< Lévitique 23 >

1 Yahvé parla à Moïse et dit:
Yehova anawuza Mose kuti,
2 Parle aux enfants d'Israël et dis-leur: « Les fêtes de Yahvé, que vous proclamerez comme des convocations saintes, sont mes fêtes.
“Yankhula ndi Aisraeli ndipo uwawuze kuti, ‘Awa ndi masiku anga osankhika a chikondwerero, masiku osankhika olemekeza Yehova amene uyenera kulengeza kuti akhale masiku opatulika a misonkhano.
3 "'On travaillera six jours, mais le septième jour est un sabbat de repos solennel, une sainte convocation; vous ne ferez aucune espèce de travail. Vous ne ferez aucune espèce de travail. C'est un sabbat pour Yahvé dans toutes vos habitations.
“‘Pa masiku asanu ndi limodzi muzigwira ntchito, koma tsiku lachisanu ndi chiwiri ndi Sabata lopuma, tsiku la msonkhano wopatulika. Kulikonse kumene inu mukukhala musamagwire ntchito iliyonse tsiku limeneli popeza ndi tsiku la Sabata la Yehova.
4 "'Voici les fêtes fixes de l'Éternel, les convocations saintes, que vous annoncerez au temps fixé.
“‘Awa ndiwo masiku osankhidwa a zikondwerero za Yehova, masiku woyera a misonkhano amene muti mudzalengeze pa nthawi yake:
5 Le premier mois, le quatorzième jour du mois, au soir, c'est la Pâque de Yahvé.
Chikondwerero cha Paska chiziyamba madzulo a tsiku la 14 la mwezi woyamba.
6 Le quinzième jour du même mois, c'est la fête des pains sans levain pour Yahvé. Pendant sept jours, vous mangerez des pains sans levain.
Tsiku la 15 la mwezi womwewo ndi tsiku lolemekeza Yehova ndipo muziyamba Chikondwerero cha Buledi Wopanda Yisiti. Muzidya buledi wopanda yisiti kwa masiku asanu ndi awiri.
7 Le premier jour, vous aurez une sainte convocation. Vous ne ferez aucun travail régulier.
Pa tsiku loyamba muzichita msonkhano wopatulika. Musamagwire ntchito iliyonse.
8 Mais pendant sept jours, tu offriras à l'Éternel un sacrifice consumé par le feu. Le septième jour, c'est une convocation sainte. Tu ne feras aucun travail régulier.'"
Pa masiku asanu ndi awiri muzipereka nsembe yopsereza kwa Yehova. Ndipo tsiku lachisanu ndi chiwiri muzikhala ndi msonkhano wopatulika ndipo musamagwire ntchito yolemetsa.’”
9 Yahvé parla à Moïse et dit:
Yehova anawuza Mose kuti,
10 Parle aux enfants d'Israël, et dis-leur: « Quand vous serez entrés dans le pays que je vous donne et que vous en aurez fait la moisson, vous apporterez au prêtre la gerbe des prémices de votre récolte.
“Yankhula ndi Aisraeli ndipo uwawuze kuti, ‘Mukakalowa mʼdziko limene ndikukupatsanilo ndi kukolola za mʼminda mwanu, mudzabwere kwa wansembe ndi mtolo wa tirigu woyambirira kucha wa mʼminda mwanu.
11 Il agitera la gerbe devant Yahvé, qui l'acceptera pour vous. Le lendemain du sabbat, le prêtre l'agitera.
Wansembeyo auweyule mtolowo pamaso pa Yehova kotero mtolowo udzalandiridwa mʼmalo mwanu. Wansembe auweyule tsiku lotsatana ndi la Sabata.
12 Le jour où tu agiteras la gerbe, tu offriras un agneau mâle sans défaut d'un an en holocauste à Yahvé.
Pa tsiku limene muweyula mtolowo, muperekenso mwana wankhosa wa mwamuna wa chaka chimodzi, wopanda chilema kuti akhale nsembe yopsereza ya kwa Yehova.
13 L'offrande qui l'accompagnera sera de deux dixièmes d'épha de fleur de farine pétrie à l'huile, un sacrifice consumé par le feu à l'Éternel, d'une agréable odeur; et la libation qui l'accompagnera sera de vin, la quatrième partie d'un hin.
Chopereka chachakudya chake chikhale cha makilogalamu awiri a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta kuti chikhale nsembe yopsereza yopereka kwa Yehova, ya fungo lokoma. Ndipo chopereka cha chakumwa chake chikhale vinyo wa malita anayi ndi theka.
14 Tu ne mangeras ni pain, ni grain rôti, ni grain frais, jusqu'à ce jour même, jusqu'à ce que tu aies apporté le sacrifice de ton Dieu. C'est une loi perpétuelle pour vos générations, dans toutes vos habitations.
Musadye buledi aliyense kapena tirigu wokazinga, kapena wamuwisi mpaka tsiku limene mwabwera ndi chopereka ichi kwa Mulungu wanu. Limeneli ndi lamulo lamuyaya pa mibado yanu yonse, kulikonse kumene mukakhale.
15 "'Tu compteras à partir du lendemain du sabbat, depuis le jour où tu as apporté la gerbe de l'offrande ondulée: sept sabbats seront accomplis.
“‘Kuyambira tsiku lotsatana ndi la Sabata lija, tsiku limene munabwera ndi mtolo wa nsembe yoweyula, muziwerenga masabata asanu ndi awiri athunthu.
16 Le lendemain du septième sabbat, tu compteras cinquante jours, et tu offriras une nouvelle offrande à l'Éternel.
Ndiye kuti muwerenge masiku makumi asanu kuchokera pa tsiku lotsatana ndi Sabata la chisanu ndi chiwiri, ndipo kenaka mupereke nsembe ya tirigu watsopano kwa Yehova.
17 Vous apporterez de vos habitations deux pains pour l'offrande par agitation, faits de deux dixièmes d'épha de fleur de farine. Ils seront cuits au levain, comme prémices à Yahvé.
Kuchokera kulikonse kumene mukukhala, mubwere pamaso pa Yehova ndi buledi muwiri wa ufa wosalala wa makilogalamu awiri, ophikidwa ndi yisiti kuti akhale nsembe yoweyula ya zakudya zoyamba kucha.
18 Tu présenteras avec les pains sept agneaux sans défaut d'un an, un jeune taureau et deux béliers. Ils seront un holocauste à l'Éternel, avec l'offrande et la libation, un sacrifice consumé par le feu, d'une agréable odeur à l'Éternel.
Pamodzi ndi bulediyu muperekenso ana ankhosa aamuna asanu ndi awiri, aliyense akhale wa chaka chimodzi ndi wopanda chilema. Pakhalenso ngʼombe yayingʼono yayimuna ndi nkhosa zazimuna ziwiri. Zimenezi zidzakhala nsembe zopsereza zopereka kwa Yehova pamodzi ndi nsembe za zakudya ndi nsembe za zakumwa. Zonsezi zikhale nsembe zopsereza za fungo lokomera Yehova.
19 Tu offriras un bouc en sacrifice pour le péché et deux agneaux mâles d'un an en sacrifice d'actions de grâces.
Kenaka mupereke mbuzi imodzi yayimuna kuti ikhale nsembe yopepesera machimo ndiponso ana ankhosa awiri, aliyense wa chaka chimodzi kuti akhale nsembe yachiyanjano.
20 Le prêtre les agitera avec le pain des prémices en sacrifice d'agitation devant l'Éternel, avec les deux agneaux. Ils seront consacrés à l'Éternel pour le prêtre.
Wansembe aweyule ana ankhosa awiriwo pamaso pa Yehova monga nsembe yoweyula, pamodzi ndi buledi wa tirigu woyambirira kucha. Zimenezi ndi zopereka zopatulika za Yehova zopatsidwa kwa ansembe.
21 Le jour même, vous proclamerez qu'il y aura pour vous une convocation sainte. Vous ne ferez aucun travail régulier. C'est une loi pour toujours dans toutes vos habitations, de génération en génération.
Pa tsiku lomwelo mulengeze za msonkhano wopatulika ndipo musagwire ntchito zolemetsa. Limeneli ndi lamulo lamuyaya pa mibado yanu yonse, kulikonse kumene mukakhale.
22 "'Quand tu moissonneras la récolte de ton pays, tu ne moissonneras pas entièrement dans les coins de ton champ. Tu ne recueilleras pas les glanures de ta récolte. Tu les laisseras aux pauvres et à l'étranger. Je suis Yahvé ton Dieu. »
“‘Pamene mukukolola zinthu mʼmunda mwanu, musakolole munda wanu mpaka mʼmalire mwenimweni, ndipo musatole khunkha lake. Zimenezo musiyire anthu osauka ndi alendo. Ine ndine Yehova Mulungu wanu.’”
23 Yahvé parla à Moïse, et dit:
Yehova anawuza Mose kuti,
24 Parle aux enfants d'Israël, et dis: « Au septième mois, le premier jour du mois, il y aura pour vous un repos solennel, un mémorial où l'on sonnera des trompettes, une sainte convocation.
“Uza Aisraeli kuti, ‘Tsiku loyamba la mwezi wachisanu ndi chiwiri, likhale tsiku lopumula, la msonkhano wopatulika, mulilengeze poyimba lipenga.
25 Vous ne ferez aucun travail régulier. Vous offrirez à Yahvé un sacrifice consumé par le feu. »
Musagwire ntchito zolemetsa koma mupereke nsembe yopsereza kwa Yehova.’”
26 Yahvé parla à Moïse, et dit:
Yehova anawuza Mose kuti,
27 « Le dixième jour de ce septième mois, ce sera le jour des expiations. Ce sera pour vous une convocation sainte. Vous vous humilierez et vous offrirez à Yahvé un sacrifice consumé par le feu.
“Tsiku lakhumi la mwezi wachisanu ndi chiwiri ndi tsiku lochita Mwambo Wopepesera Machimo. Muzichita msonkhano wopatulika. Muzidzichepetsa pamaso pa Yehova ndi kupereka nsembe zopsereza kwa Yehova.
28 Ce jour-là, vous ne ferez aucune espèce de travail, car c'est un jour d'expiation, afin de faire l'expiation pour vous devant l'Éternel, votre Dieu.
Tsiku limeneli musamagwire ntchito chifukwa ndi tsiku la Mwambo Wopepesera Machimo, kupepesera machimo anu pamaso pa Yehova Mulungu wanu.
29 En effet, celui qui ne renoncera pas à lui-même en ce même jour sera retranché de son peuple.
Munthu aliyense amene sasala zakudya pa tsiku limeneli ayenera kuchotsedwa pakati pa anthu a mtundu wake.
30 Celui qui fera un travail quelconque ce jour-là, je le ferai disparaître du milieu de son peuple.
Aliyense wogwira ntchito tsiku limeneli ndidzamuwononga pakati pa anthu a mtundu wake.
31 Vous ne ferez aucune espèce de travail: c'est une loi perpétuelle, de génération en génération, dans toutes vos habitations.
Inu musadzagwire ntchito iliyonse. Limeneli ndi lamulo lamuyaya pa mibado yanu yonse, kulikonse kumene mukakhale.
32 Ce sera pour vous un sabbat de repos solennel, et vous renoncerez à vous-mêmes. Le neuvième jour du mois, le soir, d'un soir à l'autre, vous observerez votre sabbat. »
Limeneli kwa inu ndi tsiku la Sabata lopumula, ndipo muyenera kusala zakudya. Kuyambira madzulo a tsiku lachisanu ndi chinayi la mwezi mpaka madzulo ena otsatirawo muzisunga tsikulo ngati Sabata lanu.”
33 Yahvé parla à Moïse et dit:
Yehova anawuza Mose kuti,
34 Parle aux enfants d'Israël, et dis: Le quinzième jour de ce septième mois, c'est la fête des tentes, pendant sept jours, pour Yahvé.
“Uwawuze Aisraeli kuti pa masiku asanu ndi awiri kuyambira pa tsiku la 15 la mwezi wachisanu ndi chiwiri pazikhala Chikondwerero cha Misasa cholemekeza Yehova.
35 Le premier jour, il y aura une convocation sainte. Vous ne ferez aucun travail régulier.
Tsiku loyamba ndi la msonkhano wopatulika, musagwire ntchito zolemetsa.
36 Pendant sept jours, vous offrirez un sacrifice consumé par le feu à l'Éternel. Le huitième jour sera pour vous une convocation sainte. Vous offrirez un sacrifice consumé par le feu à Yahvé. C'est une assemblée solennelle; vous ne ferez aucun travail régulier.
Pa masiku asanu ndi awiri muzipereka nsembe zopsereza kwa Yehova. Ndipo pa tsiku lachisanu ndi chitatu muzikhala ndi msonkhano wopatulika ndipo muzipereka nsembe yopsereza kwa Yehova. Kumeneku ndi kutsekera kwa msonkhano waukulu. Musagwire ntchito zolemetsa.
37 "'Voici les fêtes fixées par Yahvé, que vous proclamerez comme des convocations saintes, pour offrir à Yahvé un sacrifice consumé par le feu, un holocauste, une offrande de repas, un sacrifice et des libations, chacun à son jour -
(“‘Amenewa ndi masiku osankhika a chikondwerero cha Yehova, amene muziwalengeza kuti ndi nthawi ya msonkhano wopatulika. Masiku amenewa muzipereka nsembe zopsereza, nsembe za chakudya, nsembe zanyama ndi zopereka zachakumwa za tsiku ndi tsiku.
38 en plus des sabbats de Yahvé, et en plus de vos dons, et en plus de tous vos vœux, et en plus de toutes vos offrandes volontaires, que vous donnez à Yahvé.
Zopereka zimenezi ndi zowonjezera pa zopereka za Yehova za pa Sabata, zopereka zanu zolumbira ndiponso mphatso zanu zaufulu zopereka kwa Yehova.)
39 "'Le quinzième jour du septième mois, lorsque vous aurez récolté les fruits du pays, vous célébrerez la fête de Yahvé pendant sept jours. Le premier jour, il y aura un repos solennel, et le huitième jour, un repos solennel.
“‘Choncho kuyambira pa tsiku la 15 la mwezi wachisanu ndi chiwiri, mutakolola zinthu mʼmunda mwanu, muchite chikondwerero cha Yehova kwa masiku asanu ndi awiri. Tsiku loyamba ndi tsiku lopumula, ndipo tsiku lachisanu ndi chitatu ndi lopumulanso.
40 Tu prendras le premier jour les fruits des arbres majestueux, les branches des palmiers, les rameaux des arbres touffus et les saules du ruisseau, et tu te réjouiras devant l'Éternel, ton Dieu, pendant sept jours.
Pa tsiku loyamba muzitenga zipatso zabwino kwambiri zothyola mʼmitengo, nthambi za kanjedza, nthambi zazikulu za mitengo ya masamba ambiri, ndi za misondozi yakumtsinje, ndipo muzikondwera pamaso pa Yehova Mulungu wanu kwa masiku asanu ndi awiri.
41 Tu le célébreras comme une fête de l'Éternel sept jours par an. C'est une loi pour toujours, de génération en génération. Vous la célébrerez au septième mois.
Chaka chilichonse muzichita chikondwerero cha Yehova kwa masiku asanu ndi awiri. Limeneli ndi lamulo lamuyaya pa mibado yanu yonse. Muzichita chikondwerero chimenechi mwezi wachisanu ndi chiwiri.
42 Vous habiterez dans des abris temporaires pendant sept jours. Tous ceux qui sont nés en Israël habiteront dans des abris temporaires,
Muzikhala mʼmisasa masiku asanu ndi awiri. Onse amene ali mbadwa mʼdziko la Israeli azikhala mʼmisasa
43 afin que vos générations sachent que j'ai fait habiter les enfants d'Israël dans des abris temporaires lorsque je les ai fait sortir du pays d'Égypte. Je suis Yahvé ton Dieu. »
kuti zidzukulu zanu zidzadziwe kuti ndine amene ndinakhazika Aisraeli mʼmisasa nditawatulutsa ku Igupto. Ine ndine Yehova Mulungu wanu.’”
44 Moïse déclara aux enfants d'Israël les fêtes fixées par Yahvé.
Choncho Mose analengeza kwa Aisraeli masiku osankhika a zikondwerero za Yehova.

< Lévitique 23 >