< Osée 13 >

1 Dès qu’Ephraïm parlait, on tremblait; il s’éleva en Israël. Mais il se rendit coupable par Baal, et il mourut.
Kale Efereimu ankati akayankhula, anthu ankanjenjemera; anali wolemekezeka mu Israeli. Koma analakwa popembedza Baala, motero anafa.
2 Et maintenant, ils continuent à pécher; de leur argent ils ont fait une statue de fonte, des idoles selon leur idée: œuvre d’artisans que tout cela! On dit d’eux: « Sacrificateurs d’hommes, ils baisent des veaux! »
Tsopano akunka nachimwirachimwirabe; akudzipangira mafano pogwiritsa ntchito siliva wawo, zifanizo zopangidwa mwaluso, zonsezo zopangidwa ndi amisiri. Amanena za anthu awa kuti, “Amatenga munthu ndi kumupereka nsembe ndipo amapsompsona fano la mwana wangʼombe.”
3 C’est pourquoi ils seront comme une nuée du matin, et comme la rosée matinale qui se dissipe, comme la balle que le vent emporte de l’aire, et comme la fumée qui s’en va par la fenêtre.
Choncho adzakhala ngati nkhungu yammawa, ngati mame amene amakamuka msanga, ngati mungu wowuluka kuchokera pa malo opunthira tirigu, ngati utsi umene ukutulukira pa zenera.
4 Et moi, je suis Yahweh, ton Dieu, depuis le pays d’Égypte; tu ne connaîtras pas d’autre Dieu que moi, et en dehors de moi il n’y a pas de Sauveur.
Koma Ine ndine Yehova Mulungu wanu, amene ndinakutulutsani mu Igupto. Simuyenera kudziwa Mulungu wina, koma Ine ndekha, palibe Mpulumutsi wina kupatula Ine.
5 Je t’ai connu dans le désert, dans le pays de la sécheresse.
Ndinakusamalira mʼchipululu, mʼdziko lotentha kwambiri.
6 Quand ils ont eu leur pâture, ils se sont rassasiés; ils se sont rassasiés, et leur cœur s’est élevé, et à cause de cela ils m’ont oublié.
Pamene ndinawadyetsa, iwo anakhuta; iwo atakhuta anayamba kunyada; ndipo anandiyiwala Ine.
7 Je serai pour eux comme un lion, comme une panthère, je les guetterai au bord du chemin.
Motero ndidzawalumphira ngati mkango, ndidzawabisalira mu msewu ngati kambuku.
8 Je fondrai sur eux comme l’ourse privée de ses petits; je déchirerai l’enveloppe de leur cœur, et je les dévorerai là comme une lionne; la bête des champs les mettra en pièces.
Ngati chimbalangondo cholandidwa ana ake, ndidzawambwandira ndi kuwathyolathyola. Ndidzawapwepweta ngati mkango; chirombo chakuthengo chidzawakhadzula.
9 Ce qui te perd. Israël, c’est que tu es contre moi, contre celui qui est ton secours.
“Iwe Israeli, wawonongedwa, chifukwa ukutsutsana ndi Ine, ukutsutsana ndi mthandizi wako.
10 Où donc est ton roi, pour qu’il te sauve dans toutes les villes? Et où sont tes juges dont tu as dit: « Donne-moi un roi et des princes? »
Kodi mfumu yako ili kuti, kuti ikupulumutse? Olamulira ako a mʼmizinda yonse ali kuti, amene iwe unanena za iwo kuti, ‘Patseni mfumu ndi akalonga?’
11 Je te donne un roi dans ma colère, je te le prendrai dans ma fureur.
Choncho Ine ndinakupatsani mfumu mwachipseramtima, ndipo ndinayichotsa mwaukali.
12 L’iniquité d’Ephraïm est liée, son péché est mis en réserve.
Kulakwa kwa Efereimu kwasungidwa, machimo ake alembedwa mʼbuku.
13 Les douleurs de l’enfantement viennent pour lui; c’est un enfant dénué de sagesse; car, le moment venu, il ne se présente pas pour naître.
Zowawa zonga za mayi pa nthawi yobala mwana zamugwera, koma iye ndi mwana wopanda nzeru, pamene nthawi yake yobadwa yafika iyeyo safuna kutuluka mʼmimba mwa amayi ake.
14 Je les délivrerai de la puissance du schéol, je les rachèterai de la mort. Où est ta peste, ô mort? Où est ta destruction, ô schéol? Le repentir est caché à mes yeux. (Sheol h7585)
“Ndidzawapulumutsa ku mphamvu ya manda; ndidzawawombola ku imfa. Kodi iwe imfa, miliri yako ili kuti? Kodi iwe manda, kuwononga kwako kuli kuti? “Sindidzachitanso chifundo, (Sheol h7585)
15 Car Ephraïm fructifiera au milieu de ses frères! mais le vent d’orient viendra; le souffle de Yahweh montera du désert; sa source se desséchera, sa fontaine tarira; il pillera les trésors de tous les objets précieux.
ngakhale Efereimu akondwe pakati pa abale ake, mphepo ya kummawa yochokera kwa Yehova idzabwera, ikuwomba kuchokera ku chipululu. Kasupe wake adzaphwa ndipo chitsime chake chidzawuma. Chuma chake chonse chamtengowapatali chidzafunkhidwa ndipo chidzatengedwa.
16 Samarie sera punie, car elle s’est révoltée contre son Dieu; ils tomberont par l’épée! Leurs petits enfants seront écrasés, et l’on fendra le ventre de leurs femmes enceintes.
Anthu a ku Samariya adzalangidwa chifukwa cha zolakwa zawo, chifukwa anawukira Mulungu wawo. Adzaphedwa ndi lupanga; ana awo adzaphedwa mowamenyetsa pansi, akazi awo oyembekezera adzatumbulidwa pa mimba.”

< Osée 13 >