< Isaïe 23 >
1 Le fardeau de Tyr. Hurlez, navires de Tarsis! Car elle est dévastée, il n'y a plus de maison, plus d'entrée. C'est du pays de Kittim qu'il leur est révélé.
Uthenga wonena za Turo: Lirani mofuwula, inu oyendetsa sitima za pa madzi za ku Tarisisi: pakuti mzinda wa Turo wawonongedwa ndipo mulibe nyumba kapena dooko. Zimenezi anazimva pochokera ku Kitimu.
2 Soyez tranquilles, habitants de la côte, vous que les marchands de Sidon, qui passent par la mer, ont rassasiés.
Khalani chete inu anthu okhala mʼmbali mwa nyanja, inu amalonda a ku Sidoni, iwe amene unalemera ndi anthu oyenda pa nyanja.
3 Sur les grandes eaux, la semence du Shihor, la récolte du Nil, était son revenu. Elle était le marché des nations.
Pa nyanja zazikulu panabwera tirigu wa ku Sihori; zokolola za ku Nailo, ndipo munachita malonda ndi anthu a mitundu ina.
4 Honte à toi, Sidon! Car la mer a parlé, la forteresse de la mer, en disant: « Je n'ai pas enfanté, je n'ai pas accouché, je n'ai pas nourri de jeunes gens, je n'ai pas élevé de vierges. »
Chita manyazi, iwe Sidimu pakuti nyanja yayankhula, linga la ku nyanja (Turo) layankhula kuti, “Sindinamvepo zowawa za kubereka kapena kuberekapo mwana; sindinalerepo ana aamuna kapena kulera ana aakazi.”
5 Quand la nouvelle arrivera en Égypte, elle sera dans l'angoisse à la nouvelle de Tyr.
Mawuwa akadzamveka ku Igupto, iwo adzachita mantha akadzamva kuti Turo wawonongeka.
6 Passez à Tarsis! Gémissez, habitants de la côte!
Wolokerani ku Tarisisi, lirani mofuwula, inu anthu okhala mʼmbali mwa nyanja.
7 Est-ce là votre ville joyeuse, Dont l'antiquité est ancienne, Et dont les pieds l'ont portée au loin pour voyager?
Kodi uwu si mzinda wachisangalalo uja, mzinda wakalekale, umene anthu ake ankapita kukakhala ku mayiko akutali?
8 Qui a projeté cela contre Tyr, la dispensatrice de couronnes, dont les marchands sont des princes, dont les négociants sont les hommes d'honneur de la terre?
Kodi ndani anakonza zimenezi kuti zigwere Turo, mzinda umene unakhazikitsa mizinda ina, mzinda umene amalonda ake ndi akalonga ndi otchuka pa dziko lapansi?
9 L'Éternel des armées l'a projeté, pour souiller l'orgueil de toute gloire, pour mépriser tous les hommes d'honneur de la terre.
Yehova Wamphamvuzonse anakonza zimenezi kuti athetse kunyada kwawo ndi kutsitsa anthu otchuka a pa dziko lapansi.
10 Passe par ton pays comme le Nil, fille de Tarsis. Il n'y a plus de frein.
Mubalalike mʼdziko mwanu ngati mtsinje wa Nailo inu anthu a ku Tarisisi, pakuti mulibenso chokutetezani.
11 Il a étendu sa main sur la mer. Il a fait trembler les royaumes. Yahvé a ordonné la destruction des forteresses de Canaan.
Yehova watambasula dzanja lake kuloza ku nyanja ndipo wagwedeza maufumu ake. Iye walamula kuti Kanaani agwetse malinga ake.
12 Il a dit: « Tu ne te réjouiras plus, vierge opprimée, fille de Sidon. Lève-toi, passe à Kittim. Là aussi tu n'auras pas de repos. »
Iye anati, “Simudzakondwanso konse, inu anthu opanikizidwa a ku Sidoni, tsopano wamphwanyidwa! “Ngakhale muwolokere ku Kitimu, kumeneko simukapezako mpumulo.”
13 Voici le pays des Chaldéens. Ce peuple n'existait pas. Les Assyriens l'ont fondé pour ceux qui habitent dans le désert. Ils ont érigé leurs tours. Ils ont renversé ses palais. Ils en ont fait une ruine.
Onani dziko la Ababuloni, anthu amenewa tsopano atheratu! Asiriya asandutsa Turo kukhala malo a zirombo za ku chipululu; anamanga nsanja zawo za nkhondo, anagumula malinga ake ndipo anawasandutsa bwinja.
14 Hurlez, navires de Tarsis, car votre forteresse est détruite!
Lirani mofuwula, inu anthu oyendetsa sitima za pa madzi za ku Tarisisi; chifukwa malinga ako agwetsedwa!
15 En ce jour-là, Tyr sera oubliée pendant soixante-dix ans, selon les jours d'un seul roi. Au bout de soixante-dix ans, il en sera pour Tyr comme dans le chant de la prostituée.
Pa nthawi imeneyo Turo adzayiwalika pa zaka 70, amene ndi masiku a moyo wa mfumu. Koma potsiriza pa zaka 70 zimenezi, Turo adzakhala ngati mkazi wachiwerewere woyimbidwa mu nyimbo:
16 Prends une harpe, parcours la ville, prostituée oubliée. Fais des mélodies douces. Chantez beaucoup de chansons, afin qu'on se souvienne de vous.
“Tenga zeze wako uzungulire mzinda, iwe mkazi wachiwerewere woyiwalika; imba zeze mokometsera, imba nyimbo zambiri, kuti anthu akukumbukire.”
17 Au bout de soixante-dix ans, l'Éternel visitera Tyr. Elle retournera à son salaire et se prostituera avec tous les royaumes du monde sur la surface de la terre.
Pakutha pa zaka 70, Yehova adzachitapo kanthu pa Turo. Iye adzabwerera ku ntchito yake yakale monga mkazi wachiwerewere ndipo adzachita zachiwerewere ndi maufumu onse a dziko lapansi.
18 Sa marchandise et son salaire seront saints pour Yahvé. On n'en fera ni des trésors ni des réserves, car sa marchandise sera pour ceux qui habitent devant Yahvé, pour manger à leur faim et pour se vêtir durablement.
Koma phindu lake ndi malipiro ake adzazipereka kwa Yehova; sadzazikundika kapena kuzisunga. Phindu lake lidzapita kwa mtumiki wa Yehova kuti agule zakudya zambiri ndi zovala zokongola.