< Michée 3 >
1 J’ai dit: Ecoutez donc, chefs de Jacob, et magistrats de la maison d’Israël! N’est-ce pas à vous de connaître le droit,
Ndipo ine ndinati, “Tamverani, inu atsogoleri a Yakobo, inu olamulira nyumba ya Israeli. Kodi sindinu oyenera kudziwa kuweruza molungama,
2 vous qui haïssez le bien et aimez le mal, qui leur arrachez la peau de dessus le corps, et la chair de dessus les os?
inu amene mumadana ndi zabwino ndi kukonda zoyipa; inu amene mumasenda khungu la anthu anga, ndipo mumakungunula mnofu pa mafupa awo;
3 Ils dévorent la chair de mon peuple: ils lui arrachent la peau de dessus le corps, ils brisent ses os, ils les mettent en pièces comme ce qui est dans la marmite; et comme de la viande dans une chaudière.
inu amene mumadya anthu anga, mumasenda khungu lawo ndi kuphwanya mafupa awo; inu amene mumawadula nthulinthuli ngati nyama yokaphika?”
4 Alors ils crieront à Yahweh, et il ne les exaucera point; il leur cachera sa face en ce temps-là, selon la malice qu’ils ont mise en leurs actions.
Pamenepo adzalira kwa Yehova, koma Iye sadzawayankha. Nthawi imeneyo Iye adzawabisira nkhope yake chifukwa cha zoyipa zimene anazichita.
5 Ainsi parle Yahweh sur les prophètes qui égarent mon peuple, qui, tant que leurs dents ont de quoi mordre, proclament la paix, et à quiconque ne leur met rien dans la bouche, déclarent la guerre:
Yehova akuti, “Aneneri amene amasocheretsa anthu anga, ngati munthu wina awapatsa chakudya amamufunira ‘mtendere;’ ngati munthu wina sawapatsa zakudya amamulosera zoyipa.
6 « C’est pourquoi vous aurez la nuit au lieu de visions; et vous aurez les ténèbres au lieu de divination; le soleil se couchera pour les prophètes, et le jour s’obscurcira pour eux.
Nʼchifukwa chake kudzakuderani, simudzaonanso masomphenya, mdima udzakugwerani ndipo simudzawombezanso. Dzuwa lidzawalowera aneneriwo, ndipo mdima udzawagwera.
7 Les voyants seront confus, et les devins rougiront de honte; tous, ils se couvriront la barbe, car il n’y aura plus de réponse de Dieu. »
Alosi adzachita manyazi ndipo owombeza mawula adzanyazitsidwa. Onse adzaphimba nkhope zawo chifukwa Mulungu sakuwayankha.”
8 Mais moi, je suis rempli de force, avec l’esprit de Yahweh, et de jugement et de courage, pour dénoncer à Jacob son crime, et à Israël son péché.
Koma kunena za ine, ndadzazidwa ndi mphamvu, ndi Mzimu wa Yehova, ndi kulungama, ndi kulimba mtima, kuti ndilalikire za kugalukira kwa Yakobo, kwa Israeli za tchimo lake.
9 Ecoutez donc ceci, chefs de la maison de Jacob, et magistrats de la maison d’Israël, qui avez en horreur la justice, et qui pervertissez ce qui est droit,
Imvani izi, inu atsogoleri a nyumba ya Yakobo, inu olamulira nyumba ya Israeli, inu amene mumadana ndi kuweruza kolungama; ndipo mumakhotetsa zinthu zonse zolondola;
10 bâtissant Sion avec le sang, et Jérusalem avec l’iniquité!
inu amene mukumanga Ziyoni pokhetsa magazi, ndi Yerusalemu ndi kuyipa kwanu.
11 Ses chefs jugent pour des présents, ses prêtres enseignent pour un salaire; et ses prophètes exercent la divination pour de l’argent, et ils s’appuient sur Yahweh, en disant: « Yahweh n’est-il pas au milieu de nous? Le malheur ne saurait venir sur nous! »
Atsogoleri ake amalandira chiphuphu kuti aweruze, ansembe ake amalandira malipiro kuti alalikire, ndipo aneneri ake amanenera kuti alandire ndalama. Komatu amatsamira pa Yehova nʼkumanena kuti, “Kodi Yehova sali pakati pathu? Palibe tsoka limene lidzatigwere.”
12 C’est pourquoi, à cause de vous, Sion deviendra un champ qu’on laboure, Jérusalem sera un monceau de pierres, et la montagne du temple un haut lieu boisé!
Choncho chifukwa cha inu, Ziyoni adzatipulidwa ngati munda, Yerusalemu adzasanduka bwinja, ndipo phiri la Nyumba ya Mulungu lidzasanduka nkhalango yowirira.