< Job 15 >

1 Alors Éliphaz, le Thémanite, prit la parole,
Pamenepo Elifazi wa ku Temani anayankha kuti,
2 « Si un homme sage répond par une vaine connaissance, et se remplir du vent d'est?
“Kodi munthu wanzeru angayankhe ndi mawu achabechabe otere, kapena angakhutitse mimba yake ndi mphepo yotentha yochokera kummawa?
3 Doit-il raisonner avec des propos non profitables, ou avec des discours avec lesquels il ne peut rien faire de bon?
Kodi angathe kutsutsa ndi mawu opanda pake, kapena kuyankhula mawu opanda phindu?
4 Oui, vous supprimez la peur, et entravent la dévotion devant Dieu.
Koma iwe ukuchepetsa zoopa Mulungu ndipo ukutchinga zodzikhuthulira kwa Mulungu.
5 Car ton iniquité enseigne ta bouche, et vous choisissez le langage des rusés.
Tchimo lako ndiye likuyankhulitsa pakamwa pakopo; ndipo watengera mayankhulidwe a atambwali.
6 C'est ta propre bouche qui te condamne, et non moi. Oui, tes propres lèvres témoignent contre toi.
Pakamwa pakopo ndiye pakukutsutsa osati pakamwa panga; milomo yakoyo ikukutsutsa.
7 « Es-tu le premier homme qui soit né? Ou bien on vous a fait sortir avant les collines?
“Kodi ndiwe munthu woyamba kubadwa? Kodi unalengedwa mapiri asanalengedwe?
8 Avez-vous entendu le conseil secret de Dieu? Limitez-vous la sagesse à vous-même?
Kodi unali mʼgulu la alangizi a Mulungu? Kodi ukudziyesa wanzeru ndiwe wekha?
9 Que savez-vous que nous ne savons pas? Que comprenez-vous qui n'est pas en nous?
Kodi iwe umadziwa chiyani chimene ife sitichidziwa? Kodi iwe uli ndi chidziwitso chanji chimene ife tilibe?
10 Avec nous, il y a des hommes aux cheveux gris et des hommes très âgés, beaucoup plus vieux que ton père.
Anthu a imvi ndi okalamba ali mbali yathu, anthu amvulazakale kupambana abambo ako.
11 Les consolations de Dieu sont-elles trop petites pour vous, même la parole qui est douce envers vous?
Kodi mawu otonthoza mtima ochokera kwa Mulungu sakukukwanira, mawu oyankhula mofatsawa kwa iwe?
12 Pourquoi ton cœur t'emporte-t-il? Pourquoi vos yeux clignotent-ils?
Chifukwa chiyani ukupsa mtima, ndipo chifukwa chiyani ukutuzula maso ako,
13 que vous tournez votre esprit contre Dieu, et laisser de telles paroles sortir de votre bouche?
moti ukupsera mtima Mulungu ndi kuyankhula mawu otero pakamwa pako?
14 Qu'est-ce que l'homme, pour qu'il soit pur? Qu'est-ce que celui qui est né d'une femme, pour qu'il soit juste?
“Kodi munthu nʼchiyani kuti nʼkukhala woyera mtima kapena wobadwa mwa amayi nʼchiyani kuti nʼkukhala wolungama mtima?
15 Voici, il ne fait pas confiance à ses saints. Oui, les cieux ne sont pas propres à ses yeux;
Ngati Mulungu sakhulupirira ngakhale angelo ake, ngakhale zakumwamba sizoyera pamaso pake,
16 combien moins celui qui est abominable et corrompu, un homme qui boit l'iniquité comme de l'eau!
nanga kuli bwanji munthu amene ndi wonyansa ndi wa njira zokhotakhota, amene kuchita zoyipa kuli ngati kumwa madzi.
17 « Je vais te montrer, écoute-moi; ce que j'ai vu, je vais le déclarer
“Mvetsera kwa ine ndipo ndidzakufotokozera; ndilole ndikuwuze zimene ndaziona,
18 (que les sages ont raconté par leurs pères, et ne l'ont pas caché;
zimene anandiphunzitsa anthu anzeru, sanandibisire kalikonse kamene anamva kuchokera kwa makolo awo.
19 à qui seul le pays a été donné, et aucun étranger ne passait parmi eux):
(Ndi kwa iwowa kumene dziko lino linaperekedwa pamene panalibe mlendo wokhala pakati pawo).
20 Le méchant se tord de douleur tous ses jours, même le nombre d'années qui sont réservées à l'oppresseur.
Munthu woyipa amavutika ndi masautso masiku onse a moyo wake, munthu wankhanza adzavutika zaka zake zonse.
21 Un bruit de terreur est dans ses oreilles. Dans la prospérité, le destructeur viendra sur lui.
Amamva mawu owopsa mʼmakutu mwake, pamene zonse zikuoneka ngati zili bwino, anthu achifwamba amamuthira nkhondo.
22 Il ne croit pas qu'il reviendra des ténèbres. Il est attendu par l'épée.
Iye sakhulupirira kuti angathe kupulumuka ku mdima wa imfa; iyeyo ndi woyenera kuphedwa.
23 Il erre à la recherche de pain, en disant: « Où est-il? ». Il sait que le jour des ténèbres est prêt à sa main.
Amangoyendayenda pali ponse kunka nafuna chakudya; amadziwa kuti tsiku la mdima lili pafupi.
24 La détresse et l'angoisse l'effraient. Ils l'emportent sur lui, comme un roi prêt à la bataille.
Masautso ndi nthumanzi zimamuchititsa mantha kwambiri; zimamugonjetsa iye monga imachitira mfumu yokonzekera kukathira nkhondo,
25 Parce qu'il a étendu sa main contre Dieu, et se comporte fièrement contre le Tout-Puissant,
chifukwa iye amatambasula dzanja lake kuyambana ndi Mulungu ndipo amadzitama yekha polimbana ndi Wamphamvuzonse.
26 il court vers lui avec un cou raide, avec les boucliers épais de ses boucliers,
Amapita mwa mwano kukalimbana naye atanyamula chishango chochindikala ndi cholimba.
27 parce qu'il s'est couvert le visage de sa graisse, et a accumulé de la graisse sur ses cuisses.
“Ngakhale nkhope yake ndi yonenepa ndipo mʼchiwuno mwake muli mnofu wambiri,
28 Il a habité des villes désertes, dans des maisons que personne n'habitait, qui étaient prêts à devenir des tas.
munthuyo adzakhala mʼmizinda yowonongeka ndi mʼnyumba zosayenera kukhalamo anthu, nyumba zimene zikugwa ndi kuwonongeka.
29 Il ne sera pas riche, et sa fortune ne durera pas, et leurs biens ne s'étendront pas sur la terre.
Iye sadzalemeranso ndipo chuma chake sichidzakhalitsa, ngakhale minda yake sidzabala zipatso pa dziko lapansi.
30 Il ne sortira pas des ténèbres. La flamme desséchera ses branches. Il s'en ira par le souffle de la bouche de Dieu.
Iyeyo sadzapulumuka mu mdimamo; lawi lamoto lidzawumitsa nthambi zake, ndipo mpweya wochokera mʼkamwa mwa Mulungu udzamusesa.
31 Qu'il ne se fie pas au vide, en se trompant lui-même, car le vide sera sa récompense.
Asadzinyenge yekha podalira zinthu zachabechabe, pakuti pa mapeto pake sadzaphulapo kanthu.
32 Elle s'accomplira avant son temps. Sa branche ne sera pas verte.
Iye adzalandira malipiro ake nthawi yake isanakwane, ndipo nthambi zake sizidzaphukanso.
33 Il secouera son raisin non mûr comme la vigne, et il rejettera sa fleur comme l'olivier.
Iye adzakhala ngati mtengo wamphesa wopululidwa zipatso zake zisanapse, adzakhala ngati mtengo wa olivi umene wayoyola maluwa ake.
34 Car la compagnie des impies sera stérile, et le feu consumera les tentes de la corruption.
Pakuti anthu osapembedza Mulungu adzakhala osabala ndipo moto udzapsereza nyumba za onse okonda ziphuphu.
35 Ils conçoivent la malice et produisent l'iniquité. Leur cœur prépare la tromperie. »
Iwo amalingalira zaupandu ndipo amachita zoyipa; mtima wawo umakonzekera zachinyengo.”

< Job 15 >