< Proverbes 18 >

1 Un homme qui s'isole poursuit l'égoïsme, et défie tout jugement sain.
Munthu wokonda kukhala yekha amafunafuna zomukomera yekha; iye amatsutsana ndi malangizo onse anzeru.
2 L'insensé ne prend pas plaisir à comprendre, mais seulement en révélant sa propre opinion.
Chitsiru chilibe chidwi chomvetsa zinthu, koma chimakondwera ndi kuyankhula maganizo ake okha.
3 Quand vient la méchanceté, vient aussi le mépris, et avec la honte vient le déshonneur.
Kuyipa mtima kukabwera, manyozonso amabwera. Manyazi amabwera pamodzi ndi kunyozeka.
4 Les paroles de la bouche d'un homme sont comme des eaux profondes. La fontaine de la sagesse est comme un ruisseau qui coule.
Mawu a munthu ali ngati madzi akuya, kasupe wa nzeru ndiye mtsinje wotumphuka.
5 Il n'est pas bon d'être partial à l'égard du visage des méchants, ni de priver l'innocent de justice.
Si kwabwino kukondera munthu woyipa pa milandu; kapena kupondereza munthu wosalakwa.
6 Les lèvres de l'insensé se disputent, et sa bouche invite aux coups.
Mawu a chitsiru amautsa mkangano; pakamwa pake pamayitana mkwapulo.
7 La bouche de l'insensé est sa perte, et ses lèvres sont un piège pour son âme.
Pakamwa pa chitsiru ndipo pamabweretsa chiwonongeko chake, ndipo milomo yake ili ngati msampha wa moyo wake.
8 Les paroles d'une commère sont comme des friandises: ils descendent dans les parties les plus intimes d'une personne.
Mawu a miseche ali ngati chakudya chokoma; amalowa mʼmimba mwa munthu.
9 Celui qui se relâche dans son travail est un frère pour celui qui est un maître de la destruction.
Munthu waulesi pa ntchito yake ali pachibale ndi munthu amene amawononga zinthu.
10 Le nom de Yahvé est une tour forte: les justes courent vers lui, et sont en sécurité.
Dzina la Yehova lili ngati nsanja yolimba; wolungama amathawiramo napulumuka.
11 La richesse du riche est sa ville forte, comme un mur infranchissable dans sa propre imagination.
Chuma cha anthu olemera chili ngati mzinda wake wolimba; chili ngati khoma lalitali limene amaganiza kuti limutchinjiriza.
12 Avant la destruction, le cœur de l'homme est orgueilleux, mais avant l'honneur, il y a l'humilité.
Chiwonongeko chisanafike, mtima wa munthu umakhala wonyada, koma ulemu umatsatira kudzichepetsa.
13 Celui qui répond avant d'avoir entendu, c'est de la folie et de la honte pour lui.
Ukayankha usanamvetse bwino nkhani, umenewo ndi uchitsiru ndipo umachita manyazi.
14 L'esprit d'un homme le soutient dans la maladie, mais un esprit écrasé, qui peut le supporter?
Mtima wa munthu utha kupirira pa matenda, koma munthu akataya mtima ndani angathe kumulimbitsanso.
15 Le cœur de celui qui sait discerner obtient la connaissance. L'oreille du sage cherche la connaissance.
Munthu wanzeru amawonjezera nzeru zina; amafunafuna kudziwa bwino zinthu.
16 Le don d'un homme fait de la place pour lui, et l'amène devant de grands hommes.
Mphatso ya munthu imamutsekulira njira yomufikitsa pamaso pa anthu akuluakulu.
17 Celui qui plaide le premier sa cause semble avoir raison- jusqu'à ce qu'un autre vienne l'interroger.
Amene amayamba kufotokoza mlandu wake amaoneka ngati wolungama ndiye mpaka mnzake atabwera ndi kumufunsa bwino.
18 Le lot règle les litiges, et sépare les plus forts.
Kuchita maere kumathetsa mikangano; amalekanitsa okangana amphamvu.
19 Un frère offensé est plus difficile qu'une ville fortifiée. Les litiges sont comme les barreaux d'une forteresse.
Mʼbale amene wamuthandiza amakhala ngati mzinda wolimba, koma kukangana naye kumatsekereza thandizo.
20 L'estomac d'un homme est rempli du fruit de sa bouche. Il est satisfait de la récolte de ses lèvres.
Munthu amapeza bwino malingana ndi zoyankhula zake. Adzakhuta ndi zipatso za pakamwa pake.
21 La mort et la vie sont au pouvoir de la langue; ceux qui l'aiment mangeront son fruit.
Mawu ako angathe kukuphetsa kapena kukukhalitsa moyo. Wokonda kuyankhulayankhula adzadya zipatso zake.
22 Celui qui trouve une femme trouve une bonne chose, et obtient la faveur de Yahvé.
Wapeza mkazi wapeza chinthu chabwino ndipo Yehova amamukomera mtima.
23 Les pauvres implorent la pitié, mais les riches répondent durement.
Munthu wosauka amapempha koma munthu wolemera amayankha mwaukali.
24 Un homme qui a beaucoup de compagnons peut être ruiné, mais il y a un ami qui est plus proche qu'un frère.
Pali abwenzi amene chibwenzi chawo nʼchapamaso, koma pali bwenzi limene limakukangamira kuposa mʼbale wako.

< Proverbes 18 >