< Juges 6 >

1 Les enfants d’Israël firent ce qui est mal aux yeux de Yahweh, et Yahweh les livra entre les mains de Madian, pendant sept ans.
Aisraeli anachitanso zinthu zoyipira Yehova, choncho Yehova anawapereka mʼmanja mwa Amidiyani kwa zaka zisanu ndi ziwiri.
2 La main de Madian fut puissante contre Israël. A cause de Madian, les enfants d’Israël se firent les antres qui sont dans les montagnes, les cavernes et les hauteurs fortifiées.
Amidiyani anapondereza Aisraeli. Tsono chifukwa cha Amidiyaniwa, Aisraeli anakonza malo obisalamo mʼmapiri ndi mʼmapanga. Anamanganso malinga.
3 Quand Israël avait semé, Madian montait avec Amalec et les fils de l’Orient, et ils marchaient contre lui.
Aisraeli amati akadzala mbewu, Amidiyani, Aamaleki ndi anthu ena akummawa amabwera ndi kudzawathira nkhondo.
4 Campés en face d’Israël, ils dévastaient les productions de le terre jusque prés de Gaza, et ne laissaient aucune subsistance en Israël, ni brebis, ni bœufs, ni ânes.
Iwo anamanga misasa mʼdzikomo ndi kuwononga zokolola zawo zonse mpaka ku Gaza, ndipo sanawasiyireko chamoyo chilichonse Aisraeliwo, kaya nkhosa kapena ngʼombe ndi bulu yemwe.
5 Car ils montaient avec leurs troupeaux et leurs tentes, et venaient nombreux comme des nuées de sauterelles; eux et leurs chameaux étaient innombrables, et ils venaient dans le pays pour le dévaster.
Iwo ankabwera ndi zoweta zawo ndi matenti awo omwe. Ankabwera ambiri ngati dzombe, motero kuti kunali kovuta kuwawerenga anthuwo ndi ngamira zawo. Tsono iwo ankabwera ndi kuwononga dziko lonse.
6 Israël fut très affaibli à cause de Madian, et les enfants d’Israël crièrent vers Yahweh.
Aisraeli anasauka chifukwa cha Amidiyani ndipo analirira kwa Yehova kuti awathandize.
7 Lorsque les enfants d’Israël eurent crié vers Yahweh au sujet de Madian,
Pamene Aisraeli analirira kwa Yehova chifukwa cha Amidiyaniwo,
8 Yahweh envoya un prophète aux enfants d’Israël. Il leur dit: « Ainsi parle Yahweh le Dieu d’Israël: Je vous ai fait monter de l’Égypte, et je vous ai fait sortir de la maison de servitude.
Iye anawatumizira mneneri amene anati, “Yehova Mulungu wa Israeli akuti, ‘Ndine amene ndinakutsogolerani kuchokera ku Igupto. Ndinakutulutsani mʼdziko la ukapolo.
9 Je vous ai délivrés de la main des Egyptiens et de la main de tous vos oppresseurs; je les ai chassés devant vous, et je vous ai donné leur pays.
Ine ndinakupulumutsani ku ulamuliro wa Igupto komanso mʼmanja mwa amene amakuzunzani. Ndinawathamangitsa adani anu inu mukufika, ndikukupatsani dziko lawo.’
10 Je vous ai dit: je suis Yahweh, votre Dieu; vous ne craindrez pas les dieux des Amorrhéens dans le pays desquels vous habitez. Mais vous n’avez pas écouté ma voix. »
Ndipo ndinakuwuzani kuti, ‘Ine ndine Yehova Mulungu wanu; musapembedze Milungu ya Aamori amene mukukhala mʼdziko lawo.’ Koma inu simunandimvere.”
11 Et l’Ange de Yahweh vint, et il s’assit sous le térébinthe d’Ephra, qui apporterait à Joas, de la famille d’Abiéser. Gédéon, son fils, battait le froment dans le pressoir, pour le mettre à l’abri de Madian.
Tsiku lina mngelo wa Yehova anabwera ku Ofura ndi kukhala pansi pa tsinde pa mtengo wa thundu umene unali wa Yowasi Mwabiezeri. Tsono Gideoni, mwana wake nʼkuti pa nthawiyo akupuntha tirigu mʼmalo ofinyira mphesa mowabisalira Amidiyani.
12 L’Ange de Yahweh lui apparut et lui dit: « Yahweh est avec toi, vaillant héros. »
Tsono mngelo wa Yehova uja anamuonekera Gideoni nati kwa iye, “Yehova ali nawe, iwe munthu wamphamvu ndi wolimba mtima.”
13 Gédéon lui dit: « Ah! mon seigneur, si Yahweh est avec nous, pourquoi toutes ces choses nous sont-elles arrivées? Et où sont tous ses prodiges que nos pères nous ont racontés, en disant: Yahweh ne nous a-t-il pas fait monter de l’Égypte? Et maintenant Yahweh nous abandonne et nous livre entre les mains de Madian. »
Gideoni anayankha, “Koma mbuye wanga, ngati Yehova ali nafedi, nʼchifukwa chiyani zonsezi zationekera? Nanga ntchito zake zodabwitsa zimene makolo athu anatiwuza pamene anati, ‘Yehova anatitulutsa ku dziko la Igupto,’ zili kuti? Koma tsopano Yehova watitaya ndi kutipereka mʼmanja mwa Amidiyani.”
14 Yahweh se tourna vers lui et dit: « Va avec cette force que tu as, et délivre Israël de la main de Madian; ne t’ai-je pas envoyé? »
Yehova anamuyangʼana namuwuza kuti, “Pita ndi mphamvu zomwe uli nazo, ukapulumutse Aisraeli mʼmanja mwa Amidiyani. Kodi si ndine amene ndakutuma?”
15 Gédéon lui dit: « Ah! Seigneur, avec quoi délivrerai-je Israël? Voici, ma famille est la plus pauvre en Manassé, et je suis le plus petit dans la maison de mon père. »
Koma Gideoni anafunsa kuti, “Kodi Ambuye anga ine ndingapulumutse bwanji Israeli? Mbumba yanga ndi yopanda mphamvu mu fuko la Manase, ndiponso ine ndine wamngʼono kwambiri mʼbanja mwa abambo anga.”
16 Yahweh lui dit: « Je serai avec toi, et tu battras Madian comme un seul homme. »
Yehova anamuyankha kuti, “Ine ndidzakhala nawe, ndipo Amidiyaniwo udzawagonjetsa ngati munthu mmodzi.”
17 Gédéon lui dit: « Si j’ai trouvé grâce à vos yeux, donnez-moi un signe que c’est vous qui me parlez.
Gideoni anati, “Ngati tsopano mwandikomera mtima, ndionetseni chizindikiro kusonyeza kuti ndinudi mukuyankhula ndi ine.
18 Ne vous éloignez pas d’ici jusqu’à ce que je revienne auprès de vous, que j’apporte mon offrande et que je la dépose devant vous. » Et Yahweh dit: « Je resterai jusqu’à ce que tu reviennes. »
Chonde musachoke msanga mpaka nditabwerera kwa inu ndi chopereka changa cha chakudya kudzachipereka kwa inu.” Ndipo Yehova anamuwuza kuti, “Ine ndikudikira mpaka utabweranso.”
19 Gédéon, étant entré, apprêta un chevreau et, avec un épha de farine, il fit des pains sans levain; puis, ayant mis la chair dans une corbeille et le jus dans un vase, il les lui apporta sous le térébinthe et les lui offrit.
Gideoni analowa mʼnyumba, ndipo anakakonza mwana wambuzi, nakonzanso makeke wopanda yisiti a ufa wa makilogalamu khumi. Nayika nyamayo mʼdengu ndipo msuzi wake anawuthira mu mʼphika. Anabwera nazo ndi kukazipereka kwa mngelo uja pa tsinde pa mtengo wa thundu paja.
20 L’Ange de Yahweh lui dit: « Prends la chair et les pains sans levain, pose-les sur ce rocher, et verse le jus. » Et il fit ainsi.
Mngelo wa Mulungu anamuwuza iye kuti, “Tenga nyamayi pamodzi ndi makekewa, uziyike pa mwala uwu ndi kuthirapo msuziwu.” Ndipo Gideoni anatero.
21 L’Ange de Yahweh étendit l’extrémité du bâton qu’il avait à la main, et toucha la chair et les pains sans levain. Aussitôt le feu s’éleva du rocher, et consuma la chair et les pains sans levain, et l’Ange de Yahweh disparut à ses yeux.
Mngelo wa Yehova anatenga msonga ya ndodo imene inali mʼmanja mwake nakhudza nayo nyama ndi makeke aja. Nthawi yomweyo moto unabuka pa thanthwepo ndi kupsereza nyama yonse ndi makeke aja. Ndipo mngelo wa Yehova sanaonekenso.
22 Gédéon vit que c’était l’Ange de Yahweh et Gédéon dit: « Malheur à moi, Seigneur Yahweh, car j’ai vu l’Ange de Yahweh face à face. »
Apo Gideoni anazindikira kuti analidi mngelo wa Ambuye, ndipo anati, “Kalanga ine Yehova Wamphamvuzonse! Ine ndaona mngelo wa Yehova ndi maso!”
23 Yahweh lui dit: « Sois en paix, ne crains point, tu ne mourras pas. »
Koma Yehova anamuwuza kuti, “Mtendere ukhale ndi iwe! Usachite mantha, sufa ayi.”
24 Gédéon bâtit là un autel à Yahweh et l’appela: « Yahweh-Schalôm; » cet autel existe encore aujourd’hui à Ephra d’Abiéser.
Choncho Gideoni anamanga guwa lansembe la Yehova pamenepo ndipo analitcha kuti, Yehova ndiye mtendere. Kufikira lero lino guwali lilipo ku Ofura wa Mwabiezeri.
25 Cette nuit-là, Yahweh dit à Gédéon: « Prends le jeune taureau de ton père, et le second taureau de sept ans. Renverse l’autel de Baal qui est à ton père, et coupe l’aschéra qui est auprès.
Usiku womwewo Yehova anati kwa Gideoni, “Tenga ngʼombe ya mphongo ya abambo ako, ngʼombe ina yachiwiri ya zaka zisanu ndi ziwiri ndipo ugwetse guwa la Baala limene abambo ako ali nalo, ndi kugwetsanso fano la Asera limene lili pafupi pake.
26 Tu bâtiras ensuite, au sommet de ce lieu fort, un autel à Yahweh, ton Dieu, et tu le disposeras; tu prendras le second taureau et tu offriras un holocauste avec le bois de l’aschéra que tu auras coupée. »
Kenaka umangire Yehova Mulungu wako guwa lansembe ndi miyala yoyala bwino pamwamba pa chiwunda chimenecho. Utenge ngʼombe ya mphongo yachiwiri ija ndipo uyipereke ngati nsembe yopsereza pogwiritsa ntchito mitengo ya fano la Asera imene udule ngati nkhunizo.”
27 Gédéon prit dix hommes parmi ses serviteurs, et exécuta ce que Yahweh lui avait dit: mais, comme il n’osait le faire de jour par crainte de la maison de son père et des gens de la ville, il le fit de nuit.
Choncho Gideoni anatenga antchito ake khumi nachita monga Yehova anamuwuzira. Ndipo popeza ankaopa anthu a pa banja lake ndiponso anthu a mʼmudzimo sanachite zimenezi masana koma usiku.
28 Lorsque les gens de la ville se levèrent le lendemain matin, voici que l’autel de Baal était renversé, que l’aschéra qui était auprès était coupée, et que le second taureau était offert en holocauste sur l’autel récemment bâti.
Anthu a mu mzindamo atadzuka mʼmamawa anangoona guwa la Baala litagwetsedwa ndi fano la Asera limene linali pamwamba pake litadulidwa ndiponso ngʼombe yamphongo yachiwiri ija itaperekedwa ngati nsembe yopsereza pa guwa limene linamangidwa lija.
29 Ils se dirent l’un à l’autre: « Qui a fait cela? » et ils s’informèrent et firent des recherches. On leur dit: « C’est Gédéon, fils de Joas, qui a fait cela. »
Iwo anafunsana wina ndi mnzake, “Wachita zimenezi ndani?” Atafufuza ndi kufunsafunsa, analingalira kuti, “Gideoni mwana wa Yowasi ndiye wachita zimenezi.”
30 Alors les gens de la ville dirent à Joas: « Fais sortir ton fils et qu’il meure, car il a renversé l’autel de Baal et coupé l’aschéra qui était auprès. »
Ndipo anthuwo anawuza Yowasi kuti, “Tulutsa mwana wako, ayenera kufa chifukwa wagumula guwa lansembe la Baala ndipo wadula fano la Asera lomwe linali pamwamba pake.”
31 Joas dit à tous ceux qui se tenaient là contre lui: « Est-ce à vous de prendre parti pour Baal? Ou bien est-ce à vous de le secourir? Quiconque prendra parti pour Baal sera mis à mort avant demain matin. Si Baal est Dieu, que lui-même prenne en main sa cause, puisqu’on a renversé son autel! »
Koma Yowasi anawuza anthu amene anamuzungulirawo kuti, “Kodi inu mukuti mukhale woyankhulira Baala mlandu? Kodi ndinu amene mukuti mumupulumutse? Amene akufuna kumumenyera nkhondo Baala akhala atafa pofika mmawa! Ngati Baalayo ndi mulungudi, musiyeni adzimenyere yekha nkhondo popeza munthu wina wamugwetsera guwa lansembe lake.”
32 En ce jour, un donna à Gédéon le nom de Jérobaal, en disant: « Que Baal se défende contre lui, puisqu’il a renversé son autel! »
Choncho tsiku limenelo Gideoni anatchedwa, Yeru-Baala, kutanthauza kuti, “Baala alimbana naye, popeza anagwetsa guwa lake la nsembe.”
33 Tout Madian, Amalec et les fils de l’Orient se rassemblèrent et, ayant passé le Jourdain, ils campèrent dans la plaine de Jezraël.
Tsopano Amidiyani, Amaleki ndi anthu ena akummawa anasonkhana ndipo atawoloka Yorodani anakamanga zinthando za nkhondo ku chigwa cha Yezireeli.
34 L’Esprit de Yahweh revêtit Gédéon; il sonna de la trompette, et les Abiésérites s’assemblèrent pour marcher à sa suite.
Ndipo Mzimu wa Yehova unatsikira pa Gideoni, ndipo anayimba lipenga kuyitana Abiezeri kuti amutsatire iye.
35 Il envoya des messagers dans tout Manassé, qui s’assembla aussi pour le suivre. Il envoya des messagers dans Aser, dans Zabulon et dans Nephtali, et ils montèrent à leur rencontre.
Iye anatumiza amithenga mʼdziko lonse la Manase kuti akamenye nkhondo ndipo Amanase anayitanidwanso kuti amutsate. Anatumanso amithenga kwa Aseri, Azebuloni ndi Anafutali, ndipo onsewo anapita kukakumana naye.
36 Gédéon dit à Dieu: « Si vous voulez sauver Israël par ma main, comme vous l’avez dit,
Gideoni anati kwa Mulungu, “Ngati mudzapulumutsa Israeli ndi dzanja langa monga mwalonjezeramu,
37 voici, je mettrai une toison de laine sur l’aire: si la toison seule se couvre de rosée, et que tout le sol alentour reste sec, je connaîtrai que vous délivrerez Israël par ma main, comme vous l’avez dit. »
onani, ine ndiyala ubweya wankhosa pa malo opunthira tirigu. Ngati mame adzagwera pa ubweya wankhosa pokhapa, pa nthaka ponse pakhala powuma, ndiye ndidziwa kuti mudzapulumutsadi Israeli ndi dzanja langa monga mwanenera.”
38 Et il arriva ainsi. Le jour suivant, s’étant levé de bon matin, il pressa la toison, et en fit sortir la rosée, plein une coupe d’eau.
Ndipo zimenezi zinachitikadi. Gideoni atadzuka mʼmamawa ndi kuwufinya ubweya uja, anafinya madzi odzaza mtsuko.
39 Gédéon dit à Dieu: « Que votre colère ne s’enflamme pas contre moi; que je puisse encore parler une fois: je voudrais une fois encore seulement faire une épreuve avec la toison: que la toison seule reste sèche, et que la rosée tombe sur tout le sol alentour. »
Kenaka Gideoni anati kwa Mulungu, “Musandikwiyire. Mundilole ndiyankhule kamodzi kokhaka. Ndiyeseko kamodzi kokha ndi ubweyawu kuti pa ubweya pokhapa pakhale powuma koma pa nthaka ponse pakhale ponyowa ndi mame.”
40 Et Dieu fit ainsi cette nuit-là: la toison seule resta sèche, et tout le sol se couvrit de rosée.
Ndipo Mulungu anachita zomwezo usiku umenewo. Pa ubweya pokha panali powuma, koma pa nthaka ponse panagwa mame.

< Juges 6 >