< Genèse 50 >
1 Joseph se jeta sur le visage de son père, pleura sur lui et le baisa.
Kenaka Yosefe anadzigwetsa pa nkhope ya abambo ake, nawapsompsona kwinaku akulira.
2 Puis il ordonna aux médecins à son service d’embaumer son père, et les médecins embaumèrent Israël.
Ndipo Yosefe analamula antchito ake a chipatala kuti akonze thupi la Israeli ndi mankhwala kuti lisawole. Kotero antchitowo anakonzadi thupilo.
3 Ils y employèrent quarante jours, car c’est le temps que l’on emploie à embaumer; et les Egyptiens le pleurèrent soixante-dix jours.
Antchito aja zinawatengera masiku 40 kuti akonze mtembo uja popeza ntchito ngati imeneyi inafunikira masiku monga amenewa. Ndipo Aigupto anamulira Yakobo kwa masiku makumi asanu ndi awiri.
4 Quand les jours de son deuil furent passés, Joseph s’adressa aux gens de la maison de Pharaon, et leur dit: « Si j’ai trouvé grâce à vos yeux, rapportez ceci, je vous prie, aux oreilles de Pharaon:
Yosefe atatha kulira maliro a abambo ake, anayankhula kwa nduna za Farao nati, “Ngati mungandikomere mtima, chonde mundiyankhulire kwa Farao kumuwuza kuti,
5 Mon père m’a fait jurer, en disant: Voici que je vais mourir; tu m’enterreras dans le sépulcre que je me suis creusé au pays de Canaan. Je voudrais donc y monter pour enterrer mon père; et je reviendrai. »
‘Abambo anga anandilumbiritsa ndipo anati, ‘Ndatsala pangʼono kumwalira, ukandiyike mʼmanda amene ndinakumba ndekha mʼdziko la Kanaani.’ Tsono mundilole ndikayike abambo anga, ndipo ndikabweranso.’”
6 Pharaon répondit: « Monte et enterre ton père, comme il te l’a fait jurer. »
Farao anati, “Pita ukayike abambo ako monga anakulumbiritsa kuti uchite.”
7 Joseph monta pour enterrer son père. Avec lui montèrent tous les serviteurs de Pharaon, les anciens de sa maison, et tous les anciens du pays d’Égypte,
Kotero Yosefe anapita kukayika abambo ake. Nduna zonse za Farao, akuluakulu a bwalo lake ndi akuluakulu a ku Igupto, anapita naye pamodzi.
8 toute la maison de Joseph, ses frères et la maison de son père: ils ne laissèrent dans le pays de Gessen que leurs petits enfants, leurs brebis et leurs bœufs.
Anapitanso onse a pa banja la Yosefe ndi abale ake ndi onse amene anali a pa banja la abambo ake. Ana awo okha, nkhosa ndi ngʼombe zinatsala ku Goseni
9 Il montait encore avec Joseph des chars et des cavaliers, en sorte que le cortège était très nombreux.
Asilikali okwera pa magaleta ndi asilikali a pa akavalo anapita nayenso pamodzi. Linali gulu lalikulu.
10 Arrivés à l’aire d’Atad, qui est au delà du Jourdain, ils firent entendre de grandes et profondes lamentations, et Joseph célébra en l’honneur de son père un deuil de sept jours.
Atafika pa Goreni ha-Atadi, pafupi ndi Yorodani, anachita mwambo waukulu wa maliro. Choncho Yosefe analira maliro a abambo ake masiku asanu ndi awiri.
11 Les habitants du pays, les Chananéens, ayant vu ce deuil dans l’aire d’Atad, dirent: « Voilà un grand deuil parmi les Egyptiens! » C’est pourquoi l’on a donné le nom d’Abel-Mitsraïm à ce lieu, qui est au delà du Jourdain.
Akanaani amene ankakhala ku Goreni ha-Atadi ataona mwambo wa maliro anati, “Aigupto ali ndi mwambo wa maliro a akulu.” Ndi chifukwa chake malo amenewo a pafupi ndi Yorodani amatchedwa Abeli-Mizraimu.
12 Les fils de Jacob firent donc envers lui comme il leur avait commandé.
Choncho ana a Yakobo anachita monga momwe abambo awo anawalamula:
13 Ses fils le transportèrent au pays de Canaan et l’enterrèrent dans la caverne du champ de Macpéla, qu’Abraham avait acquise d’Ephron le Hittite, avec le champ, pour avoir un sépulcre qui lui appartint, vis-à-vis de Mambré.
Ndiye kuti ana a Yakobo anamunyamula kupita naye ku Kanaani kuti akamuyike mʼphanga limene lili mʼmunda wa Makipela pafupi ndi Mamre. Abrahamu anagula mundawo kwa Efroni Mhiti kuti pakhale manda.
14 Après avoir enterré son père, Joseph retourna en Égypte avec ses frères et tous ceux qui étaient montés avec lui pour enterrer son père.
Atatha kuyika abambo ake, Yosefe anabwerera ku Igupto, pamodzi ndi abale ake ndi onse amene anapita nawo kukayika abambo ake.
15 Quand les frères de Joseph virent que leur père était mort, ils dirent: « Si Joseph nous prenait en haine, et nous rendait tout le mal que nous lui avons fait! »
Abale ake a Yosefe ataona kuti abambo awo amwalira, anati, “Nanga tidzatani ngati Yosefe anatisungira mangawa nafuna kutibwezera pa zoyipa zonse zimene tinamuchitira?”
16 Et ils firent dire à Joseph: « Ton père a donné cet ordre avant de mourir:
Motero anatumiza mawu kwa Yosefe kuti, “Abambo anu anasiya malangizo asanafe nati:
17 Vous parlerez ainsi à Joseph: Oh! pardonne le crime de tes frères et leur péché, car ils t’ont fait du mal! Maintenant donc, je te prie, pardonne le crime des serviteurs du Dieu de ton père. » Joseph pleura, en entendant ces paroles.
‘Zimene mudzayenera kunena kwa Yosefe ndi izi: Ndikukupempha kuti uwakhululukire abale ako cholakwa chawo ndi machimo awo, popeza anakuchitira zoyipa.’ Ndiye tsopano chonde tikhululukireni zolakwa zimene ife akapolo a Mulungu wa abambo anu tinachita.” Yosefe atangomva mawu amenewa anayamba kulira.
18 Ses frères vinrent eux-mêmes se prosterner devant lui, en disant: « Nous sommes tes serviteurs. »
Kenaka abale ake anabwera nadzigwetsa pansi pamaso pake, nati, “Ife ndife akapolo anu.”
19 Joseph leur dit: « Soyez sans crainte; car suis-je à la place de Dieu?
Koma Yosefe anawawuza kuti, “Musachite mantha. Kodi ine ndalowa mʼmalo mwa Mulungu?
20 Vous aviez dans la pensée de me faire du mal; mais Dieu avait dans la sienne d’en faire sortir du bien, afin d’accomplir ce qui arrive aujourd’hui, afin de conserver la vie à un peuple nombreux.
Inu munafuna kundichitira zoyipa, koma Mulungu anasandutsa zoyipazo kuti zikhale zabwino kuti zikwaniritsidwe zimene zikuchitika panozi, zopulumutsa miyoyo yambiri.
21 Soyez donc sans crainte; je vous entretiendrai, vous et vos enfants. » C’est ainsi qu’il les consola, en parlant à leurs cœurs.
Kotero, musachite mantha. Ine ndidzasamalira inu pamodzi ndi ana anu omwe.” Tsono iye anawalimbitsa mtima powayankhula moleza mtima.
22 Joseph demeura en Égypte, lui et la maison de son père. Il vécut cent dix ans.
Yosefe anakhala mu Igupto pamodzi ndi banja lonse la abambo ake. Anakhala ndi moyo zaka 110
23 Joseph vit les fils d’Ephraïm jusqu’à la troisième génération; des fils de Machir, fils de Manassé, naquirent aussi sur les genoux de Joseph.
ndipo anaona mʼbado wachitatu wa ana a Efereimu. Yosefe anatenganso ana a Makiri, mwana wa Manase kukhala ngati ana a mʼbanja lake.
24 Joseph dit à ses frères: « Pour moi, je vais mourir; mais Dieu vous visitera certainement et vous fera remonter de ce pays dans le pays qu’il a juré de donner à Abraham, à Isaac et à Jacob. »
Kenaka Yosefe anati kwa abale ake, “Ine ndatsala pangʼono kufa. Koma mosakayika Mulungu adzakuyangʼanirani nadzakutengani kukutulutsani mʼdziko lino kupita ku dziko limene Iye analonjeza kwa Abrahamu, Isake ndi Yakobo.”
25 Joseph fit jurer les fils d’Israël, en disant: « Certainement Dieu vous visitera, et vous ferez remonter mes os d’ici. »
Ndipo Yosefe analumbiritsa ana a Israeli lumbiro nati, “Lonjezani kuti Mulungu akadzakusungani mudzanyamula mafupa anga kuwachotsa ku malo kuno.”
26 Joseph mourut, âgé de cent dix ans. On l’embauma et on le mit dans un cercueil en Égypte.
Choncho Yosefe anafa ali ndi zaka 110. Motero iwo atakonza thupi lake ndi mankhwala kuti lisawole, analiyika mʼbokosi ku Igupto.