< Lévitique 25 >

1 Yahweh parla à Moïse sur la montagne de Sinaï, en disant:
Yehova anawuza Mose pa phiri la Sinai kuti,
2 « Parle aux enfants d’Israël, et dis-leur: Quand vous serez entrés dans le pays que je vous donne, la terre se reposera: ce sera un sabbat en l’honneur de Yahweh.
“Yankhula ndi Aisraeli ndipo uwawuze kuti, ‘Mukadzalowa mʼdziko limene ndikukupatsani, nthakayo iyenera kumakasunga Sabata la Yehova.
3 Pendant six ans tu ensemenceras ton champ, pendant six ans tu tailleras ta vigne, et tu en recueilleras le produit.
Pa zaka zisanu ndi chimodzi muzikalima minda yanu, ndipo kwa zaka zisanu ndi chimodzi muzikasadza mitengo yanu ya mpesa ndi kuthyola zipatso zake.
4 Mais la septième année sera un sabbat, un solennel repos pour la terre, un sabbat en l’honneur de Yahweh: tu n’ensemenceras pas ton champ et tu ne tailleras pas ta vigne.
Koma chaka chachisanu ndi chiwiri ndi chaka choti nthaka ipume, chaka cha Sabata la Yehova. Musalime mʼminda yanu kapena kusadza mitengo yanu ya mpesa.
5 Tu ne moissonneras pas ce qui poussera de soi-même, des grains tombés de ta dernière moisson, et tu ne recueilleras pas les raisins de ta vigne non taillée: ce sera une année de repos pour la terre.
Musakolole zimene zinamera zokha mʼmunda mwanu. Musakakolole kapena kuthyola mphesa za mʼmitengo imene simunasadze. Chaka chimenechi nʼchoti nthaka ipumule.
6 Ce que produira la terre pendant son sabbat vous servira de nourriture, à toi, à ton serviteur et à ta servante, à ton mercenaire et à l’étranger qui demeurent avec toi;
Chaka chimene nthakayo ipumula mudzakhala ndi chakudya chokwanira inuyo, akapolo anu aamuna ndi aakazi, antchito ndi alendo okhala nanu.
7 à ton bétail aussi et aux animaux qui sont dans ton pays, tout son produit servira de nourriture.
Ziweto zanu pamodzi ndi nyama za mʼdziko lanu zizidzadya zipatso za mʼnthaka.
8 Tu compteras sept sabbats d’années, sept fois sept ans; la durée de ces sept sabbats d’années te fera une période de quarante-neuf ans.
“‘Muzichotsera Masabata asanu ndi awiri a zaka, ndi kuchulukitsa zaka zisanu ndi ziwiri kasanu ndi kawirinso kuti Masabata asanu ndi awiri a zakawo akwane zaka 49.
9 Le dixième jour du septième mois, tu feras retentir le son éclatant de la trompette; le jour des Expiations, vous ferez passer la trompette dans tout votre pays.
Ndipo pa tsiku la khumi la mwezi wachisanu ndi chiwiri mulize lipenga mofuwula. Tsiku lochita mwambo wopepesera machimo muziliza lipenga mʼdziko lanu lonse.
10 Et vous sanctifierez la cinquantième année, et vous publierez la liberté dans le pays pour tous ses habitants. Ce sera pour vous un jubilé, et chacun de vous retournera dans sa propriété et chacun de vous retournera dans sa famille.
Mupatule chaka cha makumi asanu, ndipo mulengeze kuti pakhale ufulu mʼdziko lonse kwa onse amene ali mʼmenemo. Kwa inu chakachi chidzakhala choyimba lipenga la chikondwerero. Aliyense wa inu adzayenera kubwerera pa munda wake, ndipo aliyense wa inu adzabwerera ku fuko lake.
11 La cinquantième année sera pour vous un jubilé; vous ne sèmerez point, vous ne moissonnerez pas ce que la terre produira d’elle-même, et vous ne vendangerez pas la vigne non taillée.
Kwa inu chakachi chidzakhaladi chaka choyimba lipenga kukondwerera zaka makumi asanu. Pa chaka chimenechi musadzale kanthu ndipo musakolole mbewu zomera zokha kapenanso kuthyola mphesa pa mitengo yosasadzira.
12 Car c’est un jubilé; il sera sacré pour vous. Vous mangerez le produit tiré de vos champs.
Chimenechi ndi chaka chokondwerera zaka makumi asanu. Choncho chikhale chaka chopatulika kwa inu. Muzidya zokhazo zimene zakololedwa mʼminda.
13 Dans cette année de jubilé, chacun de vous retournera dans sa propriété.
“‘Chaka chimenechi ndi choliza lipenga, kukondwerera zaka makumi asanu, ndipo aliyense abwerere pa malo ake.
14 Si vous faites une vente à votre prochain, ou si vous achetez de votre prochain, qu’aucun de vous ne porte préjudice à son frère.
“‘Ngati unagulitsa kapena kugula malo ako kwa mnzako wa mʼdzikomo, pasakhale kuchenjeretsana.
15 Tu achèteras à ton prochain d’après le nombre des années écoulées depuis le dernier jubilé, et il te vendra d’après le nombre des années de récolte.
Ugule kwa mnzako potsata chiwerengero cha zaka zimene zatha kuyambira pa chikondwerero cha chaka cha makumi asanu chapita. Ndipo mnzakoyo akugulitse potsata chiwerengero cha zaka zokolola zomwe zatsala.
16 Plus il restera d’années, plus tu élèveras le prix, et moins il y aura d’années, plus tu abaisseras le prix; car c’est le nombre des récoltes qu’il te vend.
Zaka zikakhala zochuluka, uwonjezere mtengo, ndipo zaka zikakhala zochepa, uchepetse mtengo, pakuti chimene iye akukugulitsa ndi zaka zokolola.
17 Qu’aucun de vous ne porte préjudice à son frère; crains ton Dieu, car je suis Yahweh, votre Dieu.
Musachenjeretsane koma muope Mulungu wanu. Ine ndine Yehova Mulungu wanu.
18 Vous mettrez mes lois en pratique, vous observerez mes ordonnances et les mettrez en pratique, et vous habiterez en sécurité dans le pays.
“‘Tsatirani malangizo anga ndipo mverani mosamala malamulo anga ndipo mudzakhala mʼdzikomo mwamtendere.
19 La terre donnera ses fruits, vous mangerez à satiété et vous y habiterez en sécurité.
Ndipo nthaka idzakupatsani zipatso zake. Mudzadya mpaka kukhuta ndiponso mudzakhala mʼdzikomo mwamtendere.
20 Si vous dites: Que mangerons-nous la septième année, puisque nous ne sèmerons pas et ne recueillerons pas nos produits?
Mwina nʼkafunsa kuti, ‘Kodi chaka chachisanu ndi chiwiri tidzadya chiyani ngati sitidzala kapena kukolola mbewu zathu?’
21 Je vous enverrai ma bénédiction la sixième année, et elle produira des fruits pour trois ans.
Ine ndidzatumiza madalitso ambiri chaka chachisanu ndi chimodzi moti nthaka yanu idzabala zinthu zokwanira kudya zaka zitatu.
22 Vous sèmerez la huitième année, et vous mangerez de l’ancienne récolte; jusqu’à la neuvième année, jusqu’à ce que vienne sa récolte, vous mangerez l’ancienne.
Pamene mukudzala chaka chachisanu ndi chitatu, muzidzadya chakudya chogonera ndipo mudzapitirira kudya mpaka nthawi yokolola mʼchaka chachisanu ndi chinayi.
23 Les terres ne se vendront pas à perpétuité, car le pays est à moi, et vous êtes chez moi comme des étrangers et des gens en séjour.
“‘Malo asagulitsidwe mpaka muyaya chifukwa dzikolo ndi langa. Inu ndinu alendo okhala ndi Ine.
24 Dans tout le pays que vous posséderez, vous accorderez un droit de rachat pour les terres.
Malo onse amene ali mʼmanja mwanu mudzalole kuti amene anakugulitsani awawombole.
25 Si ton frère est devenu pauvre et vend une portion de sa propriété, son représentant, son parent le plus proche viendra et rachètera ce qu’a vendu son frère.
“‘Ngati Mwisraeli mnzanu wasauka nagulitsako gawo lina la malo ake, mʼbale wake wapaphata abwere kudzawombola malo amene mʼbale wakeyo wagulitsa.
26 Si un homme n’a personne qui le représente, et que lui-même se procure de quoi faire le rachat,
Koma ngati munthuyo alibe wachibale woti nʼkuwombola malowo koma pambuyo pake iye mwini nʼkulemera ndi kupeza zokwanira kuwombolera, awombole malowo.
27 il comptera les années écoulées depuis la vente, rendra le surplus à l’acquéreur, et retournera dans sa propriété.
Awerengerane zaka kuyambira pamene anagulitsa mundawo ndipo amubwezere amene anagulayo ndalama zimene akanayenera kuzipereka mpaka chaka chokondwerera zaka makumi asanu. Atatero angathe kubwerera pa malo ake.
28 S’il ne trouve pas de quoi lui faire cette restitution, le bien vendu restera entre les mains de l’acquéreur jusqu’à l’année du jubilé; au jubilé, il sera libéré, et le vendeur rentrera dans sa propriété.
Koma ngati sakhala nazo zokwanira kuti amubwezere amene anagula malowo, gawo limene anagulitsalo lidzakhala mʼmanja mwa munthu amene anagulayo mpaka chaka chokondwerera zaka makumi asanu. Malowo adzabwezedwa chaka chimenechi, ndipo iye adzatha kubwerera pa malo ake.
29 Si un homme vend une maison d’habitation dans une ville entourée de murs, il aura le droit de rachat jusqu’au terme de l’année de la vente; son droit de rachat durera une année pleine.
“‘Ngati munthu agulitsa nyumba ya mu mzinda umene uli mu linga, angathe kuyiwombola nyumbayo chisanathe chaka chathunthu chigulitsire. Mu nthawi imeneyi wogulitsayo atha kuyiwombola.
30 Que si la maison qui est située dans une ville murée n’est pas rachetée avant l’expiration d’une année complète, elle appartiendra à perpétuité à l’acquéreur et à ses descendants; elle ne sortira pas de leur possession au jubilé.
Ngati nyumbayo siwomboledwa chisanathe chaka chimodzicho, nyumbayo idzakhala ya amene anagulayo ndi zidzukulu zake mpaka muyaya. Sidzabwezedwanso kwa mwini wake mʼchaka chokondwerera zaka makumi asanu.
31 Mais les maisons des villages non entourés de murs seront considérées comme allant avec le fonds de terre; on pourra les racheter, et elles seront libérées au jubilé.
Koma nyumba za mʼmizinda yosazingidwa ndi linga ziwomboledwe monga mmene achitira ndi minda ya mʼdzikomo.
32 Quant aux villes des Lévites et aux maisons des villes qu’ils posséderont, les Lévites auront un droit perpétuel de rachat.
“‘Alevi ali ndi ufulu owombola nyumba zawo za mʼmidzi yawo nthawi ina iliyonse.
33 Si quelqu’un achète des Lévites une maison, la maison vendue dans la ville qui leur a été donnée sera libérée au jubilé, car les maisons des villes des Lévites sont leur propriété au milieu des enfants d’Israël.
Koma ngati Mlevi sawombola nyumba imene inagulitsidwa mʼmudzi mwake, ndiye kuti idzabwezedwe mʼchaka choliza lipenga pokondwerera zaka makumi asanu, popeza nyumba zimenezi zili mʼmidzi ya Alevi ndi yawo pakati pa Aisraeli.
34 Les champs de la banlieue des villes des Lévites ne seront pas vendus, car c’est leur possession à perpétuité.
Koma malo owetera ziweto a mʼmidzi yawoyo sayenera kugulitsidwa. Awa ndi malo awo mpaka muyaya.
35 Si ton frère devient pauvre et que sa main s’affaiblisse près de toi, tu le soutiendras, fût-il étranger ou hôte, afin qu’il vive auprès de toi.
“‘Ngati mʼbale wako akhala wosauka kuti sangathe kudzisamalira yekha, umuthandize. Ukhale naye ngati mlendo kapena ngati munthu amene ukhala naye kwa kanthawi.
36 Ne tire de lui ni intérêt ni profit, mais crains ton Dieu et que ton frère vive avec toi.
Usalandire chiwongoladzanja chilichonse kuchokera kwa iye kapena kuwonjezerapo kanthu kena, koma uziopa Mulungu kuti mʼbale wakoyo akhale nawe.
37 Tu ne lui prêteras pas ton argent à intérêt, et tu ne lui donneras pas de tes vivres pour en tirer profit.
Musakongoze mnzanu ndalama kuti mulandire chiwongoladzanja, kapena kumugulitsa chakudya kuti mupeze phindu.
38 Je suis Yahweh, ton Dieu, qui vous ai fait sortir du pays d’Égypte, pour vous donner le pays de Canaan, pour être votre Dieu.
Ine ndine Yehova Mulungu wanu, amene ndinakutulutsani mʼdziko la Igupto kuti ndikupatseni dziko la Kanaani ndi kuti ndikhale Mulungu wanu.
39 Si ton frère devient pauvre près de toi et qu’il se vende à toi, tu n’exigeras pas de lui le travail d’un esclave.
“‘Ngati mʼbale wanu asauka ndipo adzigulitsa yekha kwa inu, musamugwiritse ntchito ngati kapolo.
40 Il sera chez toi comme un mercenaire, comme un hôte; il te servira jusqu’à l’année du jubilé.
Akhale ngati wantchito kapena ngati mlendo. Akugwirireni ntchito mpaka chaka chokondwerera zaka makumi asanu.
41 Il sortira alors de chez toi, lui et ses enfants avec lui, et il retournera dans sa famille, et rentrera dans la propriété de ses pères.
Kenaka iye ndi ana ake achoke, ndipo apite ku fuko lake ndi kubwerera ku malo a makolo ake.
42 Car ils sont mes serviteurs, que j’ai fait sortir du pays d’Égypte: ils ne seront pas vendus comme on vend des esclaves.
Chifukwa Aisraeli ndi atumiki anga amene ndinawatulutsa mʼdziko la Igupto, asagulitsidwe ngati akapolo.
43 Tu ne domineras pas sur lui avec dureté, mais tu craindras ton Dieu.
Musawalamulire mwankhanza koma wopani Mulungu wanu.
44 Tes esclaves et tes servantes qui t’appartiendront, tu les prendras des nations qui t’entourent; c’est d’elles que vous achèterez serviteurs et servantes.
“‘Kunena za akapolo aamuna ndi aakazi, amenewa mungathe kuwagula kuchokera kwa mitundu ya anthu imene yakuzungulirani.
45 Vous pourrez aussi en acheter parmi les enfants des étrangers qui séjournent chez vous, et parmi leurs familles qui vivent avec vous, qu’ils auront engendrés dans votre pays; et ils seront votre propriété.
Mungathenso kugula akapolo kuchokera kwa alendo amene akukhala nanu kapena kuchokera ku mabanja amene mukukhala nawo amene ndi mbadwa za mʼdziko lanu. Iwowa akhoza kukhala akapolo anu.
46 Vous les laisserez en héritage à vos enfants après vous, pour les posséder comme une propriété; ils seront perpétuellement vos esclaves. Mais à l’égard de vos frères, les enfants d’Israël, nul d’entre vous ne dominera sur son frère avec dureté.
Akapolowo mungathe kuwasiya mʼmanja mwa ana anu inu mutafa kuti akhale cholowa chawo moyo wawo wonse. Koma musawalamulire mwankhanza Aisraeli anzanu.
47 Si un étranger ou un hôte s’est enrichi près de toi, et que ton frère, devenu pauvre près de lui, se soit vendu à l’étranger, à l’hôte qui est près de toi ou au rejeton d’une famille étrangère,
“‘Ngati mlendo kapena munthu amene akukhala nanu kwa kanthawi kochepa alemera ndipo mmodzi wa abale anu amene akukhala naye pafupi nʼkusauka, nadzigulitsa yekha kwa mlendo amene akukhala pakati panuyo kapena kwa mmodzi wa fuko la munthu wongokhala pafupi nayeyo,
48 il y aura pour lui, après qu’il se sera vendu, le droit de rachat; un de ses frères pourra le racheter;
wodzigulitsayo ali ndi ufulu wowomboledwa. Mmodzi mwa abale ake angathe kumuwombola:
49 ou son oncle, ou le fils de son oncle pourra le racheter; ou l’un de ses proches parents pourra le racheter; ou bien, s’il acquiert des richesses, il se rachètera lui-même.
amalume ake kapena mwana wa amalume ake, kapena wachibale wa mu fuko lake. Kapena ngati iye mwini alemera, atha kudziwombola yekha.
50 Il comptera, avec celui qui l’a acheté, depuis l’année où il s’est vendu à lui jusqu’à l’année du jubilé, et le prix de vente se comptera d’après le nombre des années, en évaluant les journées de son travail comme celles d’un mercenaire.
Iye pamodzi ndi munthu amene anamugulayo awerengerane kuyambira chaka chimene anadzigulitsa kwa iyeyo mpaka chaka chokondwerera zaka makumi asanu. Mtengo wodziwombolera ukhale wofanana ndi zakazo. Ndipo nthawi imene anali ndi mbuye wakeyo iwerengedwe ngati nthawi ya munthu wantchito.
51 S’il y a encore beaucoup d’années, il paiera son rachat à raison du nombre de ces années, en tenant compte du prix auquel il avait été acheté;
Ngati patsala zaka zambiri, iye ayenera kulipira mtengo woposera umene anamugulira.
52 s’il reste peu d’années jusqu’à celle du jubilé, il en fera le compte, et il paiera son rachat à raison de ces années.
Ngati kwatsala zaka zochepa kuti ifike nthawi ya chaka chokondwerera zaka makumi asanu, iye awerengerane ndi mbuye wake, ndipo apereke ndalama za zowomboledwera molingana ndi zaka zotsalazo.
53 Il sera chez lui comme un mercenaire de l’année, et son maître ne le traitera pas avec dureté sous tes yeux.
Azikhala naye ngati wantchito wolembedwa chaka ndi chaka. Ndipo muonetsetse kuti mbuye wakeyo sakumulamulira mwankhanza.
54 S’il n’est racheté d’aucune de ces manières, il sortira libre l’année du jubilé, lui et ses enfants avec lui.
“‘Ngakhale munthuyo atapanda kuwomboledwa mwa njira zimenezi, iye ndi ana ake ayenera kumasulidwa mʼchaka chokondwerera zaka makumi asanu,
55 Car c’est de moi que les enfants d’Israël sont serviteurs; ils sont mes serviteurs, que j’ai fait sortir du pays d’Égypte. Je suis Yahweh, votre Dieu. »
pakuti Aisraeli ndi atumiki anga. Iwo ndi atumiki anga amene ndinawatulutsa mʼdziko la Igupto. Ine ndine Yehova Mulungu wanu.

< Lévitique 25 >