< 1 Rois 3 >
1 Salomon s’allia par un mariage avec Pharaon, roi d’Égypte. Il prit pour femme la fille de Pharaon, et il l’amena dans la cité de David, jusqu’à ce qu’il eût achevé de bâtir sa maison et la maison de Yahweh, ainsi que le mur d’enceinte de Jérusalem.
Solomoni anachita ubale ndi Farao mfumu ya ku Igupto ndipo anakwatira mwana wake wamkazi. Mkaziyo anabwera naye mu Mzinda wa Davide mpaka anatsiriza kumanga nyumba yaufumu ndi Nyumba ya Yehova ndiponso khoma lozungulira Yerusalemu.
2 Seulement le peuple sacrifiait sur les hauts lieux, car il n’avait pas été bâti de maison au nom de Yahweh jusqu’à ces jours.
Koma anthu ankaperekabe nsembe ku malo achipembedzo osiyanasiyana chifukwa chakuti mpaka pa nthawi imeneyo Dzina la Yehova anali asanalimangire nyumba.
3 Salomon aimait Yahweh, marchant selon les préceptes de David, son père; seulement il offrait des sacrifices sur les hauts lieux et y brûlait des parfums.
Solomoni anaonetsa chikondi chake pa Yehova poyenda motsatira malamulo a abambo ake Davide, kupatula kuti ankapereka nsembe ndi kufukiza lubani ku malo osiyanasiyana achipembedzo.
4 Le roi se rendit à Gabaon pour y sacrifier, car c’était le grand haut lieu. Salomon offrit mille holocaustes sur cet autel.
Mfumu inapita ku Gibiyoni kukapereka nsembe popeza kumeneko ndiye kunali malo oposa malo ofunika kwambiri pachipembedzo. Kumeneko Solomoni anapereka nsembe zopsereza 1,000 pa guwa lansembe.
5 A Gabaon, Yahweh apparut en songe à Salomon pendant la nuit, et Dieu lui dit: « Demande ce que tu veux que je te donne. »
Ku Gibiyoniko Yehova anaonekera kwa Solomoni mʼmaloto usiku, ndipo Mulungu anati, “Pempha chilichonse chimene ukufuna ndipo ndidzakupatsa.”
6 Salomon répondit: « Vous avez montré une grande bienveillance envers votre serviteur David, mon père, selon qu’il marchait en votre présence dans la fidélité, dans la justice et dans la droiture de cœur envers vous; vous lui avez conservé cette grande bienveillance, et vous lui avez donné un fils qui est assis sur son trône, comme il paraît aujourd’hui.
Solomoni anayankha kuti, “Inu munaonetsa kukoma mtima kwanu kwakukulu kwa kapolo wanu, abambo anga Davide, chifukwa anali wokhulupirika pamaso panu, wolungama mtima ndiponso wa mtima wangwiro. Inu mukupitirizabe kukoma mtima kwanu kwakukulu kwa iye ndipo mwamupatsa mwana kuti akhale pa mpando wake waufumu lero lino.
7 Maintenant, Yahweh, mon Dieu, vous avez fait régner votre serviteur à la place de David, mon père; et moi je ne suis qu’un tout jeune homme, ne sachant pas comment me conduire.
“Tsopano Inu Yehova Mulungu wanga, mtumiki wanune mwandiyika kukhala mfumu mʼmalo mwa abambo anga Davide. Komatu ndine mwana wamngʼono ndipo sindidziwa kagwiridwe kake ka ntchito yangayi.
8 Votre serviteur est au milieu de votre peuple que vous avez choisi, peuple immense, qui ne peut être évalué ni compté, tant il est nombreux.
Mtumiki wanu ali pakati pa anthu amene munawasankha, mtundu waukulu, anthu ochuluka kwambiri osatheka kuwawerenga.
9 Accordez donc à votre serviteur un cœur attentif pour juger votre peuple, pour discerner le bien et le mal. Car qui pourrait juger votre peuple, ce peuple si nombreux? »
Choncho mupatseni mtumiki wanu nzeru zolamulira anthu anu ndi kuti azitha kusiyanitsa pakati pa chabwino ndi choyipa. Pakuti ndani amene angathe kulamulira anthu anu ochulukawa?”
10 Le Seigneur eut pour agréable que Salomon lui eût fait cette demande,
Ambuye anakondwera kuti Solomoni anapempha zimenezi.
11 et Dieu lui dit: « Parce que tu as fait cette demande, et que tu n’as pas demandé pour toi de longs jours, et que tu n’as pas demandé pour toi des richesses, et que tu n’as pas demandé pour toi la mort de tes ennemis, mais que tu as demandé pour toi de l’intelligence pour exercer la justice,
Tsono Mulungu anati kwa Solomoni, “Popeza wapempha zinthu zimenezi osati moyo wautali kapena chuma chako kapena imfa ya adani ako koma nzeru zolamulira anthu mwachilungamo,
12 voici que je fais selon ta parole: voici que je te donne un cœur sage et intelligent, de telle sorte qu’il n’y ait eu personne avant toi qui te soit semblable, et qu’il ne s’élèvera personne après toi qui te soit semblable.
Ine ndidzakuchitira zimene wapempha. Ndidzakupatsa mtima wanzeru ndi wozindikira zinthu, kotero kuti sipanakhalepo wina wofanana nawe ndipo sipadzapezekanso wina wonga iwe pambuyo pako.
13 Et même ce que tu n’as pas demandé, je te le donne, richesses et gloire, au point que parmi les rois il n’y aura personne comme toi, pendant tous tes jours.
Kuwonjeza apo, ndidzakupatsa zimene sunazipemphe: chuma ndi ulemu, kotero kuti pa masiku onse a moyo wako sipadzakhala mfumu yofanana nawe.
14 Et si tu marches dans mes voies, en observant mes lois et mes commandements, comme a marché David, ton père, je prolongerai tes jours. »
Ndipo ngati udzayenda mʼnjira zanga ndi kumvera malamulo anga ndiponso malangizo anga monga abambo ako Davide anachitira, ndidzakupatsa moyo wautali.”
15 Salomon s’éveilla, et il comprit que c’était un songe. De retour à Jérusalem, il se tint devant l’arche de l’alliance de Yahweh; il offrit des holocaustes et des sacrifices pacifiques, et il donna un festin à tous ses serviteurs.
Kotero Solomoni anadzuka ndipo anazindikira kuti anali maloto. Iye anabwerera ku Yerusalemu nakayimirira patsogolo pa Bokosi la Chipangano la Ambuye ndipo anapereka nsembe zopsereza ndi nsembe zachiyanjano. Kenaka anakonzera phwando atumiki ake onse.
16 Alors deux femmes de mauvaise vie vinrent vers le roi et se tinrent devant lui.
Nthawi ina amayi awiri adama anabwera kwa mfumu ndipo anayima pamaso pake.
17 L’une des femmes dit: « De grâce, mon seigneur! Cette femme et moi, nous demeurions dans la même maison, et j’ai mis au monde un enfant près d’elle dans la maison.
Mmodzi mwa amayiwo anati, “Mbuye wanga, mayi uyu ndi ine timakhala nyumba imodzi. Ine ndinabala mwana tili limodzi ndi mnzangayu.
18 Trois jours après que j’avais mis au monde mon enfant, cette femme a mis aussi au monde un enfant. Nous étions ensemble; aucun étranger n’était avec nous dans la maison, il n’y avait que nous deux dans la maison.
Tsiku lachitatu ine nditabala mwana, mnzangayunso anabereka mwana wake. Tinalipo awiriwiri mʼnyumbamo ndipo munalibe wina aliyense.
19 Le fils de cette femme mourut pendant la nuit, parce qu’elle s’était couchée sur lui.
“Nthawi ya usiku mwana wa mnzangayu anafa chifukwa anamugonera.
20 Elle se leva au milieu de la nuit, elle prit mon fils à mes côtés tandis que la servante dormait, et elle le coucha dans son sein, et son fils qui était mort, elle le coucha dans mon sein.
Tsono iyeyu anadzuka pakati pa usiku, natenga mwana wanga ku mimba kwanga pamene ine mdzakazi wanu ndinali mʼtulo. Anamuyika mwanayo ku mimba kwake ndi kuyika mwana wake wakufayo ku mimba kwanga.
21 Lorsque je me suis levée le matin pour allaiter mon fils, voici qu’il était mort; mais, l’ayant considéré attentivement le matin, je m’aperçus que ce n’était pas mon fils que j’avais enfanté. »
Mmawa nditadzuka kuti ndiyamwitse mwana wanga ndinapeza kuti ndi wakufa! Koma kutacha nditamuyangʼanitsitsa ndinaona kuti si mwana amene ine ndinabala.”
22 L’autre femme dit: « Non! C’est mon fils qui est vivant, et c’est ton fils qui est mort. » Mais la première répliqua: « Nullement, c’est ton fils qui est mort, et c’est mon fils qui est vivant. » Et elles se disputaient devant le roi.
Koma mayi winayo anati, “Ayi! Mwana wamoyoyu ndi wanga, mwana wakufayu ndi wako.” Koma mayi woyambayo analimbikira kuti. “Ayi! Mwana wakufayu ndi wako; wamoyoyu ndi wanga.” Motero akaziwa anatsutsana pamaso pa mfumu.
23 Le roi dit: « L’une dit: C’est mon fils qui est vivant, et c’est ton fils qui est mort; et l’autre dit: Nullement, c’est ton fils qui est mort, et c’est mon fils qui est vivant. »
Pamenepo mfumu inati, “Wina akuti, ‘Mwana wanga ndi wamoyoyu ndipo mwana wako ndi wakufayu,’ pamene winanso akuti, ‘Ayi! Mwana wako ndi wakufayu wanga ndi wamoyoyu.’”
24 Et le roi dit: « Apportez-moi une épée. » On apporta l’épée devant le roi.
Pamenepo mfumu inati, “Patseni lupanga.” Ndipo anabwera nalo lupanga kwa mfumu.
25 Et le roi dit: « Partagez en deux l’enfant qui vit, et donnez-en la moitié à l’une et la moitié à l’autre. »
Tsono mfumu inagamula kuti, “Muduleni pakati mwana wamoyoyu ndipo wina mumupatse gawo limodzi, gawo linalo mumupatse winayo.”
26 Alors la femme dont le fils était vivant dit au roi, car elle sentait ses entrailles s’émouvoir pour son fils: « Ah! mon seigneur, donnez-lui l’enfant qui vit, et qu’on ne le tue pas! » Et l’autre disait: « Qu’il ne soit ni à moi ni à toi; partagez-le. »
Mayi amene mwana wake anali moyo anagwidwa ndi chisoni chifukwa cha mwana wakeyo ndipo anawuza mfumu kuti, “Chonde mbuye wanga, mupatseni mnzangayu mwana wamoyoyu! Musamuphe!” Koma winayo anati, “Ayi, asandipatse ine kapena iwe. Muduleni pakati!”
27 Et le roi répondit et dit: « Donnez à la première l’enfant qui vit, et qu’on ne le tue pas; c’est elle qui est sa mère. »
Choncho mfumu inagamula kuti, “Perekani mwana wamoyoyu kwa mayi woyambayu. Musamuphe, iyeyu ndiye mayi wake wa mwanayu.”
28 Tout Israël apprit le jugement que le roi avait prononcé, et l’on craignit le roi, en voyant qu’il y avait en lui une sagesse divine pour rendre la justice.
Pamene Aisraeli onse anamva za chigamulo chimene mfumu inapereka, anaopa mfumuyo kwambiri, chifukwa anaona kuti mfumu inali ndi nzeru zochokera kwa Mulungu zoweruzira mwachilungamo.