< Osée 1 >
1 Parole de Yahvé adressée à Osée, fils de Beéri, aux jours d'Ozias, de Jotham, d'Achaz et d'Ézéchias, rois de Juda, et aux jours de Jéroboam, fils de Joas, roi d'Israël.
Awa ndi mawu amene Yehova anayankhula kwa Hoseya mwana wa Beeri pa nthawi ya ulamuliro wa Uziya, Yotamu, Ahazi ndi Hezekiya, mafumu a ku Yuda ndiponso pa nthawi ya ulamuliro wa Yeroboamu mwana wa Yowasi mfumu ya ku Israeli.
2 Lorsque Yahvé parla d'abord par Osée, il dit à Osée: « Va, prends pour toi une femme de prostitution et des enfants d'infidélité; car le pays commet un grand adultère, en abandonnant Yahvé. »
Yehova atayamba kuyankhula kudzera mwa Hoseya, Yehova anati kwa Hoseyayo, “Pita kakwatire mkazi wachiwerewere ndipo ubereke naye ana mʼchiwerewere chake pakuti anthu a mʼdziko muno achimwa pochita chigololo choyipitsitsa, posiya Yehova.”
3 Et il alla prendre Gomer, fille de Diblaïm; et elle conçut, et lui donna un fils.
Motero Hoseya anakwatira Gomeri mwana wamkazi wa Dibulaimu, ndipo mkaziyo anakhala woyembekezera nabala mwana wamwamuna.
4 Yahvé lui dit: « Appelle-le du nom de Jizreel, pour un peu de temps encore, et je vengerai le sang de Jizreel sur la maison de Jéhu, et je ferai cesser le règne de la maison d'Israël.
Tsono Yehova anati kwa Hoseya, “Umutche dzina loti Yezireeli, pakuti ndili pafupi kulanga banja la Yehu chifukwa cha anthu amene anawapha ku Yezireeli ndipo ndidzathetsa ufumu wa Israeli.
5 Il arrivera en ce jour-là que je briserai l'arc d'Israël dans la vallée de Jizreel. »
Tsiku limenelo ndidzathyola uta wa Israeli mʼchigwa cha Yezireeli.”
6 Elle conçut de nouveau, et enfanta une fille. Et il lui dit: « Appelle-la du nom de Lo-Ruhamah, car je n'aurai plus pitié de la maison d'Israël, et je ne leur pardonnerai plus d'aucune manière.
Gomeri anakhala woyembekezeranso ndipo anabereka mwana wamkazi. Ndipo Yehova anati kwa Hoseya, “Umutche dzina loti ‘Sakondedwa’ pakuti sindidzaonetsanso chikondi changa pa nyumba ya Israeli, kuti ndingawakhululukire konse.
7 Mais j'aurai pitié de la maison de Juda, et je les sauverai par Yahvé, leur Dieu, et je ne les sauverai ni par l'arc, ni par l'épée, ni par la bataille, ni par les chevaux, ni par les cavaliers. »
Komatu ndidzaonetsa chikondi pa nyumba ya Yuda; ndipo ndidzawapulumutsa, osati ndi uta, lupanga kapena nkhondo, kapena akavalo ndi okwerapo ake, koma ine Yehova Mulungu wawo ndidzawapulumutsa.”
8 Or, lorsqu'elle eut sevré Lo-Ruhamah, elle conçut et enfanta un fils.
Sakondedwa ataleka kuyamwa, Gomeri anabereka mwana wina wamwamuna.
9 Il dit: « Appelle-le Lo-Ammi, car vous n'êtes pas mon peuple, et je ne serai pas le vôtre.
Pamenepo Yehova anati, “Umutche dzina loti Sianthuanga,” pakuti inu si ndinu anthu anga ndipo Ine si ndine Mulungu wanu.
10 Mais le nombre des enfants d'Israël sera comme le sable de la mer, qui ne peut être ni mesuré ni compté; et là où on leur a dit: « Vous n'êtes pas mon peuple », on les appellera « fils du Dieu vivant ».
“Komabe Aisraeli adzachuluka ngati mchenga wa mʼmbali mwa nyanja umene sangathe kuwuyeza kapena kuwuwerenga. Pamalo omwe ananena kuti, ‘Sindinu anthu anga,’ pomweponso adzawatchula kuti ‘Ana a Mulungu wamoyo.’
11 Les enfants de Juda et les enfants d'Israël s'assembleront, ils se donneront une tête, et ils monteront du pays; car grand sera le jour de Jizreel.
Anthu a ku Yuda ndi anthu a ku Israeli adzasonkhananso pamodzi ndipo adzasankha mtsogoleri mmodzi ndi kutuluka mʼdzikomo, pakuti tsiku la Yezireeli lidzakhala lalikulu kwambiri.”