< Daniel 5 >

1 Le roi Belschatsar fit un grand festin à mille de ses seigneurs, et il but du vin en leur présence.
Tsiku lina mfumu Belisazara anakonza phwando lalikulu la akalonga ake 1,000 ndipo anamwa vinyo pamodzi ndi iwo.
2 Pendant qu'il buvait le vin, Belschatsar ordonna qu'on lui apportât les vases d'or et d'argent que Nabuchodonosor, son père, avait enlevés du temple de Jérusalem, afin que le roi et ses grands, ses femmes et ses concubines, en boivent.
Pamene Belisazara ankamwa vinyo, analamula kuti ziwiya zagolide ndi zasiliva zimene Nebukadinezara abambo ake anakatenga mʼNyumba ya Mulungu ku Yerusalemu zikatengedwe kuti mfumu ndi akalonga ake, akazi ake ndi azikazi amweremo.
3 On apporta les vases d'or qui avaient été pris dans le temple de la maison de Dieu à Jérusalem, et le roi et ses grands, ses femmes et ses concubines, en burent.
Choncho anabweretsa ziwiya zagolide zimene anazitenga mʼNyumba ya Mulungu; ndipo mfumu ndi akalonga ake, akazi ake ndi azikazi ake anamweramo.
4 Ils burent du vin, et louèrent les dieux d'or, d'argent, d'airain, de fer, de bois et de pierre.
Akumwa vinyo, anatamanda milungu yagolide ndi siliva, yamkuwa, chitsulo, yamtengo ndi mwala.
5 A la même heure, les doigts de la main d'un homme sortirent et écrivirent près du chandelier, sur le plâtre du mur du palais du roi. Le roi vit la partie de la main qui écrivait.
Mwadzidzidzi zala za dzanja la munthu zinaonekera ndi kulemba pa khoma, pafupi ndi choyikapo nyale mʼnyumba yaufumu. Mfumu inapenyetsetsa dzanjalo pamene limalemba.
6 Alors le visage du roi fut changé, et ses pensées le troublèrent; les articulations de ses cuisses se relâchèrent, et ses genoux se heurtèrent l'un contre l'autre.
Nkhope yake inasandulika ndipo inachita mantha, nkhongono zii, mawondo gwedegwede.
7 Le roi cria à haute voix de faire venir les enchanteurs, les Chaldéens et les devins. Le roi prit la parole et dit aux sages de Babylone: « Celui qui lira cet écrit et m'en montrera l'interprétation sera vêtu de pourpre, aura une chaîne d'or au cou, et sera le troisième chef du royaume. »
Mfumu inafuwula kuyitana owombeza, alawuli ndi amawula kuti abwere. Ndipo anawawuza anthu anzeru a ku Babuloni kuti, “Aliyense amene awerenge malembawa ndi kundiwuza tanthauzo lake adzavekedwa chovala cha pepo ndi mkanda wa golide udzavekedwa mʼkhosi mwake, ndipo adzakhala wolamulira wachitatu mu ufumuwu.”
8 Alors tous les sages du roi entrèrent; mais ils ne purent lire l'écriture, et ne purent faire connaître au roi l'interprétation.
Pamenepo anzeru onse a mfumu anabwera, koma sanakwanitse kuwerenga malembawo kapena kumutanthauzira mfumu.
9 Alors le roi Belschatsar fut grandement troublé, et son visage fut changé en lui, et ses seigneurs furent perplexes.
Choncho mfumu Belisazara anachita mantha koposa ndipo nkhope yake inapitirira kusinthika. Akalonga ake anathedwa nzeru.
10 La reine, à cause des paroles du roi et de ses seigneurs, entra dans la maison du banquet. La reine prit la parole et dit: « O roi, vis à jamais; que tes pensées ne te troublent pas, et que ton visage ne change pas.
Mfumukazi, pakumva mawu a mfumu ndi akalonga ake, analowa mʼchipinda cha phwando ndipo anati, “Mfumu mukhale ndi moyo wautali! Musavutike! Nkhope yanu isasinthike!
11 Il y a dans ton royaume un homme dans lequel se trouve l'esprit des dieux saints; aux jours de ton père, on trouvait en lui la lumière, l'intelligence et la sagesse, comme la sagesse des dieux. Le roi Nebucadnetsar, ton père - oui, le roi, ton père - l'a établi maître des magiciens, des enchanteurs, des Chaldéens et des devins,
Pali munthu wina mu ufumu wanu uno amene mwa iye muli mzimu wa milungu yoyera. Pa nthawi ya ulamuliro wa abambo anu iye anapezeka kuti ali ndi chidziwitso, luntha ndi nzeru zonga za milungu. Mfumu Nebukadinezara, abambo anu, Ine ndikukuwuzani anamusankha iye kukhala mkulu wa amatsenga, owombeza, alawuli ndi amawula.
12 parce qu'un esprit excellent, de la connaissance, de l'intelligence, l'interprétation des songes, la révélation des phrases obscures et la dissolution des doutes se trouvaient dans le même Daniel, que le roi a appelé Beltschatsar. Qu'on appelle maintenant Daniel, et il donnera l'interprétation. »
Munthu ameneyu dzina lake ndi Danieli, koma mfumu inamutcha Belitesezara ndipo ali ndi nzeru zapadera, ndi wodziwa ndi kuzindikira zinthu, ndiponso luso lakutanthauzira maloto, kufotokozera miyambi ndi kuthetsa mavuto osautsa. Muyitaneni Danieli, ndipo adzakuwuzani chomwe mawuwa akutanthauza.”
13 Alors Daniel fut amené devant le roi. Le roi prit la parole et dit à Daniel: « Es-tu ce Daniel des fils de la captivité de Juda, que le roi mon père a fait sortir de Juda?
Choncho anabwera naye Danieli pamaso pa mfumu ndipo inati kwa iye, “Kodi ndiwe Danieli, mmodzi mwa akapolo omwe abambo anga mfumu anabwera nawo kuchoka ku Yuda?
14 J'ai entendu dire de toi que l'esprit des dieux est en toi et que la lumière, l'intelligence et une excellente sagesse se trouvent en toi.
Ndamva kuti mzimu wa milungu uli mwa iwe ndi kuti uli ndi chidziwitso, luntha ndi nzeru zapadera.
15 Or, on a fait venir devant moi les sages, les enchanteurs, pour qu'ils lisent cette écriture et m'en donnent l'interprétation; mais ils n'ont pas pu donner l'interprétation de la chose.
Anzeru ndi owombeza anabwera pamaso panga kuti awerenge zolembedwazi ndi kundiwuza tanthauzo lake koma sanakwanitse kundifotokozera.
16 Mais j'ai entendu dire de toi que tu peux donner des interprétations et dissiper les doutes. Maintenant, si tu peux lire l'écriture et me faire connaître son interprétation, tu seras vêtu de pourpre, tu auras une chaîne d'or à ton cou, et tu seras le troisième chef du royaume. »
Tsopano ndamva kuti iwe ukhoza kupereka matanthauzo ndi kuthetsa mavuto. Ngati ungawerenge zolembedwazi ndi kundiwuza tanthauzo lake, udzavekedwa chovala cha pepo ndi kuyikidwa mkanda wa golide mʼkhosi mwako, ndipo udzakhala wolamulira wachitatu mu ufumu uno.”
17 Alors Daniel prit la parole devant le roi: « Que tes dons soient pour toi, et que tes récompenses soient pour un autre. Néanmoins, je lirai l'écriture au roi, et je lui ferai connaître l'interprétation.
Pamenepo Danieli anayankha mfumu kuti, “Inu musunge mphatso zanuzo kwa inu nokha ndipo mupereke mphothoyo kwa wina aliyense. Komabe ine ndi kuwerengerani malembawa mfumu; ndikukuwuzani tanthauzo lake.
18 « A toi, roi, le Dieu Très-Haut a donné à Nabuchodonosor, ton père, le royaume, la grandeur, la gloire et la magnificence.
“Inu mfumu, Mulungu Wammwambamwamba anapatsa abambo anu Nebukadinezara mphamvu ndi ukulu ndi ulemerero ndi ufumu.
19 A cause de la grandeur qu'il lui a donnée, tous les peuples, toutes les nations et toutes les langues ont tremblé et ont eu peur devant lui. Il tuait qui il voulait, et il faisait vivre qui il voulait. Il élevait qui il voulait, et il abaissait qui il voulait.
Chifukwa cha udindo waukulu umene anapatsidwanso, anthu onse ndi mitundu ndi anthu aziyankhulo zosiyanasiyana ankanjenjemera ndikumuopa iye. Amene mfumu inafuna anawaphadi; amene inafuna kuwasunga, inawasunga; amene inafuna kuwakweza, inawakweza; ndipo amene inafuna kuwatsitsa, inawatsitsa.
20 Mais comme son cœur s'élevait et que son esprit s'endurcissait au point de s'enorgueillir, il fut déchu de son trône royal, et on lui ôta sa gloire.
Koma pamene inayamba kudzitama ndi kuwumitsa mtima wake ndi kuyamba kunyada, inachotsedwa pa mpando wake waufumu ndi kulandidwa ulemerero wake.
21 Il fut chassé des fils de l'homme, et son cœur devint semblable à celui des animaux, et sa demeure fut avec les ânes sauvages. Il était nourri d'herbe comme les bœufs, et son corps était mouillé de la rosée du ciel, jusqu'à ce qu'il sache que le Dieu Très-Haut règne sur le royaume des hommes, et qu'il y établit qui il veut.
Iyo inachotsedwa pakati pa anthu ndi kupatsidwa mtima ngati wa nyama; inakhala pamodzi ndi abulu akutchire ndi kudya udzu ngati ngʼombe; ndipo thupi lake linanyowa ndi mame akumwamba, mpaka pamene anavomereza kuti Mulungu Wammwambamwamba ndiye wolamulira maufumu a anthu ndipo amawupereka kwa aliyense amene Iye wafuna.
22 « Toi, son fils Belschatsar, tu n'as pas humilié ton cœur, bien que tu aies su tout cela,
“Koma inu mwana wake, Belisazara, simunadzichepetse, ngakhale kuti mumadziwa zonsezi.
23 mais tu t'es élevé contre le Seigneur des cieux; on a apporté devant toi les vases de sa maison, et toi et tes grands, tes femmes et tes concubines, vous en avez bu le vin. Tu as loué les dieux d'argent et d'or, d'airain, de fer, de bois et de pierre, qui ne voient pas, n'entendent pas et ne savent pas; et tu n'as pas glorifié le Dieu dans la main duquel est ton souffle, et dans la main duquel sont toutes tes voies.
Mʼmalo mwake, mwadzikweza nokha kutsutsana ndi Ambuye wakumwamba. Inu mwatenga ziwiya za mʼNyumba mwake, ndipo inu ndi akalonga anu, akazi anu ndi azikazi anu mwamwera vinyo mu zimenezi. Inu munatamanda milungu yasiliva ndi golide, yamkuwa, chitsulo, mtengo ndi mwala, imene singaone kapena kumva kapena kuzindikira. Koma simunamupatse ulemu Mulungu amene asunga mʼmanja mwake moyo wanu ndi njira zanu zonse.
24 Alors la partie de la main fut envoyée de devant lui, et cette écriture fut inscrite.
Choncho Iye watumiza dzanja limene lalemba mawu amenewa.
25 « Voici l'écriture qui a été inscrite: « MENE, MENE, TEKEL, UPHARSIN.
“Mawu amene analembedwa ndi awa: MENE, MENE, TEKELI, PARASINI.
26 « Voici l'interprétation de la chose: MENE: Dieu a compté votre royaume, et y a mis fin.
“Zimene mawuwa akutanthauza ndi izi:
27 TEKEL: vous êtes pesés dans la balance, et vous êtes trouvés déficients.
Tekeli: Inu mwayesedwa pa sikelo ndipo mwapezeka kuti mukuperewera.
28 PERES: votre royaume est divisé et donné aux Mèdes et aux Perses. »
Parasini: Ufumu wanu wagawidwa ndi kupatsidwa kwa Amedi ndi Aperezi.”
29 Belschatsar ordonna qu'on habille Daniel de pourpre, qu'on lui mette au cou un collier d'or et qu'on annonce qu'il sera le troisième chef du royaume.
Mwa lamulo la Belisazara, Danieli anavekedwa chovala cha pepo, mkanda wagolide unayikidwa mʼkhosi mwake, ndipo analengeza kuti anali wachitatu mu ulamuliro mu ufumuwo.
30 Cette nuit-là, Belschatsar, roi des Chaldéens, fut tué.
Usiku womwewo Belisazara, mfumu ya anthu a ku Babuloni, inaphedwa,
31 Darius le Mède reçut le royaume, âgé d'environ soixante-deux ans.
ndipo Dariyo Mmedi analanda ufumuwo ali ndi zaka 62.

< Daniel 5 >