< Juges 5 >

1 Ce jour-là, Déborah et Barak, fils d'Abinoam, chantèrent, en disant,
“Tsiku limenelo Debora ndi Baraki mwana wa Abinoamu anayimba nyimbo iyi:
2 « Parce que les dirigeants ont pris la tête en Israël, parce que le peuple s'est offert de plein gré, sois béni, Yahvé!
“Popeza kuti atsogoleri anatsogoleradi mʼdziko la Israeli; ndipo anthu anadzipereka okha mwa ufulu, tamandani Yehova:
3 « Écoutez, vous, les rois! Écoutez, princes! Moi, même moi, je chanterai à Yahvé. Je chanterai les louanges de Yahvé, le Dieu d'Israël.
“Imvani inu mafumu! Tcherani khutu, atsogoleri inu! Ndidzayimba nyimbo, ndidzayimbira Yehova, Mulungu wa Israeli nyimbo yokoma.
4 « Yahvé, quand tu es sorti de Séir, quand vous avez marché hors du champ d'Édom, la terre a tremblé, le ciel aussi. Oui, les nuages ont laissé tomber de l'eau.
“Inu Yehova, pamene munkatuluka mu Seiri, pamene mumayenda kuchokera mʼdziko la Edomu, dziko linagwedezeka, mitambo inasungunuka nigwetsa madzi.
5 Les montagnes tremblaient devant la présence de Yahvé, même le Sinaï en présence de Yahvé, le Dieu d'Israël.
Mapiri anagwedezeka pamaso pa Yehova, Mulungu wa Israeli.
6 « Au temps de Shamgar, fils d'Anath, à l'époque de Jaël, les routes étaient inoccupées. Les voyageurs marchaient dans des chemins de traverse.
“Pa nthawi ya Samugara mwana wa Anati, pa nthawi ya Yaeli, misewu inasiyidwa; alendo ankangoyenda mʼtinjira takumbali.
7 Les chefs ont cessé d'exister en Israël. Ils ont cessé jusqu'à ce que moi, Deborah, je me lève; Jusqu'à ce que je devienne une mère en Israël.
Anthu a ku midzi anathawa; mu Israeli munalibe midzi mpaka pamene iwe Debora unafika; unafika ngati mayi ku Israeli.
8 Ils ont choisi de nouveaux dieux. Puis la guerre était aux portes. A-t-on vu un bouclier ou une lance parmi quarante mille personnes en Israël?
Pamene anasankha milungu ina, nkhondo inabwera ku zipata za mzinda, ndipo chishango kapena mkondo sizinapezeke pakati pa anthu 40,000 mu Israeli.
9 Mon cœur se tourne vers les gouverneurs d'Israël, qui se sont offerts volontairement parmi le peuple. Bénissez Yahvé!
Mtima wanga uli ndi atsogoleri a Israeli, uli ndi anthu amene anadzipereka okha mwaufulu pakati pa anthu. Tamandani Yehova!
10 « Parlez, vous qui montez des ânes blancs, vous qui êtes assis sur de riches tapis, et vous qui marchez sur le chemin.
“Inu okwera pa abulu oyera, okhala pa zishalo, ndi inu oyenda pa msewu, yankhulani.
11 Loin du bruit des archers, dans les lieux où l'on puise l'eau, ils y répéteront les actes justes de Yahvé, les actes justes de son règne en Israël. « Alors le peuple de Yahvé descendit aux portes.
Ku zitsime, kutali ndi phokoso la a mauta; kumeneko akusimba za kuti Yehova wapambana; akusimba kuti Yehova walipsira anthu ake mu Israeli. “Choncho anthu a Yehova anasonkhana ku zipata za mzinda.
12 « Réveille-toi, réveille-toi, Déborah! Réveillez-vous, réveillez-vous, chantez une chanson! Lève-toi, Barak, et emmène tes captifs, fils d'Abinoam.
Anati, ‘Tsogolera ndiwe, Debora, tsogolera; tsogolera ndiwe, tsogolera, imba nyimbo. Iwe Baraki! nyamuka Tsogolera akapolo ako, iwe mwana wa Abinoamu.’
13 « Alors un reste des nobles et du peuple descendit. Yahvé est descendu pour moi contre les puissants.
“Kenaka anthu okhulupirika anatsatira atsogoleri awo; anthu a Yehova anapita kukamenyera Yehova nkhondo kulimbana ndi adani amphamvu.
14 Ceux dont la racine est en Amalek sont sortis d'Ephraïm, après toi, Benjamin, parmi tes peuples. Les gouverneurs descendent de Machir. Ceux qui manient le bâton du maréchal sont venus de Zabulon.
Anakalowa mʼchigwa kuchokera ku Efereimu; akutsatira iwe Benjamini ndi abale ako. Akulu a ankhondo anachokera ku Makiri, ndipo onyamula ndodo ya udindo anachokera ku Zebuloni.
15 Les princes d'Issachar étaient avec Déborah. Comme Issachar, Barak l'était aussi. Ils se sont précipités dans la vallée à ses pieds. Par les cours d'eau de Reuben, il y avait de grandes résolutions de cœur.
Olamulira a Isakara anali pamodzi ndi Debora; inde, anthu ochokera ku Isakara anatsatanso Baraki, ndipo anathamangira ku chigwa akumutsatira. Koma pakati pa mafuko a Rubeni panali kusinkhasinkha mtima kwambiri osadziwa chenicheni choyenera kuchita.
16 Pourquoi vous êtes-vous assis parmi les bergeries? Pour entendre le sifflement des troupeaux? Aux cours d'eau de Reuben, il y avait de grandes recherches dans le cœur.
Chifukwa chiyani munangokhala ku makola a nkhosa nʼkumangomvetsera zitoliro zoyitanira nkhosa? Pakati pa anthu a fuko la Rubeni panali kusinkhasinkha mtima kwambiri osadziwa chenicheni choyenera kuti achite.
17 Galaad vivait au-delà du Jourdain. Pourquoi Dan est-il resté dans les navires? Asher s'est assis tranquillement au bord de la mer, et vivait près de ses ruisseaux.
Agiliyadi anatsala pa tsidya la Yorodani. Ndipo nʼchifukwa chiyani anthu afuko la Dani anatsarira mʼsitima za pa madzi? Aseri anali pa gombe la Nyanja; anangokhala mʼmadooko mwawo.
18 Zabulon était un peuple qui mettait sa vie en danger jusqu'à la mort; Nephtali aussi, sur les hauts lieux des champs.
Azebuloni ndi anthu amene anayika moyo wawo mʼzoopsa. Nawonso anthu a fuko la Nafutali anayika miyoyo yawo pa chiswe pomenya nkhondo pamwamba pa mapiri.
19 « Les rois sont venus et ont combattu, puis les rois de Canaan ont combattu à Taanach, près des eaux de Megiddo. Ils n'ont pas pris de butin en argent.
“Mafumu anabwera, anachita nkhondo; mafumu Akanaani anachita nkhondo ku Tanaki pafupi ndi madzi a ku Megido, koma sanatengeko zofunkha zasiliva.
20 Du ciel, les étoiles se sont battues. A partir de leurs cours, ils ont combattu Sisera.
Ngakhalenso nyenyezi zakumwamba zinachita nkhondo, zinathira nkhondo Sisera, zikuyenda mʼnjira zake.
21 Le fleuve Kishon les a emportés, cette ancienne rivière, la rivière Kishon. Mon âme, marche avec force.
Mtsinje wa Kisoni unawakokolola, chigumula cha mtsinje wa Kisoni chinawakokolola. Mtima wanga, yenda mwamphamvu, limbika!
22 Alors les sabots des chevaux claquèrent à cause des cabrioles, le cabriolage de leurs forts.
Ndipo ziboda za ngʼombe zazimuna zinachita phokoso lalikulu, akavalo ali pa liwiro, akuthamanga kwambiri.
23 « Maudissez Méroz », dit l'ange de Yahvé. « Maudissez amèrement ses habitants, parce qu'ils ne sont pas venus pour aider Yahvé, pour aider Yahvé contre les puissants.
Mngelo wa Yehova anati ‘Tembererani Merozi.’ ‘Tembererani nzika zake mwaukali, chifukwa sanabwere kudzathandiza Yehova, kulimbana ndi adani ake amphamvu.’
24 « Jaël sera béni par-dessus les femmes, l'épouse de Héber le Kenite; Elle sera bénie par rapport aux femmes de la tente.
“Akhale wodala kupambana akazi onse, Yaeli mkazi wa Heberi Mkeni; inde mwa akazi onse okhala mʼdziko, akhale wodala iyeyu.
25 Il a demandé de l'eau. Elle lui a donné du lait. Elle lui a apporté du beurre dans un plat seigneurial.
Munthu uja anapempha madzi akumwa, koma iye anamupatsa mkaka; anamupatsa chambiko mʼchikho cha wolemekezeka.
26 Elle a mis sa main sur le piquet de la tente, et sa main droite au marteau de l'ouvrier. Avec le marteau, elle a frappé Sisera. Elle a frappé à travers sa tête. Oui, elle a percé et frappé à travers ses tempes.
Anatenga chikhomo cha tenti mʼdzanja lake, anatenganso nyundo ndi dzanja lake lamanja. Ndipo anakhoma nacho Sisera, anamuphwanya mutu wake, ndi kumubowola mu litsipa mwake.
27 A ses pieds, il s'est incliné, il est tombé, il s'est couché. A ses pieds, il s'est incliné, il est tombé. Là où il s'est incliné, il est tombé raide mort.
Anathifukira ku mapazi a mkaziyo nagwa, anagwa; iye anagona pamenepo. Anagwera pa mapazi a mkaziyo, iye anagwa; pamene anagwera, pamenepo anaferapo.
28 « Par la fenêtre, elle regarda dehors et cria: La mère de Sisera a regardé à travers le treillis. Pourquoi son char tarde-t-il à venir? Pourquoi les roues de ses chars attendent-elles?
“Amayi ake a Sisera anasuzumira pa zenera; nafuwula mokweza kuti, ‘Nʼchifukwa chiyani galeta lake lachedwa kufika? Nʼchifukwa chiyani phokoso la magaleta ake silikumveka?’
29 Ses dames sages lui répondirent, Oui, elle s'est répondu à elle-même,
Amayi ake anzeru kwambiri anamuyankha, ndithudi, mwiniwake anadziyankha yekha kuti,
30 « N'ont-ils pas trouvé, n'ont-ils pas partagé le butin? Une dame, deux dames pour chaque homme; à Sisera un butin de vêtements teints, un butin de vêtements teints et brodés, de vêtements teints brodés des deux côtés, sur le cou du butin?
‘Kodi iwo sakufunafuna zofunkha kuti agawane; akugawana wankhondo aliyense mtsikana mmodzi kapena awiri. Sisera akumupatsa zofunkha: zovala zonyikidwa mu utoto, zoti ndizivala mʼkhosi zovala zopeta zonyika mu utoto, ndi zopeta zomavala mʼkhosi?’
31 « Que tous tes ennemis périssent donc, Yahvé, mais que ceux qui l'aiment soient comme le soleil quand il se lève dans sa force. » Ensuite, le pays s'est reposé pendant quarante ans.
“Choncho Yehova! adani anu onse awonongeke, koma iwo amene amakukondani inu akhale ngati dzuwa pamene lituluka ndi mphamvu zake.” Ndipo dziko linakhala pa mtendere zaka makumi anayi.

< Juges 5 >