< Genèse 27 >
1 Isaac était devenu vieux, et ses yeux s’étaient obscurcis au point de ne plus voir. Il appela Esaü, son fils aîné, et lui dit: « Mon fils! » Celui-ci lui–répondit: « Me voici. »
Isake atakalamba maso ake anachita khungu mwakuti sankatha kuona. Iye anayitana mwana wake wamkulu Esau nati kwa iye, “Mwana wanga.” Iye anayankha, “Ine abambo.”
2 Isaac dit: « Voici donc, je suis vieux; je ne connais pas le jour de ma mort.
Isake anati, “Tsopano ine ndakalamba, ndipo sindidziwa tsiku langa lakufa.
3 Maintenant donc, prends tes armes, ton carquois et ton arc, va dans la campagne et tue-moi du gibier.
Tsono tenga zida zako, muvi wako ndi uta, pita kuthengo ukandiphere nyama.
4 Fais-m’en un bon plat, selon mon goût, et apporte-le-moi, que je le mange, afin que mon âme te bénisse avant que je meure. »
Undikonzere chakudya chabwino monga muja ndimakonderamu ndipo ubwere nacho kwa ine kuti ndidye ndi kuti ndikudalitse ndisanamwalire.”
5 — Rebecca entendait pendant qu’Isaac parlait à Esaü, son fils. — Et Esaü s’en alla dans la campagne pour tuer du gibier et l’apporter.
Koma Rebeka amamvetsera pamene Isake amayankhula ndi mwana wake Esau. Esau atanyamuka kupita kuthengo kukaphera abambo ake nyama,
6 Alors Rebecca parla ainsi à Jacob, son fils: « Voici, j’ai entendu ton père qui parlait ainsi à ton frère Esaü:
Rebeka anati kwa mwana wake Yakobo, “Taona ndamva abambo ako akuwuza mʼbale wako Esau kuti,
7 Apporte-moi du gibier et fais-m’en un bon plat, afin que je le mange et que je te bénisse devant Yahweh avant de mourir.
‘Bweretsere nyama yakutchire ndipo undikonzere chakudya chokoma kuti ndidye; kuti ndikudalitse pamaso pa Yehova ndisanamwalire.’
8 Maintenant, mon fils, écoute ma voix dans ce que je vais te commander.
Tsopano mwana wanga, mvetsetsa ndipo uchite zimene ndikuwuze:
9 Va au troupeau et prends-moi deux beaux chevreaux; j’en ferai pour ton père un bon plat, selon son goût,
Pita ku khola, ukatenge ana ambuzi abwino awiri, kuti ndikonzere abambo ako chakudya chokoma monga amakondera.
10 et tu le porteras à ton père, et il en mangera, afin qu’il te bénisse avant de mourir. »
Kenaka upite nacho chakudyacho kwa abambo ako kuti adye ndi kukudalitsa asanafe.”
11 Jacob répondit à Rebecca, sa mère: « Voici, Esaü, mon frère, est velu, et moi j’ai la peau lisse.
Koma Yakobo anati kwa Rebeka amayi ake, “Komatu mʼbale wanga Esau ndi munthu wa khungu la ubweya zedi, ndipo ine ndine munthu wa khungu losalala.
12 Peut-être que mon père me touchera, et je passerai à ses yeux pour m’être joué de lui, et j’attirerai sur moi une malédiction au lieu d’une bénédiction. »
Mwina abambo anga adzandikhudza, ndipo ndidzaoneka kuti ndawapusitsa. Tsono ndizadzitengera temberero mʼmalo mwa madalitso.”
13 Sa mère lui dit: « Je prends sur moi ta malédiction, mon fils. Ecoute seulement ma voix et va me prendre les chevreaux. »
Amayi ake anati kwa iye, “Mwana wanga, temberero limenelo ligwere ine. Iwe ungochita zimene ine ndikukuwuza; pita kanditengere timbuzito.”
14 Jacob alla les prendre et les apporta à sa mère, qui en fit un bon plat, selon le goût de son père.
Choncho anapita nakatenga timbuzito ndi kubwera nato kwa amayi ake. Choncho Rebeka anaphika chakudya chokoma monga momwe Isake amakondera.
15 Et Rebecca prit les habits d’Esaü, son fils aîné, les plus beaux, qu’elle avait dans la maison, et elle en revêtit Jacob, son fils cadet.
Tsono Rebeka anatenga zovala zabwino kwambiri za Esau mwana wake wamkulu zimene zinali mʼnyumba namuveka Yakobo.
16 Puis elle lui couvrit les mains de la peau des chevreaux, ainsi que la partie lisse du cou.
Anamuvekanso manja ake ndi khosi lake ndi zikopa za mwana wambuzi.
17 Et elle mit dans la main de Jacob, son fils, le bon plat et le pain qu’elle avait préparés.
Kenaka, anamupatsa Yakobo chakudya chokoma chija chimene anaphika pamodzi ndi buledi.
18 Il vint vers son père et dit: « Mon père! » — « Me voici, dit Isaac; qui es-tu, mon fils? »
Yakobo anapita kwa abambo ake ndipo anati, “Abambo anga.” Ndipo anayankha, “Eya, kodi ndiwe mwana wanga uti?”
19 Jacob répondit à son père: « Je suis Esaü, ton premier-né; j’ai fait ce que tu m’as dit. Lève-toi, je te prie, assieds-toi et mange de ma chasse, afin que ton âme me bénisse. »
Yakobo anati kwa abambo ake, “Ndine Esau mwana wanu woyamba. Ndachita monga munandiwuzira. Chonde dzukani ndi kukhala tsonga kuti mudyeko nyama ndakukonzeraniyi kuti tsono mundidalitse.”
20 Isaac dit à son fils: « Comment as-tu trouvé si vite, mon fils? » Jacob, répondit: « C’est que Yahweh, ton Dieu, l’a fait venir devant moi. »
Isake anafunsa mwana wake, “Wayipeza msanga chotere bwanji mwana wanga?” Iye anayankha, “Yehova Mulungu wanu anandithandiza kuti ndiyipeze.”
21 Et Isaac dit à Jacob: « Approche donc, que je te touche, mon fils, pour savoir si tu es bien mon fils Esaü, ou non. »
Pamenepo Isake anati kwa Yakobo, “Tabwera pafupi ndikukhudze mwana wanga, kuti ndidziwedi ngati uli mwana wanga Esau kapena ayi.”
22 Jacob s’étant approché d’Isaac, son père, celui-ci le toucha et dit: « La voix est la voix de Jacob, mais les mains sont les mains d’Esaü. »
Yakobo anasendera kufupi ndi abambo ake Isake ndipo anamukhudza nati, “Mawuwa ndi mawu a Yakobo koma mikonoyi ndi mikono ya Esau.”
23 Il ne le reconnut pas, parce que ses mains étaient velues, comme les mains d’Esaü, son frère, et il le bénit.
Sanamuzindikire, popeza mikono yake inali ndi ubweya ngati ya mʼbale wake Esau; choncho anamudalitsa.
24 Il dit: « C’est bien toi qui es mon fils Esaü? » — « C’est moi », répondit Jacob.
Isake anafunsa, “Kodi ndiwedi mwana wanga Esau?” Yakobo anayankha, “Inde ndine.”
25 Et Isaac dit: « Sers-moi, que je mange du gibier de mon fils et que mon âme te bénisse. » Jacob le servit, et il mangea; il lui présenta aussi du vin, et il but.
Ndipo iye anati, “Mwana wanga, patseko nyama yakoyo ndidye kuti ndikudalitse.” Yakobo anabwera ndi nyama ija kwa Isake ndipo anadya. Kenaka anamupatsanso vinyo ndipo anamwa.
26 Alors Isaac, son père, lui dit: « Approche-toi donc et baise-moi, mon fils. »
Tsono Isake anati kwa Yakobo, “Bwera kuno mwana wanga undipsompsone.”
27 Jacob s’approcha et le baisa; et Isaac sentit l’odeur de ses vêtements, et il le bénit en disant: « Voici, l’odeur de mon fils est comme l’odeur d’un champ qu’a béni Yahweh. »
Choncho anapita namupsompsona. Apa Isake anamva fungo la zovala zake, ndipo anamudalitsa nati, “Haa, fungo la mwana wanga lili ngati fungo la munda umene Yehova waudalitsa.
28 Que Dieu te donne de la rosée du ciel et de la graisse de la terre, et abondance de froment et de vin!
Mulungu akugwetsere mame akumwamba ndipo minda yako ibale tirigu wambiri ndi vinyo watsopano.
29 Que des peuples te servent, et que des nations se prosternent devant toi! Sois le maître de tes frères, et que les fils de ta mère se prosternent devant toi! Maudit soit qui te maudira, et béni soit qui te bénira!
Mitundu ya anthu ikutumikire iwe ndipo anthu akugwadire iwe. Ukhale wolamula abale ako, ndipo ana aamuna a amayi ako akugwadire. Amene akutemberera iwe atembereredwe ndipo amene adalitsa iwe adalitsike.”
30 Isaac avait achevé de bénir Jacob, et Jacob venait de quitter Isaac, son père, lorsqu’Esaü, son frère, revint de la chasse.
Isake atatsiriza kudalitsa Yakobo, atangochoka pamaso pa abambo akewo, Esau anabwera kuchokera kosaka kuja.
31 Il prépara, lui aussi, un bon plat, et l’apporta à son père; et il dit à son père: « Que mon père se lève et mange de la chasse de son fils, afin que ton âme me bénisse. »
Nayenso anakonza chakudya chokoma nabwera nacho kwa abambo ake. Ndipo anati kwa iye, “Chonde abambo, dzukani mukhale tsonga kuti mudye nyamayi ndi kuti mundidalitse.”
32 Isaac, son père, lui dit: « Qui es-tu? » Il répondit: « Je suis ton fils, ton premier-né, Esaü. »
Abambo ake, Isake, anamufunsa kuti, “Ndiwe yani?” Iye anayankha, “Ndine mwana wanu woyamba Esau.”
33 Isaac fut saisi d’une terreur extrême, et il dit: « Qui est donc celui qui a chassé du gibier et m’en a apporté? J’ai mangé de tout avant que tu vinsses, et je l’ai béni; et il sera béni en effet. »
Isake ananjenjemera kwambiri nati, “Nanga ndani uja anakapha nyama kutchire nʼkudzandipatsa? Ine ndadya kale, ndadya nyamayo iwe utangotsala pangʼono kubwera ndipo ndamudalitsa ndipo adzakhaladi wodalitsika.”
34 Lorsqu’Esaü eut entendu les paroles de son père, il jeta un grand cri, une plainte très amère, et il dit à son père: « Bénis-moi, moi aussi, mon père. »
Esau atamva mawu a abambo ake, analira mokweza ndi mowawidwa mtima nati kwa abambo ake, “Inenso dalitseni abambo anga!”
35 Isaac dit: « Ton frère est venu avec ruse, et il a pris ta bénédiction. »
Koma iye anati, “Mʼbale wako anabwera mwachinyengo ndipo watenga madalitso ako.”
36 Esaü dit: « Est-ce parce qu’on l’appelle Jacob qu’il m’a supplanté deux fois? Il a pris mon droit d’aînesse, et voilà maintenant qu’il a pris ma bénédiction! » Il ajouta: « N’as-tu pas réservé pour moi une bénédiction? »
Esau anati, “Kodi nʼchifukwa chake iyeyu dzina lake lili Yakobo eti? Aka nʼkachiwiri kundinyenga: Anatenga ukulu wanga, pano watenga madalitso anga!” Kenaka anafunsa, “Kodi simunandisungireko ena madalitsowo?”
37 Isaac répondit et dit à Esaü: « Voici, je l’ai établi ton maître et je lui ai donné tous ses frères pour serviteurs, et je l’ai pourvu de froment et de vin; et pour toi donc, que puis-je faire, mon fils?
Koma Isake anamuyankha nati, “Ndamudalitsa iye kuti akhale wokulamulira iwe. Ndaperekanso abale ake onse kuti akhale omutumikira iye, ndipo ndamudalitsa ndi tirigu wambiri, ndi vinyo watsopano. Ndiye ndingakuchitirenso chiyani mwana wanga?”
38 Esaü dit à son père: « N’as-tu que cette seule bénédiction, mon père? Bénis-moi, moi aussi, mon père! » Et Esaü éleva la voix et pleura.
Esau anati kwa abambo ake, “Kodi muli ndi dalitso limodzi lokhali, abambo anga? Inenso mundidalitse chonde abambo anga!” Pomwepo Esau analira mokuwa.
39 Isaac, son père, lui répondit: « Privée de la graisse de la terre sera ta demeure, privée de la rosée qui descend du ciel.
Tsono Isake abambo ake anamuyankha kuti, “Malo ako okhalapo sadzabala dzinthu, ndipo mvula sidzagwa pa minda yako.
40 Tu vivras de ton épée, et tu seras asservi à ton frère; mais il arrivera que, en secouant son joug, tu le briseras de dessus ton cou. »
Udzakhala ndi moyo podalira lupanga ndipo udzatumikira mʼbale wako. Koma idzafika nthawi pamene udzakhala mfulu udzachotsa goli lake mʼkhosi mwako.”
41 Esaü conçut de la haine contre Jacob à cause de la bénédiction que son père lui avait donnée, et Esaü dit en son cœur: « Les jours où je ferai le deuil de mon père approchent; alors je tuerai Jacob, mon frère. »
Ndipo Esau anamusungira chiwembu Yakobo chifukwa cha madalitso amene abambo ake anamupatsa. Esau anati kwa iye yekha, “Masiku olira abambo anga ayandikira; pambuyo pake ndidzamupha mʼbale wangayu Yakobo.”
42 On rapporta à Rebecca les paroles d’Esaü, son fils aîné. Elle fit appeler Jacob, son fils cadet, et lui dit: « Voici qu’Esaü, ton frère, veut se venger de toi en te tuant.
Pamene Rebeka anamva zimene mwana wake wamkulu Esau ankaganiza, anayitanitsa Yakobo nati kwa iye, “Mʼbale wako Esau akulingalira zakuti akuphe kuti akulipsire.
43 Maintenant donc, mon fils, écoute ma voix: lève-toi, fuis vers Laban, mon frère, à Haran;
Tsopano mwana wanga, chita zimene ndinene: Nyamuka tsopano, uthawire kwa mlongo wanga Labani ku Harani.
44 et tu resteras quelque temps auprès de lui, jusqu’à ce que la fureur de ton frère soit apaisée,
Ukakhale naye kwa kanthawi mpaka mkwiyo wa mʼbale wako utatsika.
45 jusqu’à ce que la colère de ton frère se soit détournée de toi, et qu’il ait oublié ce que tu lui as fait; alors je t’enverrai chercher de là. Pourquoi serais-je privée de vous deux en un même jour? »
Tsono mkwiyo wa mʼbale wakoyo ukadzatsika ndi kuyiwala zonse wamuchitirazi, ndidzatuma munthu kuti adzakutenge. Nanga nditayirenji nonse awiri nthawi imodzi?”
46 Rebecca dit à Isaac: « Je suis dégoûtée de la vie, à cause des filles de Heth. Si Jacob prend une femme, comme celles-là, parmi les filles de Heth, parmi les filles de ce pays, à quoi me sert la vie? »
Tsono Rebeka anati kwa Isake, “Ine sindikukondwera nawo anamwali a Chihiti. Ndipo ngati Yakobo angapeze mbeta kuno mwa anamwali a Chihitiwa, ndiye kuli bwino kungofa.”