< Job 28 >

1 Il y a pour l’argent un lieu d’où on l’extrait, pour l’or un lieu où on l’épure.
Pali mgodi wa siliva ndiponso malo oyengerapo golide.
2 Le fer se tire de la terre, et la pierre fondue donne le cuivre.
Chitsulo amachikumba pansi, ndipo mkuwa amawusungunula ku miyala yamkuwa.
3 L’homme met fin aux ténèbres, il explore, jusqu’au fond des abîmes, la pierre cachée dans les ténèbres et l’ombre de la mort.
Munthu amalowa mu mdima atatenga nyale, amafunafuna miyala mpaka ku malire a mgodiwo, kufuna mkuwa mu mdima wandiweyani.
4 Il creuse, loin des lieux habités, des galeries, qu’ignore le pied des vivants; suspendu, il vacille, loin des humains.
Amakumba njira zapansi mu mgodimo, kutali ndi kumene kumakhala anthu, kumalo kumene phazi la munthu silinapondeko; iye amakhala ali lende pansipo namazungulira uku ndi uku.
5 La terre, d’où sort le pain, est bouleversée dans ses entrailles comme par le feu.
Nthaka, imene imatulutsa zakudya, kunsi kwake kumachita ngati kwasandulizika ndi moto;
6 Ses roches sont le lieu du saphir, et l’on y trouve de la poudre d’or.
miyala ya safiro imachokera mʼmatanthwe ake, ndipo mʼfumbi lake mumakhala miyala yagolide.
7 L’oiseau de proie n’en connaît pas le sentier, l’œil du vautour ne l’a pas aperçu.
Palibe mbalame yodya zinzake imene imadziwa njira yobisikayi, palibe kamtema amene anayiona.
8 Les animaux sauvages ne l’ont pas foulé, le lion n’y a jamais passé.
Zirombo zolusa sizipondamo mʼnjiramo, ndipo mkango sudzeranso mʼmenemo.
9 L’homme porte sa main sur le granit, il ébranle les montagnes dans leurs racines.
Munthu amaphwanya matanthwe olimba, ndipo amagubuduza mapiri kuyambira mʼtsinde.
10 Il perce des galeries dans les rochers; rien de précieux n’échappe à son regard.
Amabowola njira mʼmatanthwewo; ndipo amaona chuma chonse cha mʼphirimo.
11 Il sait arrêter le suintement des eaux, il amène à la lumière tout ce qui était caché.
Amaletsa mitsinje ya pansipo kuti isayendenso, motero amatulutsira poyera zinthu zobisika.
12 Mais la Sagesse, où la trouver? Où est le lieu de l’Intelligence?
“Koma nzeru zingapezeke kuti? Kodi kumvetsa zinthu kumakhala kuti?
13 L’homme n’en connaît pas le prix, on ne la rencontre pas sur la terre des vivants.
Munthu sadziwa kufunika kwake kwa nzeruzo; nzeruyo sipezeka pa dziko lino la anthu amoyo.
14 L’abîme dit: « Elle n’est pas dans mon sein; » la mer dit: « Elle n’est pas avec moi. »
Phompho likuti, ‘Sizipezeka mwa ine muno.’ Nyanja ikuti, ‘Mwa ine munonso ayi.’
15 Elle ne se donne pas contre de l’or pur, elle ne s’achète pas au poids de l’argent.
Nzeru sungazigule ndi golide wabwino kwambiri, mtengo wake sungawuyerekeze ndi siliva wambiri.
16 On ne la met pas en balance avec de l’or d’Ophir, avec l’onyx précieux et avec le saphir.
Nzeru singagulidwe ndi golide wa ku Ofiri, kapena ndi miyala ya onikisi kapena ya safiro.
17 L’or et le verre ne peuvent lui être comparés, on ne l’échange pas pour un vase d’or fin.
Nzeru sungayiyerekeze ndi golide kapena mwala wa galasi, sungayigule ndi zokometsera zagolide.
18 Qu’on ne fasse pas mention du corail et du cristal: la possession de la sagesse vaut mieux que les perles.
Miyala ya korali ndi krisitali siyoyeneranso ndi kuyitchula nʼkomwe; mtengo wa nzeru ndi woposa miyala ya rubi.
19 La topaze d’Ethiopie ne l’égale pas, et l’or pur n’atteint pas sa valeur.
Nzeru sungayiyerekeze ndi miyala ya topazi ya ku Kusi; nzeru singagulidwe ndi golide wabwino kwambiri.
20 D’où vient donc la sagesse? Où est lieu de l’Intelligence?
“Kodi tsono nzeru zimachokera kuti? Kodi kumvetsa zinthu kumakhala kuti?
21 Elle est cachée aux yeux de tous les vivants, elle se dérobe aux oiseaux du ciel.
Malo ake ndi obisika kwa zamoyo zonse, ndi obisika ngakhale kwa mbalame zamlengalenga.
22 L’enfer et la mort disent: « Nous en avons entendu parler. » (questioned)
Chiwonongeko ndi imfa zikuti, ‘Tangomva mphekesera chabe ya zimenezo!’
23 C’est Dieu qui connaît son chemin, c’est lui qui sait où elle réside.
Mulungu yekha ndiye amadziwa njira yake yopita kumeneko, ndipo Iye yekha amadziwa kumene nzeru imakhala,
24 Car il voit jusqu’aux extrémités de la terre, il aperçoit tout ce qui est sous le ciel.
pakuti Iye amayangʼana mpaka ku malekezero a dziko lapansi ndipo amaona zonse za kunsi kwa thambo.
25 Quand il réglait le poids des vents, qu’il mettait les eaux dans la balance,
Iye atapatsa mphepo mphamvu zake, nayeza kuzama kwa nyanja,
26 quand il donnait des lois à la pluie, qu’il traçait la route aux éclairs de la foudre,
atakhazikitsa lamulo loti mvula izigwa ndi kukonza njira ya chingʼaningʼani cha bingu,
27 alors il l’a vue et l’a décrite, il l’a établie et en a sondé les secrets.
pamenepo ndi pamene anayangʼana nzeruzo naziyeza mtengo wake; nazikhazikitsa ndi kuzisanthula bwino lomwe.
28 Puis il a dit à l’homme: La crainte du Seigneur, voilà la sagesse; fuir le mal, voilà l’intelligence.
Ndipo Iye anati kwa munthu, ‘Taonani, kuopa Ambuye, ndiye nzeru zimenezo ndipo kuthawa zoyipa ndiye kumvetsa zinthu kumeneko.’”

< Job 28 >