< Jérémie 49 >

1 Contre les enfants d’Ammon. Ainsi parle Yahweh: Israël n’a-t-il pas de fils, n’a-t-il pas d’héritier? Pourquoi Melchom a-t-il pris possession de Gad, et son peuple s’est-il installé dans ses villes?
Yehova ananena izi: Amoni, “Kodi Israeli alibe ana aamuna? Kapena alibe mlowamʼmalo? Tsono nʼchifukwa chiyani anthu opembedza Moleki alanda dziko la Gadi? Nʼchifukwa chiyani anthu ake akukhala mʼmizinda ya Gadi?
2 C’est pourquoi voici que des jours viennent, — oracle de Yahweh, où je ferai retentir à Rabba des enfants d’Ammon le cri de guerre. Elle deviendra un monceau de ruines, et ses filles seront livrées au feu, et Israël héritera de ceux qui ont hérité de lui, — oracle de Yahweh.
Koma nthawi ikubwera,” akutero Yehova, “pamene ndidzamveketse mfuwu wankhondo ku Raba, likulu la Amoni; ndipo malo awo opembedzera milungu yawo adzatenthedwa ndi moto. Choncho Aisraeli adzalandanso dziko lawo kuchokera kwa amene anawalanda poyamba dzikolo,” akutero Yehova.
3 Lamente-toi, Hésébon, car Haï a été saccagée; poussez des cris, filles de Rabbah, ceignez-vous de sacs, lamentez-vous; errez le long des clôtures; car Melchom s’en va en exil, et avec lui, ses prêtres et ses chefs.
“Lirani, inu anthu a ku Hesiboni chifukwa wowononga uja wafika! Fuwulani, inu anthu okhala ku Raba! Valani ziguduli ndi kulira mwamphamvu; thamangani uku ndi uku mʼkati mwa malinga, chifukwa mulungu wanu Moleki adzapita ku ukapolo, pamodzi ndi ansembe ake ndiponso akuluakulu ake.
4 Pourquoi te glorifier de tes vallées? — elle est riche, ta vallée! — fille rebelle, toi qui te confies dans tes trésors, disant: « Qui oserait venir contre moi? »
Chifukwa chiyani mukunyadira chigwa chanu, inu anthu osakhulupirika amene munadalira chuma chanu nʼkumati: ‘Ndani angandithire nkhondo?’
5 Voici que j’amène contre toi la terreur, — oracle du Seigneur Yahweh des armées, de tous les alentours; vous serez chassés, chacun droit devant soi, et personne ne ralliera les fuyards.
Ndidzabweretsa zoopsa pa iwe zochokera kwa onse amene akuzungulira,” akutero Ambuye, Mulungu Wamphamvuzonse. “Mudzathawa, ndipo aliyense adzathawitsa moyo wake. Sipadzapezeka munthu wosonkhanitsanso othawawo.
6 Mais après cela, je ramènerai les captifs des enfants d’Ammon, — oracle de Yahweh.
“Komabe pambuyo pake, ndidzabwezera kwawo Aamoni,” akutero Yehova.
7 Contre Edom. Ainsi parle Yahweh, des armées: N’y a-t-il plus de sagesse en Théman? Les avisés sont-ils à bout de conseils? Leur sagesse s’est-elle évanouie?
Yehova Wamphamvuzonse ananena izi za Edomu: “Kodi nzeru sizikupezekanso ku Temani? Kodi anzeru analeka kupereka uphungu? Kodi nzeru zawo zinatheratu?
8 Fuyez, retournez sur vos pas, blottissez-vous, habitants de Dédan car j’amènerai sur Esaü la ruine, au temps où je le visite.
Inu anthu a ku Dedani, thawani, bwererani ndi kukabisala ku makwalala chifukwa ndidzagwetsa mavuto pa zidzukulu za Esau popeza nthawi yawo ya chiweruzo yafika.
9 Si des vendangeurs viennent chez toi, ils ne laissent rien à grappiller; si ce sont des voleurs de nuit, ils pillent tout leur soûl.
Kodi anthu othyola mphesa akanafika kwa inu akanakusiyiraniko mphesa pangʼono pokha? Anthu akuba akanafika usiku akanangotengako zimene akuzifuna zokha?
10 Car c’est moi qui ai mis à nu Esaü et découvert ses retraites, et il ne peut plus se cacher; sa race est ravagé, ses frères, ses voisins, — et il n’est plus.
Koma ine ndazivula zidzukulu za Esau. Ndaonetsa poyera malo awo obisalamo, kotero kuti sadzathanso kubisala. Ana ake, abale ake pamodzi ndi anansi ake awonongeka. Palibe wonena kuti,
11 Abandonne tes orphelins, c’est moi qui les ferai vivre, et que tes veuves se confient en moi!
‘Siyani ana anu amasiye; Ine ndidzawateteza. Amayi anu amasiye akhoza kudalira Ine.’”
12 Car ainsi parle Yahweh: Voici que ceux qui ne devaient pas boire cette coupe la boiront sûrement; et toi, tu en serais tenu quitte? Non, tu n’en seras pas tenu quitte, tu la boiras sûrement!
Yehova akuti, “Ngati iwo amene sanali oyenera kulangidwa adzamwa chikho cha chiweruzo, ndiye muyesa kuti inuyo simudzalangidwa? Ayi ndithu simudzakhala osalangidwa. Mudzamwa ndithu chikhocho.
13 Car je l’ai juré par moi-même, — oracle de Yahweh: Bosra sera un sujet d’étonnement et d’opprobre, un lieu désert et maudit, et toutes ses villes seront des ruines à jamais.
Ine ndikulumbira, akutero Yehova, kuti mzinda wa Bozira udzasanduka bwinja, chinthu chochititsa mantha, chomachiseka ndiponso chotembereredwa. Mizinda yake yonse idzakhala mabwinja mpaka muyaya.”
14 J’en ai appris de Yahweh la nouvelle, et un messager a été envoyé parmi les nations: « Rassemblez-vous et marchez contre lui! Levez-vous pour le combat! »
Ndamva uthenga wochokera kwa Yehova: Nthumwi yatumidwa kupita kwa anthu a mitundu ina kukanena kuti, “Sonkhanani pamodzi kuti muthire nkhondo Edomu! Konzekerani nkhondo!”
15 Car voici que je t’ai rendu petit parmi les nations, méprisé parmi les hommes.
“Ndidzakuchepetsani pakati pa anthu a mitundu ina. Mudzakhala anthu onyozeka pakati pa anthu.
16 La terreur que tu inspirais t’a égaré, ainsi que la fierté de ton cœur, toi qui habites le creux des rochers, qui occupes le sommet de la colline. Mais quand tu élèverais ton aire comme l’aigle, de là je te ferai descendre, — oracle de Yahweh.
Kuopseza kwako kwakunyenga; kudzikuza kwa mtima wako kwakusocheretsa, iwe amene umakhala mʼmapanga a mʼmatanthwe ndi mʼmapiri. Ngakhale utamanga chisa chako pamwamba kwambiri ngati chiwombankhanga, ndidzakutsitsa pansi kuchokera kumeneko,” akutero Yehova.
17 Edom sera un sujet d’étonnement; tous les passants s’étonneront, et siffleront à la vue de toutes ses plaies.
“Dziko la Edomu lidzasanduka chinthu chochititsa mantha. Onse odutsamo adzadabwa ndi kupukusa mitu yawo chifukwa cha kuwonongeka kwake.
18 Ce sera comme la catastrophe de Sodome, de Gomorrhe et des villes voisines, dit Yahweh; personne n’y habitera, aucun fils de l’homme n’y séjournera.
Monga momwe anawonongekera Sodomu ndi Gomora, pamodzi ndi mizinda yake yozungulira,” akutero Yehova, “motero palibe munthu amene adzakhala mu Edomu.
19 Pareil à un lion, voici qu’il monte des halliers du Jourdain au pâturage perpétuel; soudain j’en ferai fuir Edom, et j’y établirai celui que j’ai choisi. Car qui est semblable à moi? Qui me provoquerait, et quel est le berger qui me tiendrait tête?
“Monga mkango wotuluka ku nkhalango za ku Yorodani kupita ku malo a msipu wobiriwira, Ine ndidzapirikitsa anthu a ku Edomu mwadzidzidzi kuchoka mʼdziko lawo. Pambuyo pake ndidzawayikira owalamulira amene ndamufuna Ine. Kodi ndani wofanana nane, ndipo angatsutsane nane ndani? Ndipo ndi mʼbusa uti amene angalimbane nane?”
20 Ecoutez donc la résolution qu’a prise Yahweh contre Edom, et les desseins qu’il a médités contre les habitants de Théman: Oui, on les entraînera comme de faibles brebis; oui, leur pâturage en sera dans la stupeur.
Nʼchifukwa chake imvani. Izi ndi zimene Ine Yehova ndakonza zolangira anthu a ku Edomu ndi a ku Temani. Ngakhale ana omwe adzatengedwa ukapolo ndipo aliyense adzachita mantha chifukwa cha iwo.
21 Au bruit de leur chute, la terre tremble; le bruit de leur voix se fait entendre jusqu’à la mer Rouge.
Akadzagwa Edomu padzakhala mfuwu waukulu ndipo dziko lapansi lidzanjenjemera; kulira kwawo kudzamveka mpaka ku Nyanja Yofiira.
22 Voici qu’il monte et prend son vol comme l’aigle, il étend ses ailes sur Bosra; et le cœur des guerriers d’Edom est en ce jour comme le cœur d’une femme en travail.
Taonani, mtundu wina udzachita kuwuluka nʼkudzatera pa Bozira ngati chiwombankhanga chimene chatambalitsa mapiko ake. Pa tsiku limenelo mitima ya ankhondo a ku Edomu idzagunda ngati mtima wa mayi pa nthawi yake yochira.
23 Contre Damas. Hamath et Arphad sont dans la confusion, parce qu’elles ont reçu une mauvaise nouvelle; elles se fondent de peur; c’est la mer en tourmente, qui ne peut s’apaiser.
Mawu a Yehova onena za Damasiko ndi awa: “Anthu a ku Hamati ndi a ku Aripadi akuchita mantha chifukwa amva nkhani yoyipa. Mitima yawo yagwidwa ndi mantha ndipo ali ngati muja ichitira nyanja yosakhazikika.
24 Damas est sans force, elle se tourne pour fuir, et l’effroi s’empare d’elle; l’angoisse et les douleurs la saisissent, comme une femme qui enfante.
Anthu a ku Damasiko alefuka. Abwerera mʼmbuyo kufuna kuthawa chifukwa agwidwa ndi mantha aakulu. Ali ndi nkhawa komanso mantha ngati za mayi pa nthawi yake yochira.
25 A quel pas n’est-elle pas abandonnée, la ville glorieuse, la cité de délices, de joie!
Mzinda wotchuka ndi wachikondwerero uja wasiyidwa!
26 Aussi ses jeunes gens tomberont sur ses places, ainsi que tous ses hommes de guerre; ils périront en ce jour-là, — oracle de Yahweh des armées.
Nʼchifukwa chake anyamata ake adzagwa mʼmisewu ndi kufa; ankhondo ake onse adzawonongedwa tsiku limenelo,” akutero Yehova Wamphamvuzonse.
27 J’allumerai un feu dans les murs de Damas, et il dévorera les palais de Ben-Hadad.
“Ndidzatentha malinga a Damasiko; moto udzanyeketsa nyumba zaufumu za Beni-Hadadi.”
28 Contre Cédar et les royaumes de Hasor, que frappa Nabuchodonosor, roi de Babylone. Ainsi parle Yahweh: Debout! Marchez contre Cédar, exterminez les fils de l’Orient!
Mawu a Yehova onena za Kedara ndi maufumu a ku Hazori, amene Nebukadinezara mfumu ya Babuloni anawagonjetsa ndi awa: “Nyamukani mukathire nkhondo ku Kedara. Kawonongeni anthu a kummawako.
29 Qu’on prenne leurs tentes et leurs troupeaux! Qu’on leur enlève leurs tentures, tous leurs bagages et leurs chameaux! Et qu’on leur crie: Terreur de toutes parts!
Landani matenti awo ndi nkhosa zawo, ndiye kuti, mutenge nsalu zawo ndi katundu wawo. Mutengenso ngamira zawo. Anthu adzafuwula kwa iwo kuti, ‘Kuli zoopsa mbali zonse!’
30 Sauvez-vous, fuyez de toutes vos forces, blottissez-vous, habitants de Hasor! — oracle de Yahweh. Car Nabuchodonosor, roi de Babylone, a formé contre vous un dessein, il a conçu un projet contre vous.
“Thawani mofulumira! Kabisaleni mʼmakhwawa, inu anthu ku Hazori,” akutero Yehova. “Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni wakukonzerani chiwembu; wakonzekera zoti alimbane nanu.
31 Debout! Marchez contre un peuple tranquille, en assurance dans sa demeure, — oracle de Yahweh, qui n’a ni portes ni barres, qui vit à l’écart.
“Nyamukani kathireni nkhondo mtundu wa anthu umene uli pamtendere, umene ukukhala mosatekeseka,” akutero Yehova, “mzindawo ulibe zipata ngakhalenso mipiringidzo; anthu ake amakhala pa okha.
32 Leurs chameaux seront votre butin, et la multitude de leurs troupeaux vos dépouilles. Je les disperserai à tous les vents, ces hommes aux tempes rasées, et de tous côtés je ferai venir sur leur ruine, — oracle de Yahweh.
Ngamira zawo zidzafunkhidwa, ndipo makola a ngʼombe zawo adzalandidwa. Ndidzabalalitsira ku mphepo zinayi onse amene amameta tsitsi lawo chamʼmbali. Ndidzawagwetsera mavuto kuchokera ku mbali zonse,” akutero Yehova.
33 Et Hasor deviendra un repaire de chacals, une solitude pour toujours; personne n’y demeurera, aucun fils d’homme n’y séjournera.
“Hazori adzasanduka bwinja, malo okhalamo nkhandwe mpaka muyaya. Palibe munthu amene adzayendemo.”
34 La parole de Yahweh qui fut adressée à Jérémie, le prophète, pour Élam, au commencement du règne de Sédécias, roi de Juda, en ces termes:
Uthenga umene Yehova anapatsa mneneri Yeremiya wonena za Elamu, Zedekiya mfumu ya Yuda atangoyamba kulamulira ndi uwu:
35 Ainsi parle Yahweh des armées: Voici que je vais briser l’arc d’Élam, principe de sa force.
Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Taonani, ndidzathyola uta wa Elamu, umene uli chida chawo champhamvu.
36 Je ferai venir sur Élam quatre vents, des quatre coins du ciel, et je le disperserai à tous ces vents; et il n’y aura pas une nation où n’arrivent pas des fugitifs d’Élam.
Ndidzabweretsa mphepo zinayi pa Elamu kuchokera ku zigawo zinayi zamlengalenga; ndidzawabalalitsira ku mphepo zinayi, ndipo sipadzakhala dziko limene anthu a ku Elamu sadzafikako.
37 Je ferai trembler Élam devant ses ennemis, et devant ceux qui en veulent à sa vie. Et j’amènerai sur eux des malheurs, le feu de mon ardente colère, — oracle de Yahweh. Et j’enverrai après eux l’épée, jusqu’à ce que je les aie anéantis.
A ku Elamuwo ndidzachititsa mantha pamaso pa adani awo komanso pamaso pa iwo amene akufuna kuwononga moyo wawo. Ndidzawagwetsera mkwiyo wanga ndipo adzakhala pa mavuto,” akutero Yehova. “Ndidzawapirikitsa ndi lupanga mpaka nditawatheratu.
38 Je placerai mon trône en Élam, et j’en exterminerai roi et chefs, — oracle de Yahweh.
Ndidzakhazika mpando wanga waufumu ku Elamu ndipo ndidzawononga mfumu yake pamodzi ndi akuluakulu ake,” akutero Yehova.
39 Mais à la fin des jours, je ramènerai les captifs d’Élam, — oracle de Yahweh.
“Komabe mʼtsogolomo ndidzabwezera anthu a ku Elamu dziko lawo,” akutero Yehova.

< Jérémie 49 >