< Jérémie 48 >
1 A Moab. Ainsi parle Yahweh des armées, Dieu d’Israël: Malheur à Nabo, car elle est ravagée; Cariathaïm est couverte de honte, elle est prise; la forteresse est couverte de honte, elle est abattue;
Ponena za Mowabu: Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti, “Tsoka kwa mzinda wa Nebo, chifukwa wawonongedwa. Mzinda wa Kiriyataimu wachititsidwa manyazi ndipo wagonjetsedwa; linga lichititsidwa manyazi ndipo lagumulidwa.
2 elle n’est plus, la gloire de Moab! A Hésebon on médite contre lui le mal: Allons et exterminons-le d’entre les nations! Toi aussi, Madmen, tu seras réduite au silence, l’épée marche derrière toi.
Palibenso amene akutamanda Mowabu; ku Hesiboni anthu anamupanganira zoyipa: ‘Bwerani, tiyeni timuwonongeretu kuti asakhalenso mtundu wa anthu.’ Inunso anthu a ku Madimena, adzakukhalitsani chete; ankhondo adzakupirikitsani.
3 Des cris partent de Horonaïm; dévastation et grande ruine!
Tamvani mfuwu wa anthu a ku Horonaimu. Iwo akulira kuti, ‘Kusakazika ndi kuwonongeka kwakukulu.’
4 Moab est brisé; ses petits enfants font entendre des cris.
Mowabu wawonongeka; ana ake angʼonoangʼono akulira kwambiri.
5 Oui! à la montée de Luith il y a des pleurs, on la gravit en pleurant; oui! à la descente de Horonaïm, on entend les cris de détresse.
Anthu akukwera chikweza cha ku Luhiti, akulira kwambiri pamene akupita. Kulira chifukwa cha chiwonongeko kukumveka pa njira yotsikira ku Horonaimu.
6 Fuyez, sauvez vos vies! Qu’elles soient comme une bruyère dans la lande!
Thawani! Dzipulumutseni; khalani ngati mbidzi ya mʼchipululu.
7 Car, puisque tu as mis ta confiance en tes ouvrages et en tes trésors, toi aussi tu seras conquis; et Chamos ira en exil, avec ses prêtres et ses princes, tous ensemble.
Popeza inu munkadalira ntchito zanu ndi chuma chanu, nanunso mudzatengedwa ukapolo, ndipo Kemosi adzapita ku ukapolo, pamodzi ndi ansembe ake ndi akuluakulu ake.
8 Le dévastateur viendra contre toutes les villes, et pas une ville n’échappera; la vallées sera ruinée, et le plateau saccagé, comme l’a dit Yahweh.
Wowononga adzabwera ndi kusakaza mzinda uliwonse, ndipo palibe mzinda umene udzapulumuke. Chigwa chidzasanduka bwinja ndipo malo athyathyathya a pamwamba pa phiri adzawonongedwa monga Yehova wayankhulira.
9 Donnez des ailes à Moab, car il faut qu’il s’envole; ses villes seront dévastées, sans qu’il y ait d’habitant.
Mtsineni khutu Mowabu chifukwa adzasakazika; mizinda yake idzasanduka mabwinja, wopanda munthu wokhalamo.
10 Maudit soit celui qui fait mollement l’œuvre du Seigneur! Maudit celui qui refuse le sang à son épée!
“Wotembereredwa munthu amene amagwira ntchito ya Yehova monyinyirika! Wotembereredwa munthu amene amaletsa lupanga lake kupha anthu!
11 Moab a été tranquille depuis sa jeunesse; il a reposé sur sa lie; il n’a pas été vidé d’un vase dans un autre, et il n’est pas allé en captivité. Aussi son goût lui est-il resté, et son parfum ne s’est pas altéré.
“Mowabu wakhala pa mtendere kuyambira ubwana wake, ngati vinyo wokhazikika pa masese ake, osapungulidwa kuchoka mu mtsuko wina kuthira mu mtsuko wina; iye sanatengedwepo ukapolo. Nʼchifukwa chake kukoma kwake nʼkomwe kuja ndipo fungo lake silinasinthe.
12 C’est pourquoi voici que des jours viennent, — oracle Yahweh, où je lui enverrai des transvaseurs qui le transvaseront; ils videront ses vases, et ils briseront ses cruches.
Nʼchifukwa chake masiku akubwera,” akutero Yehova, “pamene ndidzatuma anthu amene amakhuthula vinyo mʼmitsuko ndipo adzamukhutula; adzakhuthula vinyo yense mitsuko yake pambuyo pake nʼkuphwanya mitsukoyo.
13 Et Moab aura honte de Chamos, comme la maison d’Israël a eu honte de Béthel, en qui était sa confiance.
Pamenepo Mowabu adzachita manyazi ndi Kemosi, monga momwe Aisraeli anachitira manyazi ndi Beteli amene ankamukhutulira.
14 Comment pouvez-vous dire: « Nous sommes des guerriers, des hommes vaillants au combat? »
“Kodi munganene bwanji kuti, ‘Ife ndife asilikali. Ife ndife ngwazi, anthu amphamvu pa nkhondo?’
15 Moab est ravagé, ses villes montent en fumée, l’élite de ses jeunes gens descend pour la boucherie; — oracle du roi, dont le nom est Yahweh des armées.
Owononga Mowabu ndi mizinda yake abwera ndipo ankhondo adzalowa mʼmidzi yake; anyamata ake okongola apita kukaphedwa,” ikutero Mfumu, imene dzina lake ndi Yehova Wamphamvuzonse.
16 La ruine de Moab approche, son malheur vient en grande hâte.
Kugwa kwa Mowabu kuli pafupi; masautso ake akubwera posachedwa.
17 Consolez-le, vous tous, ses voisins, et vous tous qui connaissez son nom, dites: « Comment a été brisé un bâton si fort, un sceptre si magnifique? »
Mulireni kwambiri, inu nonse amene mwamuzungulira, inu nonse amene mumadziwa za kutchuka kwake; nenani kuti, “Taonani momwe yathyokera ndodo yamphamvu yaufumu ija, taonani momwe ndodo yaulemu yathyokera!”
18 Descends de ta gloire et assieds-toi sur la terre aride, habitante, fille de Dibon; car le dévastateur de Moab est monté contre toi, il a renversé tes remparts.
“Tsikani pa ulemerero wanu ndipo khalani pansi powuma, inu anthu okhala ku Diboni, pakuti wowononga Mowabu wabwera kudzamenyana nanu, wasakaza mizinda yanu yotetezedwa.
19 Tiens-toi sur le chemin, et observe, habitante d’Aroër; interroge celui qui fuit et celle qui s’échappe; dis: « Qu’est-il arrivé? —
Inu amene mumakhala ku Aroeri, imani mʼmbali mwa msewu ndi kumaonerera. Funsani mwamuna amene akuthawa ndiponso mkazi amene wapulumuka, afunseni kuti, ‘Kodi chachitika nʼchiyani?’”
20 « Moab est confus, car il est renversé. Poussez des gémissements et des cris! Annoncez sur l’Arnon que Moab est ravagé! »
Iwo adzayankha kuti, “Mowabu wachititsidwa manyazi, pakuti wasakazika. Lirani mwachisoni ndipo fuwulani! Lengezani ku mtsinje wa Arinoni kuti Mowabu wawonongedwa.
21 Un jugement est venu sur le pays de la plaine, sur Hélon, sur Jasa, sur Méphaath,
Chiweruzo chabwera ku mizinda ya ku mapiri, ndiyo Holoni, Yaza, Mefaati,
22 sur Dibon, sur Nabo, sur Beth-Deblathaïm,
Diboni, Nebo, Beti-Dibilataimu,
23 sur Cariathaïm, sur Beth-Gamul, sur Beth-Maon,
Kiriyataimu, Beti-Gamuli, Beti-Meoni,
24 sur Carioth, sur Bosra et sur toutes les villes du pays de Moab, éloignées et proches.
Keriyoti ndi Bozira ndi mizinda yonse ya Mowabu, yakutali ndi yapafupi yomwe.
25 La corne de Moab est abattue, et son bras est brisé, — oracle de Yahweh.
Mphamvu za Mowabu zawonongeka; mkono wake wathyoka,” akutero Yehova.
26 Enivrez-le; car il s’est élevé contre Yahweh! que Moab se vautre dans son vomissement, et qu’il devienne un objet de risée, lui aussi!
“Muledzeretseni Mowabu, chifukwa anadzikuza powukira Yehova. Mulekeni Mowabu avivinizike mʼmasanzi ake; mulekeni akhale chinthu chomachiseka.
27 Israël n’a-t-il pas été pour toi un objet de risée? L’a-t-on surpris avec des voleurs, pour que, chaque fois que tu parlés de lui, tu hoches la tête?
Kodi suja Israeli anali kwa iwe ngati chinthu chomachiseka? Kodi Israeli anapezeka pakati pa akuba kuti nthawi zonse poyankhula za iye, iwe uzimupukusira mutu momunyoza?
28 Abandonnez les villes; demeurez dans les rochers, habitants de Moab, et soyez comme la colombe qui fait son nid au-dessus du précipice béant.
Inu amene mumakhala ku Mowabu, siyani mizinda yanu ndi kukakhala pakati pa matanthwe. Khalani ngati nkhunda imene imamanga chisa chake pa khomo la phanga.
29 Nous avons entendu l’orgueil de Moab, le très orgueilleux, sa hauteur, son orgueil, sa fierté, et la fierté de son cœur.
“Tamva za kunyada kwa Mowabu, kunyada kwake nʼkwakukulu. Ndi wodzitama, wonyada ndi wodzitukumula. Ali ndi mtima wodzikweza.
30 Moi aussi je connais, — oracle de Yahweh, sa jactance, et ses vains discours, et ses œuvres vaines.
Ine ndikuzidziwa ntchito zake, akutero Yehova. Ntchitozo ndi nʼzosapindulitsa kanthu.
31 C’est pourquoi je me lamente sur Moab; sur tout Moab je pousse des cris; on gémit sur les gens de Qir-Hérès.
Nʼchifukwa chake ndidzamulira Mowabu, ine ndikulira chifukwa cha anthu onse a ku Mowabu, ndikubuwula chifukwa cha anthu a ku Kiri Heresi.
32 Plus encore que sur Jazer, je pleure sur toi, vigne de Sabama. Tes sarments dépassaient la mer, ils touchaient à la mer de Jazer. Sur ta récolte et sur ta vendange le dévastateur s’est jeté.
Ndikukhetsa misozi chifukwa cha inu, kupambana momwe ndinalirira Yazeri. Inu anthu a ku Sibina muli ngati mipesa imene nthambi zake zatambalala mpaka ku Nyanja; zafika mpaka ku nyanja ya Yazeri. Wowononga wasakaza zipatso zake zachilimwe ndi mpesa.
33 La joie et l’allégresse ont disparu des vergers et de la terre de Moab; j’ai fait tarir le vin des cuves; on ne le foule plus au bruit des hourrahs; le hourrah n’est plus le hourrah.
Chimwemwe ndi chisangalalo zatha ku minda ya zipatso ya ku Mowabu. Ndaletsa kuchucha kwa vinyo mopsinyira mphesa; palibe amene akufuwula mokondwa akamapsinya mphesa. Ngakhale kufuwula kulipo, koma sikufuwula kwa chimwemwe.
34 A cause du cri de Hésébon jusqu’à Eléalé; jusqu’à Jasa, ils font entendre leur cri; de Segor jusqu’à Horonaïm, jusqu’à Eglath-Sélisia; Car même les eaux de Nemrim seront taries.
“A ku Hesiboni ndi Eleali akulira ndipo mfuwu wawo ukumveka mpaka ku Yahazi, kuchokera ku Zowari mpaka ku Horonaimu ndi ku Egilati Selisiya. Ngakhale madzi a ku Nimurimu aphwa.
35 Je veux, en finir avec Moab, — oracle de Yahweh, avec celui qui monte à son haut-lieu et offre de l’encens à son dieu.
Ndidzawaletsa anthu a ku Mowabu kupereka nsembe mʼmalo awo opembedzera ndi kufukiza lubani kwa milungu yawo,” akutero Yehova.
36 C’est pourquoi mon cœur au sujet de Moab, gémit comme une flûte, oui, mon cœur au sujet des gens de Qir-Hérès, gémit comme une flûte. C’est pourquoi le gain qu’ils avaient fait est perdu.
“Nʼchifukwa chake mtima wanga ukulirira Mowabu ngati chitoliro. Mtima wanga ukulirira anthu a ku Kiri Heresi ngati chitoliro chifukwa chuma chimene anachipata chatha.
37 Car toute tête est rasée, et toute barbe coupée; sur toutes les mains il y a des incisions; et sur les reins des sacs.
Aliyense wameta mutu wake ndi ndevu zake; manja a munthu aliyense ndi ochekacheka, ndipo munthu aliyense wavala chiguduli mʼchiwuno mwake.
38 Sur tous les toits de Moab et sur ses places, ce ne sont que lamentations; car j’ai brisé Moab comme un vase dont on ne veut plus, — oracle de Yahweh.
Pa madenga onse a ku Mowabu ndiponso mʼmisewu yake anthu akungolira, pakuti ndaphwanya Mowabu ngati mtsuko wopanda ntchito,” akutero Yehova.
39 Comme il est brisé! Gémissez! Comme Moab a honteusement tourné le dos! Moab est devenu un objet de risée, et d’épouvante pour tous ses voisins.
“Taonani mmene waphwanyikira! Tamvani momwe akulirira! Taonani momwe Mowabu wachititsidwira manyazi. Mowabu wasanduka chinthu chonyozeka, chinthu chochititsa mantha kwa onse amene amuzungulira.”
40 Car ainsi parle Yahweh: Voici qu’il prend son vol comme l’aigle, il étend ses ailes sur Moab.
Yehova akuti, “Mtundu wina udzachita kuwuluka nʼkugwera pa Mowabu ngati chiwombankhanga chimene chatambalitsa mapiko ake.
41 Carioth est prise, les forteresses sont emportées, et le cœur des guerriers de Moab est, en ce jour, comme le cœur d’une femme en travail.
Mizinda idzagwidwa ndipo malinga adzalandidwa. Pa tsiku limenelo mitima ya ankhondo a ku Mowabu idzakhala ngati mtima wa mayi pa nthawi yake yochira.
42 Moab est exterminé du rang des peuples, parce qu’il s’est élevé contre Yahweh.
Mowabu sudzakhala mtundu wa anthu chifukwa unadzikuza powukira Yehova.
43 Epouvante, fosse et filet, sont sur toi, habitant de Moab! — oracle de Yahweh.
Zoopsa, dzenje ndi msampha zikudikira inu anthu a ku Mowabu,” akutero Yehova.
44 Celui qui fuit devant l’objet d’épouvante tombera dans la fosse, et celui qui remontera de la fosse sera pris au filet; car je vais faire venir sur lui, sur Moab, l’année de sa visitation, — oracle de Yahweh.
“Aliyense wothawa zoopsa adzagwera mʼdzenje, aliyense wotuluka mʼdzenje adzakodwa mu msampha. Ndigwetsa zimenezi pa Mowabu pa nthawi ya chilango chake,” akutero Yehova.
45 A l’ombre de Hésébon ils s’arrêtent, les fuyards à bout de forces; mais il est sorti un feu de Hésébon, et une flamme du milieu de Séhon; elle a dévoré les flancs de Moab et le crâne des fils du tumulte.
“Anthu othawa nkhondo ayima pa mthunzi wa Hesiboni chifukwa chotopa. Koma moto wayaka kuchokera ku Hesiboni, malawi a moto abuka kuchokera ku nyumba ya mfumu Sihoni. Motowo ukuwononga mapiri a ku Mowabu, dziko la anthu onyada.
46 Malheur à toi, Moab! Il est perdu, le peuple de Chamos; car tes fils sont emmenés en exil, et tes filles en captivité.
Tsoka kwa iwe Mowabu! Anthu opembedza Kemosi awonongeka. Ana ako aamuna ndi aakazi atengedwa ukapolo.
47 Mais je ramènerai les captifs de Moab; à la fin des jours, — oracle de Yahweh. Jusqu’ici le jugement de Moab.
“Komabe masiku akutsogolo ndidzabwezeranso Mowabu chuma chake,” akutero Yehova. Chiweruzo cha Mowabu chathera pamenepa.