< Jérémie 9 >
1 Qui changera ma tête en eaux, et mes yeux en source de larmes, pour que je pleure nuit et jour les morts de la fille de mon peuple?
Aa, ndikanakonda kuti mutu wanga ukanakhala chitsime cha madzi, ndi maso anga ngati kasupe wa misozi! Ndikanalira usana ndi usiku kulirira anthu anga amene aphedwa.
2 Qui me donnera au désert un abri de voyageurs? J’abandonnerai mon peuple, je me retirerai d’avec eux! Car ils sont tous des adultères; une assemblée d’infidèles.
Ndani adzandipatsa malo ogona mʼchipululu kuti ndiwasiye anthu anga ndi kuwachokera kupita kutali; pakuti onse ndi achigololo, ndiponso gulu la anthu onyenga.
3 Ils bandent leur langue comme leur arc, pour décocher le mensonge; ce n’est pas par la vérité qu’ils sont puissants dans le pays, car ils vont de péché en péché; et ils ne me connaissent pas, — oracle de Yahweh.
“Amapinda lilime lawo ngati uta. Mʼdzikomo mwadzaza ndi mabodza okhaokha osati zoonadi. Amapitirirabe kuchita zoyipa; ndipo sandidziwa Ine.” Akutero Yehova.
4 Gardez vous chacun de votre ami, et ne vous fiez à aucun frère; car tout frère ne fait que supplanter, et tout ami s’en va répandant la calomnie.
“Aliyense achenjere ndi abwenzi ake; asadalire ngakhale abale ake. Aliyense amafuna kumudyera mʼbale wake masuku pa mutu. Choncho aliyense amachitira bwenzi lake ugogodi.
5 Ils se dupent dupent l’un l’autre; ils ne disent pas la vérité; ils exercent leur langue à mentir; ils s’étudient à mal faire.
Aliyense amamunamiza mʼbale wake ndipo palibe amene amayankhula choonadi. Anapazoloweza pakamwa pawo kunena zabodza; amalimbika kuchita machimo.
6 Tu habites au milieu de la mauvaise foi; c’est par mauvaise foi qu’ils refusent de me connaître, — oracle de Yahweh.
Iwe wakhalira mʼchinyengo ndipo ukukana kundidziwa Ine,” akutero Yehova.
7 C’est pourquoi ainsi parle Yahweh des armées: Je vais les fondre au creuset et les éprouver; car que faire autre chose avec la fille de mon peuple?
Nʼchifukwa chake Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Taonani, Ine ndidzawasungunula ngati chitsulo ndi kuwayesa. Kodi ndingachite nawonso bwanji chifukwa cha machimo awo?
8 C’est un dard meurtrier que leur langue; elle ne profère que mensonge; de la bouche on dit: Paix à son prochain, et dans le cœur on lui dresse des embûches.
Lilime lawo lili ngati muvi wakuthwa; limayankhula zachinyengo. Aliyense ndi pakamwa pake amayankhula mawu achikondi kwa mnansi wake, koma mu mtima mwake amakonzekera zomuchita chiwembu.
9 Et je ne les punirais pas pour tous ces crimes, — oracle de Yahweh, et d’une nation telle que celle-là je ne me vengerais pas!
Kodi ndilekerenji kuwalanga chifukwa cha zimenezi? akutero Yehova. ‘Kodi ndisawulipsire mtundu wotere wa anthu?’”
10 Sur les montagnes je ferai entendre une plainte et une lamentation, sur les pâturages du désert un chant de deuil! Car ils sont brûlés au point que personne n’y passe; on n’y entend plus la voix des troupeaux; depuis l’oiseau du ciel jusqu’au bétail, tous ont fui, ont disparu.
Ndidzakhetsa misozi ndi kulira kwamphamvu chifukwa cha mapiri ndipo ndidzadandaula chifukwa cha msipu wa ku chipululu. Malo onsewo awonongeka ndipo palibe amene amapitako, ndipo sikumveka kulira kwa ngʼombe. Mbalame zamlengalenga zathawa ndipo nyama zakuthengo zachokako.
11 Et je ferai de Jérusalem des tas de pierres, un repaire de chacals; et je ferai des villes de Juda une solitude, où personne n’habite.
Ndipo Yehova anati, “Ndidzasandutsa Yerusalemu kukhala bwinja, malo okhalamo ankhandwe; ndipo ndidzawononga mizinda ya Yuda kotero kuti palibe munthu amene adzakhalemo.”
12 Quel est l’homme sage qui comprendra ces choses; celui à qui la bouche de Yahweh a parlé, pour qu’il les annonce? Pourquoi le pays est-il détruit, brûlé comme le désert où personne ne passe?
Ine ndinati, “Kodi munthu wanzeru ndani woti nʼkumvetsa zimenezi? Kodi ndani amene Yehova anayankhula naye zimenezi kuti akafotokozere ena? Nʼchifukwa chiyani dziko lawonongeka ndi kusanduka chipululu, mʼmene anthu sadutsamo?”
13 Et Yahweh dit: C’est parce qu’ils ont abandonné ma loi, que j’avais mise devant eux, qu’ils n’ont pas écouté ma voix et ne l’ont pas suivie.
Yehova anati, “Nʼchifukwa chakuti anthuwa analeka kutsata malamulo anga amene ndinawapatsa; sanandimvere kapena kuwasamala.
14 Mais ils ont marché selon l’obstination de leur cœur, et après les Baals, que leurs pères leur ont enseignés.
Mʼmalo mwake, anatsatira zolakwa za mʼmitima yawo; anapembedza Abaala ngati momwe makolo awo anawaphunzitsira.”
15 C’est pourquoi ainsi parle Yahweh, le Dieu d’Israël: « Voici que je vais les nourrir d’absinthe, — ce peuple — et je leur donnerai à boire des eaux empoisonnées.
Tsono chimene Ine Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli ndidzachite ndi anthu amenewa ndi ichi: “Ndidzawadyetsa chakudya cha ziphe ndi kuwamwetsa madzi a ndulu.
16 Je les disperserai parmi des nations que n’ont connues ni eux, ni leurs pères, et j’enverrai contre eux le glaive, jusqu’à ce que je les aie exterminés.
Ndidzawabalalitsa pakati pa mitundu ya anthu imene iwowo kapena makolo awo sanayidziwe, ndipo ndidzawalondola ndi ankhondo mpaka nditawawononga.”
17 Ainsi parle Yahweh des armées: Pensez à commander les pleureuses, et qu’elles viennent! Envoyez vers les plus habiles, et qu’elles viennent!
Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Tsopano ganizirani! Muyitane akazi olira mwachisoni kuti abwere; itanani akazi odziwa kulira bwino.”
18 Qu’elles se hâtent, qu’elles entonnent sur nous des lamentations; que les larmes coulent de nos yeux, et que de nos paupières les pleurs ruissellent!
Anthu akuti, “Abwere mofulumira kuti adzatilire mpaka mʼmaso mwathu mutatuluka misozi ndi kuti msidze zathu zinyowe ndi madzi.
19 Car un bruit de lamentations a été entendu dans Sion: « Comment sommes-nous dévastés, couverts de honte, au point d’abandonner le pays, parce qu’on a jeté bas nos demeures? »
Kulira mwachisoni kukumveka kuchokera mu Ziyoni akuti, ‘Aa! Ife tawonongeka! Tachita manyazi kwambiri! Tiyenera kuchoka mʼdziko lathu chifukwa atipirikitsa mʼnyumba zathu.’”
20 Femmes, écoutez donc la parole de Yahweh, et que votre oreille reçoive la parole de sa bouche! Enseignez à vos filles une lamentation, et chacune à vos compagnes un chant de deuil.
Tsono inu amayi, imvani mawu a Yehova; tcherani makutu anu kuti mumve mawu a Yehova. Phunzitsani ana anu aakazi kulira mwachisoni; aliyense aphunzitse mnzake nyimbo ya maliro.
21 Car la mort est montée par nos fenêtres, et elle est entrée dans nos palais, pour faire disparaître l’enfant de la rue, et les jeunes gens des places publiques.
Imfa yatifikira kudzera mʼmazenera athu ndipo yalowa mʼnyumba zathu zotetezedwa; yapha ana athu mʼmisewu, ndi achinyamata athu mʼmabwalo.
22 Parle: Ainsi... — oracle de Yahweh: Le cadavre de l’homme tombera, comme du fumier sur un champ, et comme la javelle derrière le moissonneur, sans que personne la ramasse.
Yehova anandiwuza kuti ndinene izi kuti, “‘Mitembo ya anthu idzakhala ili lambalamba ngati ndowe mʼminda, ngati mapesi mʼmbuyo mwa wokolola, popanda munthu woyitola.’”
23 Ainsi parle Yahweh: Que le sage ne se glorifie pas de sa sagesse; que le fort ne se glorifie pas de sa force; que le riche ne se glorifie pas de sa richesse.
Yehova akuti, “Munthu wanzeru asanyadire nzeru zake, kapena munthu wamphamvu kunyadira nyonga zake, kapena munthu wolemera kunyadira chuma chake,
24 Mais que celui qui se glorifie se glorifie en ceci: d’avoir de l’intelligence et de me connaître. Car je suis Yahweh, qui exerce la miséricorde, le droit et la justice sur la terre; car c’est à cela que je prends plaisir, — oracle de Yahweh.
koma ngati munthu akufuna kunyadira, anyadire chinthu ichi: kuti iye amamvetsa za Ine ndipo amandidziwa, kuti ndine Yehova, amene ndimakonda chifundo, chilungamo ndiponso ungwiro pa dziko lapansi. Zimenezi ndizo ndimakondwera nazo,” akutero Yehova.
25 Voici que des jours viennent, — oracle de Yahweh, où je châtierai tout circoncis avec l’incirconcis:
“Nthawi ikubwera,” akutero Yehova, “pamene ndidzalanga onse amene anachita mdulidwe koma mu mtima sasamala nʼkomwe.
26 L’Égypte, Juda, Edom, les fils d’Ammon, Moab, et tous ceux qui se rasent les tempes, qui habitent le désert; car toutes les nations sont incirconcises, et toute la maison d’Israël est incirconcise de cœur.
Ndidzalanga anthu a ku Igupto, Yuda, Edomu, Amoni, Mowabu, ndiponso onse amene amakhala kutali ku chipululu. Mitundu ina yonseyi ndi yosachita mdulidwe, ngakhalenso Aisraeli nawonso sanachite mdulidwe wa mu mtima.”