< 2 Samuel 1 >

1 Après la mort de Saül, David était revenu de battre les Amalécites, et David demeurait depuis deux jours à Siceleg.
Atamwalira Sauli, Davide anabwerako kumene anakagonjetsa Aamaleki ndipo anakakhala ku Zikilagi masiku awiri.
2 Le troisième jour, voici qu’un homme arriva du camp, d’auprès de Saül, les vêtements déchirés et de la terre sur la tête. Lorsqu’il arriva près de David, il se jeta par terre et se prosterna.
Pa tsiku lachitatu munthu wina wochokera ku msasa wa Sauli anafika, zovala zake zitangʼambika ndiponso anali atathira dothi pamutu pake. Atafika kwa Davide, anadzigwetsa pansi, kupereka ulemu kwa Davideyo.
3 David lui dit: « D’où viens-tu? » Et il lui répondit: « Je me suis sauvé du camp d’Israël. »
Davide anamufunsa iye kuti, “Kodi iwe wachokera kuti?” Iye anayankha kuti, “Ine ndathawa ku misasa ya Aisraeli.”
4 David lui dit: « Qu’est-il arrivé? Raconte-le-moi donc. » Il dit: « Le peuple s’est enfui de la bataille, et un grand nombre parmi le peuple sont tombés et ont péri; Saül même et son fils Jonathas sont morts. »
Davide anafunsa, “Tandiwuza, chachitika ndi chiyani?” Iye anati, “Anthu athawa ku nkhondo ndipo ambiri aphedwa. Sauli ndi mwana wake Yonatani aphedwa.”
5 David dit au jeune homme qui lui apportait ces nouvelles: « Comment sais-tu que Saül et son fils Jonathas sont morts? »
Ndipo Davide anati kwa mnyamata amene anabweretsa nkhaniyi, “Ukudziwa bwanji kuti Sauli ndi mwana wake Yonatani afa?”
6 Et le jeune homme qui lui apportait la nouvelle répondit: « Je me trouvais par hasard sur la montagne de Gelboé; et voici que Saül s’appuyait sur sa lance, et voici que les chars et les cavaliers étaient près de l’atteindre.
Mnyamatayo anati, “Zinangochitika kuti ndinali pa phiri la Gilibowa, ndipo Sauli anali komweko ataweramira pa mkondo wake, pamodzi ndi magaleta ndi okwera ake atamuyandikira.
7 Il se retourna et, m’ayant aperçu, il m’appela, et je dis: « Me voici. »
Pamene anatembenuka ndi kundiona ine, iye anandiyitana, ndipo ndinati, ‘Kodi ndichite chiyani?’”
8 Et il me dit: « Qui es-tu? » Je lui répondis: « Je suis un Amalécite. »
Iye anandifunsa, “Iwe ndiwe yani?” Ine ndinayankha kuti, “Ndine Mwamaleki.”
9 Et il me dit: « Approche-toi donc de moi et donne-moi la mort; car je suis pris de vertige, et ma vie est encore tout entière en moi. »
“Kenaka iye anati kwa ine, ‘Bwera pafupi ndipo undiphe! Ndikumva ululu kwambiri, koma ndikanali ndi moyo!’
10 Je m’approchai de lui et je lui donnai la mort, car je savais bien qu’il ne survivrait pas à sa défaite. J’ai pris le diadème qui était sur sa tête et le bracelet qu’il avait au bras, et je les apporte ici à mon seigneur. »
“Kotero ndinabwera pafupi ndi kumupha, chifukwa ndinadziwa kuti mmene anagweramo sakanakhalanso ndi moyo. Ndipo ndatenga chipewa chaufumu chimene chinali pamutu pake ndi khoza la pa dzanja lake ndipo ndazibweretsa kwa inu mbuye wanga.”
11 David saisit ses vêtements et les déchira, et tous les hommes qui étaient auprès de lui firent de même.
Apo Davide ndi anthu onse amene anali nawo anangʼamba zovala zawo.
12 Ils célébrèrent leur deuil, pleurant et jeûnant jusqu’au soir, sur Saül, sur son fils Jonathas, sur le peuple de Yahweh et sur la maison d’Israël, parce qu’ils étaient tombés par l’épée.
Iwo analira maliro ndi kusala zakudya mpaka madzulo chifukwa cha Sauli ndi mwana wake Yonatani, komanso chifukwa cha gulu la ankhondo la Yehova ndi nyumba ya Israeli, chifukwa anaphedwa ndi lupanga.
13 David dit au jeune homme qui lui avait apporté la nouvelle: « D’où es-tu? » Il répondit: « Je suis fils d’un étranger, d’un Amalécite. »
Davide anati kwa mnyamata amene anabweretsa uthengawo, “Iwe umachokera kuti?” Iye anayankha kuti, “Ine ndine mwana wa mlendo Mwamaleki.”
14 David lui dit: « Comment n’as-tu pas craint d’étendre ta main pour donner la mort à l’oint de Yahweh? »
Davide anamufunsanso kuti, “Nʼchifukwa chiyani sunaope kukweza dzanja lako ndi kupha wodzozedwa wa Yehova?”
15 Et David, appelant un des jeunes gens, dit: « Approche et tue-le. » Cet homme frappa l’Amalécite, et il mourut.
Kenaka Davide anayitana mmodzi mwa anyamata ake ndipo anati, “Pita ukamukanthe!” Kotero iye anapita kukamukantha, ndipo mnyamata uja anafa.
16 Et David lui dit: « Que ton sang soit sur ta tête! Car ta bouche a déposé contre toi quand tu as dit: C’est moi qui ai donné la mort à l’oint de Yahweh. »
Pakuti Davide anali atanena kwa iye kuti, “Iwe wadzipha wekha. Pakamwa pako pakunena zokutsutsa wekha, pamene unanena kuti, ‘Ine ndapha wodzozedwa wa Yehova.’”
17 David entonna ce chant funèbre sur Saül et sur Jonathas, son fils,
Davide anayimba nyimbo iyi ya maliro, kulira Sauli ndi mwana wake Yonatani.
18 et il ordonna de l’enseigner aux enfants de Juda; c’est le chant de l’Arc. Voici qu’il est écrit dans le Livre du Juste:
Ndipo analamula kuti anthu a ku Yuda aphunzitsidwe nyimbo ya maliroyi imene yalembedwa mʼbuku la Yasari:
19 La splendeur d’Israël a-t-elle péri sur tes hauteurs? Comment sont tombés les héros?
“Ulemerero wako iwe Israeli, wagona utaphedwa ku zitunda. Taonani amphamvu agwa kumeneko!
20 Ne l’annoncez pas à Geth, ne le publiez pas dans les rues d’Ascalon, de peur que les filles des Philistins ne s’en réjouissent, de peur que les filles des incirconcis ne sautent de joie!
“Musakanene zimenezi ku Gati, musazilengeze ku misewu ya ku Asikeloni, kuti ana aakazi a Afilisti angasangalale, ana aakazi a osachita mdulidwe angakondwere.
21 Montagnes de Gelboé, qu’il n’y ait sur vous ni rosée ni pluie, ni champs de prémices! Car là fut jeté bas le bouclier des héros. Le bouclier de Saül n’était pas oint d’huile,
“Inu mapiri a ku Gilibowa, musakhalenso ndi mame kapena mvula, kapena minda yobereka zopereka za ufa. Pakuti kumeneko chishango cha munthu wamphamvu chinadetsedwa, chishango cha Sauli sanachipakenso mafuta.
22 mais du sang des blessés, de la graisse des vaillants; l’arc de Jonathas ne recula jamais en arrière, et l’épée de Saül ne revenait pas inactive.
“Pa magazi a ophedwa, pa mnofu wa amphamvu, uta wa Yonatani sunabwerere, lupanga la Sauli silinabwere chabe.
23 Saül et Jonathas, chéris et aimables dans la vie et dans la mort, ils ne furent pas séparés. Ils étaient plus agiles que les aigles, ils étaient plus forts que les lions.
“Sauli ndi Yonatani, pa moyo wawo anali okondedwa ndi okoma mtima, ndipo pa imfa yawo sanasiyanitsidwe. Iwo anali ndi liwiro loposa ziwombankhanga, anali ndi mphamvu zoposa mkango.
24 Filles d’Israël, pleurez sur Saül, qui vous revêtait de pourpre au sein des délices, qui mettait des ornements d’or sur vos vêtements!
“Inu ana aakazi a Israeli, mulireni Sauli, amene anakuvekani zovala zofiira ndi zofewa, amene anakometsera zovala zanu ndi zokometsera zagolide.
25 Comment les héros sont-ils tombés dans la bataille? Jonathas a été percé sur tes hauteurs!
“Taonani amphamvu agwa ku nkhondo! Yonatani wagona ataphedwa ku zitunda.
26 L’angoisse m’accable à cause de toi, Jonathas, mon frère. Tu faisais toutes mes délices; ton amour m’était plus précieux que l’amour des femmes.
Ine ndikuvutika mumtima chifukwa cha iwe mʼbale wanga Yonatani, unali wokondedwa kwambiri kwa ine. Chikondi chako pa ine chinali chopambana, chopambana kuposa chikondi cha akazi.
27 Comment les héros sont-ils tombés? Comment les guerriers ont-ils péri?
“Taonani amphamvu agwa! Zida zankhondo zawonongeka!”

< 2 Samuel 1 >