< Job 16 >

1 Alors Job répondit,
Pamenepo Yobu anayankha kuti,
2 « J'ai entendu beaucoup de choses semblables. Vous êtes tous de misérables consolateurs!
“Ndinamvapo zambiri monga zimenezi; nonsenu ndinu anthu osatha kutonthoza mtima mnzanu.
3 Les paroles vaines auront-elles une fin? Ou qu'est-ce qui vous provoque pour que vous répondiez?
Kodi mawu anu ochulukawo adzatha? Kodi chikukuvutani nʼchiyani kuti muzingoyankhula mawu otsutsawa?
4 Je pourrais aussi parler comme vous le faites. Si ton âme était à la place de mon âme, Je pourrais joindre des mots contre vous, et je te fais signe de la tête,
Inenso ndikanatha kuyankhula monga inu, inuyo mukanakhala monga ndilili inemu; Ine ndikanatha kuyankhula mawu omveka bwino kutsutsana nanu ndi kukupukusirani mutu wanga.
5 mais je te fortifierais de ma bouche. La consolation de mes lèvres te soulagerait.
Ndipo mawu a pakamwa panga akanakulimbikitsani; chitonthozo chochokera pa milomo yanga chikanachepetsa ululu wanu.
6 « J'ai beau parler, mon chagrin ne s'apaise pas. Même si je m'abstiens, qu'est-ce qui me soulage?
“Koma ine ndikati ndiyankhule ululu wanga sukuchepa; ndipo ndikati ndikhale chete, ululu wanga sukuchokabe.
7 Mais maintenant, Dieu, tu m'as épuisé. Tu as fait de toute ma compagnie une désolation.
Ndithudi, Inu Mulungu mwanditha mphamvu; mwawononga banja langa lonse.
8 Vous m'avez ratatiné. Ceci est un témoignage contre moi. Ma maigreur se dresse contre moi. Il témoigne de mon visage.
Inu mwandimanga ndipo kundimangako kwakhala umboni; kuwonda kwanga kwandiwukira ndipo kukuchita umboni wonditsutsa.
9 Il m'a déchiré dans sa colère et m'a persécuté. Il a grincé des dents contre moi. Mon adversaire aiguise son regard sur moi.
Mulungu amabwera kwa ine mwankhanza ndipo amadana nane, amachita kulumira mano; mdani wanga amandituzulira maso.
10 Ils ont ouvert leur bouche sur moi. Ils m'ont frappé sur la joue avec reproche. Ils se rassemblent contre moi.
Anthu amatsekula pakamwa pawo kundikuwiza; amandimenya pa tsaya mwachipongwe ndipo amagwirizana polimbana nane.
11 Dieu me livre aux impies, et me jette entre les mains des méchants.
Mulungu wandipereka kwa anthu ochita zoyipa ndipo wandiponyera mʼmanja mwa anthu oyipa mtima.
12 J'étais à l'aise, et il m'a brisé. Oui, il m'a pris par le cou, et m'a mis en pièces. Il a aussi fait de moi sa cible.
Ine ndinali pamtendere, koma Mulungu ananditswanya; anandigwira pa khosi ndi kundiphwanya. Iye anandisandutsa choponyera chandamale chake;
13 Ses archers m'entourent. Il divise mes reins, et ne les épargne pas. Il déverse ma bile sur le sol.
anthu ake oponya mauta andizungulira. Mopanda kundimvera chisoni, Iye akulasa impsyo zanga ndipo akutayira pansi ndulu yanga.
14 Il me brise, brèche après brèche. Il court vers moi comme un géant.
Akundivulaza kawirikawiri, akuthamangira pa ine monga munthu wankhondo.
15 J'ai cousu un sac sur ma peau, et j'ai poussé ma corne dans la poussière.
“Ndasokerera chiguduli pa thupi langa ndipo ndayika mphamvu zanga pa fumbi.
16 Mon visage est rouge de pleurs. L'obscurité profonde est sur mes paupières,
Maso anga afiira ndi kulira, ndipo zikope zanga zatupa;
17 bien qu'il n'y ait aucune violence dans mes mains, et ma prière est pure.
komatu manja anga sanachite zachiwawa ndipo pemphero langa ndi lolungama.
18 « Terre, ne couvre pas mon sang. Que mon cri n'ait pas de place pour se reposer.
“Iwe dziko lapansi, usakwirire magazi anga; kulira kwanga kofuna thandizo kusalekeke!
19 Maintenant même, voici, mon témoin est dans le ciel. Celui qui se porte garant pour moi est en haut.
Ngakhale tsopano mboni yanga ili kumwamba; wonditchinjiriza pa mlandu wanga ali komweko.
20 Mes amis se moquent de moi. Mes yeux versent des larmes à Dieu,
Wondipembedzera ndi bwenzi langa, pamene maso anga akukhuthula misozi kwa Mulungu;
21 qu'il maintiendrait le droit d'un homme avec Dieu, d'un fils d'homme avec son prochain!
iye, mʼmalo mwanga, amamudandaulira Mulungu monga munthu amadandaulira bwenzi lake.
22 Car lorsque quelques années se seront écoulées, Je prendrai le chemin du non-retour.
“Pakuti sipapita zaka zambiri ndisanayende mʼnjira imene sindidzabwerera.”

< Job 16 >