< Michée 5 >

1 Maintenant, fille de troupes, rassemble tes troupes! On a mis le siège contre nous, on frappe de la verge sur la joue le juge d’Israël.
Iwe mzinda wa anthu ankhondo, sonkhanitsa anthu ako ankhondo, pakuti anthu atizungulira kuti alimbane nafe. Adzakantha ndi ndodo pa chibwano cha wolamulira wa Israeli.
2 Et toi, Bethléem Ephrata, petite pour être entre les milliers de Juda, de toi sortira pour moi celui qui doit être dominateur en Israël, et ses origines dateront des temps anciens, des jours de l’éternité.
“Koma iwe Betelehemu Efurata, ngakhale uli wonyozeka pakati pa mafuko a Yuda, mwa iwe mudzatuluka munthu amene adzalamulira Israeli, amene chiyambi chake nʼchakalekale, nʼchamasiku amakedzana.”
3 C’est pourquoi il les livrera, jusqu’au temps où celle qui doit enfanter aura enfanté; et le reste de ses frères reviendra aux enfants d’Israël.
Nʼchifukwa chake Israeli adzasiyidwa mpaka pa nthawi imene mayi amene ali woyembekezera adzachire. Ndipo abale ake onse otsalira adzabwerera kudzakhala pamodzi ndi Aisraeli.
4 Il se tiendra ferme, et il paîtra ses brebis, dans la force de Yahweh, dans la majesté du nom de Yahweh, son Dieu; et on demeurera en sécurité, car maintenant il sera grand, jusqu’aux extrémités de la terre.
Iye adzalimbika, ndipo adzaweta nkhosa zake mwa mphamvu ya Yehova, mu ulemerero wa dzina la Yehova Mulungu wake. Ndipo iwo adzakhala mu mtendere, pakuti ukulu wake udzakhala ponseponse pa dziko lapansi.
5 C’est lui qui sera la paix. Quand l’Assyrien viendra dans notre pays, et que son pied foulera nos palais, nous ferons lever contre lui sept pasteurs, et huit princes du peuple.
Ndipo Iye adzakhala mtendere wawo. Asiriya akadzalowa mʼdziko lathu ndi kuyamba kuthira nkhondo malo athu otetezedwa, tidzawadzutsira abusa asanu ndi awiri, ngakhalenso atsogoleri asanu ndi atatu.
6 Ils paîtront le pays d’Assur avec l’épée, et le pays de Nemrod dans ses portes; Il nous délivrera de l’Assyrien, lorsqu’il viendra dans notre pays, et que son pied foulera notre territoire.
Iwo adzagonjetsa dziko la Asiriya ndi lupanga, dziko la Nimurodi adzalilamulira mwankhondo. Adzatipulumutsa kwa Asiriya akadzafika mʼmalire a mʼdziko lathu kudzatithira nkhondo.
7 Et le reste de Jacob sera, au milieu de peuples nombreux, comme une rosée venant de Yahweh, comme des gouttes de pluie sur le gazon, lequel n’attend personne, et n’espère pas dans les enfants des hommes.
Otsalira a Yakobo adzakhala pakati pa mitundu yambiri ya anthu ngati mame ochokera kwa Yehova, ngati mvumbi pa udzu, omwe sulamulidwa ndi munthu kapena kudikira lamulo la anthu.
8 Et le reste de Jacob sera aussi parmi les nations, au milieu de peuples nombreux, comme un lion parmi les bêtes de la forêt, comme un jeune lion parmi les troupeaux de brebis; lorsqu’il passe, foule et déchire, personne ne délivre.
Otsala a Yakobo adzakhala pakati pa mitundu ya anthu, mʼgulu la anthu a mitundu yambiri, ngati mkango pakati pa nyama za mʼnkhalango. Ngati mwana wa mkango pakati pa gulu la nkhosa, amene pozidutsa amazidya ndi kuzikhadzula, ndipo palibe angathe kuzilanditsa.
9 Que votre main se lève contre vos adversaires, et que vos ennemis soient exterminés!
Mudzagonjetsa adani anu, ndipo adani anu onse adzawonongeka.
10 En ce jour-là, — oracle de Yahweh, j’exterminerai tes chevaux du milieu de toi, et je détruirai tes chars.
Yehova akuti, “Tsiku limenelo ndidzawononga akavalo anu onse ndi kuphwasula magaleta anu.
11 Je ruinerai les villes de ton pays, et je démolirai toutes tes forteresses.
Ndidzawononga mizinda ya mʼdziko mwanu ndi kugwetsa malinga anu onse.
12 Je retrancherai de ta main les sortilèges, et il n’y aura plus chez toi de devins.
Ndidzawononga ufiti wanu ndipo sikudzakhalanso anthu owombeza mawula.
13 J’exterminerai du milieu de toi tes idoles et tes stèles, et tu n’adoreras plus l’ouvrage de tes mains.
Ndidzawononga mafano anu osema pamodzi ndi miyala yanu yopatulika imene ili pakati panu; simudzagwadiranso zinthu zopanga ndi manja anu.
14 J’arracherai du milieu de toi tes aschéras, et je détruirai tes villes.
Ndidzazula mitengo ya mafano a Asera imene ili pakati panu, ndipo ndidzawononga mizinda yanu.
15 Et dans ma colère et dans ma fureur, je tirerai vengeance des peuples qui n’auront pas écouté.
Ndidzayilanga mwaukali ndi mokwiya mitundu imene sinandimvere Ine.”

< Michée 5 >