< Isaïe 39 >
1 En ce même temps, Mérodach-Baladan fils de Baladan, roi de Babylone, envoya une lettre et des présents à Ezechias, car il avait appris qu’il avait été malade et qu’il était rétabli.
Nthawi imeneyo Merodaki-Baladani, mwana wa Baladani mfumu ya ku Babuloni anatumiza nthumwi kwa Hezekiya nawapatsira makalata ndi mphatso, pakuti anamva za kudwala kwake ndi kuti anachira.
2 Ezéchias se réjouit de la venue des envoyés, et il leur montra la maison de son trésor, l’argent et l’or, les aromates et l’huile de prix, tout son arsenal et tout ce qui se trouvait dans ses trésors; il n’y eut rien qu’Ezéchias ne leur fit voir dans sa maison et dans tous ses domaines.
Hezekiya anawalandira mwasangala ndipo anawaonetsa zonse zimene zinali mʼnyumba zake zosungiramo siliva, golide, zokometsera zakudya, mafuta abwino kwambiri, zida zonse zankhondo ndiponso zonse zimene zinkapezeka mʼnyumba zake zosungiramo chuma. Panalibe kanthu kalikonse ka mʼnyumba yaufumu kapena mu ufumu wake onse kamene sanawaonetse.
3 Mais Isaïe, le prophète, vint auprès du roi Ezéchias, et lui dit: « Qu’ont dit ces gens-là, et d’où sont-ils venus vers toi? » Ezéchias répondit: « Ils sont venus vers moi d’un pays éloigné, de Babylone. »
Tsono mneneri Yesaya anapita kwa mfumu Hezekiya ndipo anamufunsa kuti, “Kodi anthu aja anakuwuzani chiyani, ndipo anachokera kuti?” Hezekiya anayankha kuti, “Anachokera ku dziko lakutali, ku Babuloni.”
4 Isaïe dit: « Qu’ont-ils vu dans ta maison? » Et Ezéchias répondit: « Ils ont vu tout ce qui est dans ma maison; il n’y a rien dans mes trésors que je ne leur aie fait voir. »
Mneneri anafunsanso kuti, “Kodi mʼnyumba yanu yaufumu anaonamo chiyani?” Hezekiya anati, “Anaona chilichonse cha mʼnyumba yanga yaufumu. Palibe ndi chimodzi chomwe za mʼnyumba yosungiramo chuma changa chimene sindinawaonetse.”
5 Et Isaïe dit à Ezéchias: « Ecoute la parole de Yahweh des armées:
Pamenepo Yesaya anati kwa Hezekiya, “Imvani mawu a Yehova Wamphamvuzonse:
6 Voici que des jours viendront où l’on emportera à Babylone tout ce qui est dans ta maison et ce que tes pères ont amassé jusqu’à ce jour; il n’en restera rien, dit Yahweh.
Yehova akuti, nthawi idzafika ndithu pamene zonse za mʼnyumba mwanu ndi zonse zimene makolo anu anazisonkhanitsa mpaka lero lino, zidzatengedwa kupita nazo ku Babuloni. Sipadzatsalapo ndi kanthu kamodzi komwe.
7 Et l’on prendra de tes fils, qui seront sortis de toi, que tu auras engendrés, pour en faire des eunuques dans le palais du roi de Babylone. »
Ndipo ena mwa ana anu, obala inu amene adzatengedwanso, ndipo adzawasandutsa adindo ofulidwa mʼnyumba ya mfumu ya ku Babuloni.”
8 Ezéchias répondit à Isaïe: « La parole de Yahweh que tu as prononcée est bonne. » Et il ajouta: « Car, il y aura paix et stabilité pendant ma vie ».
Hezekiya anayankha kuti, “Mawu a Yehova amene mwayankhula ndi abwino.” Ponena izi iye ankaganiza kuti, “Padzakhala mtendere ndi chitetezo masiku a moyo wanga onse.”