< Proverbes 24 >
1 Ne soyez pas envieux des hommes mauvais, ni le désir d'être avec eux;
Usachitire nsanje anthu oyipa, usalakalake kuti uzikhala nawo,
2 pour la violence du complot de leurs cœurs et leurs lèvres parlent de méchanceté.
pakuti mitima yawo imalingalira chiwawa, ndipo pakamwa pawo pamayankhula zoyambitsa mavuto.
3 C'est par la sagesse que l'on construit une maison; par l'entendement, il est établi;
Nyumba imamangidwa ndi anthu anzeru, ndipo imakhazikika ndi anthu odziwa zinthu;
4 par connaissance les chambres sont remplies avec tous les trésors rares et magnifiques.
Munthu wodziwa zinthu angathe kudzaza zipinda zake ndi chuma chamtengowapatali ndiponso chabwino.
5 Un homme sage a un grand pouvoir. Un homme bien informé accroît sa force,
Munthu wodziwa zinthu ali ndi mphamvu yayikulu kuposa munthu wanyonga zambiri, ndipo munthu wachidziwitso amaposa munthu wamphamvu.
6 car c'est par des conseils avisés que tu fais la guerre, et la victoire est dans de nombreux conseillers.
Pafunika malangizo kuti ukamenye nkhondo. Pakakhala aphungu ambiri kupambana kumakhalapo.
7 La sagesse est trop élevée pour un fou. Il n'ouvre pas sa bouche dans la porte.
Nzeru ndi chinthu chapatali kwambiri kwa chitsiru; chilibe choti chiyankhule pabwalo la milandu pa chipata.
8 Celui qui complote pour faire le mal sera appelé un magouilleur.
Amene amakonzekera kuchita zoyipa adzatchedwa mvundulamadzi.
9 Les projets de la folie sont des péchés. Le moqueur est détesté par les hommes.
Kukonzekera kuchita za uchitsiru ndi tchimo, ndipo munthu wonyoza amanyansa anthu.
10 Si vous chancelez au moment de la détresse, votre force est faible.
Ngati utaya mtima nthawi ya mavuto ndiye kuti mphamvu yako ndi yochepadi!
11 Sauvez ceux qui sont conduits à la mort! En effet, retenez ceux qui titubent vers le massacre!
Uwapulumutse amene akutengedwa kuti akaphedwe; uwalanditse amene akuyenda movutika kupita kokaphedwa.
12 Si vous dites: « Voici, nous ne savions pas cela, » Celui qui pèse les cœurs ne le considère-t-il pas? Celui qui garde ton âme, ne le sait-il pas? Ne doit-il pas rendre à chacun selon son travail?
Ukanena kuti, “Koma ife sitinadziwe kanthu za izi,” kodi Iye amene amasanthula mtima sazindikira zimenezi? Kodi Iye amene amateteza moyo wako sazidziwa zimenezi? Kodi Iye sadzalipira munthu malingana ndi ntchito zake?
13 Mon fils, mange du miel, car il est bon, les excréments du rayon de miel, qui sont doux à votre goût;
Mwana wanga, uzidya uchi popeza ndi wabwino; uchi wochokera mʼchisa cha njuchi ndi wokoma ukawulawa.
14 Ainsi tu connaîtras la sagesse pour ton âme. Si vous l'avez trouvé, il y aura une récompense: Votre espoir ne sera pas coupé.
Udziwe kuti nzeru ndi yoteronso pa moyo wako; ngati uyipeza nzeruyo, zinthu zidzakuyendera bwino mʼtsogolo, ndipo chiyembekezo chako sichidzapita pachabe.
15 Ne fais pas d'embuscades, méchant, contre la demeure des justes. Ne détruisez pas son lieu de repos;
Usachite zachifwamba nyumba ya munthu wolungama ngati munthu woyipa. Usachite nayo nkhondo nyumba yake;
16 car le juste tombe sept fois et se relève, mais les méchants sont renversés par la calamité.
paja munthu wolungama akagwa kasanu nʼkawiri amadzukiriranso. Koma woyipa adzathedwa tsoka likadzawafikira.
17 Ne te réjouis pas quand ton ennemi tombe. Ne laissez pas votre cœur se réjouir quand il sera renversé,
Usamakondwera ndi kugwa kwa mdani wako. Mtima wako usamasangalale iye akapunthwa.
18 de peur que Yahvé ne le voie et que cela ne lui déplaise, et il détourne de lui sa colère.
Kuopa kuti Yehova ataziona zimenezi nayipidwa nazo, angaleke kukwiyira mdaniyo.
19 Ne vous inquiétez pas à cause des méchants, ne soyez pas envieux des méchants;
Usavutike mtima chifukwa cha anthu ochita zoyipa kapena kuchitira nsanje anthu oyipa,
20 car il n'y aura pas de récompense pour l'homme mauvais. La lampe des méchants sera éteinte.
paja munthu woyipa alibe tsogolo. Moyo wa anthu oyipa adzawuzimitsa ngati nyale.
21 Mon fils, crains Yahvé et le roi. Ne vous joignez pas à ceux qui sont rebelles,
Mwana wanga, uziopa Yehova ndi mfumu, ndipo usamagwirizana ndi anthu owachitira mwano,
22 car leur calamité se lève soudainement. Qui sait quelle destruction peut venir de ces deux-là?
awiri amenewa amagwetsa tsoka mwadzidzidzi. Ndani angadziwe mavuto amene angagwetse?
23 Ce sont là des paroles de sages: Faire preuve de partialité dans le jugement n'est pas bon.
Malangizo enanso a anthu anzeru ndi awa: Kukondera poweruza mlandu si chinthu chabwino:
24 Celui qui dit au méchant: « Tu es juste, » les peuples le maudiront, et les nations l'abhorreront -
Aliyense amene amawuza munthu wolakwa kuti, “Iwe ndi munthu wosalakwa,” anthu a mitundu yonse adzamutemberera, ndi mitundu ya anthu idzayipidwa naye.
25 mais il ira bien avec ceux qui condamnent les coupables, et une riche bénédiction viendra sur eux.
Koma olanga anthu oyipa zinthu zidzawayendera bwino ndipo madalitso ochuluka adzakhala pa iwo.
26 Une réponse honnête est comme un baiser sur les lèvres.
Woyankhula mawu owona ndiye amaonetsa chibwenzi chenicheni.
27 Préparez votre travail à l'extérieur, et préparez vos champs. Ensuite, construisez votre maison.
Ugwiriretu ntchito zako zonse, makamaka za ku munda ndipo pambuyo pake uyambe kumanga nyumba.
28 Ne sois pas un témoin contre ton prochain sans raison. Ne trompez pas avec vos lèvres.
Usakhale mboni yotsutsa mnzako popanda chifukwa, kapena kugwiritsa ntchito pakamwa pako kunena zachinyengo.
29 Ne dites pas: « Je lui ferai ce qu'il m'a fait »; Je rendrai à l'homme ce qu'il a fait. »
Usanene kuti, “Ine ndidzamuchitira iye monga momwe wandichitira ine; ndidzamubwezera munthu ameneyo zimene anandichitira.”
30 Je suis passé par le champ du paresseux, par la vigne de l'homme dépourvu d'intelligence.
Ndinkayenda mʼmbali mwa munda wa munthu waulesi ndinadutsa munda wamphesa wa munthu wopanda nzeru.
31 Voici, elle était couverte d'épines. Sa surface était couverte d'orties, et son mur de pierre a été démoli.
Ndinapeza kuti paliponse mʼmundamo munali mutamera minga, mʼnthaka imeneyo munali mutamera khwisa, ndipo mpanda wake wamiyala unali utawonongeka.
32 Alors j'ai vu, et j'ai bien réfléchi. J'ai vu, et reçu des instructions:
Tsono nditaona ndinayamba kuganizira mu mtima mwanga ndipo ndinatolapo phunziro ili:
33 un peu de sommeil, un peu d'assoupissement, un petit pliage des mains pour dormir,
Ukati, “Bwanji ndigone pangʼono,” kapena “Ndiwodzereko pangʼono,” kapenanso “Ndipinde manja pangʼono kuti ndipumule,”
34 alors ta pauvreté viendra comme un voleur et votre volonté en tant qu'homme armé.
umphawi udzafika pa iwe ngati mbala ndipo usiwa udzakupeza ngati munthu wachifwamba.