< Jérémie 11 >

1 La parole qui fut adressée à Jérémie de la part de Yahweh, en ces termes:
Yehova anayankhula ndi Yeremiya kuti,
2 Entendez les paroles de cette alliance, et parlez aux hommes de Juda et aux habitants de Jérusalem.
“Imvani mawu a pangano ili, ndipo uwawuze anthu a ku Yuda ndi a ku Yerusalemu.
3 Et tu leur diras: Ainsi parle Yahweh, Dieu d’Israël: Maudit soit l’homme qui n’écoute pas les paroles de cette alliance,
Awuze kuti Yehova, Mulungu wa Israeli akuti ‘adzakhala wotembereredwa munthu amene samvera mawu a pangano ili.
4 que j’ai prescrites à vos pères, au jour où je les ai fait sortir de la terre d’Égypte, de la fournaise à fer, en leur disant: Ecoutez ma voix et faites ces choses, selon tout ce que je vous commanderai, et vous serez mon peuple et moi je serai votre Dieu,
Awa anali mawu amene ndinalamulira makolo anu nditawatulutsa mu Igupto, kuchoka mʼngʼanjo yamoto.’ Ine ndinati, ‘Mverani Ine ndi kuchita chilichonse chimene ndakulamulirani. Mukatero mudzakhala anthu anga ndi Ine ndidzakhala Mulungu wanu.
5 afin que j’accomplisse le serment que j’ai fait à vos pères de leur donner un pays où coulent le lait et le miel, comme cela se voit aujourd’hui. Et je répondis: « Oui! Yahweh! »
Tsono Ine ndidzakwaniritsa lumbiro lomwe ndinalumbira kwa makolo anu kuti ndidzawapatsa dziko loyenda mkaka ndi uchi,’ dziko lomwe inu lero mukukhalamo.” Tsono Ine ndinayankha kuti, “Ameni, Yehova.”
6 Et Yahweh me dit: Crie toutes ces paroles dans les villes de Juda et dans les rues de Jérusalem, en disant: Ecoutez les paroles de cette alliance et mettez-les en pratique.
Yehova anandiwuza kuti, “Lengeza mawu onsewa mʼmizinda yonse ya ku Yuda ndi mʼmisewu ya mu Yerusalemu: ‘Mverani mawu a pangano ili ndi kuzitsatira.
7 Car j’ai instamment averti vos pères depuis le jour où je les ai fait monter du pays d’Égypte jusqu’à ce jour; je les ai sans cesse avertis, en disant: Ecoutez ma voix.
Kuyambira nthawi imene ndinatulutsa makolo anu ku Igupto mpaka lero, ndakhala ndi kuwachenjeza kawirikawiri kuti, ‘Mverani Ine.’
8 Et ils n’ont ni écouté ni prêté l’oreille; chacun d’eux a marché selon l’opiniâtreté de son mauvais cœur. Et j’ai exécuté sur eux toutes les paroles de cette alliance, que je leur avait prescrit d’observer, et qu’ils n’ont pas observée.
Koma sanamvere kapena kulabadirako. Aliyense anawumirira kuchita zoyipa za mʼmitima yawo. Ngakhale ndinawalamulira kuti asunge pangano langa koma iwo sanasunge. Choncho ndinawalanga monga ndinaneneramo.’”
9 Yahweh me dit: Il s’est trouvé une conjuration chez les hommes de Juda, et chez les habitants de Jérusalem.
Kenaka Yehova anandiwuza kuti, “Anthu a ku Yuda ndi ku Yerusalemu andiwukira.
10 Ils sont retournés aux iniquités de leurs premiers pères qui ont refusé d’écouter mes paroles, et ils sont allés après d’autres dieux pour les servir. La maison d’Israël et la maison de Juda ont violé mon alliance que j’avais conclue avec leurs pères.
Abwereranso ku machimo a makolo awo, amene anakana kumvera mawu anga. Akutsata milungu ina ndi kumayitumikira. Aisraeli ndi Ayuda aphwanya pangano limene ndinachita ndi makolo awo.
11 C’est pourquoi ainsi parle Yahweh: Voici que je vais amener sur eux des malheurs, dont ils ne pourront sortir; et, s’ils crient vers moi, je ne les écouterai pas.
Choncho Yehova akuti, ‘Ndidzawagwetsera mavuto amene sadzatha kuwalewa. Ngakhale adzandilirire, sindidzawamvera.
12 Et les villes de Juda et les habitants de Jérusalem iront invoquer les dieux auxquels ils offrent de l’encens; mais ces dieux ne les sauveront sûrement pas, au temps de leur malheur.
Anthu a mʼmizinda ya Yuda ndi anthu a ku Yerusalemu adzapita ndi kukalirira milungu imene ankayifukizira lubani, koma milunguyo sidzawathandiza ndi pangʼono pomwe mavuto akadzafika.
13 Car aussi nombreux que tes villes, sont tes dieux, ô Juda, et aussi nombreux que les rues de Jérusalem, sont les autels que vous avez dressés à une infâme idole, les autels que vous avez dressés pour encenser Baal.
Iwe Yuda, uli ndi milungu yochuluka ngati chiwerengero cha mizinda yako; chiwerengero cha maguwa ansembe amene umafukizirapo lubani kwa Baala chili ngati misewu ya mu Yerusalemu.’
14 Et toi, n’intercède pas pour ce peuple, et n’élève pas en leur faveur de supplication ni de prière; car je n’écouterai pas lorsqu’ils m’invoqueront, au temps de leur malheur.
“Tsono iwe Yeremiya usawapempherere anthu amenewa ngakhale kuwadandaulira kapena kuwapepesera, chifukwa sindidzawamvera akadzandiyitana pa nthawi ya mavuto awo.
15 Qu’est-ce que ma bien-aimée a à faire dans ma maison? Des fourberies? Est-ce que les vœux et la chair sacrée enlèveront de dessus toi tes malheurs, que tu puisses te livrer à l’allégresse?
“Kodi anthu anga okondedwa akudzachita chiyani mʼNyumba yanga? Kodi suja iwowa amachita zoyipa zambiri? Kodi mungathe kupulumuka, tsoka osakugwerani chifukwa cha nsembe zanuzo?”
16 Olivier verdoyant, orné de beaux fruits: c’est le nom que t’avait donné Yahweh. Au bruit d’un grand fracas, il y met le feu, et ses rameaux sont brisés.
Kale Yehova ankakutchani mtengo wa olivi wa masamba obiriwira, wokhala ndi zipatso zokongola. Koma tsopano adzawutentha ndi mkuntho wamkokomo ndipo nthambi zake zidzapserera.
17 Yahweh des armées, qui t’avait planté, a décrété le malheur contre toi, à cause du crime de la maison d’Israël et de la maison de Juda, qu’ils ont commis pour m’irriter, en encensant Baal.
Yehova Wamphamvuzonse, amene anakudzalani, walamula kuti mavuto akugwereni. Inu a banja la Yuda ndi a banja la Israeli munachitira Yehova zoyipa ndi kumukwiyitsa pamene munkapereka nsembe zanu kwa Baala.
18 Yahweh m’en a informé, et je l’ai su; ... alors vous m’avez fait connaître leurs œuvres!
Yehova anandiwululira ndipo ndinadziwa. Iye anatsekula maso anga kuti ndione chiwembu chawocho.
19 Moi, j’étais comme un agneau familier, qu’on mène à la boucherie, et je ne savais qu’ils formaient des desseins contre moi: « Détruisons l’arbre avec son fruit! Retranchons-le de la terre des vivants, et qu’on ne se souvienne plus de son nom! »
Ndinali ngati mwana wankhosa wofatsa amene akupita naye kukamupha; sindinkadziwa kuti chiwembu chimene ankakonzekeracho chinkaloza ine. Iwo amati: “Tiyeni timuphe munthu ameneyu kuti dzina lake lisadzakumbukiridwenso.”
20 Mais Yahweh des armées juge avec justice; il sonde les reins et les cœurs; je verrai la vengeance que vous tirerez d’eux, car c’est à vous que j’ai confié ma cause.
Koma, Inu Yehova Wamphamvuzonse, Inu amene mumaweruza molungama ndi kuyesa mitima ndi maganizo, lolani kuti ine ndione kuti mwawalipsira, pakuti mlandu wanga ndawupereka mʼmanja mwanu.
21 C’est pourquoi ainsi parle Yahweh au sujet des hommes d’Anathoth qui en veulent à ta vie et qui disent: « Ne prophétise pas au nom de Yahweh, si tu ne veux mourir de notre main! »
“Nʼchifukwa chake Yehova akunena za anthu a ku Anatoti amene akufuna kuwononga moyo wako namanena kuti, ‘Usanenere mʼdzina la Yehova, ukatero ife tidzakupha ndi manja athu,’
22 C’est pourquoi ainsi parle Yahweh des armées: Je vais les punir; les jeunes hommes mourront par l’épée; leurs fils et leurs filles mourront de faim.
koma Yehova Wamphamvuzonse akuti, ‘Ine ndidzawalanga. Achinyamata awo adzaphedwa ndi lupanga, ana awo aamuna ndi aakazi adzafa ndi njala.
23 Aucun d’eux n’échappera; car j’amènerai le malheur sur les hommes d’Anathoth, l’année où je les visiterai.
Sipadzakhala otsala ndi mmodzi yemwe, chifukwa ndidzalanga anthu a ku Anatoti chikadzafika chaka chawo cha chilango.’”

< Jérémie 11 >