< Genèse 37 >

1 Jacob s’établit dans le pays où son père avait séjourné dans le pays de Canaan.
Yakobo ankakhala mʼdziko la Kanaani kumene abambo ake ankakhala.
2 Voici l’histoire de Jacob. Joseph, âgé de dix-sept ans, faisait paître les brebis avec ses frères; comme il était encore jeune, il se trouvait avec les fils de Bala et avec les fils de Zelpha, femmes de son père; et Joseph rapporta à leur père de mauvais bruits qui couraient sur leur compte.
Mbiri ya banja la Yakobo ndi iyi: Yosefe, mnyamata wa zaka 17 ankaweta nkhosa ndi abale ake, pamodzi ndi ana a Biliha ndi Zilipa, akazi a abambo ake. Tsono Yosefe ankabwera kudzawuza abambo ake zoyipa za abale ake.
3 Or Israël aimait Joseph plus que tous ses autres fils, parce que c’était un fils de sa vieillesse; et il lui fit une robe longue.
Tsono Israeli ankakonda Yosefe koposa ana ake ena onse, chifukwa anali mwana wobadwa muukalamba wake. Ndipo anamusokera mkanjo wa manja aatali.
4 Ses frères, voyant que leur père l’aimait plus qu’eux tous, le prirent en haine, et ils ne pouvaient plus lui parler amicalement.
Pamene abale ake anaona kuti abambo awo ankakonda Yosefe kuposa aliyense wa iwo, anayamba kumuda Yosefe ndipo sankayankhula naye zamtendere.
5 Joseph eut un songe, et il le raconta à ses frères, qui le haïrent encore davantage.
Tsiku lina Yosefe analota maloto ndipo pamene anawuza abale ake za malotowo, iwo anawonjeza kumuda.
6 Il leur dit: « Ecoutez, je vous prie, le songe que j’ai eu:
Iye anawawuza kuti, “Tamvani maloto amene ndinalota:
7 Nous étions à lier des gerbes au milieu des champs; et voici, ma gerbe s’est levée et s’est tenue debout, et vos gerbes l’ont entourée et se sont prosternées devant elle. »
Ife timamanga mitolo ya tirigu ku munda ndipo mwadzidzidzi mtolo wanga unayimirira chilili, pamene mitolo yanu inazungulira mtolo wangawo nʼkumawugwadira.”
8 Ses frères lui dirent: « Est-ce que tu régneras sur nous? est-ce que tu nous domineras? » Et ils le haïrent encore davantage pour ses songes et pour ses paroles.
Abale ake aja anamufunsa nati, “Kodi ukuyesa kuti ungakhale mfumu yathu? Ungadzatilamuliredi iweyo?” Ndipo anamuda kuposa kale chifukwa cha maloto ake ndi zimene ankakonda kunena kwa abambo awo.
9 Il eut encore un autre songe, qu’il raconta à ses frères. Il dit: « J’ai eu encore un songe: le soleil, la lune et onze étoiles se prosternaient devant moi. »
Tsiku lina analotanso maloto ena, ndipo anafotokozera abale ake za malotowo. Iye anati, “Tamverani, ndinalotanso maloto ena. Ulendo uno dzuwa ndi mwezi pamodzi ndi nyenyezi khumi ndi imodzi zimandigwadira.”
10 Il le raconta à son père et à ses frères, et son père le réprimanda, en disant: « Que signifie ce songe que tu as eu? Faudra-t-il que nous venions, moi, ta mère et tes frères, nous prosterner à terre devant toi? »
Atawuza abambo ake ndi abale ake malotowa, abambo ake anamukalipira nati, “Ndi maloto anji umalotawa? Kodi uganiza kuti ine, amayi ako pamodzi ndi abale ako onsewa tingadzabwere kudzakugwandira iwe?”
11 Et ses frères furent jaloux de lui, mais son père conservait la chose dans son cœur.
Abale ake anamuchitira nsanje, koma abambo ake anasunga nkhaniyi mu mtima.
12 Les frères de Joseph allèrent paître les troupeaux de leur père à Sichem.
Tsono abale ake anapita kukadyetsa ziweto za abambo awo ku Sekemu,
13 Et Israël dit à Joseph: « Tes frères ne paissent-ils pas le troupeau à Sichem? Viens, que je t’envoie vers eux. » Il répondit: « Me voici. »
ndipo Israeli anati kwa Yosefe, “Tsono, ndikufuna kukutuma kwa abale ako.” Iye anayankha nati, “Chabwino.”
14 Et Israël lui dit: « Va donc, et vois si tes frères vont bien et si le troupeau est en bon état, et tu m’en apporteras des nouvelles. » Et il l’envoya de la vallée d’Hébron, et Joseph alla à Sichem.
Choncho anati kwa iye, “Pita ukaone ngati abale ako ali bwino. Ukaonenso nkhosa ngati zili bwino. Kenaka ubwere udzandiwuze.” Choncho Israeli anatuma Yosefe kuchokera ku chigwa cha Hebroni. Yosefe atafika ku Sekemu,
15 Un homme, l’ayant rencontré errant dans la campagne, le questionna, en disant: « Que cherches-tu? »
munthu wina anamupeza akungozungulirazungulira mʼmunda ndipo anamufunsa, “Ukufunafuna chiyani?”
16 Il répondit: « Je cherche mes frères; indique-moi, je te prie, où ils font paître leur troupeau. »
Iye anayankha, “Ndikufuna abale anga. Mungandiwuze kumene akudyetsa ziweto zawo?”
17 Et l’homme dit: « Ils sont partis d’ici; car je les ai entendus dire: Allons à Dothaïn. » Joseph alla après ses frères, et il les trouva à Dothaïn.
Munthuyo anayankha nati, “Anasamukako kuno. Ndinawamva akuti, ‘Tiyeni tipite ku Dotani.’” Choncho Yosefe analondola abale ake ndipo anakawapeza ku Dotani.
18 Ils l’aperçurent de loin et, avant qu’il fût près d’eux, ils complotèrent de le faire mourir.
Abale ake aja anamuonera patali. Ndipo asanafike nʼkomwe kumene kunali iwo kuja, anayamba kale kumupangira chiwembu choti amuphe.
19 Ils se dirent l’un à l’autre: « Voici l’homme aux songes; c’est bien lui qui arrive.
Iwo anawuzana nati, “Uyo akubwera apo wamaloto uja.
20 Venez donc, tuons-le et jetons-le dans une des citernes, et nous dirons qu’une bête féroce l’a dévoré; nous verrons ce qui en sera de ses songes! »
Tsono tiyeni timuphe ndi kuponya thupi lake mu chimodzi mwa zitsime izi ndipo tidzati anadyedwa ndi nyama zakuthengo zolusa. Tsono timuonera zomwe ziti zichitike ndi maloto ake aja.”
21 Ruben entendit et il le délivra de leurs mains. Il dit: « Ne le frappons pas à mort. »
Koma Rubeni atamva izi, anapulumutsa Yosefe. Iye anati kwa abale ake, “Ayi, tisamuphe,
22 Ruben leur dit: « Ne versez pas le sang; jetez-le dans cette citerne qui est dans le désert, et ne portez pas la main sur lui. » — Son dessein était de le délivrer de leurs mains, pour le faire retourner vers son père. —
tisakhetse magazi. Tiyeni timuponye mʼchitsime ku chipululu konkuno. Koma tisamuvulaze nʼkomwe. Rubeni ananena zonsezi kuti apulumutse Yosefe ndi kuti pambuyo pake akamupereke kwa abambo awo.”
23 Lorsque Joseph arriva auprès de ses frères, ils le dépouillèrent de sa robe, de la robe longue qu’il portait;
Choncho Yosefe atafika kwa abale ake, iwo anamuvula mkanjo wake wamanja aatali uja umene anavala
24 et, l’ayant pris, ils le jetèrent dans la citerne. Cette citerne était vide: il n’y avait pas d’eau.
ndipo anamutenga namuponya mʼchitsime chopanda madzi komanso mopanda chilichonse.
25 Puis ils s’assirent pour manger. Levant les yeux, ils virent, et voici qu’une caravane d’Ismaélites venait de Galaad; leurs chameaux étaient chargés d’astragale, de baume et de ladanum, qu’ils transportaient en Égypte.
Atakhala pansi kuti adye chakudya, anatukula maso naona gulu la Aismaeli akubwera kuchokera ku Giliyadi. Ngamira zawo zinanyamula zonunkhiritsa bwino zakudya zamitundumitundu, ndipo zimenezi ankapita nazo ku Igupto.
26 Alors Juda dit à ses frères: « Que gagnerons-nous à tuer notre frère et à cacher son sang?
Yuda anafunsa abale ake nati, “Kodi tidzapindula chiyani tikapha mʼbale wathuyu ndi kuphimbitsa magazi ake?
27 Allons le vendre aux Ismaélites et ne portons pas la main sur lui; car il est notre frère, notre chair. » Ses frères l’écoutèrent
Bwanji timugulitse kwa Aismaeliwa, koma ife tisamuchite kanthu kalikonse. Ameneyu ndi mʼbale wathu thupi limodzi ndi ife.” Abale ake anavomereza zimenezi.
28 et, quand les marchands madianites passèrent, ils tirèrent Joseph et le firent remonter de la citerne; et ils le vendirent pour vingt pièces d’argent aux Ismaélites, qui l’emmenèrent en Égypte.
Amalonda ena a ku Midiyani ankadutsa pomwepo. Tsono abale ake a Yosefe anamutulutsa Yosefe uja mu chitsime chija ndipo anamugulitsa kwa Aismaeli aja pamtengo wa masekeli makumi awiri. Choncho anapita naye Yosefe ku Igupto.
29 Ruben revint à la citerne, et voici que Joseph n’était plus dans la citerne.
Rubeni atabwerera ku chitsime kuja anapeza kuti Yosefe mulibe mʼchitsimemo. Pamenepo iye anangʼamba zovala zake
30 Il déchira ses vêtements et, étant retourné vers ses frères, il dit: « L’enfant n’y est plus, et moi, où irai-je? »
nabwerera kwa abale ake nati, “Mnyamata uja mulibemo! Nanga ndilowere kuti ine tsopano?”
31 Ils prirent alors la robe de Joseph et, ayant tué un bouc, ils plongèrent la robe dans le sang.
Tsono anapha kamwana ka mbuzi, natenga mkanjo wa Yosefe ndi kuwunyika mʼmagazi ake.
32 Et ils envoyèrent à leur père la longue robe, en lui faisant dire: « Voilà ce que nous avons trouvé; reconnais si c’est la robe de ton fils, ou non. »
Iwo anatenga mkanjo uja nabwerera nawo kwa abambo awo nati, “Ife tapeza mkanjowu. Tawuyangʼanitsitsani muone ngati uli wa mwana wanu.”
33 Jacob la reconnut et dit: « C’est la robe de mon fils! Une bête féroce l’a dévoré! Joseph a été mis en pièces! »
Iye anawuzindikira ndipo anati, “Ndi mkanjo wa mwana wanga umenewu! Nyama yakuthengo yolusa yamudya. Mosakayika, mwana wanga Yosefe wakhadzulidwa.”
34 Et il déchira ses vêtements, mit un sac sur ses reins et fit le deuil de son fils pendant longtemps.
Pamenepo Yakobo anangʼamba zovala zake, navala chisaka mʼchiwuno mwake. Iye analira maliro a mwana wake masiku ambiri.
35 Tous ses fils et toutes ses filles vinrent pour le consoler; mais il refusa d’être consolé; il disait: « Je descendrai dans le deuil vers mon fils au séjour des morts. » Et son père le pleura. (Sheol h7585)
Ngakhale kuti ana ake onse aamuna ndi aakazi anasonkhana kudzamutonthoza, iye anakana kutonthozedwa. Iye anati, “Ayi. Ndidzalira mpaka ndidzapite kwa mwana wanga ku manda.” Choncho Israeli anapitirirabe kulira mwana wake. (Sheol h7585)
36 Les Madianites le vendirent en Égypte à Putiphar, officier de Pharaon, chef des gardes.
Amidiyani aja anagulitsa Yosefe kwa Potifara, mmodzi mwa nduna za Farao ku Igupto. Potifarayu anali mkulu wa asilikali olonda nyumba ya Farao.

< Genèse 37 >