< Jérémie 27 >
1 Au commencement du règne de Jojakim, fils de Josias, roi de Juda, cette parole fut adressée à Jérémie de la part de Yahvé, en ces termes:
Zedekiya mwana wa Yosiya, mfumu ya ku Yuda, atangoyamba kulamulira, Yehova anawuza Yeremiya kuti,
2 Yahvé me dit: « Fais des liens et des barres, et mets-les sur ton cou.
“Tenga zingwe zomangira ndi mitengo ya goli ndipo uzimangirire mʼkhosi mwako.
3 Puis envoie-les au roi d'Édom, au roi de Moab, au roi des enfants d'Ammon, au roi de Tyr et au roi de Sidon, par la main des messagers qui viennent à Jérusalem auprès de Sédécias, roi de Juda.
Tsono utumize uthenga kwa mafumu a Edomu, Mowabu, Amoni, Turo ndi Sidoni kudzera mwa amithenga amene abwera ku Yerusalemu kwa Zedekiya, mfumu ya Yuda.
4 Donne-leur l'ordre de dire à leurs maîtres: « L'Éternel des armées, le Dieu d'Israël, dit: « Vous direz à vos maîtres:
Uwapatse uthenga wokapereka kwa ambuye awo ndipo uwawuze kuti: Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti, ‘Mukawuze ambuye anu kuti:
5 J'ai fait la terre, les hommes et les animaux qui sont à la surface de la terre par ma grande puissance et par mon bras étendu. Je la donne à qui me semble bon.
Ndi mphamvu zanga ndi dzanja langa lamphamvu ndinalenga dziko lapansi ndi anthu ake onse pamodzi ndi nyama zili mʼmenemo, ndipo ndimalipereka kwa aliyense amene ndikufuna.
6 Maintenant, j'ai livré toutes ces terres entre les mains de Nabuchodonosor, roi de Babylone, mon serviteur. Je lui ai aussi donné les animaux des champs pour qu'ils le servent.
Tsopano ndidzapereka mayiko anu onse kwa mtumiki wanga Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni. Ndamupatsanso nyama zakuthengo zonse kuti zimutumikire.
7 Toutes les nations le serviront, lui, son fils et le fils de son fils, jusqu'à ce que vienne le temps de son propre pays. Alors, de nombreuses nations et de grands rois feront de lui leur serviteur.
Anthu a mitundu yonse adzamutumikira iyeyo, mwana wake ndi chidzukulu chake mpaka nthawi itakwana yoti dziko lake liwonongedwe. Pamenepo mitundu yambiri ndi mafumu amphamvu adzamugonjetsa.
8 ""« Il arrivera que je punirai la nation et le royaume qui ne serviront pas le même Nabuchodonosor, roi de Babylone, et qui ne mettront pas leur cou sous le joug du roi de Babylone, dit Yahvé, par l'épée, la famine et la peste, jusqu'à ce que je les aie consumés par sa main »".
“‘Koma ngati anthu a mtundu wina uliwonse kapena ufumu wina uliwonse adzakana kutumikira Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni kapena kusenza goli lake, Ine ndidzalanga mtundu umenewo ndi lupanga, ndi njala ndi mliri, akutero Yehova, mpaka nditawapereka mʼmanja mwake kotheratu.
9 Mais toi, n'écoute pas tes prophètes, ni tes devins, ni tes songes, ni tes devins, ni tes sorciers, qui te disent: « Tu ne serviras pas le roi de Babylone »;
Choncho musamvere aneneri anu, owombeza anu, otanthauza maloto anu, amawula anu kapena amatsenga anu akamakuwuzani kuti, ‘Simudzatumikira mfumu ya ku Babuloni.’
10 car ils te prophétisent le mensonge, pour t'éloigner de ton pays, afin que je te chasse et que tu périsses.
Iwo akukuloserani zabodza kotero kuti adani adzakuchotsani mʼdziko lanu nʼkupita nanu ku dziko lakutali. Ndidzakupirikitsani ndi kukuwonongani kotheratu.
11 Mais la nation qui mettra son cou sous le joug du roi de Babylone et qui le servira, je la laisserai dans son pays, dit Yahvé, elle le cultivera et y habitera.
Koma ngati mtundu wina uliwonse udzagonjera mfumu ya ku Babuloni ndi kuyitumukira, ndidzawusiya kuti ukhale mʼdziko lake kuti uzilima ndi kukhalamo, akutero Yehova.’”
12 Je parlai à Sédécias, roi de Juda, selon toutes ces paroles, et je dis: « Placez votre cou sous le joug du roi de Babylone, servez-le, lui et son peuple, et vivez.
Uthenga womwewu ndinawuzanso Hezekiya mfumu ya Yuda. Ndinati, “Gonjerani mfumu ya ku Babuloni. Itumikireni iyoyo pamodzi ndi anthu ake ndipo mudzakhala ndi moyo.
13 Pourquoi mourrez-vous, vous et votre peuple, par l'épée, par la famine et par la peste, comme Yahvé l'a dit au sujet de la nation qui ne veut pas servir le roi de Babylone?
Nanga inu ndi anthu anu, muferenji ndi lupanga, ndi njala, ndi mliri, zimene Yehova waopsezera mtundu wina uliwonse umene sudzatumikira mfumu ya ku Babuloni?
14 N'écoutez pas les paroles des prophètes qui vous disent: « Vous ne servirez pas le roi de Babylone », car ils vous prophétisent le mensonge.
Musamvere mawu a aneneri akamakuwuzani kuti, ‘Simudzatumikira mfumu ya ku Babuloni,’ chifukwa zimene akukuloseranizo nʼzabodza.
15 Car ce n'est pas moi qui les ai envoyés, dit Yahvé, mais ils prophétisent faussement en mon nom, afin que je vous chasse et que vous périssiez, vous et les prophètes qui vous prophétisent. »
Sindinawatume ngakhale iwo akulosera mʼdzina langa. Nʼchifukwa chake, ndidzakupirikitsani ndipo mudzawonongeka kotheratu, inu pamodzi ndi aneneri amene akunenera zabodza kwa inu.”
16 J'ai parlé aux prêtres et à tout ce peuple, en disant: « L'Éternel dit: N'écoutez pas les paroles de vos prophètes qui vous prophétisent en disant: « Voici que les ustensiles de la maison de l'Éternel vont bientôt être ramenés de Babylone », car ils vous prophétisent le mensonge.
Kenaka ndinawuza ansembe pamodzi ndi anthu ena onse kuti, “Yehova akuti: Musamvere aneneri amene akumanena kuti, ‘Posachedwapa ziwiya za mʼNyumba ya Yehova zibwera kuchokera ku Babuloni.’ Iwowo akunenera zabodza kwa inu.
17 Ne les écoutez pas. Servez le roi de Babylone, et vivez. Pourquoi cette ville deviendrait-elle une désolation?
Musawamvere. Tumikirani mfumu ya ku Babuloni, ndipo mudzakhala ndi moyo. Mzindawu usandukirenji bwinja?
18 Mais s'ils sont prophètes, et si la parole de l'Éternel est avec eux, qu'ils intercèdent maintenant auprès de l'Éternel des armées, afin que les objets qui restent dans la maison de l'Éternel, dans la maison du roi de Juda et à Jérusalem, n'aillent pas à Babylone.
Ngati iwo ndi aneneri ndipo ali ndi mawu a Yehova, apempheretu kwa Yehova Wamphamvuzonse kuti ziwiya zimene zatsala mʼNyumba ya Yehova ndi mʼnyumba ya mfumu ya Yuda ndiponso mu Yerusalemu zisatengedwe kupita ku Babuloni.
19 Car l'Éternel des armées dit, au sujet des colonnes, de la mer, des bases et du reste des ustensiles qui sont restés dans cette ville,
Pakuti Yehova akunena za zipilala, za mbiya ya madzi, maphaka ndi ziwiya zina zimene zatsala mu Yerusalemu.
20 et que Nebucadnetsar, roi de Babylone, n'a pas pris quand il emmena captif Jeconia, fils de Jehoïakim, roi de Juda, de Jérusalem à Babylone, et tous les nobles de Juda et de Jérusalem-
Izi ndi zimene Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni sanatenge pamene anatenga ukapolo Yekoniya mwana wa Yehoyakimu mfumu ya Yuda kupita ku Babuloni kuchokera ku Yerusalemu, pamodzi ndi anthu olemekezeka a ku Yuda ndi a ku Yerusalemu.
21 oui, Yahvé des armées, le Dieu d'Israël, dit au sujet des objets qui restent dans la maison de Yahvé, dans la maison du roi de Juda et à Jérusalem:
Inde, Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli, akunena za zinthu zimene zinatsala mʼNyumba ya Yehova ndi mʼnyumba ya mfumu ya Yuda ndi mu Yerusalemu kuti,
22 'Ils seront transportés à Babylone, et ils y resteront jusqu'au jour où je les visiterai, dit Yahvé; alors je les ferai remonter et je les rétablirai dans ce lieu'.'"
‘Zidzatengedwa kupita ku Babuloni ndipo zidzakhala kumeneko mpaka tsiku limene ndidzawakumbukirenso,’ akutero Yehova. ‘Pamenepo ndidzazitenganso ndi kuzibwezanso ku malo ano.’”