
13 et ses frères, chefs de famille: deux cent quarante-deux; et Amassaï, fils d’Azréel, fils d’Ahazi, fils de Mosollamoth, fils d’Emmer,
ndi abale ake, amene anali atsogoleri a mabanja. Onse pamodzi anali 242. Kuphatikiza apo panalinso Amasisai mwana wa Azaireli, mwana wa Ahazayi, mwana wa Mesilemoti, mwana wa Imeri
14 et leurs frères, hommes vaillants: cent vingt-huit. Zabdiel, fils de Hagdolim, était leur chef.
ndi abale ake. Onse pamodzi anali 128 ndipo anali anthu olimba mtima kwambiri. Mtsogoleri wawo wamkulu anali Zabidieli mwana wa Hagedolimu.
15 Des lévites: Séméïas, fils de Hasub, fils d’Azaricam, fils de Hasabias, fils de Boni;
Alevi anali awa: Semaya mwana wa Hasubu, mwana wa Azirikamu, mwana wa Hasabiya, mwana wa Buni.
16 Sabathaï et Jozabed, chargés des affaires extérieures de la maison de Dieu, du nombre des chefs des lévites;
Sabetayi ndi Yozabadi anali atsogoleri amene ankayangʼanira ntchito ya kunja kwa Nyumba ya Mulungu.
17 Mathanias, fils de Micha, fils de Zébédéi, fils d’Asaph, le chef qui entonnait le chant de louange à la prière; Becbécias, le second parmi ses frères, et Abda, fils de Samua, fils de Galal, fils d’Idithun.
Mataniya mwana wa Mika, mwana wa Zabidi, mwana wa Asafu ndiye anali wotsogolera pa mapemphero achiyamiko. Panalinso Bakibukiya amene anali wachiwiri pakati pa abale ake. Kuwonjezera apo panalinso Abida mwana wa Samuwa, mwana wa Galali, mwana wa Yedutuni.
18 Total des lévites dans la ville sainte: deux cent quatre-vingt-quatre.
Alevi onse amene anali mu mzinda woyera analipo 284.
19 Et les portiers: Accub, Telmon et leurs frères, gardiens des portes: cent soixante-douze.
Alonda a ku Nyumba ya Mulungu anali awa: Akubu, Talimoni ndi abale awo. Onse pamodzi anali 172.
20 Le reste d’Israël, les prêtres, les lévites, étaient dans toutes les autres villes de Juda, chacun dans sa propriété.
Aisraeli ena onse pamodzi ndi ansembe ndi Alevi ankakhala mʼmizinda ya Yuda, ndipo aliyense ankakhala mʼdera la makolo ake.
21 Les Nathinéens, s’établirent dans le quartier d’Ophel; Siha et Gaspha étaient préposés aux Nathinéens.
Koma antchito a ku Nyumba ya Mulungu ankakhala pa phiri la Ofeli, ndipo Ziha ndi Gisipa ndiwo anali kuwayangʼanira.
22 Le chef des lévites à Jérusalem était Azzi, fils de Bani, fils de Hasabias, fils de Mathanias, fils de Micha, d’entre les fils d’Asaph, les chantres chargés du service de la maison de Dieu.
Wamkulu wa Alevi mu Yerusalemu anali Uzi mwana wa Bani, mwana wa Hasabiya, mwana wa Mataniya, mwana wa Mika. Uzi anali mmodzi wa zidzukulu za Asafu, amene anali oyimba nyimbo pa nthawi zachipembedzo mʼNyumba ya Mulungu.
23 Car il y avait une ordonnance du roi à leur sujet, et un salaire déterminé était accordé aux chantres pour chaque jour.
Pakuti mfumu inalamula kuti tsiku ndi tsiku pa nthawi zachipembedzo oyimba nyimbowo azikhalapo.
24 Phathahias, fils de Mésézébel, d’entre les fils de Zara, fils de Juda, était commissaire du roi pour toutes les affaires du peuple.
Petahiya mwana wa Mesezabeli, mmodzi mwa zidzukulu za Zera mwana wa Yuda ndiye ankayimirira Aisraeli pa bwalo la mfumu ya Perisiya.
25 Quant aux villages et à leurs territoires, des fils de Juda s’établirent: à Cariath-Arbé et dans les villes de sa dépendance, à Dibon et dans les villes de sa dépendance, à Cabséel et dans ses villages,
Anthu ena a fuko la Yuda ankakhala ku Kiriyati-Ariba ndi midzi yake, ku Diboni ndi midzi yake, ku Yekabizeeli ndi midzi yake,
26 à Jésué, à Molada, à Beth-Phalet,
ku Yesuwa, Molada, Beti-Peleti,
27 à Hasersual, à Bersabée et dans les villes de sa dépendance,
Hazari-Suwali, Beeriseba ndi midzi yawo.
28 à Siceleg, à Mochona, et dans les villes de sa dépendance,
Ku Zikilagi, Mekona ndi midzi yawo,
29 à En-Remmon, à Saraa, à Jérimuth,
ku Eni-Rimoni, Zora, Yarimuti,
30 à Zanoé, à Odollam et dans leurs villages, à Lachis et dans son territoire, à Azéca et dans les villes de sa dépendance. Ils s’établirent depuis Bersabée jusqu’à la vallée d’Ennom.
Zanowa, Adulamu ndi midzi yake, ku Lakisi ndi minda yake, ku Beeriseba mpaka ku chigwa cha Hinomu.
31 Des fils de Benjamin s’établirent depuis Geba, à Machmas, à Haï, à Béthel et dans les villes de sa dépendance,
Nazonso zidzukulu za Benjamini zinkakhala mʼdera lawo kuyambira ku Geba mpaka ku Mikimasi, Ayiya, Beteli ndi midzi yake,
32 à Anathoth, à Nob, à Anania,
ku Anatoti, Nobu ndi Ananiya,
33 à Asor, à Rama, à Géthaïm,
ku Hazori, Rama ndi Gitaimu,
34 à Hadid, à Séboïm, à Néballat,
ku Hadidi, Zeboimu ndi Nebalati,
35 à Lod et à Ono, dans la Vallée des Ouvriers.
ku Lodi, Ono ndi ku chigwa cha Amisiri.
36 Il y eut, parmi les lévites, des classes appartenant à Juda qui se joignirent à Benjamin.
Magulu ena a Alevi a ku Yuda ankakhala ku Benjamini.