< Isaïe 21 >
1 Oracle sur le désert de la mer. Comme les ouragans passent dans le midi, cela vient du désert, d’une terre redoutable.
Uthenga wonena za chipululu cha mʼmbali mwa Nyanja. Ankhondo a ku Elamu ndi Mediya adzabwera ngati kamvuluvulu amene akuwomba modutsa mʼmbali ya nyanja, kuchokera ku chipululu, dziko lochititsa mantha.
2 Une vision terrible m’a été montrée: le pillard pille et le ravageur ravage! Monte, Elam! Assiège, Mède! Je fais cesser tous les gémissements.
Ine ndaona zinthu zoopsa mʼmasomphenya: Wonyenga akunyenga, wofunkha akufunkha komanso owononga akuwononga. Elamu, yambani nkhondo! Mediya, zingani mzinda! Ine ndidzathetsa mavuto onse amene anayambitsa Ababuloni.
3 C’est pourquoi mes reins sont remplis d’angoisses; des douleurs me saisissent, comme les douleurs d’une femme qui enfante. Je me tords à entendre, je m’épouvante à voir;
Chifukwa cha zimenezi thupi langa likunjenjemera ndi mantha, ndikumva ululu ngati wa mayi amene akubereka; ndikuvutika kwambiri ndi zimene ndikumva, ndathedwa nzeru ndi zimene ndikuziona.
4 mon cœur s’égare, l’effroi me saisit; de la nuit que je désirais on a fait pour moi un temps de terreurs.
Mtima wanga ukugunda, ndipo ndikunjenjemera ndi mantha; chisisira chimene ndakhala ndikuchifuna chasanduka chinthu choopsa kwa ine.
5 On dresse la table, la sentinelle fait le guet, on mange, on boit. — « Debout, capitaines! Oignez le bouclier! »
Ankhondo a ku Elamu ndi Mediya akukonza matebulo, akuyala mphasa, akudya komanso kumwa! Mwadzidzidzi anamva mawu akuti, “Dzukani inu ankhondo, pakani mafuta zishango zanu!”
6 Car ainsi m’a parlé le Seigneur: « Va, établis une sentinelle; qu’elle annonce ce qu’elle verra.
Zimene Ambuye akunena kwa ine ndi izi; “Pita, kayike mlonda kuti azinena zimene akuziona.
7 Et elle verra des cavaliers, deux à deux, sur des chevaux, des cavaliers sur des ânes, des cavaliers sur des chameaux. Et elle regardera avec attention, avec grande attention. »
Taonani, anthu akubwera ali pa akavalo ndipo akuyenda awiriawiri, okwera pa bulu kapena okwera pa ngamira, mlondayo akhale tcheru kwambiri.”
8 Et elle a crié comme un lion: « Sur la tour du guet, Seigneur, je me tiens, sans cesse tout le jour, et à mon poste je suis debout toutes les nuits.
Ndipo mlondayo anafuwula kuti, “Ambuye anga, tsiku ndi tsiku ndimakhala pa nsanja yolondera; Usiku uliwonse ndimakhala pa malo anga olondera.
9 Voici qu’arrive de la cavalerie; des cavaliers deux à deux. » Et elle a repris et dit: « Elle est tombée, elle est tombée, Babylone, et toutes les statues de ses dieux, il les a brisées contre terre! »
Taonani, uyo munthu akubwera atakwera pa galeta ali ndi gulu la akavalo. Mmodzi wa iwo akuti, ‘Babuloni wagwa, wagwa! Mafano onse a milungu yake agwa pansi ndipo aphwanyika!’”
10 O mon froment qu’on foule, grain de mon aire, ce que j’ai entendu de Yahweh des armées, du Dieu d’Israël, je vous l’annonce.
Inu anthu anga opunthidwa ndi kupetedwa ngati tirigu, ine ndikukuwuzani zimene ndamva ndikukuwuzani Uthenga wochokera kwa Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli.
11 Oracle sur Duma. On me crie de Séir: « Sentinelle, où en est la nuit? Sentinelle, où en est la nuit? »
Uthenga wonena za Duma: Munthu wina akundiyitana kuchokera ku Seiri kuti, “Iwe mlonda, usikuwu utha liti? Iwe mlonda, utha liti kodi usikuwu?”
12 La sentinelle répond: « Le matin vient et la nuit aussi. Si vous voulez m’interroger, interrogez; revenez une autre fois! »
Mlonda akuyankha kuti, “Kukucha, koma kudanso. Ngati ukufuna kufunsa, funsa tsopano; ndipo ubwerenso udzafunse.”
13 Oracle en Arabie. Vous passerez la nuit dans les steppes en Arabie, caravanes de Dédan. —
Uthenga wonena za Arabiya: Inu anthu amalonda a ku Dedani, amene usiku mumagona mʼzithukuluzi za ku Arabiya,
14 A la rencontre de celui qui a soif, apportez de l’eau! Les habitant du pays de Théma offrent du pain aux fugitifs.
perekani madzi kwa anthu aludzu. Inu anthu a ku Tema perekani chakudya kwa anthu othawa nkhondo.
15 Car ils ont fui devant l’épée, devant l’épée nue, devant l’arc bandé, devant la terrible bataille.
Iwo akuthawa malupanga, lupanga losololedwa, akuthawa uta wokokakoka ndiponso nkhondo yoopsa.
16 Car ainsi m’a parlé le Seigneur: Encore une année, comptée comme les années du mercenaire, et c’en est fait de toute la gloire de Cédar;
Zimene Ambuye akunena kwa ine ndi izi: “Chaka chimodzi chisanathe, potsata mmene amawerengera munthu waganyu, ulemerero wonse wa Kedara udzatheratu.
17 et des arcs nombreux des vaillants fils de Cédar il ne restera que peu de chose; car Yahweh, le Dieu d’Israël, a parlé.
Mwa anthu okoka uta, ankhondo a ku Kedara opulumuka adzakhala owerengeka.” Wayankhula ndi Yehova Mulungu wa Israeli.