< 2 Rois 11 >

1 Et lorsque Athalie, mère d'Achazia, vit que son fils était mort, elle se leva et fit périr toute la descendance royale.
Ataliya amayi ake a Ahaziya ataona kuti mwana wawo wafa, ananyamuka nakawononga banja lonse la mfumu.
2 Mais Jéhoschéba, fille du roi Joram, sœur d'Achazia, prit Joas, fils d'Achazia, et l'enleva du milieu des fils du roi qui avaient été tués, lui et sa nourrice, et les mit dans la chambre à coucher; et elles le cachèrent à Athalie, afin qu'il ne fût pas tué.
Koma Yehoseba, mwana wamkazi wa Mfumu Yehoramu, mlongo wake wa Ahaziya, anatenga Yowasi mwana wa Ahaziya, namusunga kutali ndi ana a mfumu amene ankati awaphewo. Anamuyika iye pamodzi ndi mlezi wake mʼchipinda chogona chamʼkati kubisira Ataliya kotero iye sanaphedwe.
3 Il resta caché avec elle dans la maison de Yahvé pendant six ans, pendant qu'Athalie régnait sur le pays.
Mwanayo anakhala mobisala pamodzi ndi mlezi wake mʼnyumba ya Yehova kwa zaka zisanu ndi chimodzi pamene Ataliya ankalamulira dzikolo.
4 La septième année, Jehojada envoya chercher les chefs de centaines de Carites et de la garde, et les fit venir auprès de lui dans la maison de l'Éternel; il fit alliance avec eux, dans la maison de l'Éternel, et leur montra le fils du roi.
Koma mʼchaka chachisanu ndi chiwiri, Yehoyada anatumiza mawu kukayitana atsogoleri olamulira asilikali 100 olondera mfumu ndiponso alonda olonda nyumba yaufumu ndipo anabwera nawo mʼNyumba ya Yehova. Iye anapangana nawo pangano ndipo anawalumbiritsa mʼnyumba ya Yehova. Kenaka anawaonetsa mwana wamwamuna wa mfumu uja.
5 Il leur donna cet ordre: « Voici ce que vous devez faire: un tiers d'entre vous, qui entre le jour du sabbat, sera chargé de la garde de la maison du roi;
Yehoyada anawalamulira kuti, “Chimene muti muchite ndi ichi: Inu magulu atatu amene muti mudzakhale pa ntchito tsiku la Sabata, gulu loyamba lidzalondera nyumba ya mfumu,
6 un tiers d'entre vous sera à la porte Sur; et un tiers d'entre vous à la porte derrière la garde. Vous veillerez ainsi sur la maison, et vous formerez une barrière.
gulu lachiwiri lidzalondera Chipata cha Suri, ndipo gulu lachitatu lidzalondera chipata cha kumbuyo kwa asilikali amene amasinthana polondera nyumbayo.
7 Les deux compagnies d'entre vous, tous ceux qui sortent le jour du sabbat, surveilleront la maison de l'Éternel autour du roi.
Ndipo inu amene muli mʼmagulu ena awiri amene simugwira ntchito pa tsiku la Sabata, nonse mudzalondere mfumu ku nyumbayo.
8 Vous entourerez le roi, chacun l'arme à la main, et celui qui entrera dans les rangs sera tué. Soyez avec le roi quand il sortira et quand il entrera. »
Mudzakhale mozungulira mfumuyo, munthu aliyense ali ndi chida mʼmanja mwake. Wina aliyense amene adzakuyandikireni adzayenera kuphedwa. Muzikhala pafupi ndi mfumu kulikonse kumene ikupita.”
9 Les chefs de centaines firent tout ce que le prêtre Jehojada avait ordonné; ils prirent chacun leurs hommes, ceux qui devaient entrer le jour du sabbat et ceux qui devaient sortir le jour du sabbat, et ils vinrent auprès du prêtre Jehojada.
Atsogoleri olamulira asilikali 100 aja anachitadi zonse monga analamulira wansembe Yehoyada. Aliyense anatenga anthu ake, iwo amene amakagwira ntchito pa tsiku la Sabata ndi amene amapita kukapuma ndipo anabwera kwa wansembe Yehoyada.
10 Le prêtre remit aux chefs de centaines les lances et les boucliers qui avaient appartenu au roi David et qui se trouvaient dans la maison de l'Éternel.
Ndipo wansembeyo anawapatsa asilikaliwo mikondo ndi zishango zimene zinali za mfumu Davide ndipo zinali mʼNyumba ya Yehova.
11 La garde se tenait, chacun l'arme à la main, depuis le côté droit de la maison jusqu'au côté gauche de la maison, le long de l'autel et de la maison, autour du roi.
Alondawo, aliyense ali ndi chida mʼmanja mwake, anayima mozungulira mfumu, pafupi ndi guwa lansembe ndi nyumbayo, kuchokera mbali ya kummwera mpaka mbali ya kumpoto kwa nyumbayo.
12 Alors on fit sortir le fils du roi, on lui mit la couronne et on lui donna l'alliance; on le fit roi et on l'oignit; on battit des mains et on dit: « Vive le roi! »
Yehoyada anatulutsa mwana wa mfumuyo namuveka chipewa chaufumu ndipo anamupatsa Buku la Chipangano ndi kumuyika kukhala mfumu. Iwo anamudzoza ndipo anthu anamuwombera mʼmanja akufuwula kuti, “Mfumu ikhale ndi moyo wautali!”
13 Lorsqu'Athalie entendit le bruit de la garde et du peuple, elle entra avec le peuple dans la maison de l'Éternel.
Ataliya atamva phokoso limene alonda ndi anthuwo amachita, anapita ku Nyumba ya Yehova kumene kunali anthuwo.
14 Elle regarda, et voici, le roi se tenait près de la colonne, selon la tradition, avec les chefs et les trompettes près du roi; et tout le peuple du pays se réjouissait et sonnait des trompettes. Alors Athalie déchira ses vêtements et s'écria: « Trahison! Trahison! »
Iye anayangʼana naona mfumu itayima pa chipilala, potsata mwambo waufumu. Atsogoleri a asilikali ndi oyimba malipenga anali pafupi ndi mfumuyo, ndipo anthu onse a mʼderalo ankasangalala ndi kuyimba malipenga. Pamenepo Ataliya anangʼamba mkanjo wake nafuwula kuti, “Kuwukira! Kuwukira!”
15 Le prêtre Jehoïada donna des ordres aux chefs de centaines qui étaient à la tête de l'armée, et leur dit: « Faites-la sortir entre les rangs. Tuez par l'épée tous ceux qui la suivent. » Car le prêtre avait dit: « Qu'elle ne soit pas tuée dans la maison de l'Éternel. »
Wansembe Yehoyada analamula atsogoleri a asilikali 100 amene amayangʼanira asilikaliwo kuti, “Mutulutseni ameneyo pakati panu ndipo muphe ndi lupanga aliyense amene adzamutsata.” Pakuti nʼkuti wansembeyo atanena kuti, “Ataliyayo asaphedwere mʼNyumba ya Yehova.”
16 Ils s'emparèrent donc d'elle; elle passa par le chemin d'entrée des chevaux dans la maison du roi, et c'est là qu'elle fut tuée.
Choncho anamugwira pamene amafika pa malo amene akavalo amalowera ku nyumba ya mfumu ndipo anamuphera pamenepo.
17 Jehojada fit une alliance entre l'Éternel, le roi et le peuple, pour qu'ils soient le peuple de l'Éternel, et entre le roi et le peuple.
Tsono Yehoyada anachititsa pangano pakati pa Yehova ndi mfumu ndi anthu kuti adzakhala anthu a Yehova. Iye anachititsanso pangano pakati pa mfumu ndi anthu.
18 Tout le peuple du pays se rendit à la maison de Baal et la démolit. Ils brisèrent complètement ses autels et ses images, et ils tuèrent Mattan, le prêtre de Baal, devant les autels. Le prêtre nomma des officiers sur la maison de Yahvé.
Anthu onse a mʼdzikomo anapita ku nyumba ya Baala nakayigwetsa. Iwo anaphwanya kotheratu maguwa ansembe ndi mafano ake ndipo anapha Matani wansembe wa Baala patsogolo pa maguwa pomwepo. Pamenepo wansembe Yehoyada anasankha oyangʼanira Nyumba ya Yehova.
19 Il prit les chefs de centaines, les Carites, les gardes et tout le peuple du pays; ils firent descendre le roi de la maison de l'Éternel et vinrent par le chemin de la porte des gardes à la maison du roi. Il s'assit sur le trône des rois.
Iye anatenga atsogoleri a asilikali 100 aja, alonda olonda nyumba yaufumu pamodzi ndi anthu onse a mʼdzikomo ndipo onse pamodzi anayitulutsa mfumu mʼNyumba ya Yehova ndi kukalowa ku nyumba yaufumu podzera pa chipata cha alonda. Ndipo mfumuyo inakhala pa mpando wake waufumu.
20 Tout le peuple du pays se réjouissait, et la ville était tranquille. Ils avaient tué Athalie par l'épée à la maison du roi.
Choncho anthu onse a mʼdzikomo anasangalala. Ndipo mu mzindamo munakhala bata chifukwa Ataliya nʼkuti ataphedwa ndi lupanga ku nyumba ya mfumu.
21 Joas était âgé de sept ans lorsqu'il commença à régner.
Yowasi anali wa zaka zisanu ndi ziwiri pamene anayamba kulamulira.

< 2 Rois 11 >