< Juges 17 >
1 Il y avait un homme de la montagne d'Éphraïm, dont le nom était Michée.
Munthu wina dzina lake Mika wochokera ku dziko la mapiri la Efereimu anawuza amayi ake kuti
2 Il dit à sa mère: « Les onze cents pièces d'argent qui t'ont été enlevées, et au sujet desquelles tu as proféré une malédiction et tu l'as dit à mes oreilles, voici, l'argent est avec moi. Je l'ai pris. » Sa mère a dit: « Que Yahvé bénisse mon fils! »
“Ndinamva inu mukutemberera munthu amene anaba ndalama zanu zasiliva 1,100. Ndalamazo zili ndi ine, ndinatenga ndine.” Pamenepo amayi akewo anati, “Yehova akudalitse mwana wanga!”
3 Il rendit les onze cents pièces d'argent à sa mère, puis sa mère dit: « Je consacre très certainement l'argent de ma main à Yahvé pour mon fils, pour faire une image taillée et une image en fusion. Je vais donc maintenant te le restituer. »
Choncho Mika anabweza ndalama 1,100 za siliva kwa amayi ake, ndipo amayi akewo anati, “Ine ndapatulira Yehova ndalama za silivazi kuti mwana wanga aseme fano ndi kulikuta ndi siliva. Ndiye tsopano ndikubwezera ndalamazo.”
4 Lorsqu'il rendit l'argent à sa mère, celle-ci prit deux cents pièces d'argent et les donna à un orfèvre, qui en fit une image taillée et une image en fusion. Elle était dans la maison de Michée.
Tsono Mika atabweza ndalama zija kwa amayi ake, iwo anatengapo ndalama za siliva 200 namupatsa mmisiri wosula siliva. Iye anakonza fano, nasungunula siliva uja ndi kulikutira fano lija. Ndipo Mika anayika fanolo mʼnyumba mwake.
5 L'homme Michée avait une maison de dieux, et il fit un éphod et des théraphim, et il consacra un de ses fils, qui devint son prêtre.
Mikayu anali ndi kachisi, ndipo anapanga efodi ndi mafano otchedwa terafimu. Anapatula mwana wake mmodzi kuti akhale wansembe.
6 En ce temps-là, il n'y avait pas de roi en Israël. Chacun faisait ce qui était juste à ses propres yeux.
Masiku amenewo kunalibe mfumu ku Israeli. Aliyense amachita zomwe zinamukomera.
7 Il y avait un jeune homme de Bethléhem de Juda, de la famille de Juda, qui était lévite, et il habitait là.
Ku Betelehemu mʼdziko la Yuda kunali mnyamata wina amene anali wa fuko la Levi.
8 Cet homme sortit de la ville, de Bethléhem Juda, pour habiter là où il pourrait trouver un endroit, et il arriva dans la montagne d'Ephraïm, dans la maison de Michée, comme il voyageait.
Iyeyu anachoka mu mzinda wa Betelehemu uja ku Yuda kukafuna malo ena okhala. Akuyenda, anafika ku dziko la mapiri la Efereimu ku nyumba ya Mika.
9 Michée lui dit: « D'où viens-tu? » Il lui dit: « Je suis un lévite de Bethléem en Judée, et je cherche un endroit pour vivre. »
Tsono Mika anamufunsa kuti, “Mukuchokera kuti?” Ndipo iye anayakha kuti, “Ndine Mlevi wochokera ku Betelehemu mʼdziko la Yuda. Ndikufunafuna malo okhala.”
10 Michée lui dit: « Habite avec moi, et sois pour moi un père et un prêtre, et je te donnerai dix pièces d'argent par an, un vêtement et ta nourriture. » Le Lévite entra donc.
Tsono Mika anati kwa iye, “Khalani ndi ine. Mukhale ngati mlangizi wanga ndi wansembe, ndipo ine ndizikupatsani ndalama za siliva khumi pa chaka komanso zovala ndi zakudya.”
11 Le Lévite se contenta de demeurer avec cet homme, et le jeune homme fut pour lui comme l'un de ses fils.
Choncho Mleviyo anavomera kuti azikhala naye, ndipo mnyamatayo anakhala ngati mmodzi mwa ana ake aamuna.
12 Michée consacra le Lévite, et le jeune homme devint son prêtre, et il demeura dans la maison de Michée.
Pambuyo pake Mika anapatula Mleviyo ndipo mnyamatayu anakhala wansembe. Tsono ankakhala mʼnyumba ya Mika.
13 Et Michée dit: « Maintenant je sais que l'Éternel me fera du bien, puisque j'ai un Lévite comme prêtre. »
Ndipo Mika anati, “Tsopano ndadziwa kuti Yehova adzandikomera mtima chifukwa Mleviyu ndiye wakhala wansembe wanga.”