< Psaumes 137 >

1 Sur les bords des fleuves de Babylone, nous nous sommes assis. Oui, nous avons pleuré, quand nous nous sommes souvenus de Sion.
Mʼmbali mwa mitsinje ya ku Babuloni tinakhala pansi ndi kulira pamene tinakumbukira Ziyoni.
2 Sur les saules de ce pays, nous avons raccroché nos harpes.
Kumeneko, pa mitengo ya misondozi tinapachika apangwe athu,
3 Car là, ceux qui nous ont emmenés en captivité nous ont demandé des chants. Ceux qui nous tourmentaient exigeaient des chants de joie: « Chantez-nous une des chansons de Sion! »
pakuti anthu otigwira ukapolo anatipempha kuti tiyimbe nyimbo. Otizunza athu anafuna nyimbo zachisangalalo; iwo anati, “Tiyimbireni imodzi mwa nyimbo za ku Ziyoni!”
4 Comment pouvons-nous chanter le chant de Yahvé dans un pays étranger?
Tingayimbe bwanji nyimbo za Yehova mʼdziko lachilendo?
5 Si je t'oublie, Jérusalem, que ma main droite oublie son habileté.
Ndikakuyiwala iwe Yerusalemu, dzanja langa lamanja liyiwale luso lake.
6 Que ma langue se colle au palais si je ne me souviens pas de toi, si je ne préfère pas Jérusalem à ma principale joie.
Lilime langa limamatire ku nkhama za mʼkamwa mwanga ndikapanda kukukumbukira iwe Yerusalemu, ngati sindiyesa iwe chimwemwe changa chachikulu.
7 Souviens-toi, Yahvé, des enfants d'Édom, au jour de Jérusalem, qui a dit: « Rasez-la! Rasez-le jusqu'à ses fondations! »
Kumbukirani, Inu Yehova, zimene Aedomu anachita pa tsiku limene Yerusalemu anagonja. Iwowo anafuwula kuti, “Mugwetseni pansi, mugwetseni pansi mpaka pa maziko ake!”
8 Fille de Babylone, vouée à la destruction, celui qui vous rembourse sera heureux, comme vous l'avez fait pour nous.
Iwe mwana wa mkazi wa Babuloni, woyenera kuwonongedwa, wodalitsika ndi yemwe adzakubwezera pa zimene watichitira.
9 Il sera heureux, qui prend et écrase vos petits contre le rocher.
Amene adzagwira makanda ako ndi kuwakankhanthitsa pa miyala.

< Psaumes 137 >