< Amos 1 >
1 Paroles d’Amos, qui fut parmi les bergers de Thécué. Ce qu’il a vu au sujet d’Israël, dans les jours d’Ozias, roi de Juda, et dans les jours de Jéroboam, fils de Joas, roi d’Israël, deux ans avant le tremblement de terre.
Mawu a Amosi, mmodzi mwa anthu oweta nkhosa ku Tekowa. Zimene iye anaona mʼmasomphenya zokhudza Israeli patatsala zaka ziwiri kuti chivomerezi chichitike, nthawi imene Uziya anali mfumu ya Yuda ndipo Yeroboamu mwana wa Yowasi anali mfumu ya Israeli.
2 Il dit: Yahweh rugira de Sion; de Jérusalem il fera entendre sa voix; les pâturages des bergers seront en deuil, et le sommet du Carmel sera desséché.
Amosi anati: “Yehova akubangula mu Ziyoni ndipo akumveka ngati bingu mu Yerusalemu; msipu wa abusa ukulira, ndipo pamwamba pa Karimeli pakuwuma.”
3 Ainsi parle Yahweh: A cause de trois crimes de Damas, et à cause de quatre, — je ne le révoquerai point. Parce qu’ils ont broyé Galaad avec des traîneaux de fer,
Yehova akuti, “Chifukwa anthu a ku Damasiko akunka nachimwirachimwira, Ine sindileka kuwalanga. Popeza anapuntha Giliyadi ndi zopunthira za mano achitsulo,
4 j’enverrai le feu dans la maison d’Hazaël, et il dévorera les palais de Ben-Hadad;
Ine ndidzatumiza moto pa nyumba ya Hazaeli umene udzanyeketsa nyumba zaufumu za Beni-Hadadi.
5 je briserai le verrou de Damas, j’exterminerai de Biqath-Aven l’habitant, et de Beth-Eden, celui qui tient le sceptre; et le peuple de Syrie ira captif à Qir, dit Yahweh.
Ndidzathyola chipata cha Damasiko; ndidzawononga mfumu yokhala ku Chigwa cha Aveni, ndiponso iye amene akugwira ndodo yaufumu mu Beti-Edeni. Anthu a ku Aramu adzapita ku ukapolo ku Kiri,” akutero Yehova.
6 Ainsi parle Yahweh: A cause de trois crimes de Gaza, et à cause de quatre, — je ne le révoquerai point. Parce qu’ils ont déporté des convois entiers de captifs, pour les livrer à Edom,
Yehova akuti, “Chifukwa anthu a ku Gaza akunka nachimwirachimwira, Ine sindileka kuwalanga. Popeza anatenga ukapolo mtundu wathunthu ndi kuwugulitsa ku Edomu,
7 j’enverrai le feu dans les murs de Gaza, et il dévorera ses palais;
ndidzatumiza moto pa makoma a Gaza umene udzanyeketsa nyumba zake zaufumu.
8 j’exterminerai d’Azot l’habitant, et d’Ascalon celui qui tient le sceptre, et je tournerai ma main sur Accaron; et le reste des Philistins périra, dit le Seigneur Yahweh.
Ndidzawononga mfumu ya ku Asidodi komanso amene akugwira ndodo yaufumu ku Asikeloni. Ndidzalanga Ekroni, mpaka wotsala mwa Afilisti atafa,” akutero Ambuye Yehova.
9 Ainsi parle Yahweh: A cause de trois crimes de Tyr, et à cause de quatre, — je ne le révoquerai point. Parce qu’ils ont livré des convois entiers de captifs à Edom, et ne se sont pas souvenus de l’alliance fraternelle,
Yehova akuti, “Chifukwa anthu a ku Turo akunka nachimwirachimwira, Ine sindileka kuwalanga. Popeza iwo anagulitsa mtundu wathunthu ku ukapolo ku Edomu, osasunga pangano laubale lija,
10 j’enverrai le feu sur le mur de Tyr, et il dévorera ses palais.
Ine ndidzatumiza moto pa makoma a Turo umene udzanyeketsa nyumba zake zaufumu.”
11 Ainsi parle Yahweh: A cause de trois crimes d’Edom, et à cause de quatre, — je ne le révoquerai point. Parce qu’il a poursuivi son frère avec le glaive, et qu’il a étouffé sa compassion, et parce que sa colère déchire à jamais, et qu’il garde jusqu’à la fin sa rancune,
Yehova akuti, “Chifukwa anthu a ku Edomu akunka nachimwirachimwira, Ine sindileka kuwalanga. Popeza anathamangitsa mʼbale wake ndi lupanga, popanda nʼchifundo chomwe. Popeza mkwiyo wake unakulabe ndipo ukali wake sunatonthozeke,
12 j’enverrai le feu dans Théman, et il dévorera les palais de Bosra.
Ine ndidzatumiza moto pa Temani umene udzanyeketsa nyumba zaufumu za Bozira.”
13 Ainsi parle Yahweh: A cause de trois crimes des enfants d’Ammon, et à cause de quatre, — je ne le révoquerai point. Parce qu’ils ont fendu le ventre des femmes enceintes de Galaad, afin d’élargir leur frontière,
Yehova akuti, “Chifukwa anthu a ku Amoni akunka nachimwirachimwira, Ine sindileka kuwalanga. Popeza anatumbula akazi oyembekezera a ku Giliyadi nʼcholinga choti akuze malire awo,
14 j’allumerai un feu sur le mur de Rabbah, et il dévorera ses palais, au milieu des cris de guerre d’un jour de bataille, au milieu du tourbillon d’un jour de tempête.
Ine ndidzayatsa moto pa makoma a ku Raba umene udzanyeketsa nyumba zake zaufumu. Padzakhala kulira kwakukulu pa tsiku la nkhondoyo, kumenyana kudzakhala kwafumbi ngati mkuntho wa kamvuluvulu.
15 Et leur roi s’en ira en captivité, lui et ses princes avec lui, dit Yahweh.
Mfumu yawo idzatengedwa kupita ku ukapolo, iyo pamodzi ndi akuluakulu ake,” akutero Yehova.