< Genèse 33 >

1 Jacob leva les yeux et regarda, et voici, Esaü venait, ayant avec lui quatre cents hommes. Ayant distribué les enfants par groupes auprès de Lia, auprès de Rachel et auprès des deux servantes,
Yakobo atakweza maso ake anaona Esau akubwera ndi anthu ake 400. Choncho ana ake anawagawira Leya, Rakele ndi antchito awiri aja.
2 il plaça en tête les servantes avec leurs enfants, puis Lia avec ses enfants, et enfin Rachel avec Joseph.
Anayika antchito ndi ana awo patsogolo, kenaka nʼkubwera Leya ndi ana ake, ndipo pambuyo pawo Rakele ndi Yosefe.
3 Lui-même passa devant eux, et il se courba vers la terre sept fois, jusqu’à ce qu’il fût proche de son frère Esaü.
Iye mwini anakhala patsogolo nawerama mpaka kukhudza pansi kasanu ndi kawiri pamene amayandikira mʼbale wake.
4 Esaü courut à sa rencontre, l’embrassa, se jeta à son cou et le baisa; et ils pleurèrent.
Koma Esau anathamanga kukakumana ndi Yakobo ndipo anamukupatira namupsompsona. Onse awiri ankangolira.
5 Puis, levant les yeux, Esaü vit les femmes et les enfants, et il dit: « Qui sont ceux que tu as là? » Jacob répondit: « Ce sont les enfants que Dieu a accordés à ton serviteur. »
Kenaka Esau ataona amayi ndi ana awo anamufunsa Yakobo kuti, “Kodi anthu amene uli nawowa ndi a ndani?” Yakobo anayankha kuti, “Awa ndi ana amene Mulungu, mwa kukoma mtima kwake, wapereka kwa mtumiki wanune.”
6 Les servantes s’approchèrent, elles et leurs enfants, et se prosternèrent.
Tsono antchito aja anayandikira naweramitsa mitu pansi.
7 Lia et ses enfants s’approchèrent aussi, et ils se prosternèrent; ensuite s’approchèrent Joseph et Rachel, et ils se prosternèrent.
Kenaka, Leya ndi ana ake anabwera. Nawonso anaweramitsa mitu pansi. Potsiriza pa onse anabwera Yosefe ndi Rakele naweramitsanso mitu yawo pansi.
8 Et Esaü dit: « Que veux-tu faire avec tout ce camp que j’ai rencontré? » Et Jacob dit: « C’est pour trouver grâce aux yeux de mon seigneur. »
Esau anafunsa kuti, “Kodi gulu la ziweto ndakumana nalo lija ndi layani?” Yakobo anayankha nati, “Mbuye wanga, gulu lija ndi lanu kuti mundikomere mtima.”
9 Esaü dit: « Je suis dans l’abondance, mon frère; garde ce qui est à toi. »
Koma Esau anati, “Mʼbale wanga, ine ndili nazo kale zambiri. Zinthu zakozi sunga.”
10 Et Jacob dit: « Non, je te prie, si j’ai trouvé grâce à tes yeux, accepte mon présent de ma main; car c’est pour cela que j’ai vu ta face comme on voit la face de Dieu, et tu m’as accueilli favorablement.
Yakobo anati, “Chonde musatero. Ngati mwandikomera mtima, landirani mphatso yangayi kuchokera kwa ine. Pakuti ndi mmene mwandirandira bwinomu, ine ndikamaona nkhope yanu ndikuchita ngati ndikuona nkhope ya Mulungu.
11 Accepte donc mon offrande qui t’a été amenée, car Dieu m’a accordé sa faveur et je ne manque de rien. » Il le pressa si bien qu’Esaü accepta.
Chonde, landirani mphatso imene ndakutengeraniyi, popeza Mulungu wandikomera mtima kwambiri moti ndili ndi zonse zimene ndizifuna.” Ndipo popeza kuti Yakobo anamuwumiriza, Esau analandira.
12 Esaü dit: « Partons, mettons-nous en route; je marcherai devant toi. »
Ndipo Esau anati, “Tiyeni tizipita; nditsagana nanu.”
13 Jacob répondit: « Mon seigneur sait que les enfants sont délicats, et que je suis chargé de brebis et de vaches qui allaitent; si on les pressait un seul jour, tout le troupeau périrait.
Koma Yakobo anati kwa iye, “Mbuye wanga, inu mudziwa kuti anawa ndi a nthete ndiponso ndiyenera kusamalira nkhosa ndi ngʼombe zimene zikuyamwitsa ana awo. Ngati ndizimenya kuti zifulumire, tsiku limodzi lokha nyamazo zidzafa.
14 Que mon seigneur prenne les devants sur son serviteur, et moi, je suivrai doucement, au pas du troupeau qui marche devant moi, et au pas des enfants, jusqu’à ce que j’arrive chez mon seigneur, à Séir. »
Choncho, mbuye wanga lolani kuti mutsogole. Ine ndiziyenda pangʼonopangʼono pambuyo pa ziwetozi ndi anawa mpaka ndikafika ku Seiri.”
15 Esaü dit: « Permets du moins que je laisse auprès de toi une partie des gens qui sont avec moi. » Jacob répondit: « Pourquoi cela? Que je trouve grâce aux yeux de mon seigneur. »
Esau anati, “Ndiye bwanji ndikusiyireko ena mwa anthu anga.” Koma Yakobo anati, “Koma muchitiranji zimenezi? Chachikulu nʼkuti mwandilandira bwino, mbuye wanga.”
16 Et Esaü reprit ce jour-là le chemin de Séir.
Choncho tsiku limenelo Esau anayamba ulendo wobwerera ku Seiri.
17 Jacob partit pour Socoth et il se construisit une maison. Il fit aussi des cabanes pour ses troupeaux; c’est pourquoi on a appelé ce lieu Socoth.
Komabe Yakobo anapita ku Sukoti. Kumeneko anamanga nyumba yake ndi makola a ziweto zake. Nʼchifukwa chake malowa amatchedwa Sukoti.
18 A son retour de Paddan-Aram, Jacob arriva heureusement à la ville de Sichem, au pays de Canaan, et il campa devant la ville.
Mmene ankabwerera kuchokera ku Padanaramu, Yakobo anafika ku Salemu, mzinda wa Sekemu ku Kanaani. Anamanga msasa pamalopo moyangʼanana ndi mzindawo.
19 Il acheta des fils de Hémor, père de Sichem, pour cent késitas, la pièce de terre où il avait dressé sa tente;
Malo amenewo anagula kwa zidzukulu za Hamori, abambo a Sekemu ndi ndalama 100 zasiliva.
20 il éleva là un autel, et l’appela El-Elohé-Israël.
Pamalopo anamanganso guwa lansembe, nalitcha Eli Elohe Israeli.

< Genèse 33 >