< Jérémie 46 >

1 Parole de Yahvé adressée à Jérémie, le prophète, concernant les nations.
Yehova anamupatsa Yeremiya uthenga wonena za anthu a mitundu ina.
2 Sur l'Égypte: sur l'armée de Pharaon Néco, roi d'Égypte, qui était près du fleuve Euphrate, à Carkemish, et que Nebucadnetsar, roi de Babylone, battit la quatrième année de Jojakim, fils de Josias, roi de Juda.
Kunena za Igupto: Yehova ananena za gulu lankhondo la Farao Neko mfumu ya ku Igupto limene Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni analigonjetsa ku Karikemesi ku mtsinje wa Yufurate mʼchaka cha chinayi cha Yehoyakimu mwana wa Yosiya mfumu ya Yuda,
3 « Préparez la cuirasse et le bouclier, et s'approcher de la bataille!
anati, “Konzani zishango zanu ndi malihawo, ndipo yambanipo kupita ku nkhondo!
4 Harnachez les chevaux, et levez-vous, cavaliers, et mettez-vous debout avec vos casques. Polissez les lances, mettre les manteaux de courrier.
Mangani akavalo, ndipo kwerani inu okwerapo! Khalani pa mzere mutavala zipewa! Nolani mikondo yanu, valani malaya anu ankhondo!
5 Pourquoi l'ai-je vu? Ils sont consternés et se retournent. Leurs puissants sont battus, ont fui en hâte, et ne regardez pas en arrière. La terreur est de tous les côtés, » dit Yahvé.
Yeremiya anati: Kodi ndikuona chiyani? Achita mantha akubwerera, ankhondo awo agonjetsedwa. Akuthawa mofulumirapo osayangʼananso mʼmbuyo, ndipo agwidwa ndi mantha ponseponse,” akutero Yehova.
6 « Ne laisse pas le rapide s'enfuir, ni l'homme fort ne s'échappera. Au nord, près du fleuve Euphrate ils ont trébuché et sont tombés.
Waliwiro sangathe kuthawa ngakhale wankhondo wamphamvu sangathe kupulumuka. Akunka napunthwa ndi kugwa kumpoto kwa mtsinje wa Yufurate.
7 « Qui est celui qui s'élève comme le Nil? comme des rivières dont les eaux déferlent?
“Kodi ndani amene akukwera ngati Nailo, ngati mtsinje wa madzi amkokomo?
8 L'Égypte s'élève comme le Nil, comme des rivières dont les eaux se déchaînent. Il dit: « Je me lèverai. Je couvrirai la terre. Je détruirai les villes et leurs habitants.
Igupto akusefukira ngati Nailo, ngati mitsinje ya madzi amkokomo. Iye akunena kuti, ‘Ndidzadzuka ndi kuphimba dziko lapansi; ndidzawononga mizinda ndi anthu ake.’
9 Montez, chevaux! Ragez, chars! Que les hommes forts sortent: Cush et Put, qui s'occupent du bouclier; et les Ludim, qui manient et plient l'arc.
Tiyeni, inu akavalo! Thamangani inu magaleta! Tulukani, inu ankhondo, ankhondo a ku Kusi ndi Puti amene mumanyamula zishango, ankhondo a ku Ludi amene mumaponya uta.
10 Car ce jour-là est celui du Seigneur, Yahvé des armées, un jour de vengeance, pour qu'il se venge de ses adversaires. L'épée dévorera et sera rassasiée, et s'abreuvera de leur sang; car le Seigneur, Yahvé des Armées, a un sacrifice dans le pays du nord, près du fleuve Euphrate.
Koma tsikulo ndi la Ambuye Yehova Wamphamvuzonse; tsiku lolipsira, lolipsira adani ake. Lupanga lake lidzawononga ndi kukhuta magazi, lidzaledzera ndi magazi. Pakuti Yehova, Yehova Wamphamvuzonse, adzapereka adani ake ngati nsembe mʼdziko la kumpoto mʼmbali mwa mtsinje wa Yufurate.
11 Monte en Galaad, et prends du baume, vierge fille d'Égypte. Vous utilisez beaucoup de médicaments en vain. Il n'y a pas de guérison pour vous.
“Pita ku Giliyadi ukatenge mankhwala iwe namwali Igupto. Wayesayesa mankhwala ambiri koma osachira; palibe mankhwala okuchiritsa.
12 Les nations ont entendu parler de ta honte, et la terre est pleine de ton cri; car le puissant a trébuché contre le puissant, ils tombent tous les deux ensemble. »
Anthu a mitundu ina amva za manyazi ako; kulira kwako kwadzaza dziko lapansi. Ankhondo akunka nagwetsanagwetsana, onse awiri agwa pansi limodzi.”
13 La parole que Yahvé adressa à Jérémie, le prophète, sur la manière dont Nabuchodonosor, roi de Babylone, devait venir et frapper le pays d'Égypte:
Uthenga umene Yehova anapatsa mneneri Yeremiya wonena za kubwera kwa Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni kudzathira nkhondo Igupto ndi uwu:
14 « Déclarez en Égypte, publier à Migdol, et publier à Memphis et à Tahpanhes; dire: « Levez-vous et préparez-vous, car l'épée a dévoré autour de toi.
“Mulengeze ku Igupto. Mulengeze ku Migidoli. Mulengezenso ku Mefisi ndi ku Tapanesi. Muwawuze anthu akumeneko kuti, ‘Imani pamalo panu ndi kukhala okonzeka kudziteteza, chifukwa lupanga lidzawononga zonse zimene muli nazo.’
15 Pourquoi vos forces sont-elles balayées? Ils ne sont pas restés debout, car Yahvé les a poussés.
Chifukwa chiyani mulungu wanu wamphamvu uja Apisi wathawa? Iye sakanatha kulimba chifukwa Yehova anamugwetsa.
16 Il a fait trébucher beaucoup de gens. Oui, ils sont tombés l'un sur l'autre. Ils ont dit: « Levez-vous! Retournons auprès des nôtres, et à la terre de notre naissance, de l'épée oppressive.
Ankhondo anu apunthwa ndi kugwa. Aliyense akuwuza mnzake kuti, ‘Tiyeni tibwerere kwathu, ku dziko kumene tinabadwira, tithawe lupanga la adani athu.’
17 Ils criaient: « Pharaon, roi d'Égypte, n'est qu'un bruit; il a laissé passer le temps qui lui était imparti ».
Kumeneku iwo adzafuwula kuti, ‘Farao, mfumu ya ku Igupto mupatseni dzina lakuti, Waphokoso, Wotaya mwayi wake.’
18 « Je suis vivant », dit le roi, dont le nom est Yahvé des Armées, « sûrement comme le Thabor parmi les montagnes, et comme le Carmel au bord de la mer, pour qu'il vienne.
“Pali Ine wamoyo,” ikutero Mfumu, imene dzina lake ndi Yehova Wamphamvuzonse, “wina adzabwera amene ali ngati Tabori phiri lopambana mapiri ena, ngati phiri la Karimeli loti njoo mʼmbali mwa nyanja.
19 Fille qui habite en Égypte, fournissez-vous pour aller en captivité; car Memphis deviendra une désolation, et sera brûlé, sans habitant.
Konzani katundu wanu wopita naye ku ukapolo inu anthu a ku Igupto, pakuti Mefisi adzasanduka chipululu ndipo adzakhala bwinja mopanda wokhalamo.
20 « L'Égypte est une très belle génisse; mais la destruction est venue du nord. Il est arrivé.
“Igupto ali ngati mwana wangʼombe wokongola, koma chimphanga chikubwera kuchokera kumpoto kudzalimbana naye.
21 Et ses mercenaires, au milieu d'elle, sont comme des veaux de l'étable, car eux aussi sont retournés en arrière. Ils se sont enfuis ensemble. Ils ne se sont pas levés, car le jour de leur calamité est venu sur eux, le moment de leur visite.
Ngakhale ankhondo aganyu amene ali naye ali ngati ana angʼombe onenepa. Nawonso abwerera mʼmbuyo, nathawa pamodzi. Palibe amene wachirimika. Ndithu, tsiku la tsoka lawafikira; ndiyo nthawi yowalanga.
22 Son bruit sera comme celui du serpent, car ils vont marcher avec une armée, et viennent contre elle avec des haches, comme des coupeurs de bois.
Aigupto akuthawa ndi liwu lawo lili ngati la njoka yothawa pamene adani abwera ndi zida zawo, abwera ndi nkhwangwa ngati anthu odula mitengo.
23 Ils couperont sa forêt, dit Yahvé, « bien qu'il ne puisse pas être fouillé; car ils sont plus nombreux que les sauterelles, et sont innombrables.
Iwo adzadula nkhalango ya Igupto,” akutero Yehova, “ngakhale kuti ndi yowirira. Anthuwo ndi ochuluka kupambana dzombe, moti sangatheke kuwerengeka.
24 La fille de l'Égypte sera déçue; elle sera livrée entre les mains des gens du nord. »
Anthu a ku Igupto achita manyazi atengedwa ukapolo ndi anthu a kumpoto.”
25 Yahvé des armées, le Dieu d'Israël, dit: « Voici que je vais punir Amon de No, et Pharaon, et l'Égypte, avec ses dieux et ses rois, même Pharaon, et ceux qui se confient en lui.
Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli, akunena kuti, “Ndili pafupi kulanga Amoni mulungu wa Tebesi. Ndidzalanganso Farao ndi Igupto pamodzi ndi milungu yake yonse, mafumu ake ndi onse amene amamukhulupirira.
26 Je les livrerai entre les mains de ceux qui en veulent à leur vie, entre les mains de Nebucadnetsar, roi de Babylone, et entre les mains de ses serviteurs. Ensuite, elle sera habitée, comme aux jours d'autrefois, dit Yahvé.
Ndidzawapereka kwa amene akufuna kuwapha, ndiye kuti kwa Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni ndi atsogoleri ake ankhondo. Komabe, mʼtsogolomo Igupto adzakhalanso ndi anthu monga kale,” akutero Yehova.
27 « Mais n'aie pas peur, Jacob, mon serviteur. Ne sois pas consterné, Israël; car, voici, je vous sauverai de loin, et ta descendance du pays de leur captivité. Jacob reviendra, et sera tranquille et à l'aise. Personne ne lui fera peur.
“Iwe mtumiki wanga Yakobo, usachite mantha; usataye mtima, iwe Israeli. Ndithu Ine ndidzakupulumutsa kuchokera ku mayiko akutali, ndidzapulumutsanso zidzukulu zako kuchokera ku mayiko kumene anapita nazo ku ukapolo. Yakobo adzabwerera ndipo adzakhala motakasuka ndi pa mtendere, ndipo palibenso wina amene adzamuopsa.
28 N'aie pas peur, mon serviteur Jacob, dit Yahvé, « car je suis avec vous; car je ferai disparaître toutes les nations où je vous ai chassés, mais je n'en finirai pas avec vous, mais je vais vous corriger sur mesure, et ne vous laissera en aucun cas impuni. »
Iwe mtumiki wanga Yakobo, usachite mantha, pakuti Ine ndili nawe,” akutero Yehova. “Ndidzawonongeratu mitundu yonse ya anthu a ku mayiko kumene ndakupirikitsira, Koma iwe sindidzakuwononga kotheratu. Ndidzakulanga iwe ndithu koma moyenerera; sindidzakulekerera osakulanga.”

< Jérémie 46 >