< Isaïe 32 >
1 Voici un roi qui régnera dans la justice, et les princes gouverneront dans la justice.
Taonani, kudzakhala mfumu ina imene idzalamulira mwachilungamo, ndipo akalonga ake adzaweruza molungama.
2 L'homme sera comme une cachette contre le vent, et un abri de la tempête, comme des ruisseaux d'eau dans un endroit sec, comme l'ombre d'un grand rocher dans une terre épuisée.
Munthu aliyense adzakhala ngati pothawirapo mphepo ndi malo obisalirapo namondwe, adzakhala ngati mitsinje ya mʼchipululu, ngati mthunzi wa thanthwe lalikulu la mʼdziko lowuma.
3 Les yeux de ceux qui voient ne s'obscurcissent pas, et les oreilles de ceux qui entendent écouteront.
Ndipo maso a anthu openya sadzakhalanso otseka, ndipo makutu a anthu akumva adzamvetsetsa.
4 Le cœur de l'impétueux comprendra la connaissance, et la langue des bègues sera prête à parler clairement.
Anthu a mtima wopupuluma adzadziwa ndi kuchita zinthu mofatsa, ndipo anthu ovutika kuyankhula adzayankhula mosadodoma ndi momveka.
5 L'insensé ne sera plus appelé noble, ni le scélérat être hautement respecté.
Chitsiru sichidzatchedwanso munthu waulemu wake ndipo munthu woyipa sadzalemekezedwa.
6 Car l'insensé dira des folies, et son cœur commettra l'iniquité, de pratiquer le blasphème, et de proférer des erreurs contre Yahvé, pour vider l'âme de ceux qui ont faim, et de faire manquer le breuvage des assoiffés.
Pakuti munthu opusa amayankhula zauchitsiru, amaganiza kuchita zoyipa: Iye amachita zoyipira Mulungu, ndipo amafalitsa zolakwika zokhudza Yehova; anjala sawapatsa chakudya ndipo aludzu sawapatsa madzi.
7 Les voies du scélérat sont mauvaises. Il élabore des plans méchants pour détruire les humbles par des paroles mensongères, même quand le nécessiteux parle juste.
Munthu woyipa njira zake ndi zoyipanso, iye kwake nʼkulingalira zinthu zoyipa. Amalingalira zakuti awononge anthu aumphawi ndi mabodza ake ngakhale kuti waumphawiyo akuyankhula zoona.
8 Mais le noble conçoit des choses nobles, et il continuera dans les choses nobles.
Koma munthu wolemekezeka amalingaliranso kuchita zinthu zabwino, Iye amakhazikika pa zinthu zabwinozo.
9 Levez-vous, femmes qui êtes à l'aise! Entendez ma voix! Filles insouciantes, écoutez mon discours!
Khalani maso, inu akazi amene mukungokhala wopanda kulingalira kuti kunja kulinji ndipo imvani mawu anga. Inu akazi odzitama, imvani zimene ndikunena!
10 Pendant des jours au-delà d'une année, vous serez troublées, femmes insouciantes; pour le millésime échouera. La récolte ne viendra pas.
Pakapita chaka ndi masiku pangʼono inu akazi amatama mudzanjenjemera; chifukwa mitengo ya mphesa idzakanika ndipo zipatso sizidzaoneka.
11 Tremblez, vous les femmes qui êtes à l'aise! Soyez inquiets, bande d'insouciants! Déshabillez-vous, mettez-vous à nu, et mettez un sac sur votre taille.
Nthunthumirani inu okhala mosatekesekanu; ndipo njenjemerani, inu akazi omadzikhulupirira nokhanu. Vulani zovala zanu, ndipo valani ziguduli mʼchiwuno mwanu.
12 Battez vos poitrines pour les champs agréables, pour la vigne féconde.
Dzigugudeni pachifuwa mwachisoni chifukwa minda yachonde, ndi mphesa yawonongeka.
13 Les épines et les ronces pousseront sur la terre de mon peuple; oui, sur toutes les maisons de joie de la ville joyeuse.
Mʼdziko la anthu anga mwamera minga ndi mkandankhuku. Zoona, mulilire nyumba zonse zachikondwerero ndi mzinda uno umene unali wachisangalalo.
14 Car le palais sera abandonné. La ville populeuse sera déserte. La colline et la tour de guet seront pour toujours des repaires, un délice pour les ânes sauvages, un pâturage de troupeaux,
Nyumba yaufumu idzasiyidwa, mzinda waphokoso udzakhala wopanda anthu; malinga ndi nsanja zidzasanduka chipululu mpaka muyaya. Abulu adzasangalalamo ndipo ziweto zidzapezamo msipu.
15 jusqu'à ce que l'Esprit soit répandu sur nous d'en haut, et le désert devient un champ fertile, et le champ fructueux est considéré comme une forêt.
Yehova adzatipatsa mzimu wake, ndipo dziko lachipululu lidzasanduka munda wachonde, ndipo munda wachonde udzakhala ngati nkhalango.
16 Alors la justice habitera dans le désert; et la justice restera dans le champ fructueux.
Tsono mʼchipululu mudzakhala chiweruzo cholungama ndipo mʼminda yachonde mudzakhala chilungamo.
17 L'œuvre de la justice sera la paix, et l'effet de la justice, la tranquillité et la confiance pour toujours.
Mtendere udzakhala chipatso chachilungamo; zotsatira za chilungamo zidzakhala bata ndi kudzidalira mpaka muyaya.
18 Mon peuple vivra dans une demeure paisible, dans des logements sûrs, et dans des lieux de repos tranquilles,
Anthu anga adzakhala mʼmidzi yamtendere, mʼnyumba zodalirika, ndi malo osatekeseka a mpumulo.
19 bien que la grêle aplatisse la forêt, et la ville est complètement rasée.
Ngakhale nkhalango idzawonongedwa ndi matalala ndipo mzinda udzagwetsedwa mpaka pansi,
20 Heureux ceux qui sèment près de toutes les eaux! qui envoie les pieds du bœuf et de l'âne.
inutu mudzakhala odalitsika ndithu. Mudzadzala mbewu zanu mʼmbali mwa mtsinje uliwonse, ndipo ngʼombe zanu ndi abulu anu zidzadya paliponse.