< Amos 8 >

1 Ainsi me fit voir le Seigneur Yahweh, et voici une corbeille de fruits mûrs.
Zimene Ambuye Yehova anandionetsa ndi izi: dengu la zipatso zakupsa.
2 Et il dit: « Que vois-tu, Amos? » Je répondis: « Une corbeille de fruits mûrs. » Et Yahweh me dit: « La fin est venue pour mon peuple d’Israël; je ne lui pardonnerai pas plus longtemps.
Iye anandifunsa kuti, “Amosi nʼchiyani ukuona?” Ine ndinayankha kuti, “Dengu la zipatso zakupsa.” Ndipo Yehova anati kwa ine, “Nthawi yachimaliziro yawakwanira anthu anga Aisraeli; sindidzawakhululukiranso.
3 Les chants du palais seront des hurlements en ce jour-là, — oracle du Seigneur Yahweh. Il y aura de nombreux cadavres, en tout lieu on les jette en silence. »
“Tsiku limenelo,” Ambuye Yehova akulengeza kuti, “Nyimbo za mʼNyumba ya Mulungu zidzasanduka kulira kofuwula. Mitembo ya anthu idzachuluka, ndipo adzayiponya ponseponse! Kudzangoti zii!”
4 Écoutez ceci, vous qui engloutissez le pauvre, et qui voudriez faire disparaître les humbles du pays,
Imvani izi, inu amene mumapondereza anthu osowa ndipo simulabadira anthu osauka a mʼdzikomu.
5 en disant: « Quand la nouvelle lune sera-t-elle passée, afin que nous puissions vendre du froment, et le sabbat, pour que nous ouvrions nos magasins à blé, en diminuant l’épha et en grossissant le sicle, en faussant la balance pour tromper?
Mumanena kuti, “Kodi chikondwerero cha mwezi watsopano chidzatha liti kuti tigulitse zinthu? Ndipo tsiku la Sabata litha liti kuti tigulitse tirigu, kuti tichepetse miyeso, kukweza mitengo kuti tibere anthu ndi miyeso ya chinyengo,
6 Nous achèterons pour de l’argent les misérables, et les pauvres à cause d’une paire de sandales, et nous vendrons la criblure du froment? »
tigule osauka ndi ndalama zasiliva ndi osowa powapatsa nsapato, tigulitse ngakhale mungu wa tirigu?”
7 Yahweh l’a juré par l’orgueil de Jacob: Je n’oublierai pas jusqu’à la fin toutes leurs actions.
Yehova amene Yakobo amamunyadira, walumbira kuti: Ine sindidzayiwala chilichonse chimene anachita.
8 A cause de cela, la terre ne tremblera-t-elle pas, et tous ses habitants ne seront-ils pas dans le deuil? Elle montera tout entière comme le Nil, elle se soulèvera et s’affaissera, comme le Nil d’Égypte.
“Kodi dziko silidzagwedezeka chifukwa cha zimenezi, ndi onse okhala mʼmenemo kulira mwachisoni? Dziko lonse lidzavunduka ngati mtsinje wa Nailo; lidzagwedezeka kenaka nʼkukhala bata ngati mtsinje wa ku Igupto.
9 Il arrivera en ce jour-là, — oracle du Seigneur Yahweh, je ferai coucher le soleil en plein midi, et j’envelopperai la terre de ténèbres en un jour serein.
“Tsiku limenelo,” Ambuye Yehova akunena kuti, “Ndidzadetsa dzuwa masana ndi kugwetsa mdima pa dziko lapansi dzuwa likuswa mtengo.
10 Je changerai vos fêtes en deuil, et tous vos chants de joie en lamentations; je mettrai le sac sur tous les reins, et je rendrai chauve toute tête; je mettrai le pays comme en un deuil de fils unique, et sa fin sera comme un jour amer.
Maphwando anu achipembedzo ndidzawasandutsa kulira kwa chisoni ndipo kuyimba kwanu konse ndidzakusandutsa maliro. Ndidzakuvekani chiguduli nonsenu ndi kumeta mipala mitu yanu. Nthawi imeneyo idzakhala ngati yolira mwana wamwamuna mmodzi yekhayo, ndipo tsikulo lidzakhala lowawa mpaka kutha kwake.
11 Voici que des jours viennent, — oracle du Seigneur Yahweh, et j’enverrai une faim sur la terre, non une faim de pain, et non une soif d’eau, mais d’entendre les paroles de Yahweh.
“Nthawi ikubwera,” Ambuye Yehova akunena kuti, “Ndidzagwetsa njala mʼdziko lonse; osati njala ya chakudya kapena ludzu la madzi, koma njala yofuna kumva mawu a Yehova.
12 Et ils erreront d’une mer à l’autre, et du septentrion à l’orient; ils iront de côté et d’autre pour chercher la parole de Yahweh, et ils ne la trouveront pas.
Anthu azidzangoyendayenda kuchoka ku nyanja ina kupita ku nyanja ina. Azidzangoyendayenda kuchoka kumpoto kupita kummawa, kufunafuna mawu a Yehova, koma sadzawapeza.
13 En ces jours-là seront épuisés les belles vierges et les jeunes hommes, par la soif.
“Tsiku limenelo “anamwali okongola ndi anyamata amphamvu adzakomoka ndi ludzu.
14 Ceux qui jurent par le péché de Samarie et disent: « Par la vie de ton Dieu, ô Dan! Par la voie de Bersabée! » tomberont et ne se relèveront pas.
Onse amene amalumbira pa tchimo la Samariya, kapena kumanena kuti, ‘Iwe Dani, pali mulungu wako wamoyo,’ kapena, ‘Pali mulungu wamoyo wa ku Beeriseba.’ Iwowo adzagwa ndipo sadzadzukanso.”

< Amos 8 >