< 1 Samuel 7 >

1 Les gens de Cariathiarim vinrent et firent monter l’arche de Yahweh; ils la conduisirent dans la maison d’Abinadab, sur la colline, et ils consacrèrent son fils Eléazar pour garder l’arche de Yahweh.
Choncho anthu a ku Kiriati-Yearimu anabwera ndi kudzatenga Bokosi la Yehova. Iwo anapita nalo ku nyumba ya Abinadabu ya ku phiri ndipo anapatula Eliezara mwana wake kuti aziyangʼanira Bokosi la Yehovalo.
2 Depuis le jour où l’arche fut déposée à Cariathiarim, il se passa un long temps, vingt années, et toute la maison d’Israël poussa des gémissements vers Yahweh.
Zaka makumi awiri zinapita kuyambira pamene Bokosi la Yehova linakhala ku Kiriati-Yearimu, ndipo anthu a Israeli onse analira kupempha Yehova kuti awathandize.
3 Et Samuel dit à toute la maison d’Israël: « Si c’est de tout votre cœur que vous revenez à Yahweh, ôtez du milieu de vous les dieux étrangers et les Astartés, attachez fermement votre cœur à Yahweh et servez-le lui seul, et il vous délivrera de la main des Philistins. »
Ndipo Samueli anati kwa nyumba yonse ya Israeli, “Ngati mukubwerera kwa Yehova ndi mtima wanu wonse, muchotse milungu yachilendo ndi Asiteroti pakati panu ndipo mitima yanu ikhazikike pa Yehova ndi kutumikira Iye yekha. Mukatero Iye adzakupulumutsani mʼmanja mwa Afilisti.”
4 Alors les enfants d’Israël ôtèrent du milieu d’eux les Baals et les Astartés, et ils servirent Yahweh seul.
Choncho Aisraeli anachotsa milungu yawo ya Baala ndi Asitoreti ndi kutumikira Yehova yekha.
5 Samuel dit: « Assemblez tout Israël à Maspha, et je prierai Yahweh pour vous. »
Kenaka Samueli anati, “Sonkhanitsani Aisraeli onse ku Mizipa ndipo ine ndidzakupemphererani kwa Yehova.”
6 Et ils s’assemblèrent à Maspha. Ils puisèrent de l’eau et la répandirent devant Yahweh, et ils jeûnèrent ce jour-là, en disant: « Nous avons péché contre Yahweh. » Et Samuel jugea les enfants d’Israël à Maspha.
Choncho anasonkhana ku Mizipa, ndipo anatunga madzi ndi kuwathira pansi pamaso pa Yehova. Pa tsiku limenelo anasala kudya namanena kuti, “Ife tachimwira Yehova.” Ndipo Samueli anali mtsogoleri wa Israeli ku Mizipa.
7 Les Philistins apprirent que les enfants d’Israël s’étaient assemblés à Maspha, et les princes des Philistins montèrent contre Israël. Les enfants d’Israël l’apprirent et eurent peur des Philistins;
Afilisti anamva kuti Aisraeli asonkhana ku Mizipa, choncho akalonga awo anabwera kudzawathira nkhondo. Ndipo Aisraeli atamva anachita mantha chifukwa cha Afilisti.
8 et les enfants d’Israël dirent à Samuel: « Ne cesse pas de crier pour nous vers Yahweh, notre Dieu, afin qu’il nous sauve de la main des Philistins. »
Choncho anati kwa Samueli, “Musasiye kutipempherera kwa Yehova Mulungu wathu, kuti atipulumutse mʼdzanja la Afilistiwa.”
9 Samuel prit un agneau de lait, et l’offrit tout entier en holocauste à Yahweh; et Samuel cria vers Yahweh pour Israël, et Yahweh l’exauça.
Ndipo Samueli anatenga mwana wankhosa wamkazi woyamwa ndi kumupereka monga nsembe yopsereza kwa Yehova. Iye anapemphera kwa Yehova mʼmalo mwa Aisraeli, ndipo Yehova anamuyankha.
10 Pendant que Samuel offrait l’holocauste, les Philistins s’approchèrent pour attaquer Israël. Mais Yahweh fit retentir en ce jour le tonnerre, avec un grand bruit, sur les Philistins, et les mit en déroute, et ils furent battus devant Israël.
Samueli akupereka nsembe yopsereza, Afilisti anayandikira kuti ayambe kuwathira nkhondo Aisraeli. Koma tsiku limenelo Yehova anawaopseza Afilisti aja ndi mawu aakulu ngati bingu. Choncho anasokonezeka motero kuti Aisraeli anawagonjetsa.
11 Les hommes d’Israël, sortant de Maspha, poursuivirent les Philistins et les battirent jusqu’au-dessous de Beth-Char.
Aisraeli anatuluka ku Mizipa kuthamangitsa Afilisti aja nʼkumawapha mʼnjira yonse mpaka kumunsi kwa Beti-Kari.
12 Samuel prit une pierre, qu’il plaça entre Maspha et Sen, et il lui donna le nom d’Eben-Ezer, en disant: « Jusqu’ici Yahweh nous a secourus. »
Kenaka Samueli anatenga mwala nawuyika pakati pa Mizipa ndi Seni. Iye anawutcha Ebenezeri, popeza anati, “Yehova watithandiza mpaka pano.”
13 Ainsi humiliés, les Philistins ne revinrent plus sur le territoire d’Israël; la main de Yahweh fut sur les Philistins pendant toute la vie de Samuel.
Kotero Afilisti anagonjetsedwa ndipo sanadzalowenso mʼdziko la Israeli. Yehova analimbana ndi Afilisti masiku onse a Samueli.
14 Les villes que les Philistins avaient prises sur Israël retournèrent à Israël, depuis Accaron jusqu’à Geth; Israël arracha leur territoire des mains des Philistins. Et il y eut paix entre Israël et les Amorrhéens.
Mizinda yonse imene Afilisti analanda kuchokera ku Ekroni mpaka ku Gati inabwezedwa kwa Aisraeli. Choncho Aisraeli anapulumutsa dziko lawo. Ndipo panalinso mtendere pakati pa Aisraeli ndi Aamori.
15 Samuel jugea Israël tout le temps de sa vie.
Samueli anatsogolera Aisraeli moyo wake wonse.
16 Chaque année il s’en allait, faisant le tour par Béthel, Galgala et Maspha, et il jugeait Israël dans tous ces lieux.
Chaka ndi chaka Samueli ankakonza ulendo wozungulira kuchokera ku Beteli mpaka ku Giligala ndi Mizipa, kuweruza milandu ya Aisraeli mʼmadera onsewa.
17 Il revenait ensuite à Rama, où était sa maison, et là il jugeait Israël; il y bâtit un autel à Yahweh.
Koma pambuyo pake ankabwerera ku Rama, kumene kunali nyumba yake. Ankaweruza Aisraeli kumeneko. Ndipo iye anamanga guwa lansembe la Yehova kumeneko.

< 1 Samuel 7 >