< Psaumes 106 >
1 Louez Yahvé! Rendez grâce à Yahvé, car il est bon, car sa bonté est éternelle.
Tamandani Yehova. Yamikani Yehova chifukwa ndi wabwino; pakuti chikondi chake ndi chosatha.
2 Qui peut dire les actes puissants de Yahvé, ou de déclarer pleinement toutes ses louanges?
Ndani angathe kufotokoza za ntchito zamphamvu za Yehova kapena kumutamanda mokwanira?
3 Heureux ceux qui gardent la justice. Heureux celui qui fait ce qui est juste à tout moment.
Odala ndi amene amasunga chilungamo, amene amachita zolungama nthawi zonse.
4 Souviens-toi de moi, Yahvé, avec la faveur que tu témoignes à ton peuple. Rendez-moi visite avec votre salut,
Mundikumbukire Yehova, pamene mukuonetsa kukoma mtima kwanu kwa anthu anu, bwerani mudzandithandize pamene mukuwapulumutsa iwo,
5 afin que je voie la prospérité de tes élus, afin que je me réjouisse de l'allégresse de ta nation, afin que je puisse me glorifier avec votre héritage.
kuti ndidzasangalale ndi chuma cha anthu anu osankhika, kuti ndidzakhale nacho chimwemwe cha anthu anu ndi kukhala pamodzi ndi cholowa chanu pa kukutamandani.
6 Nous avons péché avec nos pères. Nous avons commis une iniquité. Nous avons fait le mal.
Ife tachimwa monga momwe anachitira makolo athu; tachita zolakwa ndipo tachita moyipa.
7 Nos pères n'ont pas compris tes merveilles en Égypte. Ils ne se sont pas souvenus de la multitude de tes bontés, mais se sont rebellés à la mer, même à la mer Rouge.
Pamene makolo athu anali mu Igupto, sanalingalire za zozizwitsa zanu; iwo sanakumbukire kukoma mtima kwanu kochuluka, ndipo anawukira Inu pa Nyanja Yofiira.
8 Mais il les a sauvés à cause de son nom, pour faire connaître sa puissance.
Komabe Iye anawapulumutsa chifukwa cha dzina lake, kuti aonetse mphamvu zake zazikulu.
9 Il menaça aussi la mer Rouge, et elle fut mise à sec; Il les a donc conduits dans les profondeurs, comme dans un désert.
Anadzudzula Nyanja Yofiira, ndipo inawuma; anawatsogolera mʼnyanja yakuya ngati akuyenda mʼchipululu.
10 Il les a sauvés de la main de celui qui les haïssait, et les a rachetés de la main de l'ennemi.
Anawapulumutsa mʼdzanja la amaliwongo; anawawombola mʼdzanja la mdani.
11 Les eaux ont recouvert leurs adversaires. Il n'y en avait plus un seul.
Madzi anamiza adani awo, palibe mmodzi wa iwo anapulumuka.
12 Et ils crurent à ses paroles. Ils ont chanté ses louanges.
Kenaka iwo anakhulupirira malonjezo ake ndi kuyimba nyimbo zamatamando.
13 Ils ont vite oublié ses œuvres. Ils n'ont pas attendu son conseil,
Koma posachedwa anayiwala zimene Iye anachita, ndipo sanayembekezere uphungu wake.
14 mais a cédé à la soif dans le désert, et ont testé Dieu dans le désert.
Mʼchipululu, anadzipereka ku zilakolako zawo; mʼdziko lopanda kanthu anayesa Mulungu.
15 Il leur accorda leur demande, mais a envoyé la maigreur dans leur âme.
Choncho Iye anawapatsa chimene anapempha, koma anatumiza nthenda yowondetsa.
16 Ils enviaient aussi Moïse dans le camp, et Aaron, le saint de Yahvé.
Mʼmisasa, anachitira nsanje Mose ndi Aaroni, amene Yehova anadzipatulira.
17 La terre s'ouvrit et engloutit Dathan, et a couvert la compagnie d'Abiram.
Nthaka inatsekuka ndipo inameza Datani; inakwirira gulu la Abiramu.
18 Un feu s'est allumé en leur compagnie. La flamme a brûlé les méchants.
Moto unayaka pakati pa otsatira awo; lawi lamoto linapsereza anthu oyipa.
19 Ils firent un veau à Horeb, et ont adoré une image en fusion.
Iwo anapanga mwana wangʼombe pa Horebu ndi kulambira fano loyengedwa kuchokera ku chitsulo.
20 Ils ont ainsi échangé leur gloire pour une image d'un taureau qui mange de l'herbe.
Anasinthanitsa ulemerero wawo ndi fano la ngʼombe yayimuna imene imadya udzu.
21 Ils ont oublié Dieu, leur Sauveur, qui avait fait de grandes choses en Égypte,
Anayiwala Mulungu amene anawapulumutsa, amene anachita zinthu zazikulu mu Igupto,
22 merveilles dans le pays de Ham, et des choses impressionnantes près de la Mer Rouge.
zozizwitsa mʼdziko la Hamu ndi machitidwe ake woopsa pa Nyanja Yofiira.
23 C'est pourquoi il a dit qu'il allait les détruire, si Moïse, son élu, ne s'était pas tenu devant lui sur la brèche, pour détourner sa colère, afin qu'il ne les détruise pas.
Choncho Iye anawawuza kuti adzawawononga, pakanapanda Mose, mtumiki wake wosankhidwa, kuyima pamaso pake, ndi kuletsa mkwiyo wake kuti usawawononge.
24 Oui, ils ont méprisé la terre agréable. Ils n'ont pas cru sa parole,
Motero iwo ananyoza dziko lokoma; sanakhulupirire malonjezo ake.
25 mais ils murmuraient dans leurs tentes, et n'ont pas écouté la voix de Yahvé.
Anangʼungʼudza mʼmatenti mwawo ndipo sanamvere Yehova.
26 Il leur a donc juré qu'il les renverserait dans le désert,
Kotero Iye analumbira atakweza dzanja lake, kuti adzachititsa kuti iwowo afere mʼchipululu,
27 qu'il anéantirait leur descendance parmi les nations, et les disperser dans les pays.
kuchititsa kuti zidzukulu zawo zifere pakati pa anthu a mitundu ina ndi kuwabalalitsa mʼdziko lonse.
28 Ils s'attachèrent aussi à Baal Peor, et ont mangé les sacrifices des morts.
Iwo anayamba kupembedza Baala-Peori ndi kudya nsembe zoperekedwa kwa milungu yopanda moyo;
29 Ils l'ont ainsi irrité par leurs actes. La peste s'est abattue sur eux.
anaputa mkwiyo wa Yehova pa machitidwe awo oyipa, ndipo mliri unabuka pakati pawo.
30 Alors Phinées se leva et exécuta le jugement, ainsi la peste a été arrêtée.
Koma Finehasi anayimirira ndi kulowererapo, ndipo mliri unaleka.
31 Cela lui a été crédité comme justice, pour toutes les générations à venir.
Chimenechi ndicho chinayesedwa chilungamo chake, kwa mibado yosatha imene ikubwera.
32 Ils l'ont aussi irrité aux eaux de Meriba, de sorte que Moïse a été troublé à cause d'eux;
Pa madzi a ku Meriba iwo anakwiyitsa Yehova ndipo mavuto anabwera kwa Mose chifukwa cha anthuwo,
33 parce qu'ils étaient rebelles à son esprit, il a parlé sans réfléchir avec ses lèvres.
pakuti iwowo anawukira mzimu wa Mulungu, ndipo pa milomo ya Mose panatuluka mawu osayenera.
34 Ils n'ont pas détruit les peuples, comme Yahvé le leur a ordonné,
Aisraeliwo sanawononge mitundu ya anthu monga momwe Yehova anawalamulira.
35 mais se sont mêlés aux nations, et appris leurs œuvres.
Koma anasakanizana ndi anthu a mitundu inayo ndi kuphunzira miyambo yawo.
36 Ils ont servi leurs idoles, qui est devenu un piège pour eux.
Ndipo anapembedza mafano awo, amene anakhala msampha kwa iwowo.
37 Oui, ils ont sacrifié leurs fils et leurs filles aux démons.
Anapereka nsembe ana awo aamuna ndi ana awo aakazi kwa ziwanda.
38 Ils ont versé du sang innocent, même le sang de leurs fils et de leurs filles, qu'ils ont sacrifié aux idoles de Canaan. La terre était polluée par le sang.
Anakhetsa magazi a anthu osalakwa, magazi a ana awo aamuna ndi a ana awo aakazi, amene anawapereka nsembe kwa mafano a ku Kanaani, ndipo dziko linayipitsidwa ndi magazi awo.
39 Ils se sont ainsi souillés par leurs œuvres, et se prostituaient dans leurs actes.
Iwo anadzidetsa okha ndi zimene anachita; ndi machitidwe awo amakhala ngati munthu wachigololo.
40 C'est pourquoi Yahvé s'est enflammé de colère contre son peuple. Il abhorrait son héritage.
Tsono Yehova anakwiya ndi anthu ake ndipo ananyansidwa ndi cholowa chake.
41 Il les a livrés aux mains des nations. Ceux qui les détestaient les dominaient.
Iye anawapereka kwa anthu a mitundu ina, ndipo adani awo anawalamulira.
42 Leurs ennemis les ont aussi opprimés. Ils ont été soumis à leur autorité.
Adani awo anawazunza ndi kuwakhazika pansi pa mphamvu yawo.
43 Il les a secourus à plusieurs reprises, mais ils ont été rebelles dans leurs conseils, et ont été abaissés dans leur iniquité.
Iye ankawapulumutsa nthawi zambiri, koma iwo ankatsimikiza za kuwukira ndipo anawonongeka mʼmachimo awo.
44 Mais il a considéré leur détresse, quand il a entendu leur cri.
Koma Iye anaona kuzunzika kwawo pamene anamva kulira kwawo;
45 Il s'est souvenu pour eux de son alliance, et se sont repentis selon la multitude de ses bontés.
Chifukwa cha iwo Iye anakumbukira pangano lake ndipo anawalezera mtima chifukwa cha kukula kwa chikondi chake.
46 Il a fait en sorte qu'ils soient aussi à plaindre. par tous ceux qui les ont emmenés en captivité.
Iye anachititsa kuti amene anawagwira iwo ukapolo awamvere chisoni.
47 Sauve-nous, Yahvé, notre Dieu, nous rassembler d'entre les nations, pour rendre grâce à ton saint nom, pour triompher dans ta louange!
Tipulumutseni Inu Yehova Mulungu wathu, ndipo mutisonkhanitse kuchoka kwa anthu a mitundu ina kuti tithe kuyamika dzina lanu loyera ndi kunyadira mʼmatamando anu.
48 Béni soit Yahvé, le Dieu d'Israël, de l'éternité à l'éternité! Que tout le monde dise: « Amen. » Louez Yah!
Atamandike Yehova, Mulungu wa Israeli, Kuyambira muyaya mpaka muyaya. Anthu onse anene kuti, “Ameni!” Tamandani Yehova.