< Job 34 >

1 Eliu reprit et dit:
Pamenepo Elihu anapitiriza kuyankhula kuti,
2 Sages, écoutez mes discours; hommes intelligents, prêtez-moi l’oreille.
“Imvani mawu anga, inu anthu anzeru; tcherani khutu inu anthu ophunzira.
3 Car l’oreille juge les paroles, comme le palais discerne les aliments.
Pakuti khutu limayesa mawu monga momwe mʼkamwa mumalawira chakudya.
4 Tâchons de discerner ce qui est juste; cherchons entre nous ce qui est bon.
Tsono tiyeni tizindikire chomwe chili choyenera; tiphunzire pamodzi chomwe chili chabwino.
5 Job a dit: « Je suis innocent, et Dieu me refuse justice.
“Yobu akunena kuti, ‘Ndine wosalakwa, koma Mulungu akukana kundiweruza molungama.
6 Quand je soutiens mon droit, je passe pour menteur; ma plaie est douloureuse, sans que j’aie péché. »
Ngakhale ndine wolungama mtima, akundiyesa wabodza; ngakhale ndine wosachimwa, mivi yake ikundichititsa mabala osachiritsidwa.’
7 Y a-t-il un homme semblable à Job? Il boit le blasphème comme l’eau!
Kodi munthu wofanana ndi Yobu ndani, amene amayankhula zamwano ngati akumwa madzi?
8 Il s’associe aux artisans d’iniquité, il marche avec les hommes pervers.
Iye amayenda ndi anthu ochita zoyipa; amayanjana ndi anthu oyipa mtima.
9 Car il a dit: « Il ne sert de rien à l’homme de chercher la faveur de Dieu. »
Paja iye amanena kuti, ‘Munthu sapindula kanthu poyesetsa kukondweretsa Mulungu.’
10 Ecoutez-moi donc, hommes sensés: Loin de Dieu l’iniquité! Loin du Tout-Puissant l’injustice!
“Tsono mverani ine, inu anthu anzeru zomvetsa zinthu. Mulungu sangachite choyipa ndi pangʼono pomwe, Wamphamvuzonse sangathe kuchita cholakwa.
11 Il rend à l’homme selon ses œuvres, il rétribue chacun selon ses voies.
Iye amamubwezera munthu molingana ndi ntchito zake; Mulungu amabweretsa pa munthu molingana ndi zomwe amachita.
12 Non, certes, Dieu ne commet pas l’iniquité, le Tout-Puissant ne viole pas la justice.
Nʼchosayembekezeka kuti Mulungu achite cholakwa, kuti Wamphamvuzonse apotoze chilungamo.
13 Qui lui a remis le gouvernement de la terre? Qui lui a confié l’univers?
Kodi anapatsa Mulungu udindo wolamulira dziko lapansi ndani? Ndani anayika Mulungu kuti azilamulira dziko lonse?
14 S’il ne pensait qu’à lui-même, s’il retirait à lui son esprit et son souffle,
Mulungu akanakhala ndi maganizo oti achotse mzimu wake ndi mpweya wake,
15 toute chair expirerait à l’instant, et l’homme retournerait à la poussière.
zamoyo zonse zikanawonongekeratu ndipo munthu akanabwerera ku fumbi.
16 Si tu as de l’intelligence, écoute ceci; prête l’oreille au son de mes paroles:
“Ngati ndinu omvetsa zinthu, imvani izi; mvetserani zimene ndikunena.
17 Un ennemi de la justice aurait-il le suprême pouvoir? Oses-tu condamner le Juste, le Puissant,
Kodi Mulungu wodana ndi chilungamo angathe kukhala wolamulira? Kodi iwe ungathe kuweruza Wolungama ndi Wamphamvuyo?
18 qui dit à un roi: « Vaurien! » aux princes: « Pervers! »
Kodi si Iye amene amanena kwa mafumu kuti, ‘Ndinu opanda pake,’ ndipo amawuza anthu otchuka, ‘Ndinu oyipa,’
19 qui ne fait pas acception de la personne des grands, qui ne regarde pas le riche plus que le pauvre, parce que tous sont l’ouvrage de ses mains?
Iye sakondera akalonga ndipo salemekeza anthu olemera kupambana osauka, pakuti onsewa ndi ntchito ya manja ake?
20 En un instant ils périssent, au milieu de la nuit, les peuples chancellent et disparaissent; le puissant est emporté sans main d’homme.
Iwo amafa mwadzidzidzi, pakati pa usiku; anthu amachita mantha ndipo amamwalira; munthu wamphamvu amachotsedwa popanda dzanja la munthu.
21 Car les yeux de Dieu sont ouverts sur les voies de l’homme, il voit distinctement tous ses pas.
“Maso a Mulungu amapenya njira za munthu; amaona mayendedwe ake onse.
22 Il n’y a ni ténèbres ni ombre de la mort, où puissent se cacher ceux qui commettent l’iniquité.
Palibe malo obisika kapena a mdima wandiweyani kumene anthu ochita zoyipa angabisaleko.
23 Il n’a pas besoin de regarder un homme deux fois, pour l’amener au jugement avec lui.
Mulungu sasowa kuti apitirizebe kufufuza munthu, kuti abwere pamaso pake kudzaweruzidwa.
24 Il brise les puissants sans enquête, et il en met d’autres à leur place.
Popanda kufufuza, Iye amawononga anthu amphamvu ndipo mʼmalo mwawo amayikamo ena.
25 Il connaît donc leurs œuvres; il les renverse de nuit, et ils sont écrasés.
Pakuti Iyeyo amadziwa bwino ntchito zawo amawagubuduza usiku ndipo amatswanyika.
26 Il les frappe comme des impies, en un lieu où on les regarde,
Iye amawalanga chifukwa cha kuyipa kwawo, pamalo pamene aliyense akuwaona;
27 parce qu’en se détournant de lui, en refusant de connaître toutes ses voies,
Chifukwa anasiya kumutsata ndipo sasamaliranso njira zake zonse.
28 ils ont fait monter vers lui le cri du pauvre, ils l’ont rendu attentif au cri des malheureux.
Anachititsa amphawi kuti kulira kwawo kufike pamaso pake, kotero Iyeyo anamva kulira kwa amphawiwo.
29 S’il accorde la paix, qui le trouvera mauvais; s’il cache son visage, qui pourra le contempler, qu’il soit peuple ou homme celui qu’il traite ainsi,
Koma ngati Mulungu akhala chete, ndani angamunene kuti walakwa? Akabisa nkhope yake, ndani angathe kumupenyabe? Komatu ndiye amene amayangʼana za munthu komanso mtundu wa anthu,
30 pour mettre fin au règne de l’impie, pour qu’il ne soit plus un piège pour le peuple?
kuti asalamuliridwe ndi anthu osapembedza, kuti asatchere anthu misampha.
31 Or avait-il dit à Dieu: « J’ai été châtié, je ne pécherai plus;
“Mwina munthu atanena kwa Mulungu kuti, ‘Ndine wolakwa koma sindidzachimwanso,
32 montre-moi ce que j’ignore; si j’ai commis l’iniquité, je ne le ferai plus? »
ndiphunzitseni zimene sindikuziona ngati ndachita choyipa, sindidzachitanso.’
33 Est-ce d’après ton avis que Dieu doit rendre la justice de sorte que tu puisses rejeter son jugement? Choisis à ton gré, et non pas moi; ce que tu sais, expose-le.
Kodi Mulungu akuweruzeni potsata mmene inuyo mukuganizira, pamene inu mukukana kulapa? Chisankho nʼchanu, osati changa; tsono ndiwuzeni zomwe mukudziwa.
34 Les gens sensés me diront, ainsi que l’homme sage qui m’écoute:
“Anthu omvetsa zinthu adzakambirana, anthu anzeru amene akundimva adzandiwuza kuti,
35 « Job a parlé sans intelligence, et ses discours sont dépourvus de sagesse.
‘Yobu akuyankhula mopanda nzeru; mawu ake ndi opanda fundo.’
36 Eh bien, que Job soit éprouvé jusqu’au bout, puisque ses réponses sont celles d’un impie!
Aa, kunali bwino Yobu akanayesedwa mpaka kumapeto chifukwa choyankha ngati munthu woyipa!
37 Car à l’offense il ajoute la révolte; il bat des mains au milieu de nous, il multiplie ses propos contre Dieu. »
Pa tchimo lake amawonjezerapo kuwukira; amawomba mʼmanja mwake monyoza pakati pathu, ndipo amachulukitsa mawu otsutsana ndi Mulungu.”

< Job 34 >