< 1 Chroniques 9 >

1 Ainsi tout Israël fut enregistré dans les généalogies, et voici qu’ils sont inscrits dans le livre des rois d’Israël; et Juda fut emmené captif à Babylone à cause de ses transgressions.
Aisraeli onse analembedwa potsata mibado yawo mʼbuku la mafumu a Aisraeli. Anthu a ku Yuda anatengedwa kunka ku ukapolo ku Babuloni chifukwa cha kusakhulupirika kwawo.
2 Les premiers habitants, qui demeuraient dans leurs possessions, dans leurs villes, furent les Israélites, les prêtres, les lévites et les Nathinéens.
Tsono anthu oyamba kukhala mʼmadera awo anali Aisraeli wamba, ansembe, Alevi ndi otumikira ku Nyumba ya Yehova.
3 A Jérusalem, habitèrent des fils de Juda, des fils de Benjamin, et des fils d’Ephraïm et de Manassé; —
Anthu a ku Yuda, Benjamini ndi Efereimu ndiponso Manase amene anakhala mu Yerusalemu anali awa:
4 des fils au Pharès, fils de Juda: Othéï, fils d’Ammiud, fils d’Amri, fils d’Omraï, fils de Bonni; —
Utai mwana wa Amihudi, mwana wa Omuri, mwana wa Imuri, mwana wa Bani, chidzukulu cha Perezi mwana wa Yuda.
5 des Silonites: Asaïa, le premier-né, et ses fils; —
A banja la Siloni: Asaya mwana wake woyamba pamodzi ndi ana ake.
6 des fils de Zara: Jéhuel; et leurs frères: six cent quatre vingt dix; —
A banja la Zera: Yeueli. Anthu ochokera ku Yuda analipo 690.
7 Des fils de Benjamin: Salo, fils de Mosollam, fils d’Oduia, fils d’Asana;
A fuko la Benjamini: Salu mwana wa Mesulamu, mwana wa Hodaviya, mwana wa Hasenuya;
8 Jobania, fils de Jéroham; Ela, fils d’Ozi, fils de Mochori; Mosollam, fils de Saphatia, fils de Rahuel, fils de Jébania;
Ibineya mwana wa Yerohamu; Ela mwana wa Uzi, mwana wa Mikiri; ndi Mesulamu mwana wa Sefatiya, mwana wa Reueli mwana wa Ibiniya.
9 et leurs frères, selon leurs générations: neuf cent cinquante-six. Tous ces hommes étaient chefs de famille selon leurs maisons patriarcales.
Anthu ochokera ku Benjamini monga analembedwera mwa mibado yawo, analipo 956. Anthu onsewa anali atsogoleri a mabanja awo.
10 Des prêtres: Jédaïa, Joïarib, Jachim,
Ansembe: Yedaya, Yehoyaribu; Yakini;
11 Azarias, fils d’Helcias, fils de Mosollam, fils de Sadoc, fils de Maraïoth, fils d’Achitob, prince de la maison de Dieu;
Azariya mwana wa Hilikiya, mwana wa Mesulamu, mwana wa Zadoki mwana wa Merayoti, mwana wa Ahitubi, wamkulu woyangʼanira Nyumba ya Mulungu;
12 Adaïas, fils de Jéroham, fils de Phassur, fils de Melchias; Maasaï, fils d’Adiel, fils de Jezra, fils de Mosollam, fils de Mosollamith, fils d’Emmer;
Adaya mwana wa Yerohamu, mwana wa Pasi-Huri, mwana wa Malikiya; ndi Maasai mwana wa Adieli, mwana wa Yahizera, mwana wa Mesulamu, mwana wa Mesilemoti, mwana wa Imeri.
13 et leurs frères, chefs de leurs maisons patriarcales: mille sept cent soixante hommes vaillants, pour l’œuvre du service de la maison de Dieu.
Ansembe amene anali atsogoleri a mabanja awo analipo 1,760. Anali anthu amphamvu ndi odziwa kutumikira mʼnyumba ya Mulungu.
14 Des lévites: Séméïa, fils de Hassub, fils d’Ezricam, fils d’Hasébia, des fils de Mérari;
Alevi: Semaya mwana wa Hasubu, mwana wa Azirikamu, mwana wa Hasabiya, wa mʼbanja la Merari;
15 Bacbacar, Hérès, Galal, Matthania, fils de Micha, fils de Zéchri, fils d’Asaph;
Bakibakara, Heresi, Galali ndi Mataniya mwana wa Mika, mwana wa Zikiri, mwana wa Asafu;
16 Obdia, fils de Séméïa, fils de Galal, fils d’Idithun; Barachia, fils d’Asa, fils d’Elcana, qui habitait dans les villages de Nétophatiens.
Obadiya mwana wa Semaya mwana wa Galali, mwana wa Yedutuni ndi Berekiya mwana wa Asa, mwana wa Elikana, amene ankakhala ku midzi ya Anetofati.
17 Et les portiers: Sellum, Accub, Telmon, Ahiman, et leurs frères; Sellum était le chef,
Alonda a pa makomo: Salumu, Akubu, Talimoni, Ahimani ndi abale awo. Mtsogoleri wawo anali Salumu.
18 et il est jusqu’à présent à la porte du roi, à l’orient. Ce sont là les portiers pour le camp des enfants de Lévi.
Amenewa amakhala pa chipata cha mfumu kummawa mpaka lero lino. Alonda a gulu la Alevi anali awa:
19 Sellum, fils de Coré, fils d’Abiasaph, fils de Coré, et ses frères de la maison de son père, les Coréïtes, remplissaient les fonctions de gardiens des portes du tabernacle; leurs pères avaient gardé l’entrée du camp de Yahweh;
Salumu mwana wa Kore, mwana wa Ebiyasafu, mwana wa Kora, pamodzi ndi abale ake a ku banja la makolo ake, Akora aja ankanyangʼanira khomo la Tenti monga ankachitira abambo awo polondera khomo la malo okhalapo Yehova.
20 Phinées, fils d’Eléazar, avait été autrefois leur chef, et Yahweh était avec lui.
Masiku oyamba Finehasi mwana wa Eliezara anali woyangʼanira alonda apakhomo ndipo Yehova anali naye.
21 Zacharie, fils de Mosollamia, était portier à l’entrée de la tente de réunion.
Zekariya mwana wa Meselemiya anali mlonda woyangʼanira pa chipata cha tenti ya msonkhano.
22 Tous ces hommes, choisis pour gardiens des portes, étaient au nombre de deux cent douze, enregistrés dans les généalogies de leurs villages; David et Samuel le voyant les avaient établis dans leurs fonctions.
Onse amene anasankhidwa kukhala alonda pa khonde analipo 212. Iwo analembedwa mwa mibado yawo ku midzi yawo. Davide ndi mneneri Samueli ndiwo anawayika mʼmalo awo antchito chifukwa cha kukhulupirika kwawo.
23 Eux et leurs enfants étaient aux portes de la maison de Yahweh, de la maison du tabernacle, pour les gardes.
Iwo ndi zidzukulu zawo anali oyangʼanira zipata za nyumba ya Yehova imene imatchedwa Tenti.
24 Les portiers se tenaient aux quatre vents, à l’orient, à l’occident, au nord et au midi.
Alonda apakhomowa anali mbali zonse zinayi: kummawa, kumadzulo, kumpoto ndi kummwera.
25 Leurs frères, qui demeuraient dans leurs villages, devaient venir auprès d’eux de temps à autre, pour une semaine.
Abale awo a ku midzi yawo amabwera nthawi ndi nthawi kudzagwira ntchito yawo kwa masiku asanu ndi awiri.
26 Car ces quatre chefs des portiers, qui étaient lévites, étaient constamment en fonctions, et ils avaient encore la surveillance des chambres et des trésors, à la maison de Dieu.
Koma atsogoleri akuluakulu anayi a alonda, amene anali Alevi, anapatsidwa udindo woyangʼanira zipinda ndi chuma cha nyumba ya Mulungu.
27 Ils logeaient autour de la maison de Dieu, dont ils avaient la garde, et ils devaient pourvoir à l’ouverture, chaque matin.
Iwo amakhala usiku wonse atayima mozungulira Nyumba ya Mulungu, chifukwa anayenera kuyilondera. Ndipo anali ndi kiyi wotsekulira mmawa uliwonse.
28 Quelques-uns des lévites avaient la surveillance des ustensiles du service, qu’ils rentraient et sortaient en les comptant.
Ena amayangʼanira zipangizo zimene amagwiritsa ntchito pa ntchito mʼNyumba ya Mulungu. Iwo amaziwerenga zikamalowetsedwa ndi potulutsidwa.
29 D’autres veillaient sur les ustensiles, sur tous les ustensiles du sanctuaire, et sur la fleur de farine, le vin, l’huile, l’encens et les aromates.
Ena anapatsidwa udindo wosamalira zipangizo ndi zinthu zina zonse za ku malo opatulika, pamodzi ndi ufa, vinyo, mafuta, lubani ndi zonunkhira.
30 Des fils de prêtres composaient les parfums aromatiques.
Koma ansembe ena amasakaniza zonunkhirazo.
31 Un des lévites, Mathathias, premier-né le Sellum de Coréïte, avait le soin des gâteaux cuits sur la poêle.
Mlevi wotchedwa Matitiya mwana woyamba wa Salumu wa mʼbanja la Kora, anapatsidwa udindo woyangʼanira zophikidwa mʼziwaya.
32 Et quelques-uns de leurs frères d’entre les fils des Caathites, étaient chargés de préparer pour chaque sabbat les pains de proposition.
Abale ake ena a mʼbanja la Akohati amaphika buledi wa pa Sabata lililonse amene amayikidwa pa tebulo.
33 Ce sont là les chantres, chefs de famille des lévites, demeurant dans les chambres, exempts d’autres fonctions, parce qu’ils étaient à leur œuvre jour et nuit.
Atsogoleri a mabanja a Alevi, amene anali ndi luso loyimba, amakhala mʼzipinda za Nyumba ya Mulungu ndipo samagwira ntchito zina chifukwa ankatumikira usana ndi usiku.
34 Ce sont là les chefs de famille des lévites, chefs selon leurs générations; ils habitaient à Jérusalem.
Onsewa anali atsogoleri a mabanja a Alevi, akuluakulu monga analembedwera pa mibado yawo, ndipo ankakhala mu Yerusalemu.
35 Le père de Gabaon, Jéhiel, habitait à Gabaon, et le nom de sa femme était Maacha.
Yeiyeli abambo a Gibiyoni ankakhala ku Gibiyoni. Dzina la akazi awo linali Maaka,
36 Abdon, son fils premier-né, puis Sur, Cis, Baal, Ner, Nadab,
ndipo mwana wawo woyamba kubadwa anali Abidoni, motsatana ndi Zuri, Kisi, Baala, Neri, Nadabu,
37 Gédor, Ahio, Zacharie et Macelloth.
Gedori, Ahiyo, Zekariya ndi Mikiloti.
38 Macelloth engendra Samaan. Eux aussi habitaient prés de leurs frères à Jérusalem, avec leurs frères. —
Mikiloti anabereka Simeamu. Iwonso ankakhala ndi abale awo ku Yerusalemu.
39 Ner engendra Cis; Cis engendra Saül; Saül engendra Jonathan, Melchisua, Abinadab et Esbaal. —
Neri anabereka Kisi, Kisi anabereka Sauli, ndipo Sauli anabereka Yonatani, Maliki-Suwa, Abinadabu ndi Esibaala.
40 Fils de Jonathan: Méribbaal. Méribbaal engendra Micha. —
Mwana wa Yonatani anali Meri-Baala, amene anabereka Mika.
41 Fils de Micha: Phithon, Mélech, Tharaa.
Ana a Mika anali: Pitoni, Meleki, Tahireya ndi Ahazi.
42 Ahaz engendra Jara; Jara engendra Alamath, Azmoth et Zamri; Zamri engendra Mosa.
Ahazi anabereka Yara, Yara anabereka Alemeti, Azimaveti ndi Zimuri, ndipo Zimiri anabereka Moza.
43 Mosa engendra Banaa. Raphaïa, son fils; Elasa, son fils; Asel, son fils.
Moza anabereka Bineya. Ana ake anali Refaya, Eleasa ndi Azeli.
44 Asel eut six fils, dont voici les noms: Ezricam, Bocru, Ismaël, Saria, Obdia et Hanan. Ce sont là les Fils d’Asel.
Azeli anali ndi ana asanu ndi mmodzi ndipo mayina awo anali awa: Azirikamu, Bokeru, Ismaeli, Seariya, Obadiya ndi Hanani. Awa anali ana a Azeli.

< 1 Chroniques 9 >