< Josué 18 >
1 Toute l’assemblée des enfants d’Israël se réunit à Silo, et ils y dressèrent la tente de réunion; le pays était soumis devant eux.
Atagonjetsa dziko lonse Aisraeli anasonkhana ku Silo ndipo anayimikako tenti ya msonkhano.
2 Il restait sept tribus d’entre les enfants d’Israël qui n’avaient pas encore reçu leur héritage.
Koma pa nthawiyo nʼkuti mafuko asanu ndi awiri a Aisraeli asanalandire cholowa chawo.
3 Josué dit aux enfants d’Israël: « Jusques à quand négligerez-vous de prendre possession du pays que Yahweh, le Dieu de vos pères, vous a donné?
Ndipo Yoswa anati kwa Aisraeli, “Kodi mudikira mpaka liti kuti mulowe ndi kulanda dziko limene Yehova Mulungu wa makolo anu wakupatsani?
4 Choisissez trois hommes par tribu, et je les enverrai; ils se lèveront, parcourront le pays, le décriront en vue du partage et reviendront vers moi.
Sankhani amuna atatu kuchokera ku fuko lililonse ndipo ine ndidzawatuma kuti akayendere dzikolo ndi kukalilembera bwino kuti ndiligawe kukhala lawo. Akatero, abwererenso kwa ine.
5 Ils le diviseront en sept portions; Juda restera dans ses frontières au midi, et la maison de Joseph restera dans ses frontières au nord.
Aligawe dzikolo mʼzigawo zisanu ndi ziwiri; fuko la Yuda lidzakhale ndi dziko lake la kummwera ndi nyumba ya Yosefe ikhalebe mʼdziko lawo la kumpoto.
6 Vous donc, vous dresserez l’état du pays, en en faisant sept parts, et vous me l’apporterez ici; puis je jetterai pour vous le sort ici devant Yahweh, notre Dieu.
Mudzalembe mawu ofotokoza za zigawo zisanu ndi ziwiri za dzikolo, ndi kubwera nawo kwa ine. Tsono ineyo ndidzakuchitirani maere pamaso pa Yehova Mulungu wanu.
7 Car il n’y aura pas de part pour les Lévites au milieu de vous, le sacerdoce de Yahweh étant leur héritage; et Gad, Ruben, et la demi-tribu de Manassé ont reçu de l’autre côté du Jourdain, à l’orient, leur héritage, que leur a donné Moïse, serviteur de Yahweh. »
Alevi asakhale ndi dziko pakati panu, chifukwa gawo lawo ndi kutumikira Yehova pa ntchito ya unsembe. Ndipo Gadi, Rubeni ndi theka la fuko la Manase analandira kale cholowa chawo kummawa kwa Yorodani. Mose mtumiki wa Yehova ndiye anawapatsa.”
8 Ces hommes s’étant levés se mirent en route, et Josué leur donna ses ordres à leur départ pour dresser l’état du pays, en disant: « Allez, parcourez le pays, décrivez-le et revenez auprès de moi; alors je jetterai pour vous le sort ici, devant Yahweh, à Silo. »
Anthuwo akupita kukalembera dzikolo, Yoswa anawalangiza kuti, “Pitani mukayendere ndi kulembera dzikolo. Kenaka mukabwere kwa ine, ndidzakuchitirani maere kuno ku Silo pamaso pa Yehova.”
9 Ces hommes partirent et, parcourant le pays, ils le décrivirent dans un livre selon les villes, en le partageant en sept portions; et ils revinrent auprès de Josué, dans le camp, à Silo.
Ndipo anthu anachoka ndi kukayendera dziko lonse. Iwo analemba bwinobwino mʼbuku za dzikolo, mzinda ndi mzinda. Analigawa magawo asanu ndi awiri, ndipo anabwerera kwa Yoswa ku misasa ya ku Silo.
10 Josué jeta pour eux le sort à Silo, en présence de Yahweh, et là Josué partagea le pays aux enfants d’Israël, selon leurs portions.
Pambuyo pake Yoswa anawachitira maere ku Silo pamaso pa Yehova, ndipo fuko lililonse la Israeli analigawira dziko lake.
11 Le sort tomba sur la tribu des fils de Benjamin, selon ses familles, et le territoire qui leur échut par le sort, était entre les fils de Juda et les fils de Joseph.
Maere anagwera mabanja a fuko la Benjamini. Dziko limene anapatsidwa linali pakati pa fuko la Yuda ndi fuko la Yosefe:
12 Du côté du nord, leur frontière partait du Jourdain; et la frontière montait au nord sur le versant de Jéricho, puis montait dans la montagne à l’occident, et aboutissait au désert de Bethaven.
Mbali ya kumpoto malire awo anayambira ku Yorodani nalowera chakumpoto kwa matsitso a ku Yeriko kulowera cha kumadzulo kwa dziko la ku mapiri ndi kukafika ku chipululu cha Beti-Aveni.
13 De là, la frontière passait à Luz, sur le versant de Luz, au midi, c’est Béthel; puis la frontière descendait à Ataroth-Addar, par la montagne qui est au midi de Béthoron le Bas.
Kuchokera kumeneko malirewo analoza ku Luzi nadutsa mʼmbali mwa mapiri kummwera kwa Luzi (ndiye Beteli) ndipo anatsika mpaka ku Ataroti Adari, ku mapiri a kummwera kwa Beti-Horoni wa Kumunsi.
14 Et la frontière s’étendait et tournait, du côté de l’occident, vers le midi, depuis la montagne située en face de Béthoron au sud, et aboutissait à Cariath-Baal, qui est Cariath-Jéarim, ville des fils de Juda: voilà pour le côté de l’occident.
Ndipo malirewo analowanso kwina, analunjika kummwera kuchokera kumadzulo kwake kwa phiri loyangʼanana ndi Beti-Horoni, mpaka ku mzinda wa Kiriyati Baala (ndiye Kiriati Yearimu), mzinda wa anthu a fuko la Yuda. Amenewa ndiye anali malire a mbali ya kumadzulo.
15 Pour le côté du midi, la frontière partait de l’extrémité de Cariath-Jéarim, et aboutissait à l’occident, elle aboutissait à la source des eaux de Nephtoa.
Malire a kummwera anayambira mʼmphepete mwenimweni mwa Kiriati Yearimu napita kumadzulo mpaka kukafika ku akasupe a Nefitowa.
16 Et la frontière descendait à l’extrémité de la montagne qui fait face à la vallée du fils d’Ennom, située dans la plaine des Rephaïm, au nord; puis elle descendait, par la vallée d’Ennom, vers le versant méridional des Jébuséens, elle descendait à la source de Rogel.
Malire anatsikira mʼmphepete mwa phiri loyangʼanana ndi chigwa cha Beni Hinomu, kumpoto kwa chigwa cha Refaimu. Anapitirira kutsikira ku chigwa cha Hinomu kummwera kwa chitunda cha Ayebusi mpaka ku Eni Rogeli.
17 Elle s’étendait au nord, et elle aboutissait à En-Sémès; elle aboutissait à Géliloth, qui est vis-à-vis de la montée d’Adommim, et elle descendait à la pierre de Boën, fils de Ruben.
Kenaka anakhotera kumpoto kupita ku Eni-Semesi, kupitirira mpaka ku Geliloti amene amayangʼanana ndi pokwera pa Adumimu. Kenaka malire anatsikira ku Mwala wa Bohani, mwana wa Rubeni.
18 Elle passait par le versant septentrional de la montagne en face de l’Arabah, et descendait à l’Arabah.
Anabzola cha kumpoto kwa chitunda cha Beti Araba ndi kutsikabe mpaka ku chigwa cha Yorodani.
19 La frontière passait par le versant septentrional de Beth-Hagla, et la frontière aboutissait à la langue septentrionale de la mer Salée, vers l’embouchure du Jourdain, au midi: c’était la frontière du sud.
Anabzolanso cha kumpoto kwa chitunda cha Beti-Hogila kukafika cha kumpoto ku gombe la Nyanja ya Mchere kumene mtsinje wa Yorodani umathirirako, cha kummwera kwenikweni. Awa anali malire a kummwera.
20 Le Jourdain formait sa limite du côté de l’orient. Tel fut l’héritage des fils de Benjamin, d’après ses frontières tout autour, selon leurs familles.
Yorodani ndiye anali malire a mbali ya kummawa. Awa anali malire a dziko limene mabanja a fuko la Benjamini analandira.
21 Les villes de la tribu des fils de Benjamin, selon leurs familles, étaient: Jéricho, Beth-Hagla, Emek-Casis,
Mabanja a fuko la Benjamini anali ndi mizinda iyi; Yeriko, Beti-Hogila, Emeki Kezizi,
22 Beth-Araba, Samaraïm, Béthel,
Beti-Araba, Zemaraimu, Beteli
24 Képhar-Emona, Ophni et Gabée: douze villes et leurs villages.
Kefari-Amoni, Ofini ndi Geba, mizinda khumi ndi awiri ndi midzi yake
Panalinso Gibiyoni, Rama, Beeroti,
26 Mesphé, Caphara, Amosa,
Mizipa, Kefira, Moza
27 Récem, Jaréphel, Tharéla,
Rekemu, Iripeeli, Tarala,
28 Séla, Eleph, Jébus, qui est Jérusalem, Gabaath, et Cariath: quatorze villes et leurs villages. Tel fut l’héritage des fils de Benjamin, selon leurs familles.
Zera Haelefu, mzinda wa Ayebusi (ndiye kuti Yerusalemu) Gibeya ndi Kiriati, mizinda 14 ndi midzi yake. Limeneli ndilo dziko limene mabanja a fuko la Benjamini analandira kuti likhale lawo.