< Isaïe 59 >
1 Voici, la main de Yahvé n'est pas raccourcie au point de ne pas pouvoir sauver; ni son oreille émoussée, qu'elle ne puisse entendre.
Taonani, mkono wa Yehova si waufupi kuti sungathe kupulumutsa, kapena khutu lake kuti ndilogontha kuti sangamve.
2 Mais tes iniquités t'ont séparé de ton Dieu, et vos péchés vous ont caché sa face, pour qu'il n'entende pas.
Koma zoyipa zanu zakulekanitsani ndi Mulungu wanu; ndipo wakufulatirani chifukwa cha machimo anu, kotero Iye sadzamva.
3 Car vos mains sont souillées de sang, et tes doigts avec l'iniquité. Tes lèvres ont dit des mensonges. Ta langue murmure la méchanceté.
Pakuti manja anu ali psuu ndi magazi. Munayipitsa zala zanu ndi zamphulupulu. Pakamwa panu payankhula zabodza, ndipo lilime lanu lanena zinthu zoyipa.
4 Personne n'intente un procès en justice, et personne ne plaide en vérité. Ils font confiance à la vanité et dire des mensonges. Ils conçoivent des méfaits et donnent naissance à l'iniquité.
Palibe amene akuyimba mnzake mlandu molungama, palibe amene akupita ku mlandu moona mtima. Iwo amadalira mawu opanda pake ndipo amayankhula mabodza; amalingalira za mphulupulu ndipo amachita zoyipa.
5 Ils font éclore des œufs de loups et tisser la toile d'araignée. Celui qui mange de leurs œufs meurt; et ce qui est écrasé se transforme en vipère.
Iwo amayikira mazira a mamba ndipo amaluka ukonde wakangawude. Aliyense amene adzadya mazira awo adzafa, ndipo ngati dzira limodzi lasweka limatulutsa mphiri.
6 Leurs toiles ne deviendront pas des vêtements. Ils ne se couvriront pas de leurs œuvres. Leurs œuvres sont des œuvres d'iniquité, et les actes de violence sont entre leurs mains.
Ukonde wawo wa kangawude sangawuvale ngati chovala; ndipo chimene apangacho sangachifunde. Ntchito zawo ndi zoyipa, ndipo amakonda kuchita zandewu ndi manja awo.
7 Leurs pieds courent vers le mal, et ils se dépêchent de verser du sang innocent. Leurs pensées sont des pensées d'iniquité. La désolation et la destruction sont sur leur chemin.
Amathamangira kukachita zoyipa; sachedwa kupha anthu osalakwa. Maganizo awo ndi maganizo oyipa; kulikonse kumene amapita amasiyako bwinja ndi chiwonongeko.
8 Ils ne connaissent pas le chemin de la paix; et il n'y a pas de justice dans leurs manières. Ils se sont tracés des chemins tortueux; celui qui y entre ne connaît pas la paix.
Iwo sadziwa kuchita za mtendere; zonse zimene amachita nʼzopanda chilungamo. Njira zawo zonse nʼzokhotakhota; aliyense oyenda mʼnjira zimenezo sadzapeza mtendere.
9 C'est pourquoi la justice est loin de nous, et la justice ne nous rattrape pas. Nous cherchons la lumière, mais nous voyons les ténèbres; pour la clarté, mais nous marchons dans l'obscurité.
Anthu akuti, “Chifukwa cha zimenezi chilungamo chatitalikira; ndipo chipulumutso sichitifikira. Timafunafuna kuwala koma timangopeza mdima okhaokha; tinayembekezera kuyera koma timayenda mu mdima wandiweyani.
10 Nous tâtonnons vers le mur comme des aveugles. Oui, nous tâtonnons comme ceux qui n'ont pas d'yeux. Nous trébuchons à midi comme si c'était le crépuscule. Parmi ceux qui sont forts, nous sommes comme des hommes morts.
Timapapasapapasa khoma ngati munthu wosaona, kuyangʼanayangʼana njira ngati anthu opanda maso. Timapunthwa dzuwa lili paliwombo ngati kuti ndi usiku; timakhala pansi mu mdima ngati anthu akufa.
11 Nous rugissons tous comme des ours et gémissent tristement comme des colombes. Nous cherchons la justice, mais il n'y en a pas, pour le salut, mais il est loin de nous.
Tonse timabangula ngati zimbalangondo: Timalira modandaula ngati nkhunda. Tinayembekezera kuweruza kolungama; koma sitikupeza. Timayembekezera chipulumutso koma chimakhala nafe kutali.”
12 Car nos transgressions se sont multipliées devant toi, et nos péchés témoignent contre nous; car nos transgressions sont avec nous, et quant à nos iniquités, nous les connaissons:
Pakuti zolakwa zathu nʼzochuluka pamaso panu, ndipo machimo athu akutsutsana nafe. Zolakwa zathu zili ndi ife nthawi zonse ndipo tikuvomereza machimo athu:
13 transgressant et reniant Yahvé, et se détourner de notre Dieu, parlant d'oppression et de révolte, en concevant et en prononçant du cœur des paroles mensongères.
Tawukira ndi kumukana Yehova. Tafulatira Mulungu wathu, pa kupondereza anzathu ndi kupandukira Yehova, ndi pa kuyankhula mabodza amene tawaganiza mʼmitima mwathu.
14 La justice se détourne à reculons, et la droiture se tient loin; car la vérité est tombée dans la rue, et la droiture ne peut pas entrer.
Motero kuweruza kolungama kwalekeka ndipo choonadi chili kutali ndi ife; kukhulupirika sikukupezekanso mʼmabwalo a milandu, ndipo kuona mtima sikukupezekanso mʼmenemo.
15 Oui, la vérité fait défaut; et celui qui s'éloigne du mal devient une proie. Yahvé l'a vu, et il était mécontent qu'il n'y ait pas de justice.
Choonadi sichikupezeka kumeneko, ndipo wina akakana kuchita nawo zoyipa amapeza mavuto. Yehova anaziona zimenezi ndipo zinamunyansa kuti panalibe chiweruzo cholungama.
16 Il vit qu'il n'y avait pas d'homme, et s'est étonné qu'il n'y ait pas d'intercesseur. C'est donc son propre bras qui lui a apporté le salut; et sa justice l'a soutenu.
Yehova anaona kuti panalibe ndi mmodzi yemwe, Iye anadabwa kuti panalibe ndi mmodzi yemwe woti nʼkupembedzera; Choncho mphamvu zake zomwe zinamuthandiza, ndipo anadzilimbitsa ndi kulungama kwake;
17 Il s'est revêtu de la justice comme d'une cuirasse, et un casque de salut sur sa tête. Il a mis des vêtements de vengeance pour se vêtir, et était revêtu de zèle comme d'un manteau.
Iye anavala chilungamo ngati chovala chachitsulo chapachifuwa, ndipo kumutu kwake amavala chipewa chachipulumutso; anavala kulipsira ngati chovala ndipo anadzikuta ndi mkwiyo ngati chofunda.
18 Selon leurs actes, il remboursera le cas échéant: la colère de ses adversaires, la rétribution de ses ennemis. Il rendra aux îles leur dû.
Iye adzawabwezera chilango adani a anthu ake molingana ndi zimene anachita, adzaonetsa ukali kwa adani ake ndi kubwezera chilango odana naye. Adzalanga ngakhale okhala mayiko akutali.
19 Ainsi, ils craindront le nom de Yahvé depuis l'occident, et sa gloire dès le lever du soleil; car il viendra comme un torrent impétueux, que le souffle de Yahvé conduit.
Choncho akadzabwera ngati madzi oyendetsedwa ndi mphepo yamphamvu yamkuntho. Anthu onse kuyambira kumadzulo mpaka kummawa adzaopa dzina la Yehova ndi ulemerero wake.
20 « Un rédempteur viendra à Sion, et à ceux qui se détournent de la désobéissance en Jacob, dit Yahvé.
“Mpulumutsi adzabwera ku Ziyoni kudzapulumutsa anthu a fuko la Yakobo amene analapa machimo awo,” akutero Yehova.
21 « Quant à moi, voici mon alliance avec eux, dit Yahvé. « Mon Esprit qui est sur toi et mes paroles que j'ai mises dans ta bouche ne sortiront pas de ta bouche, ni de la bouche de ta descendance, ni de la bouche de la descendance de ta descendance, dit Yahvé, dès maintenant et pour toujours. »
Yehova akuti, “Kunena za pangano lake ndi iwo, Mzimu wanga umene uli pa inu, ndiponso mawu anga amene ndayika mʼkamwa mwanu sadzachoka mʼkamwa mwanu, kapena kuchoka mʼkamwa mwa ana anu, kapena mʼkamwa mwa zidzukulu zawo kuyambira tsopano mpaka kalekale,” akutero Yehova.