< Psaumes 4 >

1 Pour le chef musicien; sur instruments à cordes. Un psaume de David. Réponds-moi quand j'appelle, Dieu de ma justice. Soulagez-moi de ma détresse. Ayez pitié de moi, et entendez ma prière.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe wa zida za zingwe. Salimo la Davide. Ndiyankheni pamene ndiyitana Inu, Inu Mulungu wa chilungamo changa. Pumulitseni ku zowawa zanga; chitireni chifundo ndi kumva pemphero langa.
2 Fils d'hommes, jusqu'à quand ma gloire sera-t-elle transformée en déshonneur? Aimerez-vous la vanité et rechercherez-vous le mensonge? (Selah)
Anthu inu, mpaka liti mudzakhala mukusandutsa ulemerero wanga kukhala manyazi? Mpaka liti mudzakonda zachabe ndi kufuna milungu yabodza? (Sela)
3 Mais sachez que Yahvé s'est réservé celui qui est pieux; Yahvé entendra quand je l'appellerai.
Dziwani kuti Yehova wadziyikira padera anthu okhulupirika; Yehova adzamva pamene ndidzamuyitana.
4 Restez dans la crainte, et ne péchez pas. Fouille ton propre cœur sur ton lit, et sois tranquille. (Selah)
Kwiyani koma musachimwe; pamene muli pa mabedi anu, santhulani mitima yanu ndi kukhala chete. (Sela)
5 Offrez les sacrifices de la justice. Mettez votre confiance en Yahvé.
Perekani nsembe zolungama ndipo dalirani Yehova.
6 Beaucoup disent: « Qui nous montrera du bien? » Yahvé, fais briller sur nous la lumière de ton visage.
Ambiri akufunsa kuti, “Ndani angationetse chabwino chilichonse?” Kuwunika kwa nkhope yanu kutiwalire, Inu Yehova.
7 Tu as mis de la joie dans mon cœur, plus que lorsque leur grain et leur vin nouveau sont augmentés.
Inu mwadzaza mtima wanga ndi chimwemwe chachikulu kuposa kuchuluka kwa tirigu wawo ndi vinyo watsopano.
8 En paix, je me coucherai et je dormirai, pour toi seul, Yahvé, fais-moi vivre en sécurité.
Ine ndidzagona ndi kupeza tulo mwamtendere, pakuti Inu nokha, Inu Yehova, mumandisamalira bwino.

< Psaumes 4 >