< 2 Rois 6 >

1 Les fils des prophètes dirent à Élisée: « Voici, le lieu où nous habitons et où nous nous réunissons avec toi est trop petit pour nous.
Ana a aneneri anati kwa Elisa, “Taonani malo amene timakhala ndi inu atichepera kwambiri.
2 Je t'en prie, allons jusqu'au Jourdain, et que chacun prenne une poutre de là, et que nous nous fassions là un lieu où nous pourrons vivre. » Il a répondu: « Vas-y! »
Tiloleni tipite ku Yorodani kumene aliyense wa ife akadule mtengo umodzi, kuti timange malo woti tizikhalamo.” Ndipo Elisa anati, “Pitani.”
3 L'un d'eux dit: « Je vous prie de bien vouloir accompagner vos serviteurs. » Il répondit: « Je vais y aller. »
Mmodzi wa iwo anati, “Chonde mulole kutsagana nawo atumiki anu.” Elisa anayankha kuti, “Ndipita nanu.”
4 Il partit donc avec eux. Lorsqu'ils arrivèrent au Jourdain, ils coupèrent du bois.
Ndipo anapita nawo. Anapita ku Yorodani nayamba kudula mitengo.
5 Mais comme l'un d'eux abattait un arbre, la tête de la hache tomba dans l'eau. Alors il s'écria: « Hélas, mon maître! Car il a été emprunté. »
Pamene wina ankadula mtengo, nkhwangwa yake inaguluka nigwera mʼmadzi. Iye anafuwula kuti, “Mayo! Mbuye wanga! Popeza ndi yobwereka!”
6 L'homme de Dieu demanda: « Où est-elle tombée? » Il lui montra l'endroit. Il coupa un bâton, le jeta dedans et fit flotter le fer.
Ndipo munthu wa Mulungu uja anafunsa, “Yagwera pati?” Pamene anamuonetsa malowo, Elisa anadula kamtengo nakaponya pamenepo, ndipo nkhwangwayo inayandama.
7 Il dit: « Prends-le. » Il tendit la main et le prit.
Elisa anati, “Itenge.” Ndipo munthuyo anatambalitsa dzanja lake nayitenga.
8 Or le roi de Syrie était en guerre contre Israël; il tenait conseil avec ses serviteurs, disant: « Mon camp sera dans tel ou tel endroit. »
Tsono mfumu ya ku Aramu inali pa nkhondo ndi Israeli. Itakambirana ndi atsogoleri ake ankhondo inati, “Ndidzamanga misasa yanga pamalo akutiakuti.”
9 L'homme de Dieu envoya dire au roi d'Israël: « Prends garde de ne pas passer par ce lieu, car les Syriens y descendent. »
Munthu wa Mulungu anatumiza mawu kwa mfumu ya ku Israeli kuti “Musamale podutsa malo akuti, chifukwa Aaramu akupita kumeneko.”
10 Le roi d'Israël se rendit au lieu que l'homme de Dieu lui avait indiqué et dont il l'avait averti, et il s'y sauva, ni une fois ni deux.
Choncho mfumu ya ku Israeli inatuma anthu kumalo kumene munthu wa Mulunguyo ananena. Nthawi ndi nthawi Elisa ankachenjeza mfumu, kotero kuti ankakhala tcheru ku malo amenewo.
11 Le cœur du roi de Syrie fut très troublé à ce sujet. Il appela ses serviteurs et leur dit: « Ne me montrerez-vous pas lequel d'entre nous est pour le roi d'Israël? »
Zimenezi zinakwiyitsa kwambiri mfumu ya ku Aramu. Mfumuyo inayitanitsa atsogoleri ake ankhondo ndipo inawafunsa kuti, “Kodi simungandiwuze munthu amene pakati pathu pano ali mbali ya mfumu ya ku Israeli?”
12 Un de ses serviteurs dit: « Non, mon seigneur, ô roi; mais Élisée, le prophète qui est en Israël, rapporte au roi d'Israël les paroles que tu prononces dans ta chambre. »
Mmodzi mwa atsogoleri a ankhondowo anati, “Palibe ndi mmodzi yemwe pakati pathu, inu mbuye wanga, koma Elisa mneneri amene ali ku Israeli amawuza mfumu ya ku Israeli mawu enieni amene inu mumayankhula ku chipinda kwanu.”
13 Il dit: « Va voir où il est, afin que j'envoie le chercher. » On lui a dit: « Voici, il est à Dothan. »
Choncho mfumu inalamula kuti, “Pitani, kafufuzeni kumene akukhala kuti ine nditume anthu kukamugwira.” Anthuwo anabweretsa mawu oti, “Taonani, Elisa ali ku Dotani.”
14 Il y envoya donc des chevaux, des chars et une grande armée. Ils arrivèrent de nuit et entourèrent la ville.
Ndipo mfumu inatumizako magaleta ndi akavalo ndiponso gulu lankhondo lamphamvu. Anapita usiku nakawuzungulira mzindawo.
15 Le serviteur de l'homme de Dieu s'était levé tôt et était sorti, et voici qu'une armée avec des chevaux et des chars entourait la ville. Son serviteur lui dit: « Hélas, mon maître! Que ferons-nous? »
Mtumiki wa munthu wa Mulungu atadzuka mmamawa ndi kutuluka panja, gulu la ankhondo pamodzi ndi akavalo ndi magaleta anali atazungulira mzindawo. Mtumikiyo anafunsa kuti, “Kalanga mbuye wanga, tidzachita chiyani?”
16 Il répondit: « N'aie pas peur, car ceux qui sont avec nous sont plus nombreux que ceux qui sont avec eux. »
Mneneri anamuyankha kuti, “Usachite mantha. Amene ali mbali yathu ndi ambiri kupambana amene ali mbali yawo.”
17 Élisée pria et dit: « Yahvé, ouvre-lui les yeux, afin qu'il voie. » Yahvé ouvrit les yeux du jeune homme, et il vit; et voici que la montagne était pleine de chevaux et de chars de feu autour d'Elisée.
Ndipo Elisa anapemphera kuti, “Inu Yehova tsekulani maso ake kuti aone.” Pamenepo Yehova anatsekula maso a mtumikiyo, ndipo anayangʼana naona kuti phiri lonse linali lodzaza ndi akavalo ndi magaleta a moto atazungulira Elisa.
18 Lorsqu'ils descendirent vers lui, Élisée pria Yahvé et dit: « Je te prie de frapper ce peuple de cécité. » Il les a frappés de cécité selon la parole d'Elisée.
Pamene adaniwo ankabwera kudzalimbana naye, Elisa anapemphera kwa Yehova kuti, “Achititseni khungu anthu awa.” Kotero Yehova anawachititsa khungu monga anapemphera Elisa.
19 Élisée leur dit: « Ce n'est pas ici le chemin, et ce n'est pas ici la ville. Suivez-moi, et je vous conduirai à l'homme que vous cherchez. » Il les conduisit en Samarie.
Elisa anawawuza ankhondowo kuti, “Njira si imeneyi ndipo mzinda sumenewunso. Tsateni, ndipo ndidzakutengerani kwa munthu amene mukumufunayo.” Ndipo anawatengera ku Samariya.
20 Lorsqu'ils furent entrés dans la Samarie, Élisée dit: « Yahvé, ouvre les yeux de ces hommes, afin qu'ils voient. » Yahvé leur ouvrit les yeux, et ils virent; et voici, ils étaient au milieu de la Samarie.
Atalowa mu mzinda wa Samariya, Elisa anati, “Yehova tsekulani maso a anthu awa kuti aone.” Choncho Yehova anatsekula maso awo ndipo anangoona kuti ali mʼkati mwenimweni mwa Samariya.
21 Le roi d'Israël dit à Élisée, lorsqu'il les vit: « Mon père, dois-je les frapper? Dois-je les frapper? »
Mfumu ya ku Israeli itawaona, inafunsa Elisa kuti, “Abambo anga, kodi ndiwaphe? Kodi ndiwaphe?”
22 Il répondit: « Tu ne les frapperas pas. Frapperais-tu de ton épée et de ton arc ceux que tu as emmenés en captivité? Mets devant eux du pain et de l'eau, qu'ils mangent et boivent, puis va chez ton maître. »
Elisa anayankha kuti, “Musawaphe. Kodi mungaphe anthu amene munawagwira pogwiritsa ntchito lupanga ndi uta? Apatseni chakudya ndi madzi kuti adye ndi kumwa kenaka apite kwa mbuye wawo.”
23 Il leur prépara un grand festin. Après qu'ils eurent mangé et bu, il les renvoya et ils s'en allèrent chez leur maître. Ainsi, les bandes de Syrie cessèrent d'attaquer le pays d'Israël.
Choncho anawakonzera mphwando lalikulu, ndipo atatsiriza kudya ndi kumwa, anawatumiza kwawo ndipo anabwerera kwa mbuye wawo. Kotero magulu a ankhondo a ku Aramu analeka kuthira nkhondo dziko la Israeli.
24 Après cela, Benhadad, roi de Syrie, rassembla toute son armée, monta et assiégea Samarie.
Patapita nthawi, Beni-Hadadi mfumu ya Aramu anasonkhanitsa gulu lake lonse la ankhondo, napita kukazungulira mzinda wa Samariya.
25 Il y eut une grande famine à Samarie. On l'assiégea jusqu'à ce qu'on vendît la tête d'un âne pour quatre-vingts pièces d'argent et le quart d'un kab de fumier de colombe pour cinq pièces d'argent.
Mu mzinda wa Samariya munali njala yoopsa. Ndipo taonani, Aaramu anazungulira mzindawu kwa nthawi yayitali kotero kuti mutu wa bulu ankawugulitsa ndalama za siliva 80, ndipo magalamu 200 a zitosi za nkhunda ankawagulitsa pa mtengo wa masekeli asanu.
26 Comme le roi d'Israël passait sur la muraille, une femme lui cria: « Au secours, mon seigneur, ô roi! »
Pamene mfumu inkayenda pa khoma la mzindawo, mayi wina anafuwulira mfumuyo kuti, “Thandizeni mbuye wanga mfumu!”
27 Il dit: « Si Yahvé ne te secourt pas, où pourrais-je trouver du secours pour toi? De l'aire de battage, ou du pressoir? »
Mfumu inayankha kuti, “Ngati Yehova sakuthandiza iwe, ine thandizo lako ndingalipeze kuti? Kuchokera ku malo opunthira tirigu kodi? Kuchokera kumalo opsinyira mphesa kodi?”
28 Alors le roi lui demanda: « Quel est ton problème? » Elle répondit: « Cette femme m'a dit: 'Donne ton fils, pour que nous le mangions aujourd'hui, et nous mangerons mon fils demain'.
Pamenepo mfumuyo inafunsa mayiyo kuti, “Kodi chakuvuta nʼchiyani?” Iye anayankha kuti, “Mayi uyu anandiwuza kuti, ‘Bweretsa mwana wako kuti timudye lero, ndipo mawa tidzadya mwana wangayu.’
29 Nous avons donc fait bouillir mon fils et nous l'avons mangé; et le lendemain, je lui ai dit: 'Donne ton fils, pour que nous le mangions'; et elle a caché son fils. »
Choncho tinaphika mwana wanga ndi kumudya. Tsiku lotsatira lakelo ine ndinati, ‘Bweretsa mwana wako kuti timudye,’ koma iye anabisa mwana wakeyo.”
30 Lorsque le roi entendit les paroles de la femme, il déchira ses vêtements. Or il passait sur la muraille, et le peuple regardait, et voici, il avait un sac en dessous de son corps.
Mfumu itamva mawu a mayiyo, inangʼamba mkanjo wake. Pamene inkayenda pa khoma, anthu anayangʼana, ndipo anaona zovala zamʼkati, pakuti anavala chiguduli.
31 Alors il dit: « Que Dieu me fasse ainsi, et plus encore, si la tête d'Élisée, fils de Shaphat, reste aujourd'hui sur lui. »
Mfumuyo inati, “Mulungu andilange, andilange kwambiri ndikapanda kudula mutu wa Elisa mwana wa Safati lero!”
32 Mais Élisée était assis dans sa maison, et les anciens étaient assis avec lui. Le roi envoya un homme de devant lui; mais avant que le messager n'arrive, il dit aux anciens: « Voyez-vous comment ce fils de meurtrier a envoyé enlever ma tête? Voici, quand le messager viendra, fermez la porte, et maintenez la porte fermée contre lui. Le bruit des pieds de son maître n'est-il pas derrière lui? »
Tsono Elisa nʼkuti atakhala mʼnyumba mwake, ndipo akuluakulu anali naye limodzi. Mfumu inatuma munthu wina kuti imutsogolere, koma asanafike, Elisa anawuza akuluakuluwo kuti, “Kodi simukuona momwe wopha munthu uja watumizira munthu wina kuti adzadule mutu wanga? Taonani mthengayo akafika, mutseke chitseko ndipo muchigwiritsitse kuti asalowe. Kodi ndikumvawo pambuyo pake si mgugu wa mbuye wake?”
33 Comme il parlait encore avec eux, voici que le messager descendit vers lui. Et il dit: « Voici, ce malheur vient de Yahvé. Pourquoi attendrais-je Yahvé plus longtemps? »
Elisa akuyankhulabe ndi anthuwo, taonani, wamthengayo anafika kwa iye. Ndipo mfumu inati, “Mavuto amenewa ndi ochokera kwa Yehova. Kodi nʼchifukwa chiyani ine ndiyenera kudikira thandizo lochokera kwa Yehova?”

< 2 Rois 6 >