< Josué 21 >

1 Les chefs de famille des Lévites s’approchèrent du prêtre Eléazar, de Josué, fils de Nun, et des chefs de famille des tribus des enfants d’Israël;
Tsono atsogoleri a mabanja a fuko la Levi anabwera kwa wansembe Eliezara, Yoswa mwana wa Nuni, ndi kwa atsogoleri a mabanja a mafuko onse a Aisraeli,
2 ils leur parlèrent à Silo, dans le pays de Canaan, en disant: « Yahweh a ordonné par Moïse qu’on nous donnât des villes pour notre habitation, et leurs banlieues pour notre bétail. »
ku Silo mʼdziko la Kanaani ndipo anati, “Yehova analamula kudzera mwa Mose kuti atipatse mizinda kuti tikhalemo, pamodzi ndi malo odyetseramo ziweto zathu.”
3 Les enfants d’Israël donnèrent aux Lévites, sur leur héritage, selon l’ordre de Yahweh, les villes suivantes et leurs banlieues.
Choncho, Aisraeli anapereka kwa fuko la Levi mizinda iyi pamodzi ndi malo owetera ziweto zawo kuchokera ku madera awo, monga Yehova analamulira:
4 Le sort fut tiré d’abord pour les familles des Caathites; et les fils du prêtre Aaron, d’entre les Lévites, obtinrent par le sort treize villes de la tribu de Juda, de la tribu de Siméon et de la tribu de Benjamin;
Maere oyamba anagwera mabanja a Kohati, Alevi amene anali zidzukulu za wansembe Aaroni anapatsidwa mizinda 13 kuchokera ku mafuko a Yuda, Simeoni ndi Benjamini.
5 les autres fils de Caath obtinrent par le sort dix villes des familles de la tribu d’Ephraïm, de la tribu de Dan et de la demi-tribu de Manassé.
Ndipo mabanja otsala a Kohati anapatsidwa mizinda khumi kuchokera ku mafuko a Efereimu, Dani ndi theka la fuko la Manase.
6 Les fils de Gerson obtinrent par le sort treize villes des familles de la tribu d’Issachar, de la tribu d’Aser, de la tribu de Nephthali et de la demi-tribu de Manassé en Basan.
Zidzukulu za Geresoni zinapatsidwa mizinda 13 kuchokera ku mabanja a mafuko a Isakara, Aseri, Nafutali ndi theka la fuko la Manase ku Basani.
7 Les fils de Mérari, selon leurs familles, obtinrent douze villes de la tribu de Ruben, de la tribu de Gad et de la tribu de Zabulon.
Mabanja a Merari anapatsidwa mizinda khumi ndi iwiri kuchokera ku mafuko a Rubeni, Gadi ndi Zebuloni.
8 Les enfants d’Israël donnèrent par le sort aux Lévites, ces villes et leurs banlieues, comme Yahweh l’avait ordonné par Moïse.
Choncho Aisraeli anapereka kwa fuko la Levi mizindayi pamodzi ndi malo odyetserako ziweto pogwiritsa ntchito maere, monga Yehova analamula kudzera mwa Mose.
9 Ils donnèrent de la tribu des fils de Juda et de la tribu des fils de Siméon les villes suivantes désignées par leurs noms;
Awa ndi mayina a mizinda ya mafuko a Yuda ndi Simeoni imene inaperekedwa kwa zidzukulu za Aaroni,
10 ce fut pour les fils d’Aaron, d’entre les familles des Caathites, d’entre les fils de Lévi, car le sort fut d’abord tiré pour eux.
ku banja la Kohati amene anali Alevi. Paja maere oyamba anagwera mabanja a Kohati kuti alandira mizinda.
11 Ils leurs donnèrent, dans la montagne de Juda, la ville d’Arbé, père d’Enac, laquelle est Hébron, et sa banlieue tout autour.
Anapatsidwa mzinda wa Kiriati Ariba. (Paja Ariba ndiye kholo la Anaaki). Dzina lina la mzindawu ndi Hebroni, ndipo unali mʼdziko la mapiri la Yuda. Pamodzi ndi mzindawu anapatsidwanso mabusa ake onse ozungulira.
12 Mais la campagne de cette ville et ses villages, ils les donnèrent en possession à Caleb, fils de Jéphoné.
Komabe minda ndi midzi yozungulira mizindayi inali itaperekedwa kale kwa Kalebe, mwana wa Yefune kuti ikhale cholowa chake.
13 Ils donnèrent aux fils du prêtre Aaron la ville de refuge pour le meurtrier, Hébron et sa banlieue, ainsi que Lebna avec sa banlieue,
Choncho zidzukulu za Aaroni wansembe, zinapatsidwa Hebroni (mzinda wopulumukirako amene wapha munthu), Libina,
14 Jéther et sa banlieue, Estémo et sa banlieue,
Yatiri, Esitemowa,
15 Holon et sa banlieue, Dabir et sa banlieue,
Holoni, Debri,
16 Aïn et sa banlieue, Jéta et sa banlieue, Bethsamès et sa banlieue: neuf villes de ces deux tribus.
Aini, Yuta, ndi Beti-Semesi pamodzi ndi mabusa odyetseramo ziweto ozungulira mizindayi. Yonse pamodzi inali mizinda isanu ndi inayi yochokera ku mafuko awiriwa.
17 De la tribu de Benjamin: Gabaon et sa banlieue, Gabaa et sa banlieue,
Fuko la Benjamini linapereka Gibiyoni, Geba,
18 Anathoth et sa banlieue, Almon et sa banlieue: quatre villes.
Anatoti ndi Alimoni, pamodzi ndi mabusa odyetsera ziweto ozungulira mizindayi. Yonse pamodzi inali mizinda inayi.
19 Total des villes des prêtres, fils d’Aaron: treize villes et leurs banlieues.
Choncho mizinda 13 pamodzi ndi malo odyetsera ziweto anapatsidwa kwa ansembe, zidzukulu za Aaroni.
20 Quant aux familles des fils de Caath, Lévites, aux autres fils de Caath, les villes qui leur échurent par le sort furent de la tribu d’Ephraïm.
Mabanja ena otsalira a Kohati a fuko la Levi anapatsidwa mizinda iyi kuchokera ku fuko la Efereimu:
21 Les enfants d’Israël leur donnèrent la ville de refuge pour le meurtrier, Sichem et sa banlieue, dans la montagne d’Ephraïm, ainsi que Gazer et sa banlieue,
Mizinda ya Sekemu ndi Gezeri ndiye inali mizinda wopulumukirako munthu aliyense wopha mnzake mwangozi. Mizindayi inali ku mapiri a Efereimu.
22 Cibsaïm et sa banlieue, Beth-Horon et sa banlieue: quatre villes.
Analandiranso mizinda ya Gezeri, Kibuzaimu, Beti-Horoni pamodzi ndi malo odyetsera ziweto ozungulira mizindayi. Yonse pamodzi inali mizinda inayi.
23 De la tribu de Dan: Elthéco et sa banlieue, Gabathon et sa banlieue,
Fuko la Dani linapereka mizinda ya Eliteke, Gibetoni,
24 Ajalon et sa banlieue, Geth-Remmon et sa banlieue: quatre villes.
Ayaloni, Gati-Rimoni pamodzi ndi mabusa odyetsera ziweto ozungulira mizindayi. Yonse pamodzi inali mizinda inayi.
25 De la demi-tribu de Manassé: Thanach et sa banlieue, et Geth-Remmon et sa banlieue: deux villes.
Kuchokera ku theka la fuko la Manase analandira Taanaki ndi Gati-Rimoni pamodzi ndi malo awo owetera ziweto, mizinda iwiri.
26 Total: dix villes avec leurs banlieues, pour les familles des autres fils de Caath.
Mizinda khumi yonseyi pamodzi ndi malo odyetsera ziweto, zinapatsidwa ku mabanja ena onse a Akohati.
27 Aux fils de Gerson, d’entre les familles des Lévites, ils donnèrent, de la demi-tribu de Manassé, la ville de refuge pour le meurtrier, Gaulon, en Basan, et sa banlieue, ainsi que Bosra et sa banlieue: deux villes.
Mabanja a Ageresoni a fuko la Levi anapatsidwa mizinda iwiri kuchokera ku theka la Manase wa kummawa, Golani ku Basani (mzinda wopulumukirako amene wapha munthu mwangozi) ndi Beesitera, pamodzi ndi malo awo odyetserako ziweto.
28 De la tribu d’Issachar: Césion et sa banlieue, Dabéreth et sa banlieue,
Fuko la Isakara linapereka mizinda ya Kisoni, Daberati,
29 Jaramoth et sa banlieue, En-Gannim et sa banlieue: quatre villes.
Yarimuti ndi Eni Ganimu, pamodzi ndi malo awo odyetsera ziweto. Yonse pamodzi inali mizinda inayi.
30 De la tribu d’Aser: Masal et sa banlieue, Abdon et sa banlieue,
Fuko la Aseri linapereka mizinda ya Misali, Abidoni,
31 Helcath et sa banlieue, Rohob et sa banlieue: quatre villes.
Helikati ndi Rehobu pamodzi ndi malo awo odyetsera ziweto. Yonse pamodzi inali mizinda inayi.
32 De la tribu de Nephthali: la ville de refuge pour le meurtrier, Cédès en Galilée et sa banlieue, ainsi que Hamoth-Dor et sa banlieue, Carthan et sa banlieue: trois villes.
Fuko la Nafutali linapereka mizinda ya Kedesi wa ku Galileya, mzinda umene unali wopulumukiramo munthu wopha mnzake mwangozi. Analandiranso mizinda ya Hamoti-Dori ndi Karitani. Kuphatikizira apa, analandira malo odyetsera ziweto a mizindayi. Yonse pamodzi inali mizinda inayi.
33 Total des villes des Gersonites, selon leurs familles: treize villes et leurs banlieues.
Mabanja onse a Ageresoni analandira mizinda 13 pamodzi ndi malo awo odyetsera a ziweto.
34 Aux familles des fils de Mérari, au reste des Lévites, ils donnèrent, de la tribu de Zabulon: Jecnam et sa banlieue, Cartha et sa banlieue,
Mabanja a Merari amene anali otsala a fuko la Levi, anapatsidwa mizinda iyi kuchokera ku fuko la Zebuloni: Yokineamu, Karita,
35 Damna et sa banlieue, Naalol et sa banlieue: quatre villes.
Dimuna ndi Nahalali, pamodzi ndi malo awo odyetsera ziweto. Yonse pamodzi inali mizinda inayi.
36 Et de la tribu de Gad: la ville de refuge pour le meurtrier, Ramoth en Galaad et sa banlieue, ainsi que Manaïm et sa banlieue,
Kuchokera ku fuko la Rubeni analandira Bezeri, Yahaza,
37 Hésebon et sa banlieue, Jaser et sa banlieue: en tout quatre villes.
Kedemoti ndi Mefaati, pamodzi ndi malo awo odyetsera ziweto. Yonse pamodzi inali mizinda inayi.
Kuchokera ku fuko la Gadi analandira mzinda wa Ramoti ku Giliyadi. Mzinda umene unali wopulumukiramo munthu wopha mnzake mwangozi.
Analandiranso mizinda ya Mahanaimu, Hesiboni, Yazeri pamodzi ndi malo odyetserako ziweto ozungulira mizinda yonseyi. Yonse pamodzi inali mizindayi anayi.
40 Total des villes assignées par le sort aux fils de Mérari, selon leurs familles, formant le reste des familles des Lévites: douze villes.
Choncho mabanja onse a Merari, amene anali otsala a fuko la Levi analandira mizinda khumi ndi iwiri pogwiritsa ntchito maere.
41 Total des villes des Lévites au milieu des possessions des enfants d’Israël: quarante-huit villes et leurs banlieues.
Motero mizinda 48 ya mʼdziko limene Aisraeli analanda inapatsidwa kwa Alevi, kuphatikizapo malo ake odyetsera ziweto.
42 Chacune de ces villes avait sa banlieue tout autour; il en était ainsi pour toutes ces villes.
Iliyonse mwa mizindayi inali ndi malo owetera ziweto oyizungulira.
43 C’est ainsi que Yahweh donna à Israël tout le pays qu’il avait juré de donner à leurs pères; ils en prirent possession et s’y établirent.
Motero Yehova anapereka kwa Israeli dziko limene analumbira kulipereka kwa makolo awo. Atalilandira anadzakhalamo.
44 Yahweh leur accorda du repos tout autour d’eux, comme il l’avait juré à leurs pères; aucun de leurs ennemis ne put leur résister, et Yahweh les livra tous entre leurs mains.
Yehova anawapatsa mtendere mʼdziko lonse monga momwe analonjezera makolo awo. Palibe ndi mmodzi yemwe mwa adani awo amene anatha kuwagonjetsa chifukwa Yehova anapereka adani awo onse mʼmanja mwawo.
45 De toutes les bonnes paroles que Yahweh avait dites à la maison d’Israël, aucune ne resta sans effet; toutes s’accomplirent.
Yehova anakwaniritsa zonse zimene analonjeza kwa Aisraeli.

< Josué 21 >