< Ézéchiel 36 >
1 « Et toi, fils de l’homme, prophétise aux montagnes d’Israël et dis: Montagnes d’Israël, écoutez la parole de Yahweh:
“Iwe mwana wa munthu, yankhula kwa mapiri a Israeli ndipo unene kuti, ‘Inu mapiri a Israeli, imvani mawu a Yehova.’
2 Ainsi parle le Seigneur Yahweh: Parce que l’ennemi a dit de vous: « Ha! Ha! les hauteurs éternelles sont devenues notre propriété! »
Ine Ambuye Yehova ndikuti: Mdani wanu ankanena kuti, ‘Aa! Dziko lamapiri lakalekale lija lasanduka lathu.’
3 à cause de cela prophétise et dis: Ainsi parle le Seigneur Yahweh: Attendu qu’on vous a dévastées et foulées aux pieds de toutes parts, pour que vous fussiez une propriété pour ce qui reste des nations, et attendu que vous avez été l’objet des discours des langues méchantes et des malins propos des gens,
Choncho nenera ndipo uwawuze kuti, ‘Ine Ambuye Yehova ndikuti: Popeza anakusakazani ndi kukuponderezani ku mbali zonse motero kuti munakhala mʼmanja mwa anthu a mitundu ina yonse ndipo anthu ankakunenani ndi kukunyozani,
4 à cause de cela, montagnes d’Israël, écoutez la parole du Seigneur Yahweh: Ainsi parle le Seigneur Yahweh aux montagnes et aux collines, aux ravins et aux vallons, aux ruines désolées et aux villes abandonnées, qui ont été livrées au pillage et à la risée de ce qui reste des nations d’alentour;
choncho, inu mapiri a Israeli, imvani zimene Ine Ambuye Yehova ndikuwuza mapiri ndi magomo, zigwembe ndi zigwa, mabwinja ndi mizinda yosiyidwa imene yakhala ikufunkhidwa komanso kunyozedwa ndi anthu a mitundu ina okuzungulirani.
5 à cause de cela, ainsi parle le Seigneur Yahweh: Oui, dans le feu de ma jalousie, j’ai parlé contre ce qui reste des nations, et contre toute l’Idumée, qui se sont adjugé en possession mon pays, dans la joie de tout leur cœur, et dans le mépris de leur âme, pour le mettre au pillage;
Tsono Ine Ambuye Yehova ndikuti: Mu mkwiyo wanga woopsa ndinayankhula kuyimba mlandu mitundu ina yonse ya anthu makamaka a ku Edomu. Iwowa mwa chimwemwe chodzaza tsaya ndi mwa nkhwidzi analanda dziko langa ndi kulisandutsa lawo ndi kutengeratu dziko la msipu kukhala lawo.’
6 à cause de cela, prophétise touchant la terre d’Israël, et dis aux montagnes et aux collines, aux ravins et aux vallons: Ainsi parle le Seigneur Yahweh: Voici que j’ai parlé dans ma jalousie et dans ma fureur, parce que vous avez porté l’opprobre des nations.
Nʼchifukwa chake, lengeza ku dziko la Israeli, ndipo uwuze mapiri ndi magomo, zigwembe ndi zigwa kuti, ‘Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ine ndikuyankhula ndi mtima wokwiya kwambiri chifukwa inu munalandira chitonzo cha anthu a mitundu ina.’
7 C’est pourquoi ainsi parle le Seigneur Yahweh: Moi, j’ai levé ma main! Les nations qui vous entourent porteront, elles aussi, leur opprobre.
Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ndikulumbira nditakweza dzanja langa kuti mitundu ya anthu idzatozedwanso.
8 Et vous, montagnes d’Israël, vous pousserez vos rameaux, et vous porterez votre fruit, pour mon peuple d’Israël; car ils sont près de venir.
“Koma Inu mapiri a Israeli mudzaphukanso nthambi ndipo mudzawabalira zipatso anthu anga a Israeli, pakuti ali pafupi kubwerera kwawo.
9 Car voici que je viens à vous; et je tourne ma face vers vous; et vous serez cultivées et ensemencées.
Taonani, Ine ndili mbali yanu ndipo ndidzakukomerani mtima. Mudzalimidwa ndi kudzalidwa.
10 Je multiplierai sur vous les hommes, la maison d’Israël tout entière; les villes seront habitées, et les ruines seront rebâties.
Ndidzachulukitsa chiwerengero cha anthu anu, nyumba yonse ya Israeli. Mʼmizinda mudzakhalanso anthu ndipo mabwinja adzamangidwanso.
11 Je multiplierai sur vous hommes et bestiaux; ils seront nombreux et se multiplieront; je vous rendrai habitées comme autrefois; je vous ferai plus de bien que dans votre commencement, et vous saurez que je suis Yahweh.
Ndidzachulukitsa chiwerengero cha amuna pamodzi ndi ziweto zomwe, ndipo adzachuluka kwambiri ndi kubereka ana ambiri. Ndidzakhazika anthu mʼdzikomo monga analili kale, ndi kukulemeretsani kuposa kale. Pamenepo inu mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.
12 J’amènerai sur vous des hommes, mon peuple d’Israël, et ils te posséderont; tu seras leur héritage, et tu ne les priveras plus de leurs enfants.
Ndidzachititsa anthu kuyenda pa inu, ndiye kuti inu anthu anga Aisraeli. Iwowo adzakhazikika pa inu, ndipo inu mudzakhala cholowa chawo. Simudzalandanso ana awo.
13 Ainsi parle le Seigneur Yahweh: Parce qu’ils vous disent: Tu as dévoré des hommes, et tu as privé ta nation de ses enfants,
“Ine Ambuye Yehova ndikuti: Popeza anthu amanena kuti, ndiwe dziko limene limadya anthu ake ‘kulanda ana a mtundu wake,’
14 à cause de cela, tu ne dévoreras plus d’hommes, et tu ne priveras plus ta nation de ses enfants, — oracle du Seigneur Yahweh.
nʼchifukwa chake, simudzadyanso anthu kapena kulanda ana a mtundu wako. Ine Ambuye Yehova ndikutero.
15 Je ne te ferai plus entendre les outrages des nations, tu ne porteras plus l’opprobre des peuples, et tu ne feras plus broncher ta nation, — oracle du Seigneur Yahweh. »
Sindidzakulolaninso kumva mnyozo wa anthu a mitundu ina, kapena kupirira kunyogodola kwawo kapenanso kupunthwitsanso anthu a mʼdziko lako. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.”
16 La parole de Yahweh me fut adressée en ces termes:
Yehova anandiyankhulanso kuti:
17 « Fils de l’homme, ceux de la maison d’Israël, quand ils habitaient sur leur terre, l’ont souillée par leur conduite et par leurs œuvres; leur conduite était devant moi comme la souillure d’une femme.
“Iwe mwana wa munthu, pamene anthu a Israeli ankakhala mʼdziko lawolawo, analiyipitsa ndi makhalidwe awo ndiponso zochita zawo. Machitidwe awo pamaso panga anali onyansa pa zachipembedzo ngati msambo wa mkazi amene ali pa nthawi yake.
18 Et j’ai versé sur eux mon courroux, à cause du sang qu’ils ont versé sur le pays, et parce qu’ils l’ont souillé par leurs infâmes idoles.
Tsono ndinawalanga chifukwa cha magazi amene anakhetsa mʼdzikomo, ndiponso chifukwa anayipitsa dziko ndi mafano awo.
19 Je les ai dispersés parmi les nations, et ils ont été disséminés dans les pays; je les ai jugés selon leur conduite et selon leurs œuvres.
Ndinawamwaza pakati pa anthu a mitundu ina ndipo anabalalikira mʼmayiko onse. Ndinawalanga molingana ndi makhalidwe awo ndi zochita zawo.
20 Arrivés chez les nations où ils sont allés, ils ont déshonoré mon saint nom, quand on disait d’eux: « C’est le peuple de Yahweh, c’est de son pays qu’ils sont sortis. »
Atafika kwa anthu a mitundu ina, kulikonse kumene anapitako, anayipitsa dzina langa loyera. Zinatero popeza anthu ponena za iwo ankanena kuti, ‘Awa ndi anthu a Yehova, komatu anachotsedwa ku dziko lake.’
21 Et j’ai eu pitié de mon saint nom, que ceux de la maison d’Israël ont déshonoré parmi les nations chez lesquelles ils sont allés.
Koma Ine ndinkadera nkhawa dzina langa loyera, limene Aisraeli analiyipitsa pakati pa anthu a mitundu ina kumene anapitako.
22 C’est pourquoi dis à la maison d’Israël: Ainsi parle le Seigneur Yahweh: Ce n’est pas à cause de vous que je le fais, maison d’Israël; c’est pour mon saint nom que vous avez déshonoré, parmi les nations chez lesquelles vous êtes allés.
“Nʼchifukwa chake awuze Aisraeliwo kuti Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ine ndidzachita zimene ndidzachitezo osati chifukwa cha inuyo Aisraelinu ayi, koma chifukwa cha dzina langa, limene mwaliyipitsa pakati pa anthu a mitundu ina kumene munapitako.
23 Je sanctifierai mon grand nom qui est déshonoré, parmi les nations au milieu desquelles vous l’avez déshonoré, et les nations sauront que je suis le Seigneur Yahweh, — oracle du Seigneur Yahweh, quand je me sanctifierai en vous, à leurs yeux.
Ndidzaonetsa chiyero cha dzina langa lotchuka, limene layipitsidwa pakati pawo. Anthu a mitundu inayo atadzazindikira kuti ndaonetsa kudzera mwa inu kuti dzina langa ndi loyera, iwo adzadziwanso kuti Ine ndine Yehova. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.
24 Je vous tirerai d’entre les nations, je vous rassemblerai de tous les pays, et je vous ramènerai sur votre terre.
“Pakuti Ine ndidzakuchotsani pakati pa anthu a mitundu ina. Ndidzakusonkhanitsani kuchoka ku mayiko onse ndi kukubwezerani ku dziko lanulanu.
25 Je ferai sur vous une aspersion d’eaux pures, et vous serez purs; de toutes vos souillures et de toutes vos abominations je vous purifierai.
Ndidzakuwazani madzi oyera, ndipo mudzakhala oyera mtima. Zonse zimene zimakuyipitsani zidzachoka. Ndidzakuyeretsani pochotsa mafano anu onse.
26 Et je vous donnerai un cœur nouveau, et je mettrai au dedans de vous un esprit nouveau; j’ôterai de votre chair le cœur de pierre; et je vous donnerai un cœur de chair.
Ndidzakupatsani mtima watsopano ndi kulowetsa mzimu watsopano mwa inu. Ndidzachotsa mwa inu mtima wanu wowuma ngati mwala ndi kukupatsani mtima wofewa ngati mnofu.
27 Je mettrai au dedans de vous mon Esprit, et je ferai que vous suivrez mes ordonnances, que vous observerez mes lois et les pratiquerez.
Ndipo ndidzayika Mzimu wanga mwa inu ndipo ndidzakuthandizani kutsatira malangizo anga ndi kukusungitsani mosamala kwambiri malamulo anga.
28 Vous habiterez le pays que j’ai donné à vos pères, vous serez mon peuple, et moi, je serai votre Dieu.
Mudzakhala mʼdziko limene ndinapatsa makolo anu. Mudzakhala anthu anga, ndipo Ine ndidzakhala Mulungu wanu.
29 Je vous sauverai de toutes vos souillures; j’appellerai le froment et le ferai abonder, et je n’enverrai plus sur vous la famine.
Ndidzakupulumutsani ku zonse zokuyipitsani. Ndidzakuchulukitsirani tirigu ndipo sindidzakugwetseraninso njala.
30 Je multiplierai les fruits des arbres, et le produit des champs, afin que vous ne portiez plus l’opprobre et la famine parmi les nations.
Ndidzachulukitsa zipatso za mʼmitengo yanu ndi zokolola za mʼmunda mwanu, kotero kuti simudzanyozedwanso pakati pa anthu a mitundu ina chifukwa cha njala.
31 Vous vous rappellerez vos voies mauvaises et vos œuvres qui n’étaient pas bonnes, et vous vous prendrez en dégoût, à cause de vos iniquités et de vos abominations.
Pamenepo mudzakumbukira makhalidwe anu oyipa ndi ntchito zanu zoyipa. Machimo anu ndi ntchito zanu zonyansa zidzakuchititsa nokha manyazi.
32 Ce n’est pas à cause de vous que je le fais, — oracle du Seigneur Yahweh, — sachez-le; ayez honte et rougissez de votre conduite, maison d’Israël.
Tsono dziwani kuti Ine sindidzachita zimenezi chifukwa cha inuyo ayi, ndikutero Ine Ambuye Wamphamvuzonse. Ndiyetu chitani manyazi ndipo mugwetse nkhope zanu, inu Aisraeli chifukwa cha makhalidwe anu!
33 Ainsi parle le Seigneur Yahweh: Le jour où je vous purifierai de toutes vos iniquités, je rendrai aux villes leurs habitants, et ce qui est en ruine sera rebâti.
“Ine Ambuye Yehova ndikuti: Pa tsiku limene ndidzayeretse machimo anu onse, ndidzayikamonso anthu mʼmizinda yanu, ndipo ndidzamanganso nyumba pa mabwinja.
34 La terre dévastée sera cultivée, elle qui n’était que désolation aux yeux de tous les passants.
Dziko limene linasanduka chipululu lizidzalimidwanso. Mʼmalo moti aliyense wopitamo alione dzikolo ngati chipululu tsopano adzaliona lolimidwa.
35 On dira: Cette terre, qui était dévastée, est devenue comme un jardin d’Eden, et les villes ruinées, désolées et renversées, sont habitées comme des places fortes.
Iwo adzati, ‘Dziko ili, limene linali chipululu, lasanduka munda wa Edeni. Mizinda imene inali mabwinja osiyidwa ndi owonongedwa, tsopano ndi yotetezedwa ndi yokhalamo anthu.
36 Et les nations qui seront restées autour de vous sauront que moi, Yahweh, j’ai rebâti ce qui était renversé, planté ce qui était ravagé. Moi, Yahweh, je dis et je fais!
Ndipo anthu a mitundu ina okhala pafupi nanu amene anatsala adzadziwa kuti Ine Yehova ndine amene ndinamanganso mizinda yowonongeka ndi kudzalanso zinthu zatsopano mʼmalo mʼmene munali chipululu. Ine Yehova ndayankhula ndipo ndidzazichitadi.’
37 Ainsi parle le Seigneur Yahweh: Encore en ceci je me laisserai chercher par la maison d’Israël, pour le faire en leur faveur: je multiplierai les hommes comme des troupeaux.
“Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ndidzalolanso Aisraeli kuti andipemphe zoti ndiwachitire: Ndidzachulukitsa anthu awo ngati nkhosa.
38 Tels que les troupeaux de brebis saintes, tels que les troupeaux de Jérusalem dans ses solennités, ainsi des troupeaux d’hommes rempliront les villes dévastées; et l’on saura que je suis Yahweh. »
Adzachulukadi ngati nkhosa zomwe ankapereka ngati nsembe ku Yerusalemu pa nthawi za chikondwerero. Choncho mizinda ya mabwinja idzadzaza ndi anthu. Zikadzatero adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.”