< Psaumes 127 >
1 Un chant d'ascension. Par Solomon. A moins que Yahvé ne construise la maison, ceux qui la construisent travaillent en vain. A moins que Yahvé ne veille sur la ville, le gardien la surveille en vain.
Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Salimo la Solomoni. Yehova akapanda kumanga nyumba, omanga nyumbayo agwira ntchito pachabe. Yehova akapanda kulondera mzinda, mlonda akanangolondera pachabe.
2 C'est en vain que tu te lèves tôt, pour se coucher tard, en mangeant le pain du labeur, car il donne le sommeil à ses proches.
Mumangodzivuta nʼkulawirira mmamawa ndi kusagona msanga madzulo, kuvutikira chakudya choti mudye, pakuti Iye amapereka tulo kwa amene amawakonda.
3 Voici, les enfants sont un héritage de Yahvé. Le fruit de ses entrailles est sa récompense.
Ana ndiye cholowa chochokera kwa Yehova, ana ndi mphotho yochokera kwa Iye.
4 Comme des flèches dans la main d'un homme puissant, Il en va de même pour les enfants de la jeunesse.
Ana a pa unyamata ali ngati mivi mʼmanja mwa munthu wankhondo.
5 Heureux l'homme qui en a plein son carquois. Ils ne seront pas déçus lorsqu'ils parleront avec leurs ennemis à la porte.
Wodala munthu amene motengera mivi mwake mwadzaza. Iwo sadzachititsidwa manyazi pamene alimbana ndi adani awo pa zipata.